< Изход 32 >

1 А като видяха людете, че Моисей се забави да слезе от планината, людете се събраха срещу Аарона и му казаха: Стани, направи ни богове, които да ходят пред нас; защото тоя Моисей, чавекът, който ни изведе из Египетската земя, не знаем що му стана.
Anthu ataona kuti Mose akuchedwa kutsika mʼphiri, anasonkhana kwa Aaroni ndipo anati, “Bwera utipangire milungu imene idzititsogolera. Kunena za Mose amene anatitulutsa mʼdziko la Igupto, sitikudziwa chimene chamuchitikira.”
2 Аарон им каза: Извадете златните обеци, които са на ушите на жените ви, на синовете ви, и на дъщерите ви, и донесете ми ги.
Aaroni anawayankha kuti, “Vulani ndolo zagolide zimene avala akazi anu, ana anu aamuna ndi aakazi ndipo muzibweretse kwa ine.”
3 И тъй, всичките люде, извадиха златните обеци, които бяха на ушите им, и донесоха ги на Аарона.
Kotero anthu onse anavula ndolo zagolide ndi kubwera nazo kwa Aaroni.
4 А той, като ги взе от ръцете им, даде на златото образ с резец, след като направи леяно теле; и те рекоха: Тия са боговете ти, о Израилю, които те изведоха из Египетската земя.
Choncho Aaroni analandira golideyo ndipo anamuwumba ndi chikombole ndi kupanga fano la mwana wangʼombe. Kenaka anthu aja anati, “Inu Aisraeli, nayu mulungu wanu amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto.”
5 И като видя това, Аарон издигна олтар пред него; и Аарон прогласи, казвайки: Утре ще бъде празник Господу.
Aaroni ataona izi, anamanga guwa lansembe patsogolo pa mwana wangʼombeyo ndipo analengeza kuti, “Mawa kudzakhala chikondwerero cha Yehova.”
6 И на следния ден, като станаха рано, пожертвуваха всеизгаряне и принесоха примирителни приноси: после людете седнаха да ядат и да пият, и станаха да играят.
Kotero tsiku linalo anthu anadzuka mmamawa ndithu ndi kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Atatha kupereka nsembezo, anthuwo anakhala pansi nayamba kudya ndi kumwa. Kenaka anayimirira nayamba kuvina mwachilendo.
7 Тогава Господ каза на Моисея: Иди, слез, защото се развратиха твоите люде, които си извел из Египетската земя.
Pamenepo Yehova anati kwa Mose, “Tsika msanga, chifukwa anthu ako amene unawatulutsa mʼdziko la Igupto aja adziyipitsa kwambiri.
8 Скоро се отклониха от пътя, в който им съм заповядал да ходят; направиха си леяно теле, поклониха му се, пожертвуваха му и рекоха: Тия са боговете ти, о Израилю, които те изведоха из Египетската земя,
Iwo apatuka mwamsanga kuleka kutsatira zimene ndinawalamula. Ndiye adzipangira fano la mwana wangʼombe. Aligwadira ndi kuliperekera nsembe nʼkumati, ‘Inu Aisraeli, nayu mulungu wanu amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto.’”
9 Рече още Господ на Моисея: Видях тия люде, и, ето, коравовратни люде са;
Yehova anati kwa Mose, “Ine ndikuwadziwa anthu amenewa. Iwowa ndi ankhutukumve.
10 сега, прочее, остави Ме, за да пламне гневът Ми против тях и да ги изтребя; а тебе ще направя велик народ.
Chifukwa chake undileke kuti mkwiyo wanga uyake pa iwo ndi kuwawononga. Ndipo Ine ndidzakusandutsa kuti ukhale mtundu waukulu.”
11 Тогава Моисей се помоли на Иеова своя Бог, казвайки: Господи, защо пламна гневът Ти против людете Ти, които си извел из Египетската земя с голяма сила и мощна ръка?
Koma Mose anapempha chifundo cha Mulungu wake ndipo anati, “Chonde Yehova, chifukwa chiyani mwakwiyira anthu awa amene munawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu.
12 Защо да говорят египтяните, казвайки: За зло ги изведе, за да ги измори в планините и да ги изтреби от лицето на земята? Повърни се от разпаления Си гняв, и разкай се за туй зло, което възнамеряваш против людете Си.
