< Romawa 1 >
1 Bulus vren koh Yesu Almasihu, wa ba you aye, kma tie ndji u toh ndu, wa ba chu zi kan nitu tre Irji.
Ndine Paulo, mtumiki wa Khristu Yesu, woyitanidwa ndi Mulungu kukhala mtumwi. Ndinapatulidwa kuti ndilalikire Uthenga Wabwino wa Mulungu
2 Wa i hi tre wa a chu nyu ni sen mu ni bi toh ndu ma ni tsatsraka ibe ma.
umene analonjeza kale mʼMalemba Oyera kudzera mwa aneneri ake.
3 Ahe ni tu vren ma, wa ba ngrji'u ni kutra kahlan Dauda ni kpa.
Uthengawu ndi wonena za Mwana wake amene mwa umunthu wake anali wochokera mwa Davide.
4 Ni Brji ndindima u suron ndindi, wa a lunde ni mi be bak tsro da Vren Irji ni gbengblen Ibrji ndindi u bi wa ba he kiklan suron u Yesu Almasihu Bachi mbu
Iyeyu ndi amene anatsimikizidwa kukhala Mwana wa Mulungu mwamphamvu za Mzimu Woyera pamene anauka kwa akufa. Kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu,
5 Ni tuma ki kpa ndindi ni toh ndu nitu kpa nyime u ndindi nimi bi korah wawu'u, nitu inde ma u ndindi.
ife tinalandira chisomo chokhala atumwi oyitana anthu a mitundu yonse kuti amukhulupirire ndi kumumvera mwachikhulupiriro kuti dzina lake lilemekezedwe.
6 Ni mi bi kora kwa, bi yi me ba you yi hi ni Yesu Almasihu.
Inunso muli mʼgulu la Amitundu oyitanidwawo kukhala ake a Yesu Khristu.
7 Lbe i ahi u bi wawu'u bi wa bi he ni mi Roman, wa Irji ni son ba, wa ba you ndji mba ndi tsarkaku. Du ndindi ni sun si rji ni Irji Bachi Iti mbu, ni Bachi Yesu Almasihu.
Ndikulembera kwa onse okhala ku Roma amene Mulungu amakukondani nakuyitanani kuti mukhale oyera mtima. Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi kwa Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi inu.
8 Ikpe u mumla misi ngyiri ni Irji mu ni tu Yesu Almasihu nitu bi wawu'u, don naki basi tre nitu njanji bi ni gbungblu wawu'u.
Poyamba, ndikuthokoza Mulungu wanga kudzera mwa Yesu Khristu chifukwa cha nonsenu, pakuti pa dziko lonse lapansi anthu akukamba za chikhulupiriro chanu.
9 Don Irji wawu yi toh me, wa misi tie ndu ma ni mi Ruhu mu ni tre Vren Ma, wa mi you nde bi chachu'u.
Mulungu amene ndimamutumikira ndi mtima wanga onse polalikira Uthenga Wabwino wa Mwana wake, ndi mboni yanga kuti ndimakupemphererani nthawi zonse.
10 Mi nji yi mu ni bre chachu'u du me toh koh wa mi ye u Hellinawa.
Mʼmapemphero anga, nthawi zonse, ndimapemphera kuti ngati nʼkotheka mwachifuniro cha Mulungu, njira inditsekukire kuti ndibwere kwanuko.
11 Nakima Irji na hi u tara na.
Ine ndikulakalaka kukuonani kuti ndikugawireni mphatso zina zauzimu kuti zikulimbikitseni
12 Ni biwa ba lah tre ni tron na, ba kwu ba tare da tron na, ni bi wa ba lah tre ni mi tron, ba hukunta ba nitu tron.
ndiponso kuti tonsefe tilimbikitsane mʼchikhulupiriro wina ndi mnzake.
