< Yohans Dooshishiyo 1 >
1 Shin shin aap'o fa'e b́tesh, aap'onwere Ik'oke b́ teshi, aap'manwere Ik'e b́ teshi.
Pachiyambi panali Mawu, ndipo Mawu anali kwa Mulungu, ndipo Mawu ndiye Mulungu.
2 Bí shin shin Ik'ontoni b́ taash.
Mawuwa anali ndi Mulungu pachiyambi.
3 Jam keewo bína bí azee, azeets jamotse ikonwor bí bíazrawo azeetso aaliye.
Zinthu zonse zinalengedwa ndi Iye; ndipo popanda Iye sikukanakhala kanthu kalikonse kolengedwa.
4 Bíyoknowere kasho fa'e b́ teshi, kashanwere ashuwotssh sháána b́ teshi.
Mwa Iye munali moyo, ndipo moyowo unali kuwunika kwa anthu.
5 Shááno t'aluwats c'eeshitwe, t'alwonu shááno da'aratse.
Kuwunika kunawala mu mdima, koma mdimawo sunakuzindikire.
6 Ik'oke wosheetso Yohanisi eteets ash iko fa'e b́ tesh.
Kunabwera munthu amene anatumizidwa kuchokera kwa Mulungu; Iyeyo dzina lake linali Yohane.
7 B́ gawts gawon jamo bíamanitwok'o bí shááni jangosh gaw wotat b́weyi.
Iye anabwera ngati mboni kudzachitira umboni kuwunikako kuti kudzera mwa iye anthu onse akhulupirire.
8 Bíwere shááni jangoni gawosh b́ weyi bako bí b́tookon sháánaliye.
Iyeyu sanali kuwunika; koma anabwera ngati mboni ya kuwunika.
9 Ash jamwotssh c'eshitwo ariko wottso shááno dats jamwats woke b́ fa'oni.
Kuwunika koona kumene kuwunikira munthu aliyense kunabwera ku dziko lapansi.
10 Bíwere datsanatse b́ teshi, datsanwere bí'azee bíne, datsanmó bín danatsane.
Iye anali mʼdziko lapansi, ndipo ngakhale kuti dziko lapansi linalengedwa ndi Iye, dziko lapansilo silinamuzindikire Iye.
11 B́ik wottswotsok waare, b́ jirwotsmó bín de'atsne.
Iye anabwera kwa iwo amene anali akeake, koma akewo sanamulandire Iye.
12 Wotowabako b́ keewu dek'tswotsnat b́ shútson amants jamwots Ik'o nana'uwotsi bowotitwok'owe alo boosh b́mi.
Koma kwa onse amene anamulandira Iye, kwa amene anakhulupirira mʼdzina lake, Iye anawapatsa mphamvu yokhala ana a Mulungu;
13 Bowere Ik'atse shuwekno bako ash naaratse, man etonwere meetsi shnunon wee nungshe mááts gonkewon shuweratsne.
ana wobadwa osati monga mwachilengedwe, kapena chisankho cha munthu, kapena chifuniro cha mwamuna koma wobadwa mwa Mulungu.
14 Aap'onu meets wotere, s'aatonat arikono s'eent no dagotse beere, b́ nihoke waats ik s'uz na'o mangok'o wottso b́ mangonowere bek'rone.
Mawu anasandulika thupi ndipo anakhala pakati pathu. Ife tinaona ulemerero wake, ulemerero wa Iye amene ndi Mwana mmodzi yekhayo wa Atate, wodzaza ndi chisomo ndi choonadi.
15 Yohanswere «Ekeew taayere il weyirumań taayere shin fa'o b́teshtsotse taayere ayidek't bogfe etaat itsh tkeewtsoniye haniye, » ett kuhat b́keewi.
Yohane achitira umboni za Iye. Iye akufuwula kuti, “Uyu ndi Iye amene ndinati, ‘Iye amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa, Iyeyo analipo ine ndisanabadwe.’”
