+ Matiyu 1 >
1 Vuvu u Yesu Kristi ivren Dauda, ivren u Ibrahim.
Buku lofotokoza za mʼbado wa Yesu Khristu mwana wa Davide, mwana wa Abrahamu:
2 Ibrahim a ngrji Ishaku, Ishaku ka ngrji Yakubu, u Yakubu a ngrji Yahuda ni ba mrli vayi ma.
Abrahamu anabereka Isake, Isake anabereka Yakobo, Yakobo anabereka Yuda ndi abale ake.
3 Yahuda a ngrji Perez mba Zerah ngrji u Tamar, Perez ngrji Hezron, u Hezron ngrji Ram.
Yuda anabereka Perezi ndi Zara, amene amayi awo anali Tamara. Perezi anabereka Hezironi, Hezironi anabereka Aramu.
4 Ram ngrji Amminadah, Amminadah ngrji Nahshon, u Nahshon ngrji Salmon.
Aramu anabereka Aminadabu, Aminadabu anabereka Naasoni, Naasoni anabereka Salimoni.
5 Salmon ngrji Boaz ngrji Rahab, Baoz ngrji Obadiya ngrji u Rautha, Obadiya ngrji Jesse.
Salimoni anabereka Bowazi amene amayi ake anali Rahabe, Bowazi anabereka Obedi amene amayi ake anali Rute, Obedi anabereka Yese.
6 U Jesse ngrji ichu Dauda. Ichu Dauda ngrji Suleman wa iyima ana wa Uraya
Yese anabereka Mfumu Davide. Ndipo Davide anabereka Solomoni, amene amayi ake anali mkazi wa Uriya.
7 Suleman a nu ngrji Rehoboam, Rehoboam a ngrji Abijah u Abijah ngrji Asa.
Solomoni anabereka Rehabiamu, Rehabiamu anabereka Abiya, Abiya anabereka Asa,
8 Asa ngrji Jehoshafat, Jehoshafat ngrji Joram, Joram ngrji Uzziya.
Asa anabereka Yehosafati, Yehosafati anabereka Yoramu, Yoramu anabereka Uziya.
9 Uzziya ngrji Jotham, Jotham ngrji Ahaz u Ahaz ngrji Hezekaya.
Uziya anabereka Yotamu, Yotamu anabereka Ahazi, Ahazi anabereka Hezekiya.
10 Hazekaya a ngrji Manaseh, Manaseh a ngrji Amon u Amon ngrji Yosiya.
Hezekiya anabereka Manase, Manase anabereka Amoni, Amoni anabereka Yosiya.
11 Yosiya ngrji Yekoniya ni mrli vayi ma wiere me ni nton wa ba vu ba hi ni Babila.
Yosiya anali atabala Yekoniya ndi abale ake pamene Ayuda anatengedwa ukapolo kupita ku Babuloni.
12 U wa ba nji ye Babila, Yekoniya ngrji Shealtiel u Shealtiel ngrji Yerubabel.
Ali ku ukapolo ku Babuloni, Yekoniya anabereka Salatieli, Salatieli anabereka Zerubabeli.
13 Yerubabel ngrji Abuid, Abuid ngrji Eliakim, u Eliakim ngrji Azor.
Zerubabeli anabereka Abiudi, Abiudi anabereka Eliakimu, Eliakimu anabereka Azoro.
14 Azor ngrji Zadok, Zadok ngrji Achim u Achim ngrji Eliud.
Azoro anabereka Zadoki, Zadoki anabereka Akimu, Akimu anabereka Eliudi.
15 Eliud ngrji Eleazer, Eleazer
Eliudi anabereka Eliezara, Eliezara anabereka Matani, Matani anabereka Yakobo.
16 ngrji Matthan, u Matthan ngrji Yakubu. U Yakubu ngrji Yusufu illon Maryamu wa a ngrji Yesu wa ba yo'u din Kristi.
Yakobo anabereka Yosefe, mwamuna wa Mariya. Mariyayu ndiye anabereka Yesu wotchedwa Khristu.
17 To inzan ba wawu rji ni Ibrahim hi Dauda ba wlon don zia, rji ni Dauda hi ntton wa ba vu hi ni Babila bahi izan zia, u rji ni ni ntton u wa bahe ni Babila hi ni ye Kristi ba nzan wlon don zia.
Kuyambira pa Abrahamu mpaka pa Davide, pali mibado khumi ndi inayi. Ndipo kuyambira pa Davide mpaka pamene Ayuda anatengedwa kupita ku ukapolo ku Babuloni, pali mibado khumi ndi inayi. Ndiponso kuyambira nthawi ya ukapolo ku Babuloni mpaka pamene Khristu anabadwa, palinso mibado khumi ndi inayi.
18 Ingrji Yesu Kristi ahe towa: wa ba nna yima Maryamu ni Yusufu gben ntton wa baka gran kpa, u nne Ruhu tsatsar ye riwu.
Kubadwa kwa Yesu Khristu kunali motere: Amayi ake, Mariya, anapalidwa ubwenzi ndi Yosefe, koma asanagone malo amodzi, anapezeka ali woyembekezera mwana mwa mphamvu ya Mzimu Woyera.
19 U Yusufu illon ma indi u klu Rji, nda na son nno shan na, a cu sron ma rju ni gran nda kama ni wu niyay'bi (aboye)
Popeza Yosefe mwamuna wake anali munthu wolungama, sanafune kumuchititsa manyazi pomuleka poyera. Choncho anaganiza zomuleka mosaonetsera.
20 Amma, asi tamre towa, u malaika Baci ka ye niwu ni rah nda tre, “Yusufu, ivren Dauda, na klu sisri ban wame Maryamu na, don ikpie a wrji anne ma, a u Ruhu tsatsar.
Koma akuganiza zimenezi, taonani, mngelo wa Ambuye anamuonekera mʼmaloto nati, “Yosefe mwana wa Davide, usaope kumutenga Mariya kukhala mkazi wako, chifukwa mwana akuyembekezerayo ndi wochokera kwa Mzimu Woyera.
21 Ani ngrji vrenlon wa u yowu ndi Yesu, don ani kpa ndi ma cuwo ni gbugbu latre mba.
Ndipo adzabala mwana wamwamuna, udzamutcha dzina lake Yesu; pakuti Iyeyo adzapulumutsa anthu ake ku machimo awo.”
22 To, ahe to yi don ndu tre Baci he na wa a hla din.
Zonsezi zinachitika kukwaniritsa zimene Ambuye ananena mwa mneneri kuti,
23 “To mba, vivren wa ri wa ana to lillona ani ye he nne nda ngrji vrenlon wa ba yo wa ndi Imanuwal” wa hi riri ni “Irji he nita”
“Onani namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli,” kutanthauza kuti, “Mulungu ali nafe.”
24 U Yusufu, gbla sh'me ni nah tie ikpie wa Malaika hla niwu nda hi ka ban wa-a hi ni kpama.
Yosefe atadzuka, anachita zomwe mngelo wa Ambuye uja anamulamulira. Iye anamutenga Mariya kukhala mkazi wake.
25 Ana rlihe toh wa-a sai wa a ngrji vren ma u mumla. Ayo nde ma di Yesu.
Koma sanagone malo amodzi mpaka mwanayo atabadwa ndipo anamutcha dzina lake Yesu.