13 Naki ma ana biwa ba wo tron, ana baba bi ndindi u Irji na, naki bi ti, ba kpa ba chuwo.
Abale, ine sindifuna kuti mukhale osadziwa kuti nthawi zambiri ndakhala ndikufuna zobwera kwanuko, koma mpaka pano pali zolepheretsa, ndi cholinga choti ndidzapezeko zipatso pakati panupo monga momwe ndakhala ndikuchitira pakati pa a mitundu ina.
14 Bi kora wa bana toh tron na, nitu da bia bati kpi wa ahi u tron.
Ine ndi wokakamizidwa ndi udindo wotumikira Agriki pamodzi ndi omwe si Agriki, kwa anzeru ndi kwa opusa omwe.
15 Nakima ba tsro ndi idu ni tron ani wa han ni suron ba, imre ba ni bla, ri mre ba ni chan ba ko ani ka'aba. Nakima ni Irji wa i ni ti ni vie wa Irji ni bla asiri wa he riri u bi he ni mi Roma
Pa chifukwa chimenechi, ine ndikufunitsitsa kulalikira Uthenga Wabwino kwa inunso amene muli ku Roma.
16 Nakima isha na time na, dume hla tre na, don kima hi gbengblen Irji don kpachuwo wa bi wa ba kpa nyime, bi mumla Yahudawa u Halleniyawa.
Ine sindichita manyazi ndi Uthenga Wabwino chifukwa ndiwo mphamvu za Mulungu zopulumutsa aliyense amene akhulupirira, poyamba Myuda, kenaka Mhelene.
17 Naki nimi ma ndindi Irji ka tsro u njanji hi ni njanji, na ba nha zi, ndji u ndindi ani sun nitu njanji.
Pakuti mu Uthenga Wabwino anawulula kuti chilungamo chimachokera kwa Mulungu. Kuyambira pachiyambi mpaka potsiriza ndi chilungamo chobwera mwachikhulupiriro, monga kwalembedwera kuti, “Wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.”
18 Nakima infu Irji a tsro rji ni shu nitu bi wa bana hu nkon ni ndindi u mri Adamu bi wa ba chan njanji nitu njanji na he ni bana.
Mkwiyo wa Mulungu ukuonekera kuchokera kumwamba. Ukutsutsana ndi kusapembedza konse ndi kuyipa kwa anthu amene amapondereza choonadi mwa chikhalidwe chawo choyipa.
19 Nakima, ikpe wa a mla duba toh ni Irji ahe ni rira me nitu mba Naki ma Irji a tsro ba wawu hi zahiri.
Za Mulungu zimene zingathe kudziwika, ndi zomveka bwino kwa iwo pakuti Mulungu anazionetsera kwa iwo.
20 Nakima idu ma wa bana ya toh na a ni rira ba he tu ni nton wa ati gbungblu'a. Ba ya toh ba nitu ikpi bi wa ati'a. Ikpi bi yi baba ba ikoma u kakle ni Allahtakarsa. Nakima indji bi bana he ni sen nyu na. (aïdios )
Pakuti kuyambira pamene dziko lapansi linalengedwa, zinthu zosaoneka za Mulungu, mphamvu zake zosatha ndi chikhalidwe cha umulungu, zakhala zikuoneka bwinobwino. Akhala akuzindikira poona zimene Mulungu analenga, kotero kuti anthu sangathe kuwiringula. (aïdios )
21 Nakima ba ndji ba toh Irji, aman bana no ninkon u matsayi Irji na, ko duba tsro ingyiri. Nakima ba kma ti ruru ni mi mre mba. Imre u suron mba hi u bu.
Ngakhale iwo anadziwa Mulungu, sanamulemekeze ngati Mulungu kapena kumuthokoza, koma maganizo awo anasanduka wopanda pake ndipo mʼmitima yawo yopusa munadzaza mdima.
22 Ba ban tumba na bi wa ba toh, aman se ba kma tie ruru.
Ngakhale ankadzitama kuti ndi anzeru, anasanduka opusa.