16 B́ s'eenatse no noúnets s'aatats s'aato dek'rone,
Kuchokera mʼkuchuluka kwa chisomo chake ife tonse talandira madalitso pamwamba pa madalitso.
17 Nemo Muse weerone imeyi, s'aatonat aronmo Iyesus Krstos weerone b́ weyi.
Pakuti lamulo linapatsidwa kudzera mwa Mose; chisomo ndi choonadi zinabwera kudzera mwa Yesu Khristu.
18 B́jamon Ik' bek'tso konwor aaliye, wotowa eree Ik'o niho sheetsotse fa'a ik s'uzo b́naayi, bíwere Ik'wottsoni noosh kish kitsiye.
Palibe munthu amene anaona Mulungu, koma Mwana mmodzi yekhayo amene ali wa pamtima pa Atate, ndiye anafotokoza za Iye.
19 Ayhudi naashwots Iyersalemitsi kahniwotsnat Lewawino etefwotsn Yohansok woshat, «Kone nee?» ett boatiyor b́ imts gawo hank'oyiye.
Tsopano uwu ndi umboni wa Yohane pamene Ayuda a ku Yerusalemu anatumiza ansembe ndi Alevi kudzamufunsa kuti iye anali yani.
20 Bí «Taa Krstos taanaliye» et b́ gawi bako gawo gawosh k'aze eraatse.
Iye sanalephere kuvomereza, koma iye anavomereza momasuka kuti, “Ine sindine Khristu.”
21 Bowere «Beree nee kone? Eliyas neeneya?» ett bín boaati. Bíwere «Taanaliye» ett boosh bíaniyi. Bowere «Weetwe eteetso nebiyiwo neeneya?» bo et. Bíwere «bí taanaliye» bí eti.
Iwo anamufunsa kuti, “Nanga iwe ndiwe yani? Kodi ndiwe Eliya?” Iye anati, “Sindine.” “Kodi ndiwe Mneneri?” Iye anayankha kuti, “Ayi.”
22 Bowere «Beree konene? Noon woshetsuwotssh nokeewish n took jangosh aawk'owe nieteti?» bo eti.
Pomaliza iwo anati, “Ndiwe yani? Tipatse yankho kuti tipite nalo kwa amene anatituma. Kodi iwe ukuti chiyani za iwe mwini?”
23 Bíwere «Nebiywo Isayas b́ keewtsok'on Taa ‹Doonzo weero katsuwre› et fere worotse kuhiru asho k'aaro taane» bí eti.
Yohane anayankha ndi mawu a mneneri Yesaya kuti, “Ine ndi mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Wongolani njira ya Ambuye.’”
24 Ashuwotswere bo woshe ferisawiwotsi etefuwotsitsna botesh,
Tsopano Afarisi ena amene anatumidwa
25 Beree, «Nee Krstosi wee Eliyasi wee weetwe eteets nebiyo woto nk'azihakon eegoshe n gupiri?» ett bínboaati.
anamufunsa Iye kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani, umabatiza ngati iwe si Khristu, kapena Eliya, kapena Mneneri?”
26 Yohansuwere hank'o ett boosh bíaaniy, «Taa tgupirye aatsone, eree it it danawo it dagotse b́ ned'iriye.
Yohane anayankha kuti, “Ine ndimabatiza ndi madzi, koma pakati panu payima amene simukumudziwa.
27 Bí taayere ile b́ weetiye, taa b́ c'aami tipi joko bitsosh dab bodktanaliye.»
Iye ndi amene akubwera pambuyo panga, ine siwoyenera kumasula zingwe za nsapato zake.”
28 Man b́ wotwere Yohans b́ gupfoke Yordanos fokoniyere bak'etse Betani kitotsna b́tesh.
Zonsezi zinachitika ku Betaniya kutsidya lina la mtsinje wa Yorodani, kumene Yohane ankabatizira.
