< Titus 2 >
1 I wu u ka hla njaaji ilan.
Koma iwe uziphunzitsa zogwirizana ndi chiphunzitso choona.
2 Gbi bi ciche lila du mba hi he vutu bey vu sunro be toh jaji ni mi kpakyeme ni itere u Irji.
Phunzitsa amuna achikulire kuti akhale osaledzera, aulemu wawo, odziletsa, okhwima mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkupirira.
3 Na ki imba be niko be ka vutu bi bana be tere totona du bana so ima u tehuwa na.
Chimodzimodzinso, phunzitsa amayi achikulire kuti akhale aulemu mʼmakhalidwe awo, asakhale osinjirira anzawo kapena zidakwa, koma akhale alangizi abwino.
4 Du ba tsoro imba be tsitsama itere sunko wa balilo.
Tsono atha kulangiza amayi achichepere kukonda amuna awo ndi ana awo.
5 Du mba hi be mlaya mba komba bata tee naki itere Irji a ni bi kerekereme.
Kuwaphunzitsa kukhala odziletsa ndi oyera mtima, osamala bwino mabanja awo, okoma mtima, ndi ogonjera amuna awo. Choncho palibe amene adzanyoze mawu a Mulungu.
6 Na ki u ka hla imirize du mba hey be sisuron.
Momwemonso, uwalimbikitse amuna achichepere kuti akhale odziletsa.
7 Ko ni konrime u ka zeren dedeme.
Pa zonse iwe mwini ukhale chitsanzo pa ntchito zabwino. Pa chiphunzitso chako uwonetsa kuona mtima ndi kutsimikiza mtima kwako.
8 Hla tere be dedema. bewa bana toh itere Irji na Ishan ka temba.
Phunzitsa choonadi kuti anthu asapeze chokutsutsa, motero wotsutsana nawe adzachita manyazi chifukwa adzasowa kanthu koyipa kuti atinenere.
9 I miri ko mba wo tere ni tei komba ni mi kogeh mba na sunyu ni mbana.
Phunzitsa akapolo kuti azigonjera ambuye awo mu zinthu zonse ndi kuwakondweretsa. Asamatsutsane nawo
10 Du ba na tee yibi na. Mba ka ji kpakyeme U Irji gbahgbah me.
kapena kumawabera, koma adzionetse kuti ndi odalirika, motero pa zochita zawo zonse adzaonetsa ubwino wa chiphunzitso cha Mulungu, Mpulumutsi wathu.
11 U imiri Irji ba toh didima wawumba.
Pakuti chisomo cha Mulungu chimene chimapulumutsa chaonekera kwa anthu onse.
12 Ani hla du keh ka memetee u gbu gblu tagah. (aiōn )
Chisomo chimatiphunzitsa kukana moyo osalemekeza Mulungu komanso zilakolako za dziko lapansi. Ndipo chimatiphunzitsa kukhala moyo odziletsa, olungama ndi opembedza Mulungu nthawi ino, (aiōn )
13 Keh ta zere di ta gbey tee lulu ni ze sunro u ye ivere Irji tee bu.
pamene tikudikira chiyembekezo chodala; kuonekera kwa ulemerero wa Mulungu wathu wamkulu ndi Mpulumutsi, Yesu Khristu,
14 Yesu a kpa hla tere u bu ni gbu gblu da ikheu ubu wawu. na ki khi ka hu hla terema.
amene anadzipereka yekha chifukwa cha ife kutiwombola ku zoyipa zonse ndi kudziyeretsera yekha anthu amene ndi akeake, achangu pa ntchito yabwino.
15 U ka tere ni gbe gble de tshoro ba jaji ndah na kpa u tsirina.
Tsono zimenezi ndi zinthu zomwe uyenera kuphunzitsa. Uziwalimbikitsa anthu ndi kuwatsutsa komwe. Uzichita zimenezi ndi ulamuliro wonse. Wina aliyense asakupeputse ayi.