Kodi mukufuna kuti Aigupto azinena kuti, ‘Munali ndi cholinga choyipa chofuna kuwaphera ku mapiri kuno ndi kuwawonongeratu pa dziko lapansi pamene munkawatulutsa ku Igupto kuja?’ Ayi, chonde mkwiyo wanu woyaka ngati motowu ubwezeni ndipo sinthani maganizo ofunira zoyipa anthu anu.
13 Спомни си за слугата си Авраама, Исаака и Израиля, на които си се клел в Себе Си, като си им казал: Ще размножа потомството ви като небесните звезди, и тая цялата земя, за която говорих, ще дам на потомството ви, и те ще я наследят за винаги.
Kumbukirani atumiki anu, Abrahamu, Isake, Israeli ndi zija munawalonjeza polumbira pa dzina lanu kuti, ‘Ine ndidzachulukitsa zidzukulu zanu ndipo zidzakhala zambiri ngati nyenyezi zakumwamba. Zidzukulu zanuzo ndidzazipatsa dziko lonseli limene ndinalonjeza. Dziko limeneli lidzakhala lawo nthawi zonse.’”
14 Тогава Господ се разкая за злото, което бе казал, че ще направи на людете Си.
Choncho Yehova analeka ndipo sanawachitire choyipa anthu ake monga anaopsezera.
15 И така, Моисей се обърна и слезе от планината с двете плочи на свидетелството в ръцете си, плочи написани и от двете страни; от едната страна и от другата бяха написани.
Mose anatembenuka ndi kutsika phiri miyala iwiri ya pangano ili mʼmanja mwake. Miyalayi inalembedwa mbali zonse, kutsogolo ndi kumbuyo komwe.
16 Плочите бяха Божие дело; и написаното беше Божие писание начертано на плочите:
Miyalayi anayikonza ndi Mulungu. Malembawo analemba ndi Mulungu mozokota pa miyalapo.
17 А като чу Исус Навиев гласа на людете, които викаха, рече на Моисея: Боен глас има в стана.
Pamene Yoswa anamva phokoso la anthu anati kwa Mose, “Ku msasa kuli phokoso la nkhondo.”
18 А той каза: Това не е глас на вик за победа, нито глас на вик за поражение; но глас на пеене чувам аз.
Mose anayankha kuti, “Phokoso limeneli sindikulimva ngati phokoso la opambana nkhondo, kapena kulira kwa ongonjetsedwa pa nkhondo. Koma ndikulimva ngati phokoso la anthu amene akuyimba.”
19 И като се приближи до стана, видя телето и игрите; и пламна Моисеевия гняв, така че хвърли плочите от ръцете си, и строши ги под планината.
Mose atayandikira msasa ndi kuona mwana wangʼombe ndiponso kuvina, anakwiya kwambiri ndipo anaponya pansi miyala imene inali mʼmanja mwake, ndi kuyiphwanya pa tsinde la phiri.
20 Тогава взе телето, което бяха направили, изгори го с огън, и като го стри на ситен прах, разпръсна праха по водата и накара Израилевите чада да я изпият.
Ndipo iye anatenga mwana wangʼombe amene anthu anapanga uja ndi kumuwotcha pa moto ndi kumuperapera ndikukhala ngati fumbi. Kenaka anawaza fumbilo mʼmadzi ndi kuwamwetsa Aisraeli madziwo.
21 После рече Моисей на Аарона: Що ти сториха тия люде та си им навлякъл голям грях?
Tsono Mose anafunsa Aaroni kuti, “Kodi anthu awa anakuchita chiyani kuti uwachimwitse koopsa chotere?”
22 И Аарон каза: Да не пламне гневът на господаря ми; ти знаеш, че людете упорствуват към злото.
Aaroni anayankha kuti, “Musakwiye mbuye wanga. Inu mukudziwa kuti anthu awa ndi ovuta.
23 Понеже ми рекоха: Направи ни богове, които да ходят пред нас; защото тоя Моисей, човекът, който ни изведе из Египетската земя, не знаем, що му стана.
Iwo anati kwa ine, ‘Bwera utipangire milungu imene idzititsogolera. Kunena za Mose amene anatitulutsa ife mʼdziko la Igupto, sitikudziwa chimene chamuchitikira.’
24 И аз им рекох: Който има злато, нека си го извади; и така те ми го дадоха. Тогава го хвърлих в огъня; и излезе това теле.
Choncho ine ndinawawuza kuti, ‘Aliyense amene ali ndi zokometsera zagolide azivule.’ Choncho iwo anandipatsa golide, ndipo ndinamuponya pa moto ndi kupanga fano la mwana wangʼombeyu.”
25 А като видя Моисей, че людете бяха съблечени, (защото Аарон ги бе съблякъл за срам между неприятелите им),
Mose anaona kuti anthuwo anali osokonezekadi chifukwa Aaroni anawalekerera mpaka kusanduka anthu osekedwa pakati pa adani awo.
26 застана Моисей при входа на стена и рече: Който е от към Господа нека дойде при мене. И събраха се при него всичките Левийци.
Choncho iye anayima pa chipata cholowera mu msasa ndipo anati, “Aliyense amene ali mbali ya Yehova abwere kwa ine.” Ndipo Alevi onse anapita mbali yake.
27 И рече им: Така говори Господ, Израилевият Бог: Препашете всички меча на бедрото си, минете насам натам от врата на врата през стана, и ибийте всеки брата си, и всеки другаря си и всеки ближния си.
Ndipo iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene Yehova Mulungu wa Israeli akunena, ‘Pitani ku misasa konse, mulowe ku zipata zonse ndipo aliyense akaphe mʼbale wake, kapena mnzake kapena mnansi wake.’”
28 И Левийците сториха според Моисеевата дума; и в тоя ден паднаха от людете около три хиляди мъже.
Alevi anachita zomwe Mose analamula, ndipo tsiku limenelo panafa anthu pafupifupi 3,000.
29 Защото Моисей беше казал: Посветете себе си днес Господу, като се дигнете всеки против сина си и против брата си, за да ви се даде днес благоволение.
Kenaka Mose anati, “Lero mwadzipatula nokha kukhala ansembe otumikira Yehova. Mwachita izi popeza aliyense wa inu wapha mwana wake kapena mʼbale wake. Tsono lero Yehova wakudalitsani.”
30 А на следния ден Моисей рече на людете: Вие сте сторили голям грях; но сега ще се възкача към Господа, дано да мога да Го умилостивя за греха ви.
Mmawa mwake Mose anati kwa anthu onse, “Inu mwachita tchimo lalikulu. Koma tsopano ine ndipita ku phiri kwa Yehova mwina ndikatha kukupepeserani chifukwa cha tchimo lanu.”
31 Тогава Моисей се върна при Господа и рече: Уви! тия люде сториха голям грях, че си направиха златни богове.
Kotero Mose anabwereranso kwa Yehova ndipo anati, “Aa! Anthu awa achita tchimo lalikulu! Iwo adzipangira milungu yagolide.
32 Но сега, ако щеш прости греха им, - но ако не, моля Ти се, мене заличи от книгата, която си написал.
Koma tsopano, chonde akhululukireni tchimo lawo. Ngati simutero, ndiye mundifute ine mʼbuku limene mwalemba.”
33 Но Господ рече на Моисея; Който е съгрешил против Мене, него ще залича от книгата Си.
Yehova anamuyankha Mose kuti, “Ndidzafuta mʼbuku aliyense amene wandichimwira.
34 А ти иди сега, води людете на мястото, за което съм ти говорил; ето, ангелът Ми ще ходи пред тебе; обаче в деня, когато го посетя, ще въздам върху тях наказанието на греха им.
Tsopano pita ukawatsogolere anthu kumalo kumene ine ndinanena, ndipo mngelo wanga adzakutsogolerani. Komabe, nthawi yanga ikadzafika kuti ndiwalange, ndidzawalanga chifukwa cha tchimo lawo.”
35 Така Господ порази людете, за гдето направиха телето, което Аарон изработи.
Ndipo Yehova anawakantha anthuwo ndi mliri chifukwa anawumiriza Aaroni kuti awapangire fano la mwana wangʼombe.

< Изход 32 >