< Matiwos Dooshishiyo 7 >
1 Manats dabt́ Iyesus hank'owa bíet, «It atsats angsherawok'o konatsor angshk'ayere,
“Musaweruze ena, kuti inunso mungadzaweruzidwe.
2 k'oshwotsats it angshtsok'o it atsowere angshetwe, mank'o it tatsts tatsi k'ac'ots itsho tatsetwe.
Pakuti momwe inu muweruzira ena, inunso mudzaweruzidwa chimodzimodzi, muyeso umene muyesera ena inunso mudzayesedwa ndi womwewo.
3 Ni ááwotse fa'a gindo nbe'aawo ni'eshu ááwitsi kiimo n s'iil eegishe?
“Chifukwa chiyani iwe uyangʼana kachitsotso ka mʼdiso la mʼbale wako koma susamalira chimtengo chili mʼdiso mwako?
4 Eshe niááwotse gindo b́befere, ni'eshuush, ‹Aab ni ááwitsi kimman kishuna› nietet ááwk'oneya?
Kodi unganene bwanji kwa mʼbale wako kuti, ‘Ndikuchotse kachitsotso mʼdiso mwako,’ pamene nthawi zonse chimtengo uli nacho mʼdiso mwako?
5 Nee git albertsono, shin niááwotse fa'a gindo kishwe, maniyere il, nieshu ááwotse fa'a kiimo kishosh shengshde bek'etune.
Wachiphamaso iwe! Yamba wachotsa chimtengo chili mʼdiso mwako ndipo pamenepo udzatha kuona bwino ndi kuchotsa kachitsotso kali mʼdiso mwa mʼbale wako.
6 Woshosh t'ints meets S'ayino kanwotssh imk'ayere, it ink'wo guritswots shinats juuk'ayere, gúritswots itko b́k'awntso shaaw gizon keewets malo botufon boneed'awok'owa, kanwotswere aanar itn shas'etunee.
“Musapatse agalu zinthu zopatulika; kapena musaponyere nkhumba ngale zanu. Pakuti ngati mutero, zidzaziponda ndipo pomwepo zidzakutembenukirani ndi kukudulani nthulinthuli.
7 «K'onwere itsh imetwe, gewoore daatsitute, fengesho k'ofore itsh k'eshetwe.
“Pemphani ndipo mudzapatsidwa; funafunani ndipo mudzapeza; gogodani ndipo adzakutsekulirani.
8 K'onitu jamo dek'etwe, geyirwonúwere daatsitwe, fengesh k'ofitwoshowere k'eshetwe.
Pakuti wopempha aliyense amalandira; ndi wofuna amapeza; ndipo iye amene agogoda, adzamutsekulira.
9 Ititse b́ na'o tusho b́k'onoor shútso imetwo kone?
“Ndani mwa inu, mwana wake akamupempha buledi amamupatsa mwala?
10 Mus'o b́k'onre dawnzo imetwá?
Kapena ngati mwana apempha nsomba, kodi amamupatsa njoka?
11 Eshe it gondwotsi wotefetsat, it nana'úwotssh sheeng keewo imo it daniyakon, bérée, darotse fa'o it nihi bín k'onitwotssh bogshde aawk'owe sheeng keewo imo b́k'azeti!
Tsono ngati inu woyipitsitsa mumadziwa kupatsa ana anu mphatso zabwino, nanga Atate anu akumwamba sadzapereka mphatso zabwino kwa iwo amene amupempha?
12 Eshe haniyak ashuwots itsh bok'alitwok'o it geyiru jamo itwere boosh mank'o k'alwere, nemonwere, nebiyiwots keewtso danonwere b́ keewirwo haniye.
Nʼchifukwa chake zinthu zilizonse mukafuna kuti anthu akuchitireni, yambani ndinu kuwachitira, pakuti izi ndi zimene malamulo ndi aneneri amaphunzitsa.
13 «Fengesh t'ebún kindúwere, t'afo maants kindshit fengesho gawne, b́ werindonúwere eene. Manmaants kindit ashuwotswere ankatnee.
“Lowani pa chipata chopapatiza. Pakuti chipata cholowera kuchiwonongeko nʼchachikulu ndipo msewu wake ndi waukulunso. Ndipo anthu ambiri amalowera pamenepo.
14 Kashomaants kindshiru werindonu t'ebee, b́ werindonwere kic'ike, bín daatsit ashuwotswere aynaliye.
Koma chipata ndi chopapatiza ndi msewu ndi waungʼono umene utsogolera anthu ku moyo wosatha ndipo ndi owerengeka okha amene ayipeza njirayo.
