< Ndu Manzaniba 16 >

1 Bulus ngame aye ni Derbe mba ni Lystra, niki vrenko wu huuri wa ndema hi Timotia he, vren wa Yahudawa ri, wa a kpanyime niwu, ama tima ana ndji Greek.
Paulo anafika ku Derbe ndi Lusitra, kumene kumakhala ophunzira wina dzina lake Timoteyo. Amayi ake anali Myuda wokhulupirira, koma abambo ake anali Mgriki.
2 Mri vayi wa bana he ni Lystra mba Iconium bata tre ndindi ni tuma.
Abale a ku Lusitra ndi Ikoniya anamuchitira iye umboni wabwino.
3 Bulus ata son du zren huu ni tuki, a bau njinda gen-mbru niwu, ni du Yahudawa wa ba he ni bubu baki du ba toh, nitu bana toh ndi tima ana Greek.
Paulo anafuna kumutenga pa ulendo, kotero anachita mdulidwe chifukwa cha Ayuda amene amakhala mʼderalo pakuti onse amadziwa kuti abambo ake anali Mgriki.
4 Niwa ba hu nkon si hi zu nimi gba ba, basia zren nihu nkon tsatsra wa manzani ba mba bi ninkon biwa ba he ni Urushelima ba m'ha yo duba hu.
Pamene amayenda mzinda ndi mzinda, amafotokoza zimene atumwi ndi akulu ampingo ku Yerusalemu anagwirizana kuti anthu azitsatire.
5 Niki ekklisiya ba ba kpa ti ngbengblen ni kri gbangban nitu hu nkon'a nda du kri mbru mba a si hon chachu.
Kotero mipingo inalimbikitsidwa mʼchikhulupiriro ndipo anthu amachulukirachulukirabe tsiku ndi tsiku.
6 Bulus mba bi zren niwu ba zren zu ni ngbran Phrygia mba Galatia, nitu Ruhu Tsatsra ana ti gbuchu ndi du ba na d'bu lan tre'a ni ngbran Asia na.
Paulo ndi anzake anadutsa mayiko a Frugiya ndi Galatiya, Mzimu Woyera atawaletsa kulalikira Mawu a Mulungu ku Asiya.
7 Niwa ba zren ye ti weiweire ni Mysia, ba yo sron zuni Bithynia, ama Ruhu Yesu a zuba.
Atafika ku malire a Musiya, anayesa kulowa ku Bituniya, koma Mzimu wa Yesu sunawalole kutero.
8 Niki ba vu Mysia y'ba nda grjiye ni gbu Troas.
Ndipo iwo anadutsa Musiya ndipo anapita ku Trowa.
9 Bulus a toh ni mira ni chu; ndji ri wu Macedonia a kri ki nda si bre'u nda ni tre ndi, “Ye nita ni Macedonia ni ye zota.”
Nthawi ya usiku Paulo anaona masomphenya, munthu wa ku Makedoniya atayimirira ndi kumupempha kuti, “Bwerani ku Makedoniya, mudzatithandize.”
10 Niwa wa Bulus a hrara toki, ki krilu si wa nkon wuhi ni Macedonia, nitu ki ban ndi Irji mba yo ta du ta ki hi bla tre ndindi ni bawu.
Paulo ataona masomphenyawa, tinakonzeka kupita ku Makedoniya, kutsimikiza kuti Mulungu anatiyitana kuti tikalalikire Uthenga Wabwino.
11 Ki kuu zren hu ni nkon ma rhini Troas, ki hu trime nkon wa ani njita zu ni Samothrace, nda duta ka rhini Neapolis ni mbewa aka wu vi kima.
Kuchokera ku Trowa tinakwera sitima ya pamadzi kupita ku Samotrake ndipo mmawa mwake tinapitirira mpaka ku Neapoli.
12 Rhiniki, ki hi ni Philippi, wandi ana kikle gbu wu Macedonia, gbu wa a zan bi ni ndu wu ngbran kima mba wa aheni wo bi tuchu wu Romawa; ki ki niki wu vi wa a fon bran.
Kuchokera kumeneko tinapita ku Filipi, boma la Aroma ndiponso mzinda waukulu wa dera la Makedoniya. Tinakhala kumeneko masiku owerengeka.
13 Ni vi Sabbath (Chachu Sati), ki zren rhu ni kikle nkontra gbu'a wa a he ni kosan ba'a, bubu wa ki ban ndi ani bi wu bre. Ki kukhi ni tre ni mmba wa ba ye zontu ki'a.
Pa tsiku la Sabata tinatuluka mu mzindawo kupita ku mtsinje kumene timayembekezera kukapeza malo opempherera. Tinakhala pansi ndipo tinayamba kuyankhula ndi amayi amene anasonkhana pamenepo.
14 Iwari wu nde Lydia, wa a ta le ni ikpi nklon sru, rhi ni gbu Thyatira, wa ata hu nkon Irji, a yo ton si wota. Bachi a bwu sron ma ni du mla wo kpe wa Bulus asia tre'a.
