< Romawa 3 >
1 Ahi ngye ha fifikon wa Bayahude he niwu? Naki ahi ngye hi mah yo gji?
Nanga kodi pali ubwino wotani pokhala Myuda, kapena muli ubwino wanjinso mu mdulidwe?
2 Akwai muhimanci ba ninkon bari. Ni mumla de ana Yahudawa irji bu tre ni bawu.
Ubwino wake ndi wambiri mʼnjira zonse! Choyambirira iwo anapatsidwa Mawu a Mulungu kuti awasunge.
3 Inde mbru Yahudawa bana kpanyime ni njanji na fa? Wa ba na kpa njani na ani zu ndindi ndu Irji?
Nanga zili bwanji ngati ena analibe chikhulupiriro? Kodi kupanda chikhulupiriro kwawo kukanalepheretsa kukhulupirika kwa Mulungu?
4 Ana he naki ma na, maimako naki, Irji ka kma ti u njanji, na ndji ba wawu ba bi tiche, na ndji ba han hla don duba tsro ndi wu u ndindi ni mi tre me la wu kpaka ni toh wa banji u hi ni shishi tron.
Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Mulungu akhale woona, ndi munthu aliyense akhale wonama. Monga kwalembedwa kuti, “Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi kupambana pamene muweruza.”
5 Ama inde meme bu a tsro ndindi Irji, naki ki tre ngye? ki ya tre ndi Irji hi meme nda nji nfu ma ni tu mbu? (Misi ti ni sen nyu u ndji).
Koma ngati kuyipa mtima kwathu kuonetsa poyera kuti Mulungu ndi wolungama, ife tinganene chiyani? Kodi tinganene kuti Mulungu ndi wosalungama pamene aonetsa mkwiyo wake pa ife? (Ine ndikuyankhula monga mmene anthu ena amayankhulira).
6 Ana taba he naki na. Naki Irji ni tron gbugbu'a ni he?
Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ngati zikanakhala zotero, kodi Mulungu akanaweruza bwanji dziko lapansi?
7 Inde njanji u Irji ni ti gbugbu ce mu ani kara ninkon ni nyu'u, angye sa mi hai ni tron na'u lah tre?
Wina atanena kuti, “Ngati kunama kwanga kukuonetsa koposa kuti Mulungu ndi woona, ndi kuwonjezera pa ulemerero wake, nanga nʼchifukwa chiyani ndikuweruzidwa kuti ndine wochimwa?”
8 Angye sa kina tre, ki yba shishi, ndi tre, bari ba krie nda tre, du ta tie meme, ndi du ndindi ye? Hukunci ba a ndindima.
Nʼchifukwa chiyani osanena kuti, monga ena amanena mosasamala kuti, “Tiyeni tichite zoyipa kuti zabwino zionekere?” Anthu onena zoterewa kulangidwa kwawo ndi koyenera.
9 Angye naki, ki no tumbu sen nyu'u? Ana he naki na don ki guchi tre Yahuda baba Hllinawa ye ndi tre ndi wawu mbawu ba he ni mi lahtre.
Kodi timalize bwanji? Kodi Ayuda ndife oposa anthu ena? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ife tinanena kale kuti Ayuda ndi a mitundu ina omwe ndi ochimwa.
10 Na ba nha, ba ndji u njanji, iriri na he na.
Monga kwalembedwa kuti, “Palibe munthu wolungama, inde palibe ndi mmodzi yemwe.
11 Ba ndji wa a toh kpie, ba wa'a ni wa Irji.
Palibe ndi mmodzi yemwe amene amazindikira, palibe amene amafunafuna Mulungu.
12 Wawu mbawu ba kankon don, wawu mbawu ba kma tibi wa bana he ni anfani na. Ba wa ani tie ndu ndindima, a'an iriri na he na.
Onse apatukira kumbali, onse pamodzi asanduka opandapake. Palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita zabwino, palibe ngakhale mmodzi.”
13 Gbugbran mba he ni ho na be, Ilbe mba a ban lilo, Itso wan a he ni mi lbe mba.
“Kummero kwawo kuli ngati manda apululu; ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.” “Ululu wa mamba uli pa milomo yawo.”
14 Inyu mba a shu ni la'ah ni ri gberjerje me.
“Mʼkamwa mwawo ndi modzaza ndi zotemberera ndi mawu owawa.”
15 Izah mba ni tsutsu gbagbla ni ka yi hle
“Mapazi awo afulumira kukakhetsa magazi.
16 Inkon mba ahi yah ni tie meme.
Kusakaza ndi chisoni kumaonekera mʼnjira zawo,
17 Ndji biyi bana toh nkon sun u si na.
ndipo njira ya mtendere sayidziwa.”
18 Bana he ni klu sissri Irji ni shishi mba na.
“Saopa Mulungu ndi pangʼono pomwe.”
19 Naki ki toh ndi du kpie wa itron a tre, itro ani tre ni bawu wa ba he ni mi ma, don duba ka iyu mba wawu, naki gbungblu a wawu'u ka no amsa ni shishi Irji.
Tsopano tikudziwa kuti chilichonse Malamulo amanena, amanena kwa amene amalamulidwa ndi Malamulowo, ndi cholinga chakuti aliyense asowe chonena, ndipo dziko lonse lidzayimbidwa mlandu ndi Mulungu.
20 Naki ni shishi ba ndji wa ba kpa chuwo ni tu ndu tron. Nitu tron, toh lah tre aye.
Chifukwa chake palibe mmodzi amene adzayesedwa wolungama pamaso pake chifukwa chosunga Malamulo, kuti ife timazindikira tchimo kupyolera mu Malamulo.
21 Naki zizan'a nitu tron ba tsro toh njanji Irji wa itron ni annabawa basi hla.
Koma tsopano chilungamo chochokera kwa Mulungu, osati chochokera ku Malamulo, chaonetsedwa. Ichi ndi chimene Malamulo ndi Aneneri amachitira umboni.
22 Naki ndindi Irji ahi njanji nimi Yesu Almasihu hi ni biwa ba kpa nyime ni njanji. Naki, kakan na he na.
Timakhala olungama pamaso pa Mulungu pamene takhulupirira Yesu Khristu. Mulungu amachitira zimenezi anthu onse amene akhulupirira Khristu. Palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina,
23 Naki, wawu'u mbawu ba lah tre, bana ya ka hi ni daraja Irji,
pakuti onse anachimwa naperewera pa ulemerero wa Mulungu
24 ni ndindima ba kpa ta chuwo ni tu kpachuwo wa'a he ni mi Yesu Almasihu.
ndipo onse alungamitsidwa mwaulere mwa chisomo chake chifukwa cha Khristu Yesu amene anawawombola.
25 Aman Irji a ban Yesu Almasihu no wa ahi hadaya u kpachuwo u njanji nimi iyi ma. A ban Almasihu na nimatsayi tabbacin hukunci ma, nitu ketarewa lah tre mbu wu kogon'a.
Mulungu anamupereka Iyeyu kuti pokhetsa magazi ake, akhale nsembe yokhululukira machimo. Mulungu anachita zimenezi kufuna kuonetsa chilungamo chake. Chifukwa cha kuleza mtima kwake, sanalange anthu chifukwa cha machimo amene anachita kale.
26 Nimi vu suron ma, naki i wa yi ati ndu tsro ndindima nimi toh i du kpanyime ni tuma u hukunci, nda tsro wawu hi u kpa konha chuwo saboda, njanji wa ahe nimi Yesu.
Iye anachita izi kuti aonetse chilungamo chake lero lino. Anthu azindikire kuti Iye ndi wolungama ndipo amalungamitsa aliyense amene akhulupirira Yesu.
27 To, i wru wo ni san he ni ntsen? Ba chu'u rju. Nitu ngye? Nitu ndu? Aman nitu ndu? Ama nitu njanji.
Nanga tsono pamenepa munthu anganyadenso? Kunyadatu kwachotsedwa. Chifukwa cha Malamulo? Kodi Malamulo samafuna ntchito za munthu? Ayi, koma mwachikhulupiriro.
28 Nakima kikle tre a ndi ba kpa ndji chuwo, ana he nitu ndu tron na.
Ife tikunenabe kuti munthu amalungamitsidwa mwachikhulupiriro osati mwakusunga Malamulo.
29 Ko naki Irji ahi Irji Yahudawa ni kankrji? Ana Irji bi kora ngame na? i ahi bi kora ngame.
Kodi Mulungu ndi Mulungu wa Ayuda okha? Kodi si Mulungu wa a mitundu inanso? Inde wa a mitundu inanso,
30 Nakima inde gbigbi ahi Irji riri, ani kpa biwa ba yo nji ni bawu chuwo nitu njani.
popeza ndi Mulungu mmodzi yemweyo amene adzalungamitsa mwachikhulupiriro ochita mdulidwe ndi osachita mdulidwe kudzera mʼchikhulupiriro chomwecho.
31 Ki ka tron hlega nitu njanji? Ana taba he nakima na, nakima kisi hu gon tro kena.
Kodi tsono ife, tikutaya Malamulo pamene tikunena kuti pafunika chikhulupiriro? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Komatu ife tikukwaniritsadi Malamulo.