15 «Mereeri gok'o tahde it maants weetwotsatse, bogitsotsnmó biik'ts boditsi Elah wotts kootets nebiyiwotsatse it atso korde'ere,
“Chenjerani nawo aneneri onyenga. Amabwera kwa inu atavala zikopa zankhosa, koma mʼkati mwawo ali mimbulu yolusa.
16 Bonowere it danet bo fini shuwonee. Angitsi t'ugi atatse weyini shuwo, koshshlatse belesi miti shuwo mec'eetwa?
Mudzawazindikira iwo ndi zipatso zawo. Kodi anthu amathyola mpesa pa mtengo wa minga, kapena nkhuyu pa nthula?
17 Mank'o miti sheeng jamo shuwi sheengo shuwitwee, gond mitonwere gond shuwo shuwitwee.
Chimodzimodzinso mtengo wabwino umabala chipatso chabwino, koma mtengo woyipa umabala chipatso choyipa.
18 Miti sheengo gond shuwo shuwosh falratse, gond mitonwere sheeng shuwo shuwosh falratse.
Mtengo wabwino sungabale chipatso choyipa, ndi mtengo woyipa sungabale chipatso chabwino.
19 Sheeng shuwo shuraw mit jamo k'ut'de tawo maants juwetwe.
Mtengo uliwonse umene subala chipatso chabwino umadulidwa ndi kuponyedwa pa moto.
20 Mansh eshe, kootets nebiyiwotsi bofini shuwon boon danetute.
Momwemonso, ndi zipatso zawo iwo mudzawazindikira.
21 « ‹Doonzono! Doonzono!› taash etiru jamo daritsi mengstots kindratse, daritsi mengstots kinditwo darotse fa'o t nih shuntso finitwoniyee.
“Si munthu aliyense amene amanena kwa Ine, ‘Ambuye, Ambuye,’ adzalowe mu ufumu wakumwamba, koma ndi yekhayo amene amachita chifuniro cha Atate anga amene ali kumwamba.
22 Angshi aawots ayuwots, ‹Doonzono! Doonzono! n shútson bek'o keewratsnowa? N shútson fo'erawo kishratsnowa? Nshútson ay adits keewwotsi k'alratsnowa?› Etetune taasha.
Ambiri adzati kwa Ine pa tsikulo, ‘Ambuye, Ambuye, kodi sitinkanenera mʼdzina lanu ndi mʼdzina lanunso tinkatulutsa ziwanda ndi kuchita zodabwitsa zambiri?’
23 Taawere manots aawots, ‹B́ jamon itn danatse! it gond finirwots tiyatse okaan wokoore!› eteetwe boosha.
Pamenepo ndidzawawuza momveka bwino kuti, ‘Sindinakudziweni inu. Chokani kwa Ine, inu ochita zoyipa!’
24 «Ti aap'an k'ewde'er finats jitsit jamo b́ moo s'alats agts s'ek ashoni bí ariye
“Nʼchifukwa chake aliyense amene amva mawu anga ndi kuwachita akufanana ndi munthu wanzeru amene anamanga nyumba yake pa thanthwe.
25 Awshonú b́butsi, di'onwere b́di'ii, jongonwere jongat maa man b́ gifniy, ernmó, maaman shútsi s'alats bí agetsotse dihratsee.
Mvula inagwa, mitsinje inadzaza, ndi mphepo zinawomba pa nyumbayo; koma sinagwe, chifukwa maziko ake anali pa thanthwe.
26 Ti aap'tsan shisht finats jitsrawonmó b́ moo shiyats agts gik'ets ashoniye bíari.
Koma aliyense amene amva mawu angawa ndi kusawachita ali ngati munthu wopusa amene anamanga nyumba yake pa mchenga.
27 Awsho b́butsi, di'o b́ di'i, jongo jongat maaman b́gifnii, moonwere manoor dihbwtsi, b́dih dihonwere dihi gondo b́dhi.»
Mvula inagwa, mitsinje inadzaza, ndi mphepo zinawomba pa nyumbayo, ndipo inagwa ndipo kugwa kwake kunali kwakukulu.”
28 Iyesus keewanotsi keewt b́ ishtsok'on ashuwots b́ danits danatse tuutson bo'adi.
Yesu atamaliza kunena zonsezi, magulu a anthu anadabwa ndi chiphunzitso chake,
29 Adtswotswere bí bo nem danifwotskok'o b́woterawo aletsok'o b́ daniyrwotsna b́tesh.
chifukwa anaphunzitsa ngati amene anali ndi ulamuliro osati ngati aphunzitsi amalamulo.