< Второзаконие 12 >

1 Ето повеленията и съдбите, на които трябва да внимавате, за да ги вършите, през всичкото време, колкото живеете на света, в земята, която Господ Бог на бащите ти ти дава да притежаваш:
Awa ndi malangizo ndi malamulo amene muyenera kusamalitsanso kuti muwatsatire mʼdziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu wakupatsani kuti mutenge pa nthawi yonse imene muti mudzakhale mʼdzikomo.
2 Да разорите всичките места гдето народите, които ще завладеете, са служили на боговете си, по високите планини, по хълмовете и под всяко зелено дърво;
Muwonongeretu kwathunthu malo onse a pamwamba pa mapiri ataliatali ndi pa mapiri angʼonoangʼono ndi pansi pa mtengo uliwonse wotambalala pamene mitundu imene muyilande dzikolo ankapembedzerapo milungu yawo.
3 и да съсипете жертвениците им, да строшите стълбовете им, да изгорите с огън ашерите им, да съсечете изваяните образи на боговете им и да изличите имената им от онава място.
Mugumule maguwa awo ansembe, ndi kuphwanya miyala yawo yachipembedzo ndipo mutenthe pa moto mafano awo a Asera: mugwetse mafano a milungu yawo ndi kufafaniza mayina awo mʼmalo amenewo.
4 А спрямо Господа вашия Бог да не постъпвате така;
Musapembedze Yehova Mulungu wanu monga mmene amachitira iwowa.
5 но да търсите мястото, което Господ вашият Бог избере между всичките ви племена, за да настани там Името Си, да бъде жилището Му, и там да идете;
Koma inu muzifunafuna kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe pakati pa mafuko anu kuti ayikeko dzina lake ndi kukhalako. Ku malo amenewa muyenera kupitako.
6 там да принасяте всеизгарянията си, жертвите си, десетъците си, възвишаемите приноси на ръцете си, обреците си, доброволните си приноси и първородните от говедата и от овците си;
Kumeneko muzipititsako zopereka zanu ndi nsembe zanu zopsereza, ndi chakhumi chanu ndi mphatso zapadera zimene munalonjeza kupereka ndi zopereka zanu zaufulu ndi ana oyamba a ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu.
7 и там, пред Господа вашия Бог, да ядете; и да се веселите, вие и челядите ви, във всичките си предприятия, и в коквото те е благословил Господ твоят Бог.
Kumeneko, pamaso pa Yehova Mulungu wanu, inu ndi mabanja anu mudzadya ndi kusangalalako pa china chilichonse chimene mudzakhudza, chifukwa Yehova Mulungu wanu wakudalitsani.
8 Да не правите никак, както ние днес правим тук, - всеки каквото му се вижда за добро.
Musadzachite monga tikuchitira lero lino, aliyense kumachita zimene akuona kuti ndi zoyenera,
9 Защото още не сте дошли в почивката и в наследството, което Господ вашият Бог ви дава.
pakuti simunafike ku malo opumulirako ndi ku cholowa chimene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
10 Но когато преминете Иордан и се заселите в земята, която Господ вашият Бог ви дава да наследите, и ви успокои от всичките неприятели около вас, та живеете безопасно,
Koma mudzawoloka Yorodani ndi kukhazikika mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu, ndipo Iye adzakupatsani inu mpumulo ku adani anu okuzungulirani kuti mukhale motchinjirizidwa.
11 тогава на мястото, което Господ вашият Бог избере, за да настани Името Си, там принасяйте всичко що ви заповядвам: всеизгарянията си, жертвите си, десетъците си, възвишаемите приноси на ръцете си и всичките отборни обреци, които сте обрекли Господу;
Tsono kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe kuti azikhalako muzikabweretsako chilichonse chimene ndikulamulirani inu: zopereka ndi nsembe zanu zopsereza, chakhumi chanu ndi mphatso zapadera, ndi chuma chanu chonse chosankhika chimene munalonjeza kwa Yehova.
