< Ndu Manzaniba 7 >
1 Ninko Prist a tre ndi, “ikpi biyi ba janji?”
Kenaka mkulu wa ansembe anafunsa Stefano kuti, “Kodi zimene akukunenerazi ndi zoona?”
2 Istifanus a tre ndi “mir ya ni bati, wo me'. Irjhi wu shulu a tsro kpama ni timbu Ibrahim, niwa ana he ni Mesopotamia, ri nda ka son ni Haran;
Stefano anayankha kuti, “Abale ndi makolo, tamverani! Mulungu waulemerero anaoneka kwa kholo lathu Abrahamu pamene ankakhala ku Mesopotamiya, asanakakhale ku Harani.
3 A lha wu ndi “Don ngbran meme me baba mir vayime, ni rhu hini ngbran meme wandi mi tsro wu.
Mulungu anati, ‘Tuluka mʼdziko lako, siya abale ako, ndipo pita ku dziko limene ndidzakusonyeza.’
4 Mle, a lu don ngran meme Chaldeans nda ka kru ni Haran, rhi niki, ni wa tima a qu'a, Irjh i a njiwu ye ni ngbran meme yi, wa bi ki nituma'a.
“Ndipo iye anatulukadi mʼdziko la Akaldeya ndi kukakhala ku Harani. Atamwalira abambo ake, Mulungu anamuchotsa kumeneko ndi kumubweretsa mʼdziko lino limene inu mukukhalamo tsopano.
5 Ana fon nklan bubu nu du kpa zi ni h'pu mana, a'an, ko wa ani kaza satuma me. Ama, a shirhi, ko da shike Ibrahim ana he ni vivren rhina-andi ani nu bubu ti uma du mba h'puma du k'ma tiwumba kasai-kasai.
Mulungu sanamupatse cholowa kuno, ngakhale kadera kakangʼono kadziko. Koma Mulungu anamulonjeza kuti adzapereka dziko lino kwa iye ndi kwa zidzukulu zake, ngakhale kuti pa nthawi imeneyi analibe mwana.
6 Irjhi a si a tre niwu tyi, andi h'puma ba son ki ni gbu ndi bari u ndhi bi bgukima ba vu ba ti grand nda du ba tiya wu se derinzia.
Mulungu anayankhula motere kwa iye: ‘Zidzukulu zako zidzakhala alendo mʼdziko lachilendo, ndipo zidzakhala akapolo ndi kuzunzidwa zaka 400.’
7 Ama mi sharanta ni dhi bi wa ba tindu gran nibawua, kpe wa irji tre'a hu gon kima, ba rhu don bubuki nda ye kuqungba rhu nda gbresan ni mu ni bubu yi.
Mulungu anati, ‘Ine ndidzalanga dziko limene zidzukulu zako zidzagwireko ukapolo, ndipo pambuyo pake akadzatuluka mʼdzikolo adzandipembedza Ine pamalo pano.’
8 Niki Irji a nu Ibrahim shirhi wu hanbru ni duta tika, rhini kima, Ibrahim a ngrjhi Ishaku nda hanbru ma ni riwu tandra baya ngrjhi. Ishaku ngame a ngrjhi Yakubu, u Yakubu a ye ngrjhi bacimbu Wlondoha ba.
Kenaka Mulungu anachita pangano la mdulidwe ndi Abrahamu. Ndipo Abrahamu, anabereka Isake, namudula ali ndi masiku asanu ndi atatu. Ndipo Isake anabereka Yakobo, Yakobo anabereka makolo khumi ndi awiri aja.
9 Bacimbu ba ti ngu ni Yusufu, ba banwu le hi ni masar ama Irjhi a he ni wu.
“Makolo athu anachita nsanje ndi Yosefe ndipo anamugulitsa kuti akakhale kapolo ku Igupto. Koma Mulungu anali naye
10 nda kpa' chuwo ni ya wa a hon tuma'a. A kpayem ni Yusufu mba mren wu tondindi ni shishi kikle Ichu Firona wu Masar wa a ban wu sa ni ruron gomna wu Masar mba nitu koma wawu.
ndipo anamupulumutsa iye kumasautso ake onse. Mulungu anamupatsa Yosefe nzeru ndi chisomo pamaso pa Farao mfumu ya ku Igupto, kotero mfumuyo inamuyika iye kukhala nduna yayikulu ya dziko la Igupto ndiponso nyumba yake yonse yaufumu.
