< Ndu Manzaniba 26 >
1 Niki Agrippa a tre ni Bulus, “Wu ka tre kime.” Nikima Bulus a nmerju ni woma nda lu tre wu kpa tuma chuwo.
Ndipo Agripa anawuza Paulo kuti, “Takulola kuti unene mawu ako.” Paulo anatambasula dzanja lake nayamba kudziteteza kuti,
2 “Mi ban ndi mi ngyiri ni kpamu, Ichu Agrippa, ni wa mi nji tre mu niye ni shishime luwa, nitu wawu kpi meme wa Yahudawa ba nji ye nha nimu niwuu;
“Mfumu Agripa ine ndikudziyesa wa mwayi kuyima pamaso panu lero lino ndi kudziteteza, kutsutsa zonse zimene Ayuda andinenera,
3 kima me nitu wu to zan tu ni tu nkon zren Yahudawa rhini sen. Niki, mi bre du u wome ni kru sron.
ndipo makamaka chifukwa inu mukudziwa bwino miyambo yonse ya Chiyuda ndiponso zonse zimene amatsutsana. Nʼchifukwa chake ndikukupemphani kuti mundimvetsere moleza mtima.
4 Njanji, Yahudawa wawu ba to zren son mu rhini wa mi vren nze ni meme mu mba ni Urushelima.
“Ayuda onse akudziwa za moyo wanga mmene ndakhalira kuyambira ndili mwana, kuchokera pachiyambi cha moyo wanga mʼdziko lathu ndiponso mu Yerusalemu.
5 Ba to nitumu rhini ni mumla, batini son nyme niki, nitu mison na Farasii, grji bi kri gbangban ni nkon hu Irji mbu.
Iwo akundidziwa kuyambira kalekale ndipo angathe kuchitira umboni kuti ndakhala ndili Mfarisi moyo wanga wonse, mmodzi wa gulu limene limasamala chipembedzo chathu koposa.
6 Zizan mi kri ni wayi du ba gaatre nimu nitu yo sron mu ni yo sron kpe ni shishi wa Irji a ti ni ba titi mbu.
Ndipo tsopano ndikuyimbidwa mlandu lero chifukwa cha chiyembekezo changa pa zimene Mulungu analonjeza makolo athu.
7 A he nitu yo sron kpe ni shishi wa ba grji wlon don ha ba ba yo sron wu kpa niwa ba nzu nde Irji hon ni chu mba ni virhi. Wa a he nitu yo sron a, Ichu Yahudawa ba ban nha me.
Ili ndi lonjezo limene mafuko athu khumi ndi awiri akuyembekezera kuti likwaniritsidwe pamene akupembedza Mulungu molimbika usana ndi usiku. Wolemekezeka Mfumu, nʼchifukwa cha chiyembekezo chimenechi Ayuda kuti akundiyimba mlandu.
8 A ngye nizu du mla ya ni kpanyme ndi Irji ni nzu indji lu rjini kwu?
Nʼchifukwa chiyani ena a inu mukuganiza kuti nʼkosatheka kuti Mulungu aukitse akufa?
9 Zizan, a toki, Ime me mina ta mren ndi mi ti kpi gbugbuwu nitu ka nde Yesu wu Nazarat su.
“Inenso ndimaganiza kuti ndimayenera kuchita zinthu zambiri pofuna kuthana ndi dzina la Yesu wa ku Nazareti.
10 Mi ti kpi biyi ni Urushelima, Mi vu loyo ni mi tratro gbugbu indji tsatsra wu Irji, ni vunvu kpanyme wa mi kpa rhini ninkon Prist, mba niwa ba sia wuuba, mi yo wo nyime mu nitu kima.
Ndipo izi ndi zimene ndinazichita ku Yerusalemu. Ndi ulamuliro wa akulu a ansembe, ine ndinayika mʼndende oyera mtima ambiri, ndipo pamene amaphedwa, ine ndimavomereza.
11 Mi ti ba ya, nton gbugbuwu ni mi Sinagog, mba ni ta tsra yoba ni gbengblen du ba tre meme ntiu Irji. Mi ta vra ni nfu nitumba, mba nini tiba ya ka rhini igbu wu meme bari.