12 и да се веселите пред Господа вашия Бог, вие, синовете ви, дъщерите ви, слугите ви, слугините ви, и левитинът, който е отвътре портите ви (защото той няма нито наследство с вас).
Ndipo kumeneko inu mukasangalale pamaso pa Yehova Mulungu wanu pamodzi ndi ana anu aamuna ndi ana anu aakazi, antchito anu aamuna ndi adzakazi anu, ndi Alevi a mʼmidzi yanu, amene alibe gawo kapena cholowa chawochawo.
13 Внимавай на себе си да не би да принасяш всеизгарянията си на кое да било място, което виждаш;
Musamalitse kuti musakaphere nsembe zanu zopsereza paliponse pamene mungafune.
14 но на мястото, което Господ избере в едно от племената ти, там да принасяш всеизгарянията си, и там да вършиш всичко що ти заповядвам.
Mukaphere pa malo okhawo amene Yehova adzawasankhe mwa limodzi la mafuko anu, ndipo kumeneko mukasunge chilichonse chimene ndikulamulireni.
15 Бива обаче да колиш и да ядеш месо във всичките си жилища до колкото желае душата ти, според колкото Господ твоят Бог ще те е благословил; нечистият и чистият могат да ядат от него, както от сърна и както от елен.
Koma mukhoza kumapha ziweto zanu mʼmizinda iliyonse ndi kudya nyama yake mmene mungafunire, ngati kuti ndi agwape kapena mbawala, monga mwadalitso limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. Woyeretsedwa ndi wosayeretsedwa akhoza kuyidya.
16 Само кръвта да не ядете; да я изливате на земята като вода.
Koma musamadye magazi. Muziwathira pansi ngati madzi.
17 А не бива да ядеш в жилищата си десетъка от житото си, или от виното си, или от дървеното си масло, или първородните от говедата си, или от овците си, или кой да било от обреците, които си обрекъл, или доброволните си приноси, или възвишаемите приноси на ръцете си;
Musamadyere mʼmizinda yanu chakhumi cha tirigu wanu ndi vinyo watsopano ndi mafuta, kapena za ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu ndi nkhosa zanu, kapena chilichonse chimene mwalonjeza kuchipereka, nsembe zanu zaufulu, kapena mphatso zapadera,
18 но пред Господа твоя Бог да ги ядеш, на мястото, което Господ твоят Бог избере, ти, синът ти, дъщерята ти, слугата ти, слугинята ти и левитинът, който е отвътре портите ти; и да се веселиш пред Господа твоя Бог във всичко на каквото туриш ръка.
mʼmalo mwake, muzidya pamaso pa Yehova Mulungu wanu, kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhira inu, ana anu aamuna ndi aakazi, antchito anu aamuna ndi adzakazi anu, ndi Alevi ochokera mʼmizinda yanu, ndipo mudzasangalale pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa chilichonse chimene mudzachikhudza.
19 Внимавай на себе си да не пренебрегваш левитина до тогаз, до когато живееш на земята си.
Muonetsetse kuti musawataye Alevi pa masiku onse amene mukhale mʼdziko lanumo.
20 Когато Господ твоят Бог разшири пределите ти, според както ти се е обещал, а ти речеш: Ще ям месо, защото душата ти желае да яде месо, то бива да ядеш месо до колкото желае душата ти.
Yehova Mulungu wanu akadzakulitsa dziko lanu monga anakulonjezerani, ndipo mukapukwa nyama mumanena kuti, “Ndikufuna nyama,” pamenepo mudzadya mmene mungafunire.
21 Ако е много далеч от тебе мястото, което Господ твоят Бог избере, за да настани Името Си там, тогава да колиш от говедата и от овците, които Господ ти е дал, според както ти заповядах, и да ядеш в жилищата си до колкото желае душата ти.
Ngati malo amene Yehova Mulungu wanu awasankha kuti ayike Dzina lake ali kutali kwambiri ndi inu, mukhoza kupha ziweto pakati pa ngʼombe ndi nkhosa zimene Yehova wakupatsani, monga ndinakulamulani, ndipo mʼmizinda yanuyanu mukhoza kuzidya mmene mungafunire.