29 Yatsok'on Yohans Iyesusi b́ maants b́waafere bek't hank'o bíet «Datsantsi morro k'aa'ubazetwo Ik'i mereero haniye!
Pa tsiku lotsatira Yohane anaona Yesu akubwera kwa iye ndipo anati, “Taonani, Mwana Wankhosa wa Mulungu, amene achotsa tchimo la dziko lapansi!
30 ‹T shutsatse weyiru ekeew taayere shino b́ teshtsotse taayere ayidek't bogfe› ti ettsoniye haniye.
Uyu ndi amene ndimatanthauza pamene ndinanena kuti, ‘Munthu amene akubwera pambuyo panga ndi wondiposa ine chifukwa analipo ine ndisanabadwe.’
31 Taawor ttookish bín danaaktana b́tesh, ernmó Isra'el ashuwotssh b́ be'eyish taa aatson gupfere t weyi.
Ine mwini sindinamudziwe Iye, koma ndinabwera kubatiza ndi madzi kuti Iye adziwike mu Israeli.”
32 Manats dabt Yohans hank'o ett gawere S'ayin shayiro erkukundok'o darotse oot't biyats b́ k'ot'efre t bek'i.
Kenaka Yohane anapereka umboni uwu: “Ine ndinaona Mzimu Woyera ngati nkhunda kuchokera kumwamba nakhala pa Iye.
33 Taawor bín danaktane, ernmó aatson tgupetwok'o taan woshtsoniye, ‹Shayiro ood'r bíats b́ beewor n bek'etwo S'ayin shayiron gupetwo bíne› ett taash keewi.
Ine sindikanamudziwa Iye, koma kuti amene anandituma ine kudzabatiza ndi madzi anati kwa ine, ‘Munthu amene udzaona Mzimu Woyera akutsika nakhazikika pa Iye ndi amene adzabatize ndi Mzimu Woyera.’
34 Tawor han bek're, bí Ik'o naayi b́wottsok'owo gawitwe.»
Ine ndaona ndipo ndikuchitira umboni kuti uyu ndi Mwana wa Mulungu.”
35 Yatsok'on Yohans b́ danif gitetswotsnton aani manoke need'dek'tni b́ tesh,
Pa tsiku lotsatira Yohane analinso pamenepo pamodzi ndi awiri a ophunzira ake.
36 Yohans Iyesus man weeron b́beshefere bek't, «Hambe! Ik'oko mereroni!» bí et.
Iye ataona Yesu akudutsa anati, “Taonani Mwana Wankhosa wa Mulungu!”
37 Yohans danif gitetswots Yohans man b́ keewfere shisht Iyesus shutsats shoydek't bo ami.
Ophunzira ake awiriwo atamva iye akunena izi, iwo anamutsatira Yesu.
38 Iyesus wongr et aanat s'ilbek't, «Eebi it geyiri?» bíet. Bowere, «Rebi! eewke n beefoni?» boet. (rebi etoni danifino eta.)
Atatembenuka, Yesu anaona iwo akumutsatira ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mukufuna chiyani?” Iwo anati, “Rabi (kutanthauza kuti Aphunzitsi), kodi mukukhala kuti?”
39 Bíwere, «Waa s'iilere» bí eti. Eshe amt aak b́byirwok'o bos'ili. Manots aawots bínton towat bojin, manwere aaw tatsi sa'atok'oyi b́tesh.
Iye anayankha kuti, “Bwerani mudzaone.” Choncho iwo anapita ndi kukaona kumene Iye amakhala, ndipo anakhala naye tsiku limenelo. Linali ngati pafupifupi ora la khumi.
40 Yohans b́ keewts keewo shisht Iyesus shuuts amts b́ danif gitetswotsitse iko Simon P'et'ros eshu Indriyasi b́teshi.
Andreya mʼbale wake wa Simoni Petro, anali mmodzi wa awiriwo amene anamva zimene Yohane ananena ndiponso amene anamutsata Yesu.
41 Indriyas shin shino b́ eshu Sim'onok amt «Mesihiyo daatsdek'rone» bí et. (mesihiya eto Krstosi eta, wee fuuteka eta)
Choncho chimene Andreya anachita ndi kukapeza mʼbale wake Simoni ndipo anamuwuza kuti, “Ife tamupeza Mesiya,” (kutanthauza kuti Khristu).