11 Ni ntukima, meme iyon a ri kagon Masar mba Canaan, ni meme ya wa a du ba timbu ba wa biri hamma.
“Kenaka munalowa njala mʼdziko la Kanaani, kotero kuti anthu anavutika kwambiri, ndipo makolo athu sanathe kupeza chakudya.
12 Niwa Yakubu a wo ndi wlo biri he ni Masar a ton ba timbu hi ni zrenmba wu mumla.
Pamene Yakobo anamva kuti ku Igupto kunali tirigu, iye anatuma makolo athu ulendo woyamba.
13 Ni zren wu ha, Yusufu a tsro tuma ni ba mirvayima, u firona a mla to mmla Yusufu nikima.
Pa ulendo wawo wachiwiri, Yosefe anadziwulula kwa abale akewo ndipo Farao anadziwa za banja la Yosefe.
14 Yusufu a ton mir vayima du ba k'ma hi hla ni timba du vu mmla wawu, ndhi saba'in don ton mba, nda ye ni Masar.
Izi zinachitika, Yosefe anayitanitsa abambo ake Yakobo ndi banja lonse, onse pamodzi analipo 75.
15 Nituki, Yakubu a grjhi hi ni Masar nda ka que niki, ni wawu ba timbu ngame.
Motero Yakobo anapita ku Igupto, kumene iye ndiponso makolo athu anamwalira.
16 Ba vu ba hi ni Shekem, nda ka rhu'ba ni ibe wa titi Ibrahim a le nitu nkle silva ni wo mir Hamor wu Shekem.
Mitembo yawo anayinyamula ndi kupita nayo ku Sekemu kumene inayikidwa mʼmanda amene Abrahamu anagula kochokera kwa ana a Hamori ku Sekemuko.
17 Niwa nton wa shirhi a ye weiweire, shirhi wa Irjhi a ti ni Ibrahim. Indhi ba ba ki bran gbugbuwu ni masar.
“Nthawi itayandikira yakuti Mulungu achite zimene analonjeza kwa Abrahamu, mtundu wathu unakula ndi kuchuluka kwambiri mu Igupto.
18 Da a tsra wa kikle chu ri a hon ni ruron wu masar wa ana to njo nitu Yusufu na.
Pambuyo pake mfumu yatsopano imene sinkamudziwa Yosefe, inayamba kulamulira dziko la Igupto.
19 A kyurh ndhimbu nda yo ba ni gbengble du ba rhuni mir nhanha lilon mbu ni duba que.
Mfumuyo inachita mwachinyengo ndi mtundu wathu ndi kuwazunza kuti ataye ana awo akhanda kuti afe.
20 Ni nton kima ba ngrhi Musa, wa ka bi kpokpome ni Rji ba lura ti wua tra ni ko tima.
“Pa nthawi imeneyo Mose anabadwa, ndipo anali wokongola kwambiri. Iye analeredwa mʼnyumba ya abambo ake kwa miyezi itatu.
21 Niwa ba banwu ka zi ni ra, vrenwa Firona a ban'u ti wuma nda njiwu ti vren ma.
Atakamutaya, mwana wamkazi wa Farao anamutola nakamulera ngati mwana wake.
22 Ba yo Musa ni bubu tsro mba, niki a mla to tsro ndindi nitu kpi kankan wu bi U bi masarawa ba, ndu ni he ma ba bi hikima.
Mose anaphunzira nzeru zonse za Aigupto, ndipo anali wamphamvu mʼmawu ndi ntchito zake.
23 Niwa isema wu ngrjhi ba ti weiweire ni tso-tra-don nza (arbain), a kpre suron du zren hi ni mir vayi ma, ih'pu Isra'ila.
“Mose ali ndi zaka makumi anayi, anaganizira zokayendera abale ake Aisraeli.
24 A krito basi ndhi Israila ri ya'. Musa alu kpa nyu ni ndhi wa basia tiwu ya'a nda wru gu masar wuh.
Iye ataona mmodzi wa iwo akuzunzidwa ndi Mwigupto, anatchinjiriza Mwisraeliyo, namupha Mwiguptoyo.
