< Ndu Manzaniba 14 >
1 Aye he toki ni Iconium, wa Bulus mba Barnaba ba ri hi nimi Synagogue wu bi Yahudawa ba, nda ka tre hu ninkon wa kpaandi, ba Yahudawa baba Greeks ba kpanyeme.
Ku Ikoniya, Paulo ndi Barnaba analowanso mʼsunagoge ya Ayuda. Kumeneko iwo anaphunzitsa momveka bwino kotero kuti anthu ambiri Achiyuda ndi anthu a mitundu ina anakhulupirira.
2 Ama Yahudawa wa ba kamba ni zren huba'a, ba chon dri bi kora ba nda duba ti nfu ni mri vayi mba.
Koma Ayuda amene anakana kukhulupirira anawutsa anthu a mitundu ina nawononga maganizo awo kutsutsana ndi abale.
3 Nitu ki, ba ki niki gbron nton, ndani bla gbangban me ni gbengblen Bachi, ndani tsro ba du ba toh tre wa a ton ba wu ya ndindi. A ti toki niwa a tsro kpanyeme wa ndji ba toh ni kikle kpi waasi ti ni shishi mba, zu ni wo bulus mba Barnaba.
Ndipo Paulo ndi Barnaba anakhala kumeneko nthawi yayitali, nalalikira molimba mtima za Ambuye amene anawapatsa mphamvu yochitira zozizwitsa ndi zizindikiro zodabwitsa pochitira umboni mawu a chisomo.
4 Ama ndji bi gbu'a ba gaanyu, bari ba kri ni ngbala Yahudawa, i bari ni manzani ba.
Anthu a mu mzindamo anagawikana; ena anali mbali ya Ayuda, ena mbali ya atumwi.
5 Wawu mba, bi kora mba Yahudawa (baba bi ninkon mba) ba wa nkon wu vu ba yo ya nda ta ba Bulus mba Barnaba ni tita,
Pamenepo anthu a mitundu ina ndi Ayuda, pamodzi ndi atsogoleri awo anakonza chiwembu choti azunze atumwiwo ndi kuwagenda ndi miyala.
6 ama niwa ba ble wo toki, ba tsutsu hi ni igbu bi Lycaonia, wu Lystra mba Derbe baba kaagon gran bi koki,
Koma atazindikira zimenezi, anathawira ku Lusitra ndi Derbe, mizinda ya ku Lukaoniya, ndiponso ku dziko lozungulira mizindayo,
7 niki ba si zren ni d'bu tre ndindi'a.
kumene anapitiriza kulalikira Uthenga Wabwino.
8 Ni Lystra, iguri a son, hamma ni gbengblen ni zama, chon kple rhi ni nne yimma, wa ana zren to ni son ma na.
Ku Lusitra kunali munthu wolumala miyendo, amene sanayendepo chibadwire chake.
9 Iguyi a wo bulus si tre. Bulus a yo shishi ma niwu nda toh ndi a he ni sron kpanyeme nitu kpa sii kpama.
Iyeyu, amamvetsera pamene Paulo amayankhula. Paulo anamuyangʼanitsitsa ndipo anaona kuti anali ndi chikhulupiriro choti achiritsidwe nacho.
10 Niki a tre niwu ni kikle lan ndi, “Lu kri ni za me.” Mleigu'a a lu za kri nda zren kaagon.
Ndipo Paulo anamuyitana mofuwula nati, “Imirira!” Atamva zimenezi, munthuyo anayimirira, nayamba kuyenda.
11 Niwa kpaandi ba bato kpewa Bulus a ti'a, ba nzu lan ba ndani tre ni el'pa Lycaonia, “Ba rji ba ba k'ma rhu too ndji nda grji ye nita.”
Gulu la anthu litaona zimene Paulo anachitazi, linafuwula mʼChilukaoniya kuti, “Milungu yatitsikira yooneka ngati anthu!”
12 Ba yo Barnaba ndi “Zeus,” mba Bulus, “Hermes,” nitu wawuyi ana ninkon wu lantre'a.
Barnaba anamutcha Zeusi ndipo Paulo anamutcha Herimesi chifukwa ndiye amatsogolera kuyankhula.
13 Priest wu irji zeus, wa koobre ma ahe ni kogon kikle gbu'a, anji kikle lando wa ba yra ni loh bre ye ni kikle nkontra gbu'a, wawu mba gbugbu ndji ba, nitu duba ye gon nton nibawu.
Wansembe wa Zeusi amene nyumba yopembedzera Zeusiyo inali kunja pafupi ndi mzindawo, anabweretsa ngʼombe yayimuna yovekedwa nkhata za maluwa pa chipata cha mzindawo chifukwa iyeyo pamodzi ndi anthu ena onse aja amafuna kudzipereka nsembe kwa Paulo ndi Barnaba.
14 Niwa manzani ba, Bulus mba Barnaba ba wo toki, ba y'ba nklon mba nda tsutsu hi nda ka kuuyi ni mi ndji ba
Koma Barnaba ndi Paulo atamva zimenezi, anangʼamba zovala zawo, nathamangira pakati pa gulu la anthuwo, akufuwula kuti,
15 nda ni hla ndi, “Indji-lon, nitu ngye bi ti kpi biyi? Kita ngame ki ndji, ni kpa too wumbi. Kisi bla tre ndindi ni yiwu nitu duyi k'ma gon don meme kpi ndi ye ni Irji wu sissren, wa a ti shulu, ni memee ni kpaama teku, mba wawu kpi wa bahe ni mi mba.
“Anthu inu, bwanji mukuchita zimenezi? Ifenso ndife anthu monga inu nomwe. Ife takubweretserani Uthenga Wabwino, kuti musiye zinthu zachabezi ndi kutsata Mulungu wamoyo, amene analenga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zimene zili mʼmenemo.
16 NI k'ba wa baka hiye, a du gbungblu du ba zren ni nkon kankan wu mba.
Kale Iye analola anthu a mitundu ina yonse kutsata njira zawozawo.
17 Ni kima me, ana hamma ni don wa ba bla kpewa ba to nituma na, niwa a ti kpiwu bi nda nuba mma-lu rhini shulu mba ntonlu wa niye nuyi klo biri bran; shuuni sron mba ni biri mba ngyiri kpukpome.
Komabe wakhala akudzichitira yekha umboni: Iye amaonetsa kukoma mtima kwake pogwetsa mvula kuchokera kumwamba ndi zipatso pa nyengo yake. Amakupatsani chakudya chambiri ndipo amadzaza mitima yanu ndi chimwemwe.”
18 Ni lantre bihi me, Bulus mba Barnaba ba mla zu ndji ba megen bubu gon nton ni bawu.
Ngakhale ndi mawu awa, anavutika kuletsa gulu la anthu kuti asapereke nsembe kwa iwo.
19 Ama Yahudawa bari wa ba rhini Antioch mba Iconium, ba ye kma tu ndji ba sran ni gyru bre. Ba taa Bulus ni tita nda ngbiwu rju hi ni kogon gbu'a, nda ban ni mren mba ndi a qu ye.
Kenaka kunabwera Ayuda ena kuchokera ku Antiokeya ndi Ikoniya nakopa gulu la anthu lija. Iwo anamugenda miyala Paulo namukokera kunja kwa mzindawo, kuganiza kuti wafa.
20 Ni kime, niwa mriko ba ka kri kaagon nitu ma, alu kri nda zren ri ni mi gbu'a. Ni vi wa a hu kima, a hi ni Derbe wawu'u mba Barnaba.
Koma ophunzira atamuzungulira, Pauloyo anayimirira nalowanso mu mzindawo. Mmawa mwake iye ndi Barnaba anachoka ndi kupita ku Derbe.
21 Hu gon wa baka d'bu bla tre ndindi nitu ma, ni mi gbu'a nda mriko gbugbu, ba k'ma ye ni Lystra, ni Iconium mba ni Antioch.
Iwo analalikira Uthenga Wabwino mu mzindawo ndipo anthu ambiri anatembenuka mtima ndi kukhala ophunzira. Kenaka anabwerera ku Lusitra, ku Ikoniya ndi ku Antiokeya.
22 Ba si nron mriko ba duba kri ni sron gbangban nda yo ni bawu du ba na k'ma ya gon ni kpa nyme mba ndani tre ndi, “Abi toki duta ri ni ko Irji hu ni nkon iya
Kumeneko analimbikitsa mitima ya ophunzira ndi kuwapatsa mphamvu kuti akhalebe woona mʼchikhulupiriro. Iwo anati, “Ife tiyenera kudutsa mʼmasautso ambiri kuti tikalowe mu ufumu wa Mulungu.”
23 Niwa ba yo bi ninkon nitu mba, ni ekklisiya ba, nda bre Irji hamma ni rhikpe, ba kaba yo ni wo Bachi wa nituma yi ba kpa nyeme.
Paulo ndi Barnaba anasankha akulu ampingo pa mpingo uliwonse, ndipo atapemphera ndi kusala kudya anawapereka kwa Ambuye amene anamukhulupirira.
24 Mle ba zrenzu ni Pisidia nda ye ri ni Pamphylia.
Atadutsa Pisidiya, anafika ku Pamfiliya.
25 Niwa ba kle bla lantre'a ni Perga, ba grji hi ni Attalia.
Atalalikira Mawu ku Perga, anapita ku Ataliya.
26 Rhi niki ba zren zu nitu mma ka rini Antioch, ni bubu wa bana nzuba yo ni toh ti Irji wu ndu wa baka kle'u zizan.
Ku Ataliyako, anakwera sitima ya pamadzi kubwerera ku Antiokeya kumene anayitanidwa mwachisomo cha Mulungu kuti agwire ntchito imene tsopano anali atayitsiriza.
27 Niwa ba ye ri nimi Antioch, ba yo ekklisiya zi ni bubu riri, nda vubla bawu wawu kpiwa Irji a ka ti niba, mba nitu wa a bwunko wu kpa gbangban ni biwa babi kora'a.
Atangofika ku Antiokeya, anasonkhanitsa pamodzi mpingo ndipo anafotokoza zonse zimene Mulungu anachita kudzera mwa iwo ndiponso mmene Iye anatsekulira a mitundu ina njira ya chikhulupiriro.
28 Ba kii wu gbron nton ni ba mriko ba,
Ndipo anakhala kumeneko ndi ophunzira nthawi yayitali.