Nthawi zambiri ndinkapita mʼsunagoge iliyonse kuti alangidwe, ndipo ndinayesera kuwakakamiza kuti achitire chipongwe Mulungu. Mu mkwiyo wangawo, ndimapita ngakhale ku mizinda yachilendo kuti ndikawazunze.
12 Niwa mi sia ti toyi, mi hini Damaskus ni yawo kpanyme mba nu nkon rhini kikle Prist;
“Pa ulendo wina wotere, ndikupita ku Damasiko ndi mphamvu ndi ulamuliro ochokera kwa akulu a ansembe,
13 mba ni nkon, hiki, ni tsutsu irji, ichu, mi to kpan lu rjini shulu wa a kpan zan irji, nda bwu kpan kagon me baba indji biwa bana si zren hume.
Wolemekezeka Mfumu, nthawi ya masana pamene ndimayenda pa msewu, ndinaona kuwala kuchokera kumwamba koposa kuwala kwa dzuwa kutandizungulira ine pamodzi ndi anzangawo.
14 Niwa wawumbu ki kurjoku ni meme mi wo ilan ni tre ni me ni ilbe Ibraniyawa ndi Shawulu, Shawulu, u i tie me ya nitu ngye? A ni he ni ya ni du chuza too kpe wu ntsen nyu.
Tonse tinagwa pansi ndipo ndinamva mawu mʼChihebri akuti, ‘Saulo, Saulo chifukwa chiyani ukundizunza Ine? Nʼkovuta kulimbikira mtunda wopanda madzi.’”
15 Niki mi tre ndi, “Wu nha, Bachi?” I Bachi a sa mu ndi, 'A hi me Yesu wa wu si tiwu ya.
Ndipo ine ndinafunsa kuti, “Ndinu ndani Ambuye?” Ambuye anayankha kuti, “Ndine Yesu, amene iwe ukumuzunza.
16 Zizan lu kri ni zande; anitu ndu yi mi tsro kpamu niwu, nitu youyo ni tindu vrenko, mba wa wu vu bla nitu kpi wa wuto nitumu zizan mba kpi wa mi tsro ni ko shishi;
Tsopano dzuka ndipo imirira. Ine ndaonekera kwa iwe kuti ndikusankhe kuti ukhale mtumiki ndiponso mboni ya zimene waziona za Ine ndiponso zimene ndidzakuonetsa.
17 i mi kpau chuwo rhini wo indji ba mba rjini Bikora wa mi si ton ni hi niba,
Ine ndidzakulanditsa mʼmanja mwa anthu a mtundu wako ndiponso mwa anthu a mitundu ina. Ine ndikukutuma kwa iwo,
18 ni du hi bwu shishi mba, ndi kma ba sran rjini bwu hini kpan mba rjini son niwobrji shango hini Irji, ni du ba kpa rjini Irji, kpa wru latre mba (gado) wa mi nu ibiwa ba kri bi nitu kpanyme ni me.
kuti ukatsekule maso awo kuti atembenuke mtima kuchoka ku mdima ndi kulowa mʼkuwala, kuchoka ku mphamvu za Satana ndi kupita kwa Mulungu, kuti alandire chikhululukiro cha machimo awo ndi kukhala mʼgulu la amene akuyeretsedwa chifukwa chokhulupirira Ine.
19 Ni tu kima, Ichu Agrippa, mina kamu ni hutre ira wa a rjini shulu na;
“Nʼchifukwa chake Mfumu Agripa, sindinakane kumvera masomphenya wochokera kumwamba.
20 Mi hi ni bi Damaskus guchi, nda ka ri ni Urushelima, nda ka kagon gbungblu Judiya, mba ni bikora ngame, mi nu ba tondua, nitu du ba kma sran nda kma ye ni Irji, nda ti ndu wa a bi tsra ni kma sran sron mba.
Kuyambira kwa anthu a ku Damasiko, a ku Yerusalemu, a ku Yudeya konse ndi kwa anthu a mitundu inanso, ndinalalikira kuti akuyenera kulapa ndi kutembenukira kwa Mulungu ndikuti aonetse kulapa kwawo mwa ntchito zawo.