25 A yotrendi vayima ba mla to ndhi a hi Irjhimba ni tindu ni wu du ba bguc'bu ni womba, ama ba ka'a na mla to na.
Mose anaganiza kuti abale ake adzazindikira kuti Mulungu anamuyika kuti awapulumutse koma iwo sanazindikire.
26 Nivi wuhama, a to ndhi harhi ba si tsi, wa ay'e gaba nda tre ndhi, 'Lilon, be mir vayi; a hi ngye du yi ni tsi kpambi?
Mmawa mwake Mose anaona Aisraeli awiri akukangana. Iye anayesa kuwayanjanitsa ponena kuti, ‘Amuna inu, ndinu abale; chifukwa chiyani mukufuna kupwetekana?’
27 Irimba wandi wa wuhi a kpa la ni kpanma'a, a tru yo kosan nda tre ndi “A nha banwu sa nitumbu ichu, wu ga tre nitawu?
“Koma munthu amene amavutitsa mnzakeyo anakankha Mose ndipo anati, ‘Ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza.
28 Wu son wu U me to wandi wu wuu gu masra laren'a?
Kodi ukufuna kundipha monga momwe unaphera Mwigupto uja dzulo?’
29 Niwa Musa a tre yi'a, a vu tsu wru nda ka son tindi u tsir ni kasa Midian, niki a ka ngrjhi mri lon ha.
Mose atamva mawu awa anathawira ku Midiyani, kumene anakhala mlendo ndipo anabereka ana amuna awiri.
30 Niwa ise tso-tsra-don-nzang ati ka hi, U malaika a tsro tuma niwu ni ngbranmiji ni kikle ngblu Sinai, ni lu ni miji.
“Ndipo patapita zaka makumi anayi mngelo anaonekera kwa Mose mʼmalawi amoto pa chitsamba mʼchipululu pafupi ndi Phiri la Sinai.
31 Niwa Musa a to ilu'a, a ti sisir kpe wa a to ni shishima, nda lu si zren hi weiweire du ni mla ya, a kri wo ilan Baci ni tre ndi,
Iye ataona zimenezi, anadabwa. Akupita kuti akaonetsetse pafupi, Mose anamva mawu a Ambuye:
32 Mmyi mi Irjhi wu ba timbi, Irjhi wu Ibrahim, mba Ishaku, mba wu Yakubu” Musa kri si tsenzankpa nda na la vu suron nda ya ngana.
‘Ine ndine Mulungu wa makolo ako, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.’ Mose ananjenjemera chifukwa cha mantha ndipo sanalimbe mtima kuyangʼananso.
33 Baci a lhawu ndi, jhu lagban wa ahe ni za me rhu domin bubu wa wu kri mba ahi tsatra bubu.
“Ndipo Ambuye anati kwa Mose, ‘Vula nsapato zako, pakuti malo amene wayimapo ndi opatulika.
34 Mi to iyawa basi nu ndhimu ni masra mi wo gran yimba, m'ba mi grjhiye ye chubachuwo. ye zizan, mi ton hi ni masra.
Ine ndaona ndithu mazunzo a anthu anga amene ali ku Igupto. Ndamva kulira kwawo choncho ndabwera kuti ndiwapulumutse. Tsopano tiye ndikutume ku Igupto.’
35 Musa yi, wa bana kamba niwu, niwa bana tre ndi, “a nha yo tituchu mba wu ga'atre nitawu'a?” a hi wawuyi wa Irjhi a ton du hi ti chu mba wu chubachuwo. Irjhi a ton wu hi zuni wo malaika wa a tsro tuma ni Musa ni miji'a.
“Uyu ndi Mose yemwe uja amene Aisraeli anamukana ndi kunena kuti, ‘Ndani anakuyika kuti ukhale wotilamulira ndi wotiweruza?’ Iyeyo anatumidwa ndi Mulungu mwini kuti akakhale wowalamulira ndiponso mpulumutsi, mothandizidwa ndi mngelo amene anamuonekera pa chitsamba.
36 Musa njiba rhuni masra, kima a hu gon ti kpi bi wa ndhi ba kaahon to tuma, baba bi tron yani masra mba kikle ma wu Reeds, mba ni tsutsu miji niwa ba ti se tsro-tra-don-nza (arbain).
Iye anawatulutsa mu Igupto ndipo anachita zodabwitsa ndi zizindikiro zozizwitsa mu Igupto, pa Nyanja Yofiira, ndiponso mʼchipululu kwa zaka makumi anayi.