22 Както се яде сърна и елен, така да ядеш и тия; нечистият и чистият могат еднакво да ядат от тях.
Muzidye ngati mukudya gwape kapena mbawala. Onse oyeretsedwa monga mwa mwambo ndi osayeretsedwa omwe akhoza kudya.
23 Само строго да се вардиш да не ядеш кръвта: защото кръвта е животът, и не бива да ядеш живота с месото.
Koma muonetsetse kuti musadye magazi, chifukwa magazi ndi moyo, ndipo musamadye moyo pamodzi ndi nyama.
24 Да я не ядеш: да я изливаш на земята като вода.
Inu musamadye magazi, muziwathira pansi ngati madzi.
25 Да я не ядеш, за да бъде добре и на тебе и на чадата ти след тебе, когато вършиш онова, което е право пред Господа.
Musamadye magazi kuti zikuyendereni bwino inu pamodzi ndi ana anu a pambuyo panu, popeza mudzakhala mukuchita zoyenera pamaso pa Mulungu.
26 Само колкото неща си посветил и обреците си да взимаш, та да отиваш на мястото, което избере Господ,
Koma mutenge zinthu zanu zoyeretsedwa ndi china chilichonse chimene munalumbira kupereka, ndi kupita kumalo kumene Yehova adzasankhe.
27 и да принасяш всеизгарянията си, месото и кръвта, върху олтара на Господа твоя Бог. Кръвта на жертвите ти да се излива върху олтара на Господа твоя Бог, а месото ти да ядеш.
Mupereke nsembe zanu zopsereza pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu, nyama pamodzi ndi magazi omwe. Magazi a nsembe zanu athiridwe pambali pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu, koma nyamayo mukhoza kudya.
28 Внимавай и слушай всички тия думи, които ти заповядвам, за да бъде добре на тебе и на чадата ти след тебе до века, когато вършиш онова, което е добро и право пред Господа твоя Бог.
Onetsetsani kuti muzimvera mawu onsewa amene ndikukupatsani kuti zinthu zizikuyenderani bwino nthawi zonse inu ndi ana anu chifukwa mudzakhala mukuchita zabwino ndi zoyenera pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
29 Когато Господ твоят Бог изтреби от пред тебе народите на земята, гдето ти отиваш да ги завладееш, и ти ги завладяваш и се заселиш в земята им,
Yehova Mulungu wanu adzachotsa pamaso panu mitundu ya anthu amene mukufuna kuwathira nkhondo ndi kuwalanda dzikolo. Koma mukawapirikitsa ndi kukhazikika mʼdziko lawo,
30 внимавай на себе си да се не улавяш в примка да ги последваш, когато бъдат изтребени от пред тебе; и да не изпитваш за боговете им, като казваш: Как служат тия народи на боговете си? - за да направя и аз така.
ndipo pamene iwo awonongeka pamaso panu, samalirani kuti musakodwe mu msampha pa kufufuza za milungu yawo, nʼkumati, “Kodi anthu a mitunduwa amatumikira bwanji milungu yawo? Ifenso tichita momwemo.”
31 Да не постъпваш така спрямо Господа твоя Бог; защото те са извършили за боговете си всяка мерзост, която Господ мрази; понеже за боговете си са изгаряли с огън и синовете си и дъщерите си.
Musapembedze Yehova Mulungu wanu momwe amachitira iwowo, chifukwa popembedza milungu yawoyo amachita zonyansa zamitundumitundu zimene Yehova amadana nazo. Amatentha ngakhale ana awo aamuna ndi aakazi pa moto ngati nsembe za kwa milungu yawo.
32 Внимавайте да вършите всичко що ви заповядвам; да не притуряш на него, нито да отнимаш от него.
Onetsetsani kuti mukuchita zimene ndikukulamulirani. Musawonjezerepo kapena kuchotserapo.

< Второзаконие 12 >