< 4 Царе 5 >
1 А Нееман, военачалникът на сирийския цар, беше човек велик и почитан пред господаря си, понеже чрез него Господ бе дал избавление на Сирия; при това, беше човек силен и храбър, но беше прокажен.
Tsono Naamani anali mtsogoleri wa gulu lankhondo a mfumu ya ku Aramu. Iye anali munthu wodalirika pamaso pa mbuye wake ndipo anali wokondedwa kwambiri, chifukwa kudzera mwa iye Yehova anapambanitsa Aaramu. Anali msilikali wolimba mtima, koma anali ndi khate.
2 И сирийците бяха излезли на чети, и бяха довели от Израилевата земя една малка мома пленница; и тя слугуваше на Неемановата жена.
Tsono magulu a Aaramu anapita ku nkhondo ndipo anakagwira ukapolo mtsikana wamngʼono wa ku Israeli, ndipo ankatumikira mkazi wa Naamani.
3 И рече на Господарката си: Ако беше господарят ми при пророка, който е в Самария, и той би го изцелил от проказата му!
Mtsikanayo anawuza mkazi wa Naamani kuti, “Mbuye wanga akanapita kukaonana ndi mneneri amene amakhala ku Samariya, akanachiritsidwa khate lawo.”
4 Тогава влезе Нееман та съобщи на господаря си, казвайки: Така и така рече момата, която е от Израилевата земя.
Naamani anapita kwa mbuye wake kukamuwuza zomwe mtsikana wochokera ku Israeli ananena.
5 И рече сирийският цар: Стани, иди, и ще пратя писмо до Израилевия цар. И тъй, той отиде, вземайки в ръката си десет таланта сребро, шест хиляди жълтици, и десет премени дрехи.
Mfumu ya ku Aramu inayankha kuti, “Iwe uyenera kupita. Ine ndilembera kalata mfumu ya ku Israeli.” Choncho Naamani ananyamuka kupita ku Samariya, atatenga ndalama za siliva 30,000, ndalama zagolide 6,000 ndiponso zovala khumi za pa chikondwerero.
6 И донесе писмоо на Израилевия цар, в което се казваше: Като пристигне това писмо до тебе, ето, същевременно пратих до тебе слугата си Неемана, за да го изцелиш от проказата му.
Kalata imene anapita nayo kwa mfumu ya ku Israeli inali ndi mawu awa: “Taonani, ndikutumiza Naamani mtumiki wanga pamodzi ndi kalatayi kwa inu kuti mumuchiritse khate lake.”
7 А Израилевият цар, като прочете писмото, раздра дрехите си и рече: Бог ли съм аз за да умъртвявам и да съживявам, та праща до мене да изцеря човека от проказата му? Моля, прочее, разсъдете и вижте как търси повод за скарване с мене.
Mfumu ya ku Israeli itangowerenga kalatayo, inangʼamba mkanjo wake ndipo inati, “Kodi ine ndine Mulungu? Kodi ndingathe kupha kapena kupereka moyo? Chifukwa chiyani munthu ameneyu wanditumizira munthu woti ndimuchiritse khate lake? Taonani, iyeyu akungofuna kuti apeze chifukwa choyambanirana nane!”
8 А Божият човек Есей, като чу, че Израилевият цар раздрал дрехите си, прати до царя да рекат: Защо си раздрал дрехите си? Нека дойде сега при мене, и ще познае, че има порок в Израиля.
Elisa munthu wa Mulungu atamva kuti mfumu ya ku Israeli yangʼamba mkanjo wake, anatumiza uthenga uwu: “Chifukwa chiyani mwangʼamba mkanjo wanu? Mutumizeni munthuyo kwa ine ndipo iyeyo adzadziwa kuti muli mneneri mu Israeli.”
9 И така, Нееман дойде с конете си и с колесниците си та застана при вратата на Елисеевата къща.
Choncho Naamani anapita pamodzi ndi akavalo ake ndi magaleta nakayima pa khomo la nyumba ya Elisa.
10 И Елисей прати до него човек да каже: Иди, окъпи се седем пъти в Иордан; и ще се обновят месата ти, и ще се очистиш.