Mmodzi wa amayi amene amamvetserawo ndi Lidiya amene amagulitsa nsalu zofiira, wochokera ku mzinda wa Tiyatira, ndipo amapembedza Mulungu. Ambuye anatsekula mtima wake kuti amve mawu a Paulo.
15 Niwawu mba bi koma, ba kpa batisma, nda bre ta ndi, “Bita kpanyme ni me ndi mi kri gbangban ni hu nkon Bachi, bi ka ye ni komu.” Nikima a weireta du ta kpanyme.
Iye ndi a mʼbanja lake atabatizidwa, anatiyitana kuti tipite ku nyumba yake. Iye anati, “Ngati mwanditenga ine kukhala wokhulupirira mwa Ambuye, bwerani mudzakhale mʼnyumba mwanga.” Ndipo anatiwumiriza ife kwambiri.
16 Niwa ki sia hi bubu bre, vrenwa ri wa ana gran, nda he ni brji wu toh kpe nda nran, a ye zontu nita. A ta nji nklen gbugbuwu ye ni ti ko ma nitu ndu nran wa ata ti'a.
Tsiku lina pamene timapita kumalo wopempherera, tinakumana ndi mtsikana wina amene anali ndi mzimu woyipa umene umanena zamʼtsogolo. Iye amapezera ndalama zambiri ambuye ake pa ulosi wake.
17 Iwa yi a zren si huba Bulus nda d'bu si hla ndi, “Biyi bi mri koh wu Irji wa a zan nzu hon. Ba ki bla nkon wu kpachuwo ni yiwu.”
Mtsikanayu anatsatira Paulo ndi ife, akufuwula kuti, “Anthu awa ndi atumiki a Mulungu Wammwambamwamba, amene akukuwuzani inu njira yachipulumutso.”
18 Asi ti toyi wu vi gbugbuwu. Ama Bulus, nitu vrenwa a yo nfu branbran, a k'ma nda hla ni brji'a ndi, “Mi mmha'u ni nde Yesu Kristi, rju ni kpa ma.” Mle a rju ni nton kima.
Iye anachita izi masiku ambiri. Kenaka Paulo anavutika mu mtima, natembenuka ndipo anati kwa mzimuwo, “Ndikukulamula iwe mʼdzina la Yesu Khristu kuti utuluke mwa iye!” Nthawi yomweyo mzimuwo unatuluka.
19 Niwa bi ti koma ba toh ndi nkon kubu mba a kle, ba vu Bulus mba Sila nda gbi ba hi ni tsutsu bubu wa ba le ni kpi, niwa bi ninkon gbu ba ki'a.
Pamene ambuye a mtsikana uja anazindikira kuti chiyembekezo chawo chopezera ndalama chatha, anagwira Paulo ndi Sila nawakokera ku bwalo la akulu.
20 Niwa ba nji ba ye nu bi blatre (Alkali), ba tre ndi ndji biyi ba nji iya rini kikle gbumbu. Ba Yahudawa.
Anawabweretsa iwo kwa oweruza milandu ndipo anati, “Anthu awa ndi Ayuda, iwo akuvutitsa mu mzinda wathu.
21 Ba bla tre njo wa ana he nitu nkon wa Romawa ba kpanyme duta hu na.
Ndipo akuphunzitsa miyambo imene ife Aroma sitiloledwa kuyilandira kapena kuyichita.”
22 Niki kpaandji ba lu hon wawu mba, nitu Bulus mba Sila; Alkali ba ba y'ba ba nklon mba ju nda mmha duba hloba ni kunkron j'bo.
Gulu la anthu linatsutsana ndi Paulo ndi Sila, ndipo woweruza milandu analamula kuti avulidwe ndi kumenyedwa.
23 Niwa ba hloba ni wo gbugbu nitu mba, ba tru ba sru ni ko wu tru nda mmha ndji wu tro'a du mla yo shishi nda na du ba gbuj'bu na.
Atawakwapula kwambiri anawaponya mʼndende, nalamula woyangʼanira kuti awasunge mosamalitsa.
24 Hu gon kpa mmha yi, ndji wu tro'a, a tru ba sru ni tra wu komi nda vu ba za mba lo nha ni kunkron gbangban.
Chifukwa cha mawu amenewa woyangʼanira ndende anakawayika mʼchipinda chamʼkati mwa ndende, nawamangirira miyendo yawo mʼzigologolo.
25 Mla tsutsu chu, Bulus mba Sila ba sia bre Irji nda ni yo se wu nzu Irji hon, i mbru biwa ba tro ba ngame'a ba sia sren ton niba.
Koma pakati pa usiku Paulo ndi Sila ankapemphera ndi kuyimba nyimbo zolemekeza Mulungu, ndipo akayidi ena ankamvetsera.
26 Niki, kikle grju meme a lu ti, nda du nchimeme wu ko tro a grju, mlee nkon ba wawu ba bwu yo hwo, mba ba sraka wa ba lo ba niwu'a ba si hle.
Mwadzidzidzi kunachitika chivomerezi champhamvu kotero kuti maziko a ndende anagwedezeka. Nthawi yomweyo zitseko zonse za ndende zinatsekuka, ndipo maunyolo a aliyense anamasuka.
