< Ndu Manzaniba 1 >

1 Ikpi biwa mina hla niwu'a, Theophilus, a ne nitu ndu u tsro wa Yesu a ti rhi ni mumla.
Mʼbuku langa loyamba, ndinakulembera iwe Teofilo zonse zimene Yesu anayamba kuchita ndi kuphunzitsa,
2 Ahe ni iri wa ba bariu hi ni shu, nikima wa a 'mmha manzani wa ana chuba'a ni ruhu tsatsra, a.
mpaka tsiku limene anatengedwa kupita kumwamba, mwamphamvu ya Mzimu Woyera, atawalangiza atumwi amene anawasankha.
3 Niwa baya wa ba tiu ya a stro tuma ni sisren ni bawu ni nkon kankan ni du ba na kpatron ni lunde ni be mana A tsro tuma nibawu wu vi tsotra don za nda tre ni ba nitu koson (shulu) Irjhi.
Zitatha zowawa zake Yesu anadzionetsa kwa ophunzira ake, ndi kuonetsanso maumboni ambiri kuti anali wamoyo. Iye anadzionetsera kwa iwo ndi kuwaphunzitsa za ufumu wa Mulungu pa masiku makumi anayi.
4 Niwa a kri ni shubimba ni wu, a'mmha ba du bana don Urishilima na, du ba gben shirjhi wu tima, wa a lha ndi, “Bi wo ni nyumu.
Nthawi ina atasonkhana nawo pamodzi, Yesu analamulira ophunzira ake kuti, “Musachoke mu Yerusalemu, koma mudikire mphatso imene Atate anga analonjeza yomwe ndinakuwuzani.
5 Ndi a hi janji, Yohanna a ti batisma ni yiwu ni ma, ama ni vi yi, bi kpa batisma wu Ruhu Tsatsra.”
Pakuti Yohane anakubatizani ndi madzi, koma posachedwapa inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.”
6 Niwa ba shu ki, ba miye ndi baci, “zizanyi ahi ton yiyi u kma tuchu gbungblua ye ni Israila?
Atumwi atasonkhana pamodzi, iwo anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi nthawi ino mubwezeretsa ufumu kwa Israeli?”
7 A lha bawu ndi “Ana wumbi du yi to nton ko vi waa timu a yo ni gbengble ma na.”
Yesu anawawuza kuti, “Sikofunika kuti mudziwe za nthawi kapena masiku amene Atate ayika mwa ulamuliro wawo.
8 Ama bi kpa gbengble wa Ruhu Tsatsra ni ku yiwu, niki bi bla ni tumu, rhi ni Urishilima baba Judiya wawu mba Samaria, ni ka ri ni klekle gbungblu meme.
Koma mudzalandira mphamvu Mzimu Woyera akadzafika pa inu; ndipo mudzakhala mboni zanga mu Yerusalemu, ku Yudeya konse ndi ku Samariya, mpaka ku malekezero a dziko lapansi.”
9 A kle tre kpi bi yi nu, niwa ba ki si ya shulu, ba ban'u lu hon, e clalu a kawu u shishi mba ka la tou na.
Atatha kuyankhula zimenezi, Yesu anatengedwa kupita kumwamba ophunzira ake akuona, ndipo anabisika mʼmitambo.
10 Niwa ba rhisi yo shishi ni ya hon ma hi shulu'a, ndhi ha ni nkon kinkla ba krirhu kri ni mimba.
Yesu akukwera kumwamba, ophunzira ake anayangʼanitsitsa ndi chidwi mʼmitambo. Mwadzidzidzi anaona anthu awiri ovala zoyera atayimirira pambali pawo.
11 Ba tre ndi, “Biyi ndhi bi Galilee, “bi ki ya gye ni shulu? Yesu yi, wa ba banwu hi ni shulu, ni kima ye bibi wa bito ba ban u hi ni shulu'a”
Iwo anati, “Inu, anthu a ku Galileya, chifukwa chiyani mukuyima ndi kumayangʼana mʼmitambo? Yesu amene wachotsedwa pakati panu ndi kupita kumwamba, adzabweranso mʼnjira yomweyi mwamuona akupita kumwamba.”
12 Mle ba k'ma grhi rhi ni ngblu wa ba yo ndi Olivet, wandi a wiewiera ni Urishilima, hi ni mi gbu Urishislima, ezren vi chanchu sati.
Pamenepo atumwi anabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku phiri la Olivi, mtunda wosakwana kilomita kuchokera mu mzindamo.
13 Niwa ba ye ri, ba tsi hunhi tra u koshu, wa bah kini mia. Bana ba Yohana, yakubu, andarawus, Filibus, Toma, barthelomen, Matiu, Yakubu Ivren Alphanso Siman wa ini wu ngyegere me, Mba Juda Ivren Yakubu.
Atafika mu mzindamo, analowa mʼchipinda chammwamba kumene amakhala. Amene analipo anali awa: Petro, Yohane, Yakobo ndi Andreya; Filipo ndi Tomasi, Bartumeyu ndi Mateyu; Yakobo mwana wa Alifeyo ndi Simoni Zelote ndi Yuda mwana wa Yakobo.
14 Wawu mba ba zontu ki ni bubu riri nda sia bre Rji, baba Mba ba, ni Maryamu ehi Yesu, baba mri vayi ma.
Onsewa ndi mtima umodzi anapitiriza kupemphera pamodzi ndi amayi, ndi Mariya amayi ake a Yesu, ndiponso abale ake a Yesu.
15 Niri baki, Bitrus a lu kri ni mi mri vayiba, bana tsra ndhi 120, nda tre ndi.
Pa nthawi imeneyo Petro anayimirira pakati pa okhulupirira (gulu la anthu pafupifupi 120).
16 “Mri vayi, a he nitu du tre wu vunvu tre baci du rhu tsra, nawa Ruhu Tsatsra ana lha ni nyu Dawuda ni tu Juda, wa a tsro biwa baye vu Yesu nkon.
Iye anati, “Abale anga, Malemba anayenera kukwaniritsidwa omwe Mzimu Woyera anayankhula kalekale kudzera mwa Davide za Yudasi, amene anatsogolera amene anamugwira Yesu.
17 Ana irimbu wa a kpa ndu wandi anuta ngame.”
Iye anali mmodzi wa gulu lathu ndipo anatumikira pamodzi ndi ife.”
18 (Zizan ndhi yi a ka le irhu ni nkle wu meme dri wandi a kpa'a, nda ka rhoku nitu u Kpama ka yrahle, ni irhenma ba ka vrale ni meme.
(Yudasi anagula munda ndi ndalama zimene anazipeza pochita zoyipa zija; kumeneko, iye anagwa chamutu, naphulika pakati ndipo matumbo ake wonse anakhuthuka.
19 Wawu ndhi bi ki ni gbu Urishilima ba wo kpe wa a zren kima ba yonde irhu kima ni lan gbu mba ndi. “Akeldama”, wandi a tsra ni nde “Irhu u yi.”)
Aliyense mu Yerusalemu anamva zimenezi, kotero anatcha mundawo mʼchiyankhulo chawo kuti Akeledama, kutanthauza, Munda wa Magazi).
20 Ba tre ni tuma ni vunvu tre zabura, ndi, “Du ba du irhukima du kri ton kpo, e du ko ndior na kruko ni kimana
Petro anati, “Pakuti kwalembedwa mʼbuku la Masalimo kuti, “Nyumba yake isanduke bwinja, ndipo pasakhale wogonamo. Ndiponso, “Wina atenge ntchito yake yautsogoleri.
21 Ani bi du lilon ri wa azi wuta rhini nton wa baci Yesu a zren ri nda rhu ni mi mbu,
Chifukwa chake ndi kofunika kusankha mmodzi wa anthu amene akhala nafe nthawi yonse imene Ambuye Yesu ankayenda nafe,
22 Rjhini baptisma wu Yohana, ye ni vi wa ba ban'wu hon ni shishi mbu, nda toh tash'men rhi ni qu ngame.
kuyambira pa nthawi ya ubatizo wa Yohane mpaka nthawi imene Yesu anatengedwa pakati pathu. Pakuti mmodzi wa anthu awa ayenera kukhala mboni pamodzi ndi ife zakuuka kwake.”
23 Ba ju nji ha zi, Yusufu wandi ba yondi Barsabbas, wandi bata yondi Justus ngame, mba Matayas.
Pamenepo anasankha anthu awiri, Yosefe wotchedwa Barsaba (wodziwikanso kuti Yusto) ndi Matiyasi.
24 Ba bre ndi “Baci, wuhi wu toh suron ndhi ko nha, tsro ta ka ahi nya nimi ndi bihi wa wu chu
Kenaka iwo anapemphera nati, “Ambuye mukudziwa mtima wa aliyense. Tionetseni amene mwamusankha mwa awiri awa
25 ni du ban bubu son manzani wu bla kpe wa ato, nitu tash'm ma ni mimbu, wandi Juda a k'ma gon tiwu nda hi kpama.”
kuti atenge ntchito iyi ya utumwi, imene Yudasi anasiya napita kumalo womuyenera.”
26 Ba yo kuriya nitu mba, wa a ku nitu Matayas, e ba bla a yo ni manzani wlo don iri ba.
Tsono anachita maere, ndipo maerewo anagwera Matiyasi. Tsono iye anawonjezedwa pa gulu la atumwi khumi ndi mmodziwo.

< Ndu Manzaniba 1 >