< Второзаконие 8 >
1 Внимавайте да вършите всичките заповеди, които днес ви заповядвам, за да живеете, да се умножите и да влезете да завладеете земята, за която се е клел Господ на бащите ви.
Samalani potsata lamulo lililonse limene ndikukupatsani lero, kuti mukhale ndi moyo ndi kuchulukana kuti mulande ndi kulowa mʼdziko limene Yehova analumbira kuti adzapereka kwa makolo anu.
2 И да помниш целия път, по който Господ твоят Бог те е водил през тия четиридесет години из пустинята, за да те смири и да те изпита, за да узнае що има в сърцето ти, дали ще пазиш заповедите Му, или не.
Kumbukirani mmene Yehova Mulungu wanu anakutsogolerani njira yonse mʼchipululu kwa zaka makumi anayi, kukutsitsani ndi kukuyesani kuti adziwe chimene chinali mu mtima mwanu ngati mungathe kusunga malamulo ake kapena ayi.
3 И те смири, и като те остави да огладнееш, храни те с манна, (която беше храна непозната на тебе и непозната на бащите ти), за да те научи, че човек не живее само с хляб, но че човек живее с всяко слово, което излиза из Господната уста.
Iye anakutsitsani nakumvetsani njala kenaka nʼkukudyetsani mana amene anali osadziwika kwa inu kapena makolo anu, kuti akuphunzitseni kuti munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha koma ndi mawu aliwonse ochokera mʼkamwa mwa Yehova.
4 Облеклото ти не овехтя на тебе нито ногата ти отече през тия четиридесет години.
Mʼzaka makumi anayi zimenezi, zovala zanu sizinangʼambike ndipo mapazi anu sanatupe.
5 Да вземеш, прочее, в съображение в сърцето си, че както човек наказва сина си, така и Господ твоят Бог наказва тебе.
Tsono dziwani mu mtima mwanu kuti monga abambo amalanga mwana wawo, momwemonso Yehova Mulungu wanu amakulangani.
6 За това, да пазиш заповедите на Господа твоя Бог, да ходиш в пътищата Му и да се боиш от Него.
Samalirani malamulo a Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira yake ndi kumuopa Iye.
7 Защото Господ твоят Бог те завежда в добра земя, в земя богата с водни потоци, които извират в долини и планини;
Pakuti Yehova Mulungu wanu akukulowetsani mʼdziko labwino, dziko lokhala ndi mitsinje ndi mathawale a madzi, akasupe oyenderera mu zigwa ndi mʼmapiri,
8 в земя богата с жито, ечемик, лозя, смокини и нарове; в земя богата с маслини и мед;
dziko lokhala ndi tirigu ndi barele, mpesa ndi mitengo ya mkuyu, makangadza, mafuta a olivi ndi uchi;
9 в земя гдето не ще ядеш хляб оскъдно и в който не ще си в нужда от нищо; в земя чиито камъни са желязо, и от чиито планини ще копаеш мед.
dziko limene buledi sadzasowa ndipo simudzasowa chilichonse; dziko limene miyala yake ndi chitsulo ndipo ku mapiri ake mukhoza kukumbako mkuwa.
10 Ще ядеш и ще се наситиш, и ще благословиш Господа твоя Бог за добрата земя, която ти е дал.
Mukadya ndi kukhuta, yamikani Yehova Mulungu wanu chifukwa cha dziko labwino limene wakupatsani.
11 Внимавай да не забравиш Господа твоя Бог и да не престъпваш заповедите Му, съдбите Му и повеленията Му, които днес ти заповядвам,
Samalani kuopa kuti mungayiwale Yehova Mulungu wanu posasunga malamulo, zikhazikitso ndi malangizo ake amene ndikukupatsani lero,
12 да не би, като ядеш и се наситиш и построиш добри къщи и живееш в тях,
kuopa kuti mukadya ndi kukhuta, mukamanga nyumba zabwino ndi kukhalamo,
13 и като се умножат говедата и овците ти и се умножат среброто ти и златото ти, и се умножи всичко що имаш,
ndi pamene ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu zaswana, ndi siliva ndi golide wanu wachuluka ndiponso kuti zonse zimene muli nazo zachuluka,
14 тогава да се надигне сърцето ти и да забравиш Господа твоя Бог, Който те е извел из Египетската земя, из дома на робството;
mtima wanu udzayamba kunyada ndi kuyiwala Yehova Mulungu wanu, amene anakutulutsani ku Igupto, kukuchotsani ku dziko la ukapolo.
15 Който те преведе през голямата и страшна пустиня, гдето имаше горителни змии, скорпии и сухи безводни змии; Който ти извади вода из кременливия камък;
Iye anakutsogolerani kudutsa mʼchipululu chachikulu ndi chochititsa mantha, dziko lija la ludzu ndi lopanda madzi, lokhala ndi njoka zaululu ndi zinkhanira. Iye anatulutsa madzi kuchokera mʼthanthwe lowuma.
16 Който те храни в пустинята с манна, храна която не знаеха бащите ти, за да те смири и да те изпита, да ти направи добро в сетнините ти;
Iye anakupatsani mana kuti mudye mʼchipululu, zinthu zoti ngakhale makolo anu sanazidziwe, kuti akuchepetseni ndi kukuyesani ndipo kuti pa mapeto pake zikuyendereni bwino.
17 и да не би да речеш в сърцето си: Моята мощ и силата на моята ръка ми спечелиха това богатство.
Mu mtima mwanu mukhoza kuganiza kuti, “Mphamvu zanga ndi kulimbika kwa dzanja langa ndi zimene zandilemeretsa chonchi.”
18 Но да помниш Господа твоя Бог, защото Той е, Който ти дава сила да придобиваш богатство; за да утвърди завета, за който се е клел на бащите ти, както прави днес.
Koma kumbukirani Yehova Mulungu chifukwa ndi amene amakupatsani mphamvu zopezera chuma chimenechi kuti atsimikize pangano limene analumbira kwa makolo anu, monga liliri lero lino.
19 Но ако забравиш Господа твоя Бог и отидеш след други богове, служиш им и им се поклониш, заявявам ви днес, че съвсем ще бъдете изтребени.
Ine ndine mboni yokutsutsani lero lino, kuti mukayiwala Yehova Mulungu wanu ndi kutsata milungu ina nʼkumayigwadira, mudzawonongeka ndithu.
20 Ще бъдете изтребени както народите, които Господ изтребва от пред вас, защото не послушахте гласа на Господа вашия Бог.
Monga mitundu ina ya anthu imene Yehova anayiwononga pamaso panu, inunso mudzawonongedwa chifukwa chosamvera Yehova Mulungu wanu.