< Ibrawiyots 2 >

1 Eshe no shishts keewatse shortarr no dihirawok'o no shishits keew man jango sheengsh kordek'o noosh geyitwe.
Nʼchifukwa chake, ife tiyenera kusamalira kwambiri zimene tinamva, kuopa kuti pangʼono ndi pangʼono tingazitaye.
2 Melakiwots weeron keewets aap'o arik wotwtsere, keewan finats jiitsrawonat keewmansho alerawo bísh wotit fayo daatsre,
Popeza uthenga umene unayankhulidwa kudzera mwa angelo unali okhazikika ndithu, choncho aliyense amene ananyozera ndi kusamvera analandira chilango choyenera.
3 Eshe, no kashts kash een wotts keewan no aatsnitka wotiyal aawk'oneya b́ shirotse keshosh nofaliti? Kashaanowere shin shin shishiyo dek'tuutso b́ tookon doonzoniye, bíyoke shishts ashuwotswere ar b́wottsok'o danirne.
Nanga ife tidzapulumuka bwanji tikapanda kusamala chipulumutso chachikulu chotere? Ambuye ndiye anayamba kuyankhula za chipulumutsochi, kenaka amenenso anamvawo anatitsimikizira.
4 Ik'onwere dabt milkiton, adits keewon, k'osh k'osh aditswotsi woshonat b́ shunok'o b́ imts shayiri S'ayin weeron bo gawts gawo kup'shre.
Mulungu anachitiranso umboni pochita zizindikiro, zinthu zodabwitsa ndi zamphamvu zamitundumitundu ndi powapatsa mphatso za Mzimu Woyera monga mwachifuniro chake.
5 Ik'o shinomaants weet datsu, no bjango nokeweyiru melakiwots bin boosh kewiratse
Mulungu sanapereke kwa angelo ulamuliro wa dziko limene likubwerali, limene ife tikulinena.
6 Dab́ S'ayin mas'aafwotsitse ikoke hank'o eteere, «Nee bín n gawitwok'osh asho eebi? Bo kis'o n detsetwok'o ash na'o eebi?
Koma palipo pena pamene wina anachitira umboni kuti, “Kodi munthu ndani kuti muzimukumbukira, kapena mwana wa munthu kuti muzimusamalira?
7 Melakiwotsiyere muk'i ndashiyi Mangonat údi zewdiyo b́ tookats n gedi
Munamuchepetsa pangʼono kusiyana ndi angelo; munamupatsa ulemerero ndi ulemu.
8 Jam keewo bí ali shirots n woshi.» Jam keewo bí ali shirots b́ woshor, bí ali shirots woshraniyere b́ ooritso eegonwor aaliye. Ernmó and jam keewo b́ fa'ok'on bí ali shirotse b́ beyirwok'o andish b́borfetso be'afa'one.
Munamupatsa ulamuliro pa zinthu zonse.” Poyika zinthu zonse pansi pa ulamuliro wake, Mulungu sanasiye kanthu kamene sikali mu ulamuliro wake. Koma nthawi ino sitikuona zinthu pansi pa ulamuliro wake.
9 Andomó muk' aawush melakiwotsiyere muk'i dashan teshts k'iri gond bek'o b́daatstsosh mangonat údi zewdiyo kurdek'tso Iyesusi bek'etwone, bí Ik'i s'aaton no únetssh k'irre.
Koma tikuona Yesu, amene kwa kanthawi kochepa anamuchepetsa pangʼono kwa angelo, koma tsopano wavala ulemerero ndi ulemu chifukwa anamva zowawa za imfa, kuti mwachisomo cha Mulungu, Iye afere anthu onse.
10 Jam keewo bínat b́tookish azdek'ts Ik'o ay nana'úwotsi mangomants dowosh bo kashit weero jishitwo Iyesusi gond bek'on s'een b́ wotitwok'o b́woshi.
Mulungu amene analenga zinthu zonse ndipo zinthu zonse zilipo chifukwa cha Iye ndi mwa Iye, anachiona choyenera kubweretsa ana ake ambiri mu ulemerero. Kunali koyenera kudzera mʼnjira ya zowawa, kumusandutsa Yesu mtsogoleri wangwiro, woyenera kubweretsa chipulumutso chawo.
11 Ashuwotsi S'ayin woshitwonat b́weeron S'ayin wotts ashuwotswere nih iko nana'úwotsiye, manatse tuwtson Iyesus bonowere «T eshwotsiye» err s'eegosh jitseratse.
Popeza iye amene ayeretsa ndi oyeresedwa onse ndi abanja limodzi. Nʼchifukwa chake Yesu sachita manyazi kuwatcha iwo abale ake.
12 Mansh S'ayin mas'aafwotsitse «N shúútso tieeshwotssh keewitwe, Ashuwots bokakwetsokee botaalotse dubon neen uditwe» etre.
Iye akuti, “Ine ndidzawuza abale anga za dzina lanu. Ndidzakuyimbirani nyimbo zamatamando pamaso pa mpingo.”
13 Mank'o «Taa bí ats t imneitiyo juwitwe» etre, Ando aani «Hamb eshe taanat Ik'o taash b́imts nana'awotsn hanok noone» etre.
Ndiponso, “Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.” Ndiponso Iye akuti, “Ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Mulungu wandipatsa.”
14 Mansh nana'anots meetsonat s'atson detsk ash bowottsotse Iyesuswere bokok'o ash b́wotiye, man b́ k'alwere b́ k'irtsatse tuutson k'iratse al detstso dablosi t'afiyoshee.
Tsono popeza kuti anawo ndi anthu, okhala ndi mnofu ndi magazi, Yesu nayenso anakhala munthu ngati iwowo kuti kudzera mu imfa yake awononge Satana amene ali ndi mphamvu yodzetsa imfa.
15 Mank'o k'ir shati jangosh bo dúr jamo guuts wotat kéweyat beyirwotsi aaniy kewdek'oshee.
Pakuti ndi njira yokhayi imene Iye angamasule amene pa moyo wawo wonse anali ngati akapolo chifukwa choopa imfa.
16 Iyesus shuno, melakiwotsi b́ woterawo, Abraham naaro tep'oshee.
Pakuti tikudziwanso kuti sathandiza angelo, koma zidzukulu za Abrahamu.
17 Mansh jam keewo bí eshwots kok'o woto bísh geyife b́teshi, mank'oon ashuwots morro orowa etosh Ik'osh finosh amanetsonat maarts kahni naashwotsatsi k'aabo b́wotiye.
Chifukwa cha zimenezi, Iye anayenera kukhala wofanana ndi abale ake pa zonse, kuti akhale mkulu wa ansembe wachifundo ndi wokhulupirika potumikira Mulungu, kuti potero achotse machimo a anthu.
18 Bí b́ tookosh fadeyat gondo b́bek'tsotse fadeyrwotsi tep'o falitwe.
Popeza Iye mwini anamva zowawa pamene anayesedwa, Iyeyo angathe kuthandiza amene akuyesedwanso.

< Ibrawiyots 2 >