37 Ahi Musa kima wa a lhani ndhi bi Israila ndi, “Irjhi ni nzu anabi ri hon yiwu rhinimi vahimbi, anabi ton me”.
“Uyu ndi Mose uja amene anati kwa Aisraeli, ‘Mulungu adzawutsa pakati pa abale anu mneneri ngati ine.’
38 Ndhi yi yi a he niba ni tsutsu miji mba malaika wa atre niwu nitu kikle ngblu Sinai, wa ahe niba timbu, mba wa a kpa lantre wu sisren ye nota.
Iyeyu anali mʼgulu la Aisraeli mʼchipululu pamodzi ndi mngelo amene anamuyankhula pa phiri la Sinai ndiponso makolo athu; ndipo Mose analandira mawu amoyo kuti atipatse ife.
39 Ama ba timbu ba kamba ni hutrema, ba tru lhega wru ni kpamba, du ni misuron mba k'ma hi ni masra.
“Koma makolo athu anakana kumumvera iye. Iwo anamukana iye ndipo mʼmitima mwawo anatembenukira ku Igupto.
40 Ni nton kima ba lha ni Hasuna, “La' mir rjhi ni tawu wa a ni njita zren hi. Musa yi, a njita wru rhini meme masra, kina toh ikpe wa a ka tiwu a na
Iwo anati kwa Aaroni, ‘Bwera utipangire milungu imene idzititsogolera. Kunena za Mose amene anatitsogolera kutuluka mʼdziko la Igupto, sitikudziwa chimene chamuchitikira.
41 Niki ba la' vrenlando ni ri baki nda nji ba hadaya (ton?) ni gunki waba la'a, nda ngiri nitu ndu wu womba.
Iyi ndi nthawi imene anapanga fano la mwana wangʼombe. Anapereka nsembe kwa fanoli nachita chikondwerero kulemekeza ntchito ya manja awo.
42 Irjhi a kaba chuwo du ba boata ni tsitse ni shulu, tohwa bana nha ni mi vunvu wu ba anabawaba. “Bi gon nimu nma miji mba haday ni ise tso-tsra-don-nza wa bi na he ni tsutsu miji'a ko mri Isra'ila?
Koma Mulungu anawafulatira, nawapereka kuti apembedze zolengedwa zakumwamba. Zimenezi zikugwirizana ndi zimene zinalembedwa mʼbuku la aneneri kuti, “‘Kodi pa zaka makumi anayi zimene munakhala mʼchipululu muja munkandibweretsera nsembe ndi zopereka, inu nyumba ya Israeli?’
43 Bi kpa ka'che' molech mba ntse wu vi irjhi Rephan, mba whi ki ba biti ni du yi kugungbarhu ni nzub hon. Nikima, mi vu yi vra zan gbran Babylon.
Ayi, inu mwanyamula tenti ya Moloki ndi nyenyezi ya mulungu wanu Refani, mafano amene munapanga kuti muziwapembedza. Chifukwa chake, Ine ndidzakutumizani kutali, kupitirira dziko la Babuloni.
44 Ba timbu bana he ni ka'che' wu kpewa ba to ni shishimba ni tsutsumiji, me wa Irjhi a noba niwa a tre ni Musa'a, andi du ti tsra ni wa a toa.
“Makolo athu anali ndi tenti ya msonkhano pakati pawo mʼchipululu. Anayipanga monga momwe Mulungu anawuzira Mose, molingana ndi chithunzi chimene Mose anachiona.
45 Hu kima, ba timbu ni wo Joshua ana njiba to ninkomba, ba kpa ka'achea nda njiwu hu kpamba niwa ba vu meme a kpa. Irjhi a kpa meme ni wo gbungblu bi bubuki nda zu ba wru ni shishi ba timbu. kaachea a son ni meme'a ye ni nton Dawuda.
Makolo athu, atayilandira Tentiyo, anabwera nayo motsogozedwa ndi Yoswa pamene analanda dziko la mitundu imene Mulungu anayipirikitsa pamaso pawo. Tentiyo inakhala mʼdzikomo mpaka nthawi ya Davide,
46 Wa Irjhi a kpanyme ni wu nda lhawu ni du wa bubu son ni ko Yakubu.
amene anapeza chisomo pamaso pa Mulungu ndipo anapempha kuti amʼmangire nyumba Mulungu wa Yakobo.