21 Nitu kima Yahudawa ba vu me lo nimi hekali nda ta son wuu me.
Ichi nʼchifukwa chake Ayuda anandigwira mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu nafuna kundipha.
22 Ni kima, me kpa zo wa a ye rji ni Irji, ye ni vi wu luwa, ndi ni kri ni nran hla ni bi tsitsa baba bi kikle ana kpe nkan na, hama niwa anabawa mba Musa ba tre ndi naiye he toki -
Koma Mulungu wakhala akundithandiza mpaka lero lino. Ine ndayima pano kuti ndichitire umboni kwa anthu onse otchuka ndi anthu wamba. Ine sindikunena zina zowonjezera koma zimene Aneneri ndi Mose ananena kuti zidzachitika.
23 ndi Kristi niye ti ya, nitu wawuyi ni guchi tashme rjini kwu, ndani bwuhla ikpan ni indji mbu mba ni bi kora.”
Iwo ananena kuti Khristu adzamva zowawa ndipo popeza Iye adzakhala woyamba kuuka kwa akufa, adzalalikira za kuwunika kwa anthu a mtundu wake ndiponso kwa anthu a mitundu ina.”
24 Niwa Bulus akle ngla kpama a, Festus a tre ni kikle lan, “Bulus, wu sran; to gbugbu tsro me du ni sran.”
Paulo akudziteteza, Festo anakweza mawu nati, “Wazungulira mutu Paulo! Kuphunzira kwako kwakuchititsa misala.”
25 I Bulus a tre ndi, “Mina sran na, wa azan bi Festus, mi si dbu bla lan tre wu njanji mba wu gaatre ndindi.
Paulo anayankha nati, “Wolemekezeka Festo, sindine wozungulira mutu. Zimene ndikunena ndi zoona ndiponso za nzeru.
26 Nitu Ichu to kpi biyi; niki mi tre ni gbengblen sron niwu, nitu mi nyme pempe ndi kpi biyi bana he ni bwu ni wu na, nitu ikpe biyi bana tiba ni kosan na.
Mfumu ikuzidziwa bwino zinthu izi, ndipo ndikuyankhula momasuka kwa iyo. Ine ndikukhulupirira kuti palibe kanthu nʼkamodzi komwe kamene sukukadziwa, chifukwa izi sizinachike mseri.
27 Wu kpanyme ni anabawa ba, Ichu Agrippa? Mi to ndi wu kpanyme.”
Mfumu Agripa, kodi mumakhulupirira mawu a aneneri? Ine ndikudziwa kuti mumakhulupirira.”
28 Agrippa hla ni Bulus nid, ni nton fiime toyi, wu son gbronmeyo dumi kma ti Krista?”
Kenaka Agripa anati kwa Paulo, “Kodi ukuganiza kuti mʼkanthawi kochepa kotere ungandikope kuti ndikhale Mkhristu?”
29 Bulus tre ndi, “Mi bre Irji ndi, anita nton fiime ka wu gbron me ana wu megen na, mba wawu biwa ba wo me luwa, du ba he too me, hama ni rjiri ij'bo wu ko tro yi.”
Paulo anayankha kuti, “Ngakhale kanthawi kochepa kapena nthawi yayitali, ine ndikupempha kwa Mulungu kuti osati inu nokha koma aliyense amene akundimva lero lino akhale monga ine, kupatulapo maunyolo okhawa.”
30 Niki Ichua lunde kri, i gomna mba Bernice ngame, baba biwa bana ki niba.
Mfumu inayimirira pamodzi ndi bwanamkubwa ndi Bernisi ndiponso anthu onse amene anakhala nawo pamodzi.
31 Niwa ba rju don kikle tra u son mba, ba si tre ni kpamba ndi, “Igu yi na ti kpe wa ani tsra u kwu ko ka u lo zi na.”
Inatuluka mʼchipindamo, ndipo pamene imayankhula inati, “Munthu uyu sanachite kanthu koyenera kuphedwa kapena kumangidwa.”
32 Agrippa a tre ni Festus ndi, kinina chu Iguyi chuwo hama wa ana bre hi to Kaisar.”
Agripa anati kwa Festo, “Munthu uyu akanamasulidwa akanakhala kuti sanapemphe zokaonekera kwa Kaisara.”