Elisa anatumiza uthenga kwa iye woti, “Pita, kasambe kasanu ndi kawiri mu mtsinje wa Yorodani, thupi lako lidzachira ndi kukhalanso monga kale ndipo udzayeretsedwa.”
11 А Нееман се разгневи, та си отиде, като казваше: Ето, аз мислех, че той непременно ще излезе при мене, ще застане, и ще призове името на Господа своя Бог, и ще помаха ръката си върху мястото, и така ще изцери прокажения.
Koma Naamani anachoka mokwiya ndipo anati, “Ine ndimaganiza kuti munthuyu atuluka ndipo ayimirira nayitana dzina la Yehova Mulungu wake, nayendetsa dzanja lake pamwamba pa nthendayi ndi kundichiritsa khate langa.
12 Реките на Дамаск, Авана и Фарфар, не струват ли повече от всичките води на Израиля? Не мога ли да се окъпя в тях и да се очистя? Затова, той се обърна и си отиде много разгневен.
Kodi Abana ndi Faripara, mitsinje ya ku Damasiko, siyoposa mitsinje ina yonse ya ku Israeli? Kodi sindikanasamba mʼmitsinje imeneyo ndi kuyeretsedwa?” Kotero anatembenuka nachoka ali wokwiya kwambiri.
13 А слугите му се приближиха та му говориха, казвайки: Татко мой, ако ти беше заръчал пророкът нещо голямо, не би ли го извършил? Колко повече, прочее, като ти казва! Окъпи се и очисти се!
Antchito ake anamuyandikira namufunsa kuti, “Abambo anga, mneneri akanakulamulani chinthu chachikulu, kodi inu simukanachita? Nanga nʼzovuta motani zomwe mneneri wanena kuti ‘Kasambeni ndipo mudzayeretsedwa!’”
14 Тогава той слезе та се потопи седем пъти в Иордан, според думите на Божия човек; и месата му се обновиха, като месата на малко дете, и очисти се.
Choncho Naamani anapita ku Yorodani nakadzimiza mʼmadzimo kasanu nʼkawiri, monga momwe munthu wa Mulungu anamuwuzira. Thupi lake linakhalanso monga kale ndipo linakhala losalala ngati la kamnyamata.
15 Тогава той се върна при Божия човек с цялата си дружина, и като дойде та застана пред наго рече: Ето, сега узнах, че няма Бог в целия свут освен в Израиля; затова, моля, приеми сега подарък от слугата си.
Pamenepo Naamani ndi atumiki ake onse anabwerera kwa munthu wa Mulungu uja. Naamani anayima pamaso pa Elisa ndipo anati, “Tsopano ndikudziwa kuti kulibe Mulungu wina pa dziko lonse lapansi koma mu Israeli mokha. Chonde, tsopano landirani mphatso ya mtumiki wanu.”
16 А той каза: Заклевам се в живота на Господа, Комуто слугувам, не ща да приема. А той го принуждаваше да приеме; но отказа.
Mneneri anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene ine ndimamutumikira, sindidzalandira zimenezi.” Ndipo ngakhale Naamani anamukakamiza, iye anakanabe.
17 Тогава Нееман рече: Ако не то нека се даде, моля, на слугата ти товар за две мъски от тая пръст; защото слугата ти не ще вече да принася ни всеизгаряне, нито жертва на други богове освен на Господа.
Naamani anati, “Ngati inu simulandira, chonde lolani mtumiki wanu kuti atengeko dothi lokwanira kunyamula abulu awiri, popeza mtumiki wanu sadzaperekanso nsembe yopsereza ndi nsembe zina kwa mulungu wina koma Yehova.
18 Господ да прости това нещо на слугата ти, ако, когато влиза господарят ми в къпищато на Ромона, за да се поклони там, и се подпира на ръката ми, се навеждам и аз в къпището на Римона; като се навеждам в капището на Римона, Господ да прости това нещо на слугата ти!
Koma Yehova andikhululukire ine pa chinthu ichi: Pamene mbuye wanga alowa mʼnyumba ya mapemphero ya Rimoni ine ndimapita naye ndipo ndimakagwada naye limodzi. Pamene ndikugwada mʼnyumba ya mapemphero ya Rimoni, Yehova azikhululukira mtumiki wanu pa chinthu chimenechi.”