23 Ba sran ninkon Irji u kakle ni kpi wa bana kakle ana na indji, cicen ni na nma bi zizia ni biwa ba nha ni ne.
Iwo anasinthanitsa ulemerero wa Mulungu wosafa ndi mafano opangidwa ndi manja wooneka ngati munthu amene amafa, kapena ngati mbalame, ndi nyama kapena zokwawa.
24 Nakima Irji ka ban no sha'awa pipi suron mba ba ti kpa yah.
Nʼchifukwa chake Mulungu anawasiya kuti azingochita zilakolako zochititsa manyazi zauchimo zomwe mitima yawo inkafuna. Zotsatira zake anachita za chiwerewere wina ndi mnzake kunyazitsa matupi awo.
25 Baba yi ba sran njanji Irji ni che, ba si tie sujada ni bauta ni kpe wa ba tie ba ni wo, maimako wa ati ta, wa a mla zu nde kakle. (aiōn )
Iwo anasinthanitsa choonadi cha Mulungu ndi bodza ndipo anapembedza ndi kutumikira zinthu zolengedwa mʼmalo mwa Mlengi amene ali woyenera kutamandidwa mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
26 Nakima Irji ban ba no sha'awoyi u ti fa ba iyah har mbah ba kasran kaida jima hi mbah ni mbah.
Chifukwa cha ichi, Mulungu anawasiya kuti azitsata zilakolako zochititsa manyazi. Ngakhale akazi omwe anasiya machitidwe achibadwidwe pa za ukwati, namachita machitidwe ena otsutsana ndi chibadwa chawo.
27 Lilon ba bame ba sran kaida jimai u lilon ni mbah hi ni lilon ni lilon ba si tie ndu fa. Lilon ba kru ni lilon nda ni tie kpi u chi basi chan sakamako indu mba u chi.
Chimodzimodzinso amuna analeka machitidwe a ukwati ndi akazi nʼkumakhumbana amuna okhaokha. Amuna ankachita zochitisa manyazizi ndi amuna anzawo, ndipo analandira chilango choyenera molingana ndi zochita zawo zachitayikozo.
28 Nakima bana kpa nyime ni Irji na ni mi duba, Irji ban ba no ni kpa risu ni mre mba, basi tie meme kpi biyi.
Ndipo popeza anaona kuti nʼchopanda nzeru kumvera Mulungu, Iye anawasiya kuti atsatire maganizo achitayiko kuti achite zosayenera kuchitazo.
29 Ba shu ni rashi ndindi, meme kyashi, keta, tigu, wudi, wa-nyu, makirci, ni meme mre.
Iwo ndi odzazidwa ndi mtundu uliwonse wa makhalidwe oyipa, zonyansa, umbombo ndi dumbo. Iwo ndi odzazidwa ndi kaduka, kupha, mikangano, chinyengo ndi udani. Iwowo ndi amiseche,
30 Bi ti pre, kage, bi wa bana son Irji na. Bi wa bana son sun si na, bi santu, ni bi gla, bi ha meme che, ni bi wa bana hu/wo ba ti/yi mba.
osinjirira, odana ndi Mulungu, achipongwe, odzitama ndi odzitukumula. Iwo amapeza njira zochitira zoyipa. Samvera makolo awo,
31 Biwa isuron mba tsro pipi me, biri amana biwa bana he ni son na, bi wa bana he ni lo suron na.
alibe nzeru, chikhulupiriro, sakhudzidwa mu mtima ndipo ndi ankhanza.
32 Ba toh tsari Irji tre bi wa bati ikpi baki, ba mla kwu, ana ti kpi ni kangrji na, hra ba hu gon biwa bati ba.
Ngakhale kuti amadziwa chiweruzo cholungama cha Mulungu chakuti amene amachita zinthu zotere amayenera imfa, iwo sangopitiriza chabe zimenezi, koma amavomerezanso amene amazichita zimenezi.