< लूका 1 >
1 जनाब थियुफिलुस, बड़े लोकेईं तैना गल्लां हेरी ज़ैना प्रभु-यीशुए कियोरी थी, ज़ैखन तै असन सेइं साथी थियो, ज़ेइसेरां तैनी अपनू सेवारू कम शुरू कियोरू थियूं। तैन मैनेईं होरि मैनन् यीशुएरे बारे मां शिक्षा देइतां परमेशरेरी सेवा की। बड़े मैनेईं तैन केरि गल्लां शुन्तां यीशुएरे बारे मां इश्शे लेइ इतिहासेरी किताब लिखी।
Ambiri anayesa kufotokoza nkhani ya zimene zinakwaniritsidwa pakati pathu,
monga mmene zinaperekedwera kwa ife ndi iwo amene anaona poyambirira ndi atumiki a mawu.
3 मीं एप्पू तैन सैरी गल्लां केरि बड़े रोड़ेच़ारे छानबीन की। एल्हेरेलेइ, मीं एन रोड़ू लग्गू, कि अवं भी तुश्शे लेइ तैन गल्लां केरे बारे मां ठीक डंगे सेइं इतिहासेरी किताब लिखी।
Popeza inenso ndafufuza mosamalitsa chilichonse kuyambira pachiyambi, zandikomera kukulemberani mwatsatanetsatane inu wolemekezeka Tiofilo,
4 अवं चाताईं कि तीं पतो लग्गे कि यीशुएरे बारे मां तैना गल्लां सच़्च़ी आन, ज़ैन केरे बारे मां तुसन शिक्षा मैल्लोरी थी।
kuti mudziwe bwinobwino zoona za zinthu zimene mwaphunzitsidwa.
5 यहूदिया इलाके मां, ज़ैखन हेरोदेस राज़ो राज़ केरतो थियो, त तैखन जकर्याह नंव्वेरो अक यहूदी याजक थियो। तै मैन्हु याजकां केरे टोली मां अबिय्याह नंव्वेरो टोली मरां थियो। तैसेरी कुआन्शारू नंव एलीशिबा थियूं। एलीशिबा हारूनेरे खानदेंनी मरां थी, (हारून इस्राएल लोकां केरो पेइलो याजक थियो)।
Mʼmasiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali wansembe dzina lake Zakariya wa gulu la ansembe la Abiya; mkazi wake Elizabeti analinso wa fuko la Aaroni.
6 तैना दुइये प्रभु-परमेशरेरी नज़री मां धर्मी थियां ते कने परमेशरेरे सारे कानून ते सारे हुक्मन पुड़ बेइलज़ाम च़लनेबालां थियां।
Onse awiri anali olungama pamaso pa Mulungu, ndipo amasunga malamulo ndi malangizo onse a Ambuye osalakwa konse.
7 पन तैन केरि कोई औलाद न थी, किजोकि एलीशिबा बाँझ थी, ते तैना दुइये बुढ़ां थियां।
Koma analibe ana chifukwa Elizabeti anali wosabereka; ndipo onse anali okalamba.
8 एक्की फेरे, जकर्याहेरी टोली यरूशलेम नगरेरे मन्दरे मां सेवारू कम केरि राओरे थी, तैखन तै प्रभु परमेशरेरी हज़ूरी मां अपनू याजकेरू कम लोगोरो थियो केरने।
Nthawi yogwira ntchito yotumikira ansembe a gulu la Zekariya, Zekariya ankatumikira ngati wansembe pamaso pa Mulungu,
9 याजकां केरे रीतरे मुताबिक तैनेईं परची छ़ेडतां जकर्याह च़ुनो कि तै प्रभु-परमेशरेरे मन्दरे मां गेइतां गुग्गल बाले।
Zakariyayo anasankhidwa mwa maere, monga mwa mwambo wa unsembe, kupita mʼNyumba ya Ambuye kukafukiza lubani.
10 ज़ैखन तै गुग्गल बालने लोरो थियो, त तैखन मैन्हु केरि सारी भीड़ मन्दरेरे बेइर प्रार्थना केरि राओरी थी।
Ndipo nthawi yofukiza lubani itafika, gulu lonse lopembedza linkapemphera kunja.
11 तैखन अचानक प्रभु-परमेशरेरो अक स्वर्गदूत गुग्गल बालनेरी ठारारे देइने पासे खड़े भोइतां जकर्याह लेइहोव।
Kenaka mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye, atayimirira ku dzanja lamanja la guwa lofukizira.
12 ज़ैखन जकर्याहे स्वर्गदूत लाव, त तै घेमरोव ते बड़ो डेरि जेव।
Zakariya ataona mngeloyo, anadzidzimuka ndipo anagwidwa ndi mantha.
13 पन स्वर्गदूते तैस सेइं ज़ोवं, “हे जकर्याह, न डर! ज़ैखन तीं प्रार्थना की, त परमेशरे तेरी प्रार्थना शुनी। एल्हेरेलेइ, तेरी कुआन्श एलीशिबाई मट्ठू भोनूए, ते तू तैसेरू नंव यूहन्ना रेख्खां।
Koma mngeloyo anati kwa iye: “Usachite mantha, Zakariya; pemphero lako lamveka. Mkazi wako Elizabeti adzakuberekera iwe mwana wamwamuna ndipo udzamutche dzina loti Yohane.
14 तैसेरे ज़र्म भोने सेइं तू बड़ो खुश भोलो। त बड़े लोक भी खुश भोले।
Ndipo adzakhala chimwemwe ndi chisangalalo kwa iwe, ndipo ambiri adzasangalala chifukwa cha kubadwa kwake,
15 तै प्रभु-परमेशरेरी नज़री मां महान भोलो, ते तैनी कोन्ची भी किसमेरी नश्शे बाले चीज़ त कने शराब कधे न लोड़े पियोरी, ते तै अपनि अम्मारे पेटे मां भोते वक्तेरां परमेशरेरी पवित्र आत्मारी शेक्ति सेइं भरपूर भोलो।
chifukwa adzakhala wamkulu pamaso pa Ambuye. Iye sadzamwa vinyo kapena chakumwa choledzeretsa, ndipo adzazadzidwa ndi Mzimu Woyera kuyambira pa kubadwa.
16 तै इस्राएली लोकन मरां बड़े लोक परमेशरेरे पासे ज़ै तैन केरो प्रभु परमेशरे वापस तैस कां आनेलो, ज़ैना अपने पापां केरि वजाई सेइं परमेशरे करां दूर भोरे थिये।
Iye adzabweretsanso Aisraeli ambiri kwa Ambuye Mulungu wawo.
17 ते तै एरो मैन्हु भोलो ज़ैस पुड़ एलिय्याहरी आत्मा ते कने शक्ति भोली। तै परमेशