< Romawa 2 >

1 Nakima u na he ni sen nyu wu ndji u sharantawa, Nakima ikpi wa u si sharantawa nitu bari, u wuu tume ni tume. Nakima u sharantawa u si tie kpi bi yi ngame.
Choncho, iwe amene umaweruza munthu wina, ulibe pokanira pakuti nthawi iliyonse pamene uweruza wina ukudzitsutsa wekha chifukwa iwe amene umaweruzawe umachitanso zinthu zomwezo.
2 Naki ki toh ndji i tron Irji a njanji ani ye joku ni biwa ba ti kpie baki.
Tsopano ife tikudziwa kuti chiweruzo cha Mulungu, chotsutsa amene amachita zinthu zotere, nʼchokhazikika pa choonadi.
3 Nakima ka toh wayi wu indji u sharanta ni biwa ti kpii, wume wu si ti me. Wu yah ndi wu gbujbu ni nfu Irji?
Kodi ukuganiza kuti udzathawa chiweruzo cha Mulungu iwe munthu wamba, pamene uweruza ena, iwe ndi kumachitanso zomwezo?
4 Ko wu kpa ndindima tsri wa infu ma ni vu suron ana ye gbagbla na? Wuna toh ndji ndindima musama du nji wu hi ni ti njanji?
Kodi kapena ukupeputsa kukoma mtima kwa Mulungu, kuleza mtima kwake ndi kupirira kwake? Kodi sukuzindikira kuti kukoma mtima kwakeko, nʼkofuna kuti iweyo ulape machimo ako?
5 Aman sabo ni son tume ni suron me wa ana tie njanji na, wu si vu'u nfu ni sru ni tume ni vie u nfu, wato ivie u ye tron njanji u Irji.
Koma pakuti ndiwe wosamvera ndi wa mtima wosafuna kulapa, ukudzisungira chilango pa tsiku la mkwiyo wa Mulungu, pamene chiweruzo cholungama cha Mulungu chidzaonetsedwa.
6 Mi no ko nha ndi dede du ma wa ati'a.
Mulungu adzabwezera aliyense molingana ndi ntchito zake.
7 Ni bi wa ba you suron ni tie ndindi chachu'u ba wa nitu zu wo daraja ni drie u kakle. (aiōnios g166)
Iye adzapereka moyo wosatha kwa amene amafunafuna ulemerero, ulemu ndi moyo pochita ntchito zabwino mopirira. (aiōnios g166)
8 Naki bi wa ba son tu, ni bi wa ba kamba ni njanji, ba ti biyaya ni rashi njanji, infu ni nfu rigra ni grji ni bawu.
Koma Mulungu adzakhuthulira mkwiyo ndi ukali wake pa amene amachita zofuna zawo ndi kukana choonadi nʼkumatsatira zoyipa.
9 Irji ni grji ni iya meme ni shinji ne bi vri wawu wa bati meme, ni Yahudawa ni muimla ni Hellinawa.
Masautso ndi zowawa zidzagwera munthu aliyense amene amachita zonyansa, kuyambira Myuda kenaka anthu a mitundu ina.
10 Nakima zuwo ni daraja ni sun si ba he ni bi wa basi ti ndu ndindi wa wu bawu, ni Yahudawa ni mumla, ni yi ni kpa nyime Irji.
Koma ulemerero, ulemu ndi mtendere zidzakhala kwa aliyense amene amachita zabwino, kuyambira Myuda kenaka anthu a mitundu ina.
11 Mi ti titan toh yi, don mini noyi baiwa ri u ruhaniya mi ni noyi gbengblen.
Pajatu Mulungu alibe tsankho.
12 Wato misi ngyiri mi ni kpa gbengblen ni mi bi u njanji mbu wato u mu, u bi.
Onse amene amachimwa osadziwa Malamulo, adzawonongeka ngakhale kuti sadziwa Malamulowo. Ndipo onse amene amachimwa akudziwa Malamulo adzaweruzidwa potsata Malamulowo.
13 Ziza'a fa mina son du yi ka toh mri ya kpo gbugbu'u mi you suron ndi mi ye ni yi, naki har zizan'a koh na he na. Mi son ndi miti nakima, don mi ni samu mri u Ruhu ndindi ni mi mbi, na ahe ni mbru bi kora.
Pakuti si amene amangomva Malamulo amene amakhala wolungama pamaso pa Mulungu, koma ndi okhawo amene amachita zili mʼMalamulomo amene adzatchedwa olungama.
14 Mi ban yah Helinawa ni baba u mbru ndji bi toh ni bi wa bana toh na.
Ndithu, pamene a mitundu ina, amene alibe Malamulo, koma mwachikhalidwe chawo amachita zimene zili mʼMalamulo, iwowo ndi Malamulo pa iwo okha, ngakhale kuti alibe Malamulowo.
15 Ni naki tie mba rju he ni kora ndi tron'a he nimi suron mba. U mi dri mba ngame ahi sheda ni bawu, u tunani mba ko ka vu ba ni meme ko ka kri ngba ni bawu
Ntchito zawo zimaonetsa kuti Malamulowo alembedwa mʼmitima mwawo. Chikumbumtima chawonso chimawachitira umboni pakuti maganizo awo amawatsutsa kapena kuwavomereza.
16 u ni Irji ngame. Ani he naki ni vi wa Irji ni rju ni mi dri ba ndji wawu'u ni kora, ni tu nkon u tre Ma, ni Yesu Kristi.
Izi zidzachitika pa tsiku limene Mulungu adzaweruza zinsinsi za anthu kudzera mwa Yesu Khristu, monga momwe Uthenga wanga Wabwino unenera.
17 Nakima wu si you tume ndi wu uhi Bayahude, wu sun ni tu tron, ndi ni wru wo ni san ni mi Irji.
Koma iweyo, amene umadzitcha kuti ndiwe Myuda, umadalira Malamulo, ndipo umanyadira ubale wako ndi Mulungu,
18 Wu toh mre ma, ndi toh kpi wa ba he ni nkanka naki, kuma u kpa bla ni mi tron.
ngati umadziwa chifuniro chake, ndi kudziwa zoyenera kuchita chifukwa unaphunzitsidwa ndi Malamulo;
19 Naki wu he ni gabagadi nitu ndi wu u vu wo ni bi fie, ndi kpah ni bi wa ba he ni mi bu'u.
ngati umadziwadi kuti ndiwe mtsogoleri wa osaona, nyale yowunikira amene ali mu mdima,
20 Gbi ton ni wa ana he ni toh na, u tsro ni mri bi tsitsa, u andi ni mi tron wu he ni kpi wa a shafi toh ni kuma njanji, u nihe ikpe yi ahe ni mi son me?
mlangizi wa anthu opusa, mphunzitsi wa makanda, chifukwa umadziwa kuti mʼMalamulo uli nayo nzeru yonse ndi choonadi,
21 Bi yi wa tsro bari, bina tsro tumbi na? Bi wa bi tre na tie y'bi na, bina y'bi?
tsono, iwe amene umaphunzitsa ena, sudziphunzitsa wekha kodi? Kodi iwe amene umalalikira kuti anthu asabe, umabanso?
22 Biyi wa bi tre duba na tie ntran na, bina ni tie ntran na? Biyi bi tre duba na ti gumaka na, bina tie gumaka na? Biyi wa bi tre duba na tie y'bi na, bina y'bi sessren me na?
Kodi iwe amene umanena kuti anthu asachite chigololo, umachitanso chigololo? Kodi iwe amene umanyasidwa ndi mafano, umalandanso za mʼnyumba zopembedzera mafanowo?
23 Biyi wa bi ngyiri nimi tron, bina kpa Irji tsri ni mi lah tree u wa ba hu tron na?
Kodi iwe amene umadzitama ndi Malamulo, umamuchititsa manyazi Mulungu posamvera Malamulowo?
24 Naki ba kpa nde Irji tie meme ni mi bi kora nitu mbi.
Monga kwalembedwa, “Dzina la Mulungu likuchitidwa chipongwe pakati pa a mitundu ina chifukwa cha inu.”
25 Gbi gbi you grji ana he ni mah ma ni yi. Inde bi kiyaye doka, aman inde bi yi wa bina hu doka na, you grji bi akam ti na ana you grji na.
Mdulidwe umakhala ndi phindu ngati usunga Malamulo, koma ngati sumvera Malamulo, iweyo umakhala ngati kuti sunachite mdulidwe.
26 Nakima inde ndji wa bana you grji ni u na, ani kiyaye bukatu tron wawu'u bana iya ban wa bana you grji ni wu ni matsayi wa ba you grji niwu?
Ngati amene sanachite mdulidwe achita zomwe zili mʼMalamulo, kodi sadzatengedwa ngati ochita mdulidwe?
27 Nakima inde ndji wa ba you grji ni wu na u yi ani kiyaye dokoki ba wawu, ana yah sharanta yi bi you grji u tron na? Naki a he inde bi hei ni tron ba nha, aman ana hu tron na.
Munthu amene sanachite mdulidwe mʼthupi koma amamvera Malamulo adzakutsutsa iwe wosamvera Malamulowe, ngakhale kuti uli nawo Malamulo olembedwawo.
28 Naki wawu na hi Bayahude ni ra na, ana wa ba you grji nda han tan na
Myuda weniweni si amene angooneka ngati Myuda pamaso pa anthu, ndipo mdulidwe weniweni si umene umangochitika mʼthupi pamaso pa anthu.
29 Naki a Bayahude u mi, naki me ba yo grji u suron mba Ruhu ndindi ana ibe na, bibi ndji kima ana ndji ni zu wo ni u na, se Irji.
Ayi, Myuda weniweni ndi amene ali Myuda mu mtima mwake, ndipo mdulidwe weniweni ndi wa mtima, wochitika ndi Mzimu, osati ndi malamulo olembedwa. Woyamikira munthu wotere ndi Mulungu, osati anthu ayi.

< Romawa 2 >