19 И рече му: Иди с мир. И така, той отиде от него известно растояние.
Elisa anati, “Pita mu mtendere.” Choncho anachoka nayenda pangʼono.
20 Но Гиезий, слугата на Божия човек Елисей, си рече: Ето, господарят ми си посвени, та не взе от ръката на тоя сириец Нееман това, което донесе; но в името на живия Господ, аз ще се завтека подер него и ще взема нещо от него.
Koma Gehazi, mtumiki wa Elisa munthu wa Mulungu, anaganiza mu mtima mwake kuti, “Taonani, mbuye wanga wamulekerera Naamani Mwaramuyu, posalandira zomwe anabweretsa. Pali Yehova wamoyo, ine ndimuthamangira ndipo ndikatengako zinthu kwa iye.”
21 И тъй, Гиезий се завтече подир Неемана. А нееман, когато видя, че тича подир него, скочи от колесницата да го посрещне и рече: Добре ли и с всички ви?
Choncho Gehazi anamuthamangira Naamani uja. Naamani ataona Gehazi akumuthamangira, anatsika mʼgaleta lake ndi kukakumana naye. Iye anafunsa Gehazi kuti, “Kodi nʼkwabwino?”
22 Той рече: Добре. Господарят ми ме прати да река: Ето тъкмо сега дойдоха у мене от хълмистата земя на Ефрема двама младежи от пророческите ученици; дай им, моля, един талант сребро и премени дрехи.
Gehazi anayankha kuti, “Inde nʼkwabwino. Mbuye wanga wandituma kuti ndidzakuwuzeni kuti, ‘Anyamata awiri mwa ana a aneneri angondipeza kumene kuchokera ku dziko la mapiri la Efereimu. Chonde apatseniko ndalama za siliva 3,000 ndi zovala ziwiri za pa phwando.’”
23 И рече на Нееман: Благоволи да вземеш два таланта. И като го принуди, върза двата таланта сребро в два мешеца заедно с две премени дрехи, и натовари ги на двама от слугите си, които ги носеха пред него.
Naamani anati, “Kuli bwino utenge ndalama zasiliva 6,000.” Iye anakakamiza Gehazi kuti alandire, ndipo kenaka anamanga matumba awiri a ndalama zasiliva pamodzi ndi zovala zinayi za pa mphwando. Naamani anazipereka kwa antchito ake awiri ndipo anazinyamula nayenda patsogolo pa Gehazi.
24 И когато стигна до хълма, взе ги от ръцете им та ги скри в къщата; и отпусна човеците, та си отидоха.
Gehazi atafika ku phiri, anawalanda antchito aja zinthu zija nazibisa mʼnyumbamo. Iye anawawuza anthu aja kuti abwerere ndipo anapita.
25 Тогава влезе та застана пред господаря си. И Елисей му рече: От где идеш, Гиезие? А той рече: Слугата ти не е ходил никъде.
Kenaka analowa mʼnyumbamo nakayima pamaso pa mbuye wake Elisa. Elisa anafunsa kuti, “Kodi Gehazi unali kuti?” Iye anayankha kuti, “Mtumiki wanu sanapite kwina kulikonse.”
26 А Елисей му каза: Не отиде ли сърцето ми с тебе, когато се върна човекът от колесницата си за да те посрещне? Време ли е да приемеш пари и да приемеш дрехи, маслини и лозя, овци и говеда, слуги и слугини?
Koma Elisa anati kwa Gehazi, “Kodi mzimu wanga sunali nawe pamene munthu uja anatsika mʼgaleta lake ndi kukumana nawe? Kodi ino ndi nthawi yolandira ndalama, kapena kulandira zovala, mitengo ya olivi, minda ya mpesa, nkhosa, ngʼombe kapena antchito aamuna kapena antchito aakazi?
27 Затова Неемановата проказа ще се засили за тебе и за рода ти до века. И той излезе от присъствието му прокажен, бял като сняг.
Khate la Naamani lidzakumatirira iwe ndi zidzukulu zako mpaka muyaya.” Ndipo Gehazi anachoka pamaso pa Elisa ali ndi khate lotuwa ngati phulusa.