42 Maniye il Indriyas Sim'oni Iyesusok dek't b́weyi. Iyesuswere t'iwintsdek't s'iilt, «Nee Yona naay Simon neene, haniye hakonmo Keefi eteyar s'egetune» bíet. (Keefi etonmu: P'et'rosi wee shútsi s'ala etee).
Kenaka iye anabweretsa Simoni kwa Yesu, amene anamuyangʼana ndipo anati, “Iwe ndiwe Simoni, mwana wa Yohane. Udzatchedwa Kefa” (limene litanthauza kuti Petro).
43 Yatsok'on Iyesus Gelilmants amo b́gee, Flip'osi daatsdek't, «T shuutso shoy de wowe» bí eti.
Pa tsiku lotsatira Yesu anaganiza zopita ku Galileya. Atamupeza Filipo, anati kwa iye, “Nditsate.”
44 Flip'os Indriyasnat P'et'rosnkok'o Bete Sayda eteets kitutsi asha b́tesh.
Filipo monga Andreya ndi Petro, anali wochokera ku mzinda mudzi Betisaida.
45 Filip'os Natna'eli daatsdek't, «Muse nemi mas'afatse, nebiyiwots bek'i mas'afatse b́ jangosh bo guut'tso daatsdek'rone, bíwere Yosef naay Nazrettso Iyesusiye» bí et.
Filipo anakapeza Natanieli ndipo anamuwuza kuti, “Ife tapeza amene Mose analemba za Iye mʼmalamulo, ndi zimene aneneri analembanso za Iye, Yesu wa ku Nazareti, mwana wa Yosefe.”
46 Natnaelmó, «Nazretitse sheeng keewo b́jamon daatsewo falitwa k'úúna?» bí eti. Filp'osuwere «Waar s'iile!» bíet.
Natanieli anafunsa kuti, “Nazareti! Kodi kanthu kalikonse kabwino kangachokere kumeneko?” Filipo anati, “Bwera udzaone.”
47 Natnael b́ maants b́waafere bek't Iyesus «Hambe! gond fino bíatse datserawo ariko Isra'el ashoni!» ett b́jangosh b́keewi.
Yesu atamuona Natanieli akuyandikira, anati kwa iye, “Uyu ndi Mwisraeli weniweni, mwa iye mulibe chinyengo.”
48 Natnaeluwere «Aawokneya taan ndani?» bíet. Iyesuswere «Filip'os neenbs'egfetsere shino Belesi mitú shirotse n befere neen bek're» ett bísh bíaniyi.
Natanieli anafunsa kuti, “Kodi mwandidziwa bwanji?” Yesu anayankha kuti, “Ine ndinakuona iwe utakhala pansi pamtengo wamkuyu Filipo asanakuyitane.”
49 Manoor Natna'el, «Danifono! nee Ik'o naay neene! nee Isra'el naasho neene!» bí et.
Kenaka Natanieli ananena kuti, “Rabi, Inu ndinu Mwana wa Mulungu; Inu ndinu Mfumu ya Israeli.”
50 Iyesusu hank'owa bíet, «Nee ni aman, ‹Belesi mitu shirotse n befere neen bek're› ti ettsosheya? Haniye bogts keewwotsi shinomaants bek'etune.
Yesu anati, “Ukukhulupirira chifukwa chakuti ndakuwuza kuti Ine ndinakuona iwe uli pansi pamtengo wamkuyu? Iwe udzaona zinthu zazikulu kuposa izo.”
51 Arikoniye neesh tkeewiri, Daro b́k'eshere melkiwots ashna'o ats keer bo'ot'fere bek'etute.»
Ndipo Iye anapitirira kuti, “Zoonadi, Ine ndikuwuza kuti iwe udzaona kumwamba, kutatsekuka ndi angelo a Mulungu akukwera ndi kutsika pa Mwana wa Munthu.”