< 2 Летописи 19 >

1 А като се връщаше Юдовият цар Иосафат с мир у дома си в Ерусалим,
Yehosafati, mfumu ya Yuda itabwerera mwamtendere ku nyumba yake yaufumu ku Yerusalemu,
2 гледачът Ииуй, Ананиевият син, излезе да го посрещне, и рече на цар Иосафата: На нечестивия ли помагаш, и тия ли, които мразят Господа, обичаш? Затова, гневът от Господа, обичаш? Затова гняв от Господа има върху тебе.
mlosi Yehu, mwana wa Hanani, anatuluka kukakumana naye ndipo anati kwa mfumu, “Kodi nʼkoyenera kuthandiza oyipa ndi kukonda iwo amene amadana ndi Yehova? Chifukwa cha zimenezi mkwiyo wa Yehova uli pa inu.
3 Все пак, обаче, намериха се в тебе добри неща, защото ти отмахна ашерите от земята, и утвърди сърцето си да търсиш Бога.
Komabe, muli zinthu zina zabwino mwa inu, pakuti inu mwachotsa mʼdziko muno mafano a Asera ndipo mwakhazikitsa mtima wanu pa kufunafuna Mulungu.”
4 И като се засели Иосафат в Ерусалим, сетне излезе пак между людете от Вирсавее до Ефремовата хълмиста земя, та го обърна към Господа Бога на бащите им.
Yehosafati anakakhala ku Yerusalemu, ndipo amayenda pakati pa anthu kuchokera ku Beeriseba mpaka ku dziko lamapiri la Efereimu ndipo anawatembenuzira kwa Yehova, Mulungu wa makolo awo.
5 И по всичките укрепени градове на Юда постави съдии в земята, град по град.
Iye anasankha oweruza mʼdzikomo, mu mzinda uliwonse wotetezedwa wa Yuda.
6 И рече на съдиите: Внимавайте какво правите; защото не съдите за човека, но за Господа, Който е с вас в съдопроизнасянето.
Ndipo anawawuza kuti, “Muganize bwino zimene mukuchita, chifukwa simukuweruza mʼmalo mwa munthu koma Yehova, amene ali nanu pamene mukupereka chiweruzo.
7 Затова нека бъде върху вас страх от Господа; внимавайте в делата си; защото у Господа нашия Бог няма неправда, нито лицеприятие, нито дароприятие.
Tsopano kuopsa kwa Yehova kukhale pa inu. Muweruze mosamala, pakuti ndi Yehova Mulungu wathu palibe kupotoza chilungamo kapena kukondera kapenanso kulandira ziphuphu.”
8 Тогава, като се върнаха в Ерусалим, Иосафат постави и в Ерусалим някои от левитите и свещениците и от началниците на Израилевите бащини домове, за Господния съд и за спорове.
Mu Yerusalemu, Yehosafati anasankha Alevi ena, ansembe ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli kuti aziyangʼanira Malamulo a Yehova ndi kuweruza milandu. Ndipo iwo amakhala mu Yerusalemu.
9 И заръча им като им рече: Така да постъпвате със страх от Господа, вярно и със съвършено сърце.
Iye anawalamula kuti, “Inu mutumikire mokhulupirika ndi mtima wanu wonse moopa Yehova.
10 И ако дойде при вас от братята ви, които живеят в градовете си, какъвто и да било спор, между кръв и кръв, между закон и заповед, между повеления и узаконения, увещавайте ги да не стават виновни пред Господа, да не би да дойде гняв върху вас и върху братята ви. Така постъпвайте и няма да станете виновни.
Pa mlandu uliwonse wobwera kwa inu kuchokera kwa abale anu amene amakhala mʼmizinda, mlandu wokhetsa magazi kapena mlandu wosamvera malamulo kapena malangizo kapena ziphunzitso zina, inu muziwachenjeza kuti asachimwire Yehova pakuti mukapanda kutero mkwiyo wake udzakhala pa inu ndi abale anu. Chitani zimenezi ndipo simudzachimwa.
11 И, ето, първосвещеникът Амария ще бъде над вас във всяко Господно дело; и началникът на Юдовия дом, Зевадия, Исмаиловия син, ще бъде във всяко царско дело; а левитите ще бъдат надзиратели пред вас. Действувайте мъжествено и Господ ще бъде с добрия.
“Amariya, mkulu wa ansembe adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza Yehova, ndipo Zebadiya mwana wa Ismaeli, mtsogoleri wa fuko la Yuda, adzakhala wokuyangʼanirani pa zonse zokhudza mfumu ndipo Alevi adzatumikira ngati okuyangʼanirani. Muchite molimba mtima ndipo Yehova akhale ndi iwo amene adzachita bwino.”

< 2 Летописи 19 >