< Rom 3 >

1 Beree ayhudiyots Ik' ashwoterawwotsiyere bok'an eegoneya? Gof amo ayhudiwotssh eebi b́ k'aliti?
Nanga kodi pali ubwino wotani pokhala Myuda, kapena muli ubwino wanjinso mu mdulidwe?
2 Arikon Ayhudi woto ay weeron k'anefe, bog keewo Ik'o aap'o ayhudiyotssh adaro bíimtsoniye.
Ubwino wake ndi wambiri mʼnjira zonse! Choyambirira iwo anapatsidwa Mawu a Mulungu kuti awasunge.
3 Eshe Ayhudiyotsitsere ik ikuwots amanek wotar daatseyo bok'azal, bo amanetsuwotsi wotbok'azo Ik'o amanek b́ woto ooritúwa?
Nanga zili bwanji ngati ena analibe chikhulupiriro? Kodi kupanda chikhulupiriro kwawo kukanalepheretsa kukhulupirika kwa Mulungu?
4 B́ jamon oriratse! «N aap'ts aap'atse tuutson arikeewetsoniye nwotiti, N mooshorowere angshon da'itune» Ett guut'etsok'on ash jamo kootetso b́ wotiyalor Ik'o arikeewetske.
Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Mulungu akhale woona, ndi munthu aliyense akhale wonama. Monga kwalembedwa kuti, “Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi kupambana pamene muweruza.”
5 Ernmó no morro Ik' kááwo b́ kitsitka wotiyal eshe eebi no'eteti? Ik'o nomorrosh noon b́seziyal kááwon angshratse eteya b́ wotiti? Hanoke t keewiruwo ashkok'one.
Koma ngati kuyipa mtima kwathu kuonetsa poyera kuti Mulungu ndi wolungama, ife tinganene chiyani? Kodi tinganene kuti Mulungu ndi wosalungama pamene aonetsa mkwiyo wake pa ife? (Ine ndikuyankhula monga mmene anthu ena amayankhulira).
6 B́ jamon woteratse! hank'o b́wotitkawotiyal Ik'o datsuwats aak'oneya b́ angshiti?
Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ngati zikanakhala zotero, kodi Mulungu akanaweruza bwanji dziko lapansi?
7 Ernmó kootetsi twoto Ik'o ar keewutsi b́woto kitsre, b́mangi ayono kitsitk b́ wotiyal, bere taa morretsok'o tiyats angshet eegoshe?
Wina atanena kuti, “Ngati kunama kwanga kukuonetsa koposa kuti Mulungu ndi woona, ndi kuwonjezera pa ulemerero wake, nanga nʼchifukwa chiyani ndikuweruzidwa kuti ndine wochimwa?”
8 Ik ik ashuwots «Bére, Sheeng keewo b́weyish gond keewo eege nok'aliyala?» etaat tdaniruwok'o woshdek't taan bo s'aamiyir, mansh mank'owwotsats angshet angsho kááwe.
Nʼchifukwa chiyani osanena kuti, monga ena amanena mosasamala kuti, “Tiyeni tichite zoyipa kuti zabwino zionekere?” Anthu onena zoterewa kulangidwa kwawo ndi koyenera.
9 Bére no ayhudiyots Ik' ash woterawwotsyere k'anefone eteya? Mank'o woteratse! k'osh ash jamo Ayhudi wotowa Ik' ashwoterawwotsi wotowa morretsuwotsi bowottsok'o shin shin kitsre.
Kodi timalize bwanji? Kodi Ayuda ndife oposa anthu ena? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ife tinanena kale kuti Ayuda ndi a mitundu ina omwe ndi ochimwa.
10 Hank'o ett guut'etsok'on, «Dab ikonúwor kááwu asho aaliye, ik doonzuwor aaliye,
Monga kwalembedwa kuti, “Palibe munthu wolungama, inde palibe ndi mmodzi yemwe.
11 Nibetsonuwere aaliye, Ik'onowere geyiruwo ikdonzwor aaliye.
Palibe ndi mmodzi yemwe amene amazindikira, palibe amene amafunafuna Mulungu.
12 Jametsuwotswere weeratse k'az keshrne, Ik wotdek't darwutserne. Doo fino finiruwo dab ikdoonzuwor aaliye.
Onse apatukira kumbali, onse pamodzi asanduka opandapake. Palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita zabwino, palibe ngakhale mmodzi.”
13 Bogogo k'eshets dook'oyiye, bo alberonowere antelcerne, bonoon keewi shuwonwere dawnz marziyok'oyiye
“Kummero kwawo kuli ngati manda apululu; ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.” “Ululu wa mamba uli pa milomo yawo.”
14 Bonoonuwere c'ashonat s'aamon bín s'eenwtskee.
“Mʼkamwa mwawo ndi modzaza ndi zotemberera ndi mawu owawa.”
15 Botufo ash úd'osh káárke,
“Mapazi awo afulumira kukakhetsa magazi.
16 Boweeratse daatsetuwere t'afonat dash aanone.
Kusakaza ndi chisoni kumaonekera mʼnjira zawo,
17 Jeeni weeronowere danatsne,
ndipo njira ya mtendere sayidziwa.”
18 Ik'onowere b́ jamon sharaatsne.»
“Saopa Mulungu ndi pangʼono pomwe.”
19 Muse nemi tzaziyo b́ s'iilfo nemmaniyere dashe fa'úwotsi b́wottsok'o danfone, manatse tuutson ashuwots bíyats boweebituwo t'ut't s'k bo etiri, dats jamonuwere Ik'i angshi shirots wotitwe.
Tsopano tikudziwa kuti chilichonse Malamulo amanena, amanena kwa amene amalamulidwa ndi Malamulowo, ndi cholinga chakuti aliyense asowe chonena, ndipo dziko lonse lidzayimbidwa mlandu ndi Mulungu.
20 Mansha asho konuwor Ik'o shinatse, Muse nemo s'eentson Kasheratse, Nemman b́kitsir ash jamo morretsi b́wotoniye.
Chifukwa chake palibe mmodzi amene adzayesedwa wolungama pamaso pake chifukwa chosunga Malamulo, kuti ife timazindikira tchimo kupyolera mu Malamulo.
21 Andmó Ik'o ashuwotsi kááwu b́ woshit weero nemalon b́ woteraawok'o be'ere, manuwere Muse nemonat nebiyiwots mas'aafotse gawere.
Koma tsopano chilungamo chochokera kwa Mulungu, osati chochokera ku Malamulo, chaonetsedwa. Ichi ndi chimene Malamulo ndi Aneneri amachitira umboni.
22 Mansha eshe Ik'o b́ k'osh k'oshirawon Iyesus Krstosi amanon amaniru jamosh kááwu woto imetuwe.
Timakhala olungama pamaso pa Mulungu pamene takhulupirira Yesu Khristu. Mulungu amachitira zimenezi anthu onse amene akhulupirira Khristu. Palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina,
23 Ash jamwots morro finernre, Ik'o boosh b́'imts mangonowere t'ut'rnee.
pakuti onse anachimwa naperewera pa ulemerero wa Mulungu
24 Mansh ashuwots Iyesus Krstos b́ k'alts kashiyi fino Ik'i s'aat mec'ron kááw wotitune.
ndipo onse alungamitsidwa mwaulere mwa chisomo chake chifukwa cha Khristu Yesu amene anawawombola.
25 Ik'o Iyesus Krstosi wosho woshdek't b́ t'ints bín amanitu jamwots b́ s'atson bomorrosh oorowe eto bodatsishee, Ik'o man b́k'al b́k'amoon morr shintso k'azoon ar wotts b́took kááwo kitsoshe.
Mulungu anamupereka Iyeyu kuti pokhetsa magazi ake, akhale nsembe yokhululukira machimo. Mulungu anachita zimenezi kufuna kuonetsa chilungamo chake. Chifukwa cha kuleza mtima kwake, sanalange anthu chifukwa cha machimo amene anachita kale.
26 And dúranatse Ik'o b́ tookon kááwu b́woto b́kitsir Iyesusi amants jamwotsi kááwu woshoshe.
Iye anachita izi kuti aonetse chilungamo chake lero lino. Anthu azindikire kuti Iye ndi wolungama ndipo amalungamitsa aliyense amene akhulupirira Yesu.
27 Haniyak bín noít'et keewo eebi fa'oni? Eegonor id'atsone! bín no id'awok'o woshitwonúwere eebi? Nemo no s'eenirwosheya? Woteratse, ernmó imneti nemone.
Nanga tsono pamenepa munthu anganyadenso? Kunyadatu kwachotsedwa. Chifukwa cha Malamulo? Kodi Malamulo samafuna ntchito za munthu? Ayi, koma mwachikhulupiriro.
28 Mansh eshe Ik'i asho kááwu b́ woshit, asho nemi fino b́kaltsosh b́woterawo imnetiyon b́wottsok'o t'iwintsdek'etwone.
Ife tikunenabe kuti munthu amalungamitsidwa mwachikhulupiriro osati mwakusunga Malamulo.
29 Himó Izar Izewer ayhudiwots s'uzshe Ik' b́woti? Izar Izewer Ik'i ash woterawwotsshor bokooshna? Arikon Izar Izewer Ik' ash woterawwotsshor boke.
Kodi Mulungu ndi Mulungu wa Ayuda okha? Kodi si Mulungu wa a mitundu inanso? Inde wa a mitundu inanso,
30 Ik'o ike, ayhudiwotsi wotowa Ik' ash woterawwotsi bo amanere kááwu woshituwo bíne.
popeza ndi Mulungu mmodzi yemweyo amene adzalungamitsa mwachikhulupiriro ochita mdulidwe ndi osachita mdulidwe kudzera mʼchikhulupiriro chomwecho.
31 Bére, imnetiyatse tuutson nemo gaketuwone eteya? Iya'a, iki nemo kup'ide'erniye nodetsetiye.
Kodi tsono ife, tikutaya Malamulo pamene tikunena kuti pafunika chikhulupiriro? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Komatu ife tikukwaniritsadi Malamulo.

< Rom 3 >