27 Igu wu troba'a a lu sh'me ni nna nda toh nkontra kotro ba ba bwu kri ni hwo, a gbron guglo Inji wu nduma ndani wuutuma, nitu a ban ndi biwa ba troba ba rju nawo ye.
Woyangʼanira ndende uja atadzuka ku tulo, anaona kuti zitseko za ndende zinali zotsekula, ndipo anasolola lupanga lake nafuna kudzipha chifukwa ankaganiza kuti amʼndende athawa.
28 Bulus a yo gro ni kikle lan nda tre ndi, “Na ti kpame kpe na, nitu wawu mbu ki he ni wayi.”
Koma Paulo anafuwula kuti, “Usadzipweteke! Tonse tilipo!”
29 Igu wu troba a yo duba nji ilu kpan njiwu, nda tsutsu ri ni tsenza kpa mba sissri nda ka kukru ni shishi Bulus mba Sila.
Woyangʼanira ndendeyo anayitanitsa nyale, nathamangira mʼkati ndipo anadzigwetsa pa mapazi a Paulo ndi Sila akunjenjemera.
30 Nda nji ba rju nda tre ndi, “Mi nuyi ninkon, mi ti ngye ni dumi kpa tumu chuwo?”
Iye anawatulutsa kunja ndipo anawafunsa kuti, “Amuna inu, ndichite chiyani kuti ndipulumuke?”
31 Ba tre ndi, “kpanyme ni Bachi Yesu, niki wu kpa kpachuwo, ni wu baba biwa ba he ni ko me.”
Iwo anayankha kuti, “Khulupirira Ambuye Yesu ndipo udzapulumuka, iwe ndi a mʼbanja lako.”
32 Ba hla lan tre wu Bachi niwu, baba ni ko nha ni mi koma.
Kenaka analalikira mawu a Ambuye kwa iyeyo ndi onse amene anali mʼnyumba mwake.
33 Niki, igu wu tro'a a vu ba ni nton kima wu chu'a, nda ka ngla mkpan mba, niki wawu mba bi koma wawu ba ti batisma ni bawu.
Usiku womwewo woyangʼanira ndendeyo anawatenga nakawatsuka mabala awo; ndipo pomwepo iye ndi a mʼbanja lake anabatizidwa.
34 Niwa a nji ba Bulus mba Sila hon hi ni koma nda ka nuba biri, a ta kpe kpukpome, ni ndji biwa ba he ni koma'a, nitu a kpanyme ni Irji.
Woyangʼanira ndendeyo anapita nawo ku nyumba yake, nakawapatsa chakudya, ndipo banja lonse linadzazidwa ndi chimwemwe chifukwa anakhulupirira Mulungu.
35 Zizan, niwa mble a nhran, alkali ba ba ton du hi ni bi gben'a, ndi “Du ndji bi mba hi kpamba.”
Kutacha, woweruza milandu uja anatuma asilikali kwa woyangʼanira ndendeyo kukanena kuti, “Amasuleni anthu aja.”
36 Igu wu tro a vu lan tre ba bla ni Bulus mba Sila andi, “Alkali baba ton lan tre ye ni me ndi du mi du yi hi. Zizan nikima, ye rju hi yi ni si sron.”
Woyangʼanira ndendeyo anawuza Paulo kuti, “Woweruza milandu walamula kuti iwe ndi Sila mumasulidwe. Tsopano muzipita. Pitani mumtendere.”
37 Ama Bulus a hla bawu ndi, “Ba vuta hlo tsi ni shishi ndji, hamma ni tsra ta toh, niwa me ki mri son meme Roma, nda tru ta sru ni kotro, zizan ba son juta rju ni rhiri? A'a! Du ba ye kimba nda ye njita rju.”
Koma Paulo anati kwa asilikaliwo: “Iwo anatikwapula pa gulu la anthu asanatiweruze, ngakhale kuti ndife nzika za Chiroma natiponya mʼndende. Kodi tsopano akufuna kutitulutsa mwamseri? Ayi! Asiyeni abwere okha kuti adzatitulutse.”
38 Bi gben ba baka vu tre biyi bla ni ba alkali ba, niwa ba wo ndi Bulus mba Sila ba mri gbungblu Roma, ikpe'a anuba sissri.
Asilikali aja anakafotokozera woweruza milandu ndipo pamene anamva kuti Paulo ndi Sila anali nzika za Chiroma, anachita mantha.
39 Alkali ba ba ye bre ba nda nji ba rju, nda bre du ba rju ni gbu'a hi kpamba.
Iye anabwera kudzawapepesa ndipo anawatulutsa mʼndende, nawapempha kuti achoke mu mzindawo.
40 Niki, Bulus mba Sila ba rju ni ko tro'a nda ye ni ko Lydia. Niwa ba Bulus mba Sila ba to mri vayi ba, ba nhronba duba ki gbangban, nda mle, rju hi kpamba rji ni gbu'a.
Paulo ndi Sila atatuluka mʼndende, anapita ku nyumba ya Lidiya, kumene anakumana ndi abale nawalimbikitsa. Kenaka anachoka.

< Ndu Manzaniba 16 >