< Изход 20 >
1 Тогава Бог изговори всички тия думи, като каза:
Ndipo Mulungu anayankhula mawu onse awa nati:
2 Аз съм Иеова твоят Бог, Който те изведох из Египетската земя, из дома на робството.
“Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo.
3 Да нямаш други богове освен мене.
“Usakhale ndi milungu ina koma Ine ndekha.”
4 Не си прави кумир, или каквото да било подобие на нещо, което е на небето горе, или което е на земята долу, или което е във водата под земята;
“Usadzipangire chofanizira chinthu chilichonse chakumwamba kapena cha pa dziko lapansi kapena cha mʼmadzi a pansi pa dziko.
5 да не им се кланяш нито да им служиш, защото Аз Господ, твоят Бог, съм Бог ревнив, Който въздавам беззаконието на бащите върху чадата до третото и четвъртото поколение на ония, които Ме мразят,
Usazigwadire kapena kuzipembedza, pakuti Ine Yehova Mulungu wako, ndine Mulungu wansanje, wolanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo mpaka mʼbado wachitatu ndi wachinayi wa iwo amene amadana nane.
6 а показвам милости към хиляда поколения на ония, които Ме любят и пазят Моите заповеди.
Koma ndimaonetsa chikondi chosasinthika ku mibado miyandamiyanda ya anthu amene amandikonda, ndi kusunga malamulo anga.
7 Не изговаряйте напразно Името на Господа твоя Бог; защото Господ няма да счита безгрешен онзи, който изговаря напразно Името Му.
“Usagwiritse ntchito molakwika dzina la Yehova Mulungu wako, pakuti Yehova adzamutenga kukhala wochimwa aliyense amene akugwiritsa ntchito dzina lakelo molakwika.
8 Помни съботния ден, за да го освещаваш.
“Uzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika.
9 Шест дни да работиш и да вършиш всичките си дела;
Uzigwira ntchito zako zonse masiku asanu ndi limodzi.
10 а на седмия ден, който е събота на Господа твоя Бог, да не вършиш никаква работа, ни ти, ни слугата ти, ни слугинята ти, нито добитъкът ти, нито чежденецът, който е отвътре вратите ни;
Koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, tsiku loperekedwa kwa Yehova Mulungu wako. Tsiku limeneli musagwire ntchito iliyonse, inuyo kapena mwana wanu wamwamuna kapena mwana wanu wamkazi, wantchito wanu wamwamuna kapena mdzakazi wanu, ziweto zanu kapena mlendo amene akukhala mʼmudzi mwanu.
11 защото в шест дни Господ направи небето и земята, морето и всичко що има в тях, а на седмия ден си почина; затова Господ благослови съботния ден и го освети.
Pakuti Yehova anapanga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zimene zili mʼmenemo mʼmasiku asanu ndi limodzi. Iye anapuma pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Kotero Yehova anadalitsa tsiku la Sabata kuti likhale loyera.
12 Почитай баща си и майка си, за да се продължават дните ти на земята, която ти дава Господ твоя Бог.
“Lemekeza abambo ako ndi amayi ako kuti ukhale ndi moyo wautali mʼdziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa.
16 Не свидетелствувай лъжливо против ближния си.
“Usapereke umboni womunamizira mnzako.
17 Не пожелавай къщата на ближния си, не пожелавай жената на ближния си, нито вола му, нито осела му, нито какво да е нещо, което е на ближния ти.
“Usasirire nyumba ya mnzako. Usasirire mkazi wa mnzako kapena wantchito wake wamwamuna kapena mdzakazi wake, ngʼombe yake kapena bulu wake, kapena chilichonse cha mnzako.”
18 И всичките люде гледаха гърмежите, светкавиците, гласа на тръбата и димящата планина; и, като видяха, людете се оттеглиха и застанаха надалеч.
Pamene anthu ankamva mabingu ndi kuona ziphaliwali ndi kumvanso lipenga ndi kuona utsi umene umafuka mʼphiri, ananjenjemera ndi mantha. Ndipo iwo anayima patali.
19 И рекоха на Моисея: Ти говори на нас, и ние ще слушаме; а Бог да не ни говори, за да не умрем.
Ndipo anati kwa Mose, “Iwe utiyankhule ndipo tidzamvera. Koma usalole kuti Mulungu atiyankhule, tingafe.”
20 Но Моисей рече на людете: Не бойте се; Бог дойде да ви опита, и за да има всред вас страх от Него, та да не съгрешавате.
Koma Mose anati kwa anthuwo, “Musachite mantha. Mulungu wabwera kudzakuyesani kuti mukhale ndi mtima woopa Mulungu kuti musamuchimwire.”
21 Така людете стояха надалеч. А Моисей се приближи пре мрака, гдето беше Бог.
Anthu aja anayima patali koma Mose anayandikira mtambo wakuda kumene kunali Mulungu.
22 Тогава рече Господ на Моисея: Така да кажеш на израилтяните: Вие сами видяхте, че ви говорих от небето.
Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Awuze izi Aisraeli: ‘Inu mwaona nokha kuti Ine ndakuyankhulani kuchokera kumwamba.
23 Покрай Мене да не правите и сребърни богове, нито да си правите и златни богове.
Choncho musadzipangire milungu yasiliva kapena yagolide kuti muziyipembedza pamodzi ndi Ine.’”
24 От пръст Ми издигай олтар, и жертвувай на него всеизгарянията си и примирителните си приноси, овците си и говедата си. На всяко място, гдето ще правя да се помни Името Ми, ще дохождам при тебе и ще те благославям.
Mundimangire guwa ladothi ndipo muziperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe zanu. Pamalo paliponse pamene Ine ndidzakonza kuti muzinditamandirapo, ndidzabwera ndi kukudalitsani.
25 Но ако ти Ми издигнеш каменен олтар, да го не съзидаш от дялани камъни; защото ако дигнеш на него сечиво, ще го оскверниш.
Ngati mudzandimangira guwa lansembe lamiyala, musagwiritse ntchito miyala yosema, pakuti mudzalidetsa mukadzagwiritsa ntchito zida.
26 И да се не качваш на олтара Ми по стъпала, за да се не открие голотата ти на него.
Musamakwere pa makwerero popita pa guwa langa lansembe kuti mungaonetse maliseche anu.