< 3 Yohana 1 >

1 Rji ni nikoh bi i hi ni Gayus wa mi sub kpokpome.
Ndine mkulu wampingo, kulembera: Gayo mnzanga wokondedwa, amene ndimamukonda mʼchoonadi.
2 I suron mu, ni bre ni u, du lulu hi u me ni mi kpei wa u si ti'a wawu; ni si kpan, na Ruhu me a hei ni si.
Wokondedwa, ndimakupempherera kuti zako zonse zikuyendere bwino, ndikuti ukhale bwino mʼthupi mwako, monga momwe ulili moyo wako wauzimu.
3 Isuron mu a ti kikla raime wadi mri vayi bari ba ye tre didi ni tu ni yo suron ni tu me na wa u si hu kon jaji.
Ine ndinali ndi chimwemwe chachikulu pamene abale ena anafika nʼkundifotokozera za kukhulupirika kwako pa choonadi ndiponso mmene umayendera motsata choonadi.
4 Ba kpei wa'a zan du suron mu ti kikla rai du me wo di mri mu ba si zran ni kon jaji.
Palibe chondikondweretsa kwambiri kuposa kumva kuti ana anga akukhala mʼchoonadi.
5 Si suron vremu, u si ti du' a ni suron me riri, hi ni mri vayi, ni bi tsri.
Wokondedwa, ndiwe wokhulupirika pa zimene ukuchitira abale, ngakhale kuti iwowo ndi alendo.
6 Bi wa ba hla tre didi ni tu me ni bi koh Irji, a ni bi du zo ba, ni zo u si suron, ni kon wa a bi, ni bi hu Irji.
Iwo anafotokozera mpingo za chikondi chako. Chonde uwathandize kupitiriza ulendo mʼnjira yokondweretsa Mulungu.
7 Ni de mu ba rju, ba na kpan kpei ni wo ndi ba na.
Pakuti ananyamuka ulendo wawo chifukwa cha dzina la Ambuye, osalandira thandizo kwa osakhulupirira.
8 Na ki ki kpa iri ndi ba, ki hei kpa udu baba u jaji.
Ife tiyenera kumathandiza anthu oterewa, kuti tigwirizane nawo pa ntchito ya choonadi.
9 Mi han vuvu hi ni tra Irji, ni ki Diyotariffis, wa a zan kohan wa ni kon ni mi ba, ana kpa ta na.
Ndinalembera mpingo, koma Diotrefe, amene amafuna kukhala wotsogolera, sanafune kutimvera.
10 Na ki inde mi ye, mi nu mre ni tu du ma, ni wa a si ga de bu'a ni shishi de ba ni meme tre. Wa yi me a mia u na, na ki me a ni kama bubu kpa mri vayi, a zu bi wa ba su ti didi ma; a ni zu ba ni mi Irji.
Tsono ndikabwera ndidzakumbutsa zimene iye amachita. Iye amafalitsa nkhani zabodza zonena ife. Ndipo sakhutira ndi zimenezo, komanso iyeyo amakana kulandira abale. Komanso amaletsa amene akufuna kutero, ndipo amawachotsa mu mpingo.
11 Isuron mu, na vu meme kpei na sei kpei didi ma, Idi wa a si ti kpei didi ma a hi u Irji, Inde 'a' a si ti kpei meme ma, a na toh Irji na.
Wokondedwa, usatsatire zinthu zoyipa koma zinthu zabwino. Aliyense amene amachita zinthu zabwino ndi wochokera kwa Mulungu. Aliyense amene amachita zoyipa sanamuonepo Mulungu.
12 Dimitiriyas, ndi ba tre didi ma har ni jaji ni tu ma wu me utuh jaji tre bu, a jaji.
Aliyense akumuchitira umboni wabwino wa Demetriyo. Ngakhale choona chomwe chimamuchitira umboni, ndipo iweyo ukudziwa kuti umboni wathu ndi woona.
13 Mei hei ni kpie gbugbu u wa me han 'u' Na ki mina kpay'm di mi han ni u ni alkalami ba tawada na.
Ndili ndi zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata.
14 Mi you suran di mi toh tu lalo mu na ki ki tre shi shi. Du si suron sun ni wu. Kpukpan bu ba si chi'u hla ni bru kpukpan bu, ni de ba wa wu.
Ndiyembekezera kufika kwanuko posachedwapa, ndipo tidzakambirana pamaso ndi pamaso. Mtendere ukhale nawe. Abwenzi anu kuno akupereka moni. Upereke moni kwa abwenzi onse mmodzimmodzi.

< 3 Yohana 1 >