47 Ana Suleimanu mba amme ko ni Irjhi.
Koma anali Solomoni amene anamanga nyumbayo.
48 Ama kitoh ndi kikle wushu na son ni ko wa wondhi mme na, toh wa anabawaba ba tre.
“Komatu, Wammwambamwambayo sakhala mʼnyumba zomangidwa ndi anthu. Monga mneneri akunena kuti,
49 “Shulu mbahi bubu son tu chu mu, u meme mba hi kpran roro saza mu. A bibi ko rime wa bi mme ni mu inj Baci, ka a ngye bubu u kusi mu?
“‘Kumwamba ndi mpando wanga waufumu, ndipo dziko lapansi ndi chopondapo mapazi anga. Kodi mudzandimangira nyumba yotani? Akutero Ambuye. Kapena malo opumuliramo Ine ali kuti?
50 Ana womu mba ti kpi biyi wawu na?
Kodi si dzanja langa linapanga zonsezi?’
51 Biyi bi sen tu, biwa bana he kacia surona mba iton mba na, chachu bi kan bi ruhu tsatsra, bi ti to ba tumbi bana ti.
“Anthu wokanika inu, osachita mdulidwe wa mu mtima ndi a makutu ogontha! Inu ofanana ndi makolo anu. Nthawi zonse mumakana kumvera Mzimu Woyera:
52 Ahi anabi rime wa ba timbu bana tibayana. Ba wuh anabawa wa ba wru guci ni ye ndi wa ba yo wu di 'Analatre na', u zizan biyiyi bibi le ni wu dini wu'u ngame.
Kodi analipo mneneri amene makolo anu sanamuzunze? Iwo anapha ngakhale amene ananeneratu za kubwera kwa Wolungamayo. Ndipo tsopano inu munamupereka ndi kumupha Iye.
53 Biyi wa bi kpa doka wa malaika mba ba mla yowozi, ama bina kpa ti dun na.
Inu amene munalandira Malamulo amene anaperekedwa ndi angelo ndipo simunawamvere.”
54 Niwa bi niko bawo kpi biyi wa ka ri ba ni suron baka tan nyren ni Istifanus.
Atamva zimenezi, iwo anakwiya kwambiri ndipo anamukukutira mano.
55 Don a shu ni Ruhu tsatsra, a nzu ya shulu nda toh dokaka Rji, nda to Yesu kri ni wo korhi wu Irjhi.
Koma Stefano, wodzaza ndi Mzimu Woyera, anayangʼana kumwamba ndipo anaona ulemerero wa Mulungu ndiponso Yesu atayimirira ku dzanja lamanja la Mulungu.
56 Istifanus a tre ndi. “Toh, mi si to ni shishimu, shulu bwu, U vren Ndhi a kri ni worhi wu Irjhi
Stefano anati, “Taonani, ndikuona kumwamba kotsekuka ndiponso Mwana wa Munthu atayimirira ku dzanja la manja la Mulungu.”
57 Nitu ki, biwaba son ni tra son bi ninkoa ba ka tonmba, nda yo gro ni kikle lan, nda lu honwu nitu kpe riri.
Koma iwo anatseka mʼmakutu mwawo, ndipo anafuwula kolimba, onse anathamangira kwa iye,
58 Ba gbi'e wru ni mi gbu'a, nda ni ta ni tita. Bi wa ba toh zren kpeyi ba ju nklonba wu kora nda kazi ni za vrenze ri wa ndema a hi shawulu.
anamukokera kunja kwa mzinda ndipo anayamba kumugenda miyala. Mboni zinasungitsa zovala zawo kwa mnyamata otchedwa Saulo.
59 Niwa basia ta Istifanus ni tita, a sia yo baci nda ni tre ndi “Baci Yesu, kpa viri mu.
Akumugenda miyala, Stefano anapemphera kuti, “Ambuye Yesu, landirani mzimu wanga.”
60 A kuqungbarhu nda yo ni kikle lan Baci, na vule nitu latre wa ba ti yi na” Niwa a tre kle, a ku rhoku kruna
Ndipo anagwada pansi nafuwula mwamphamvu kuti, “Ambuye musawawerengere tchimoli.” Atanena mawu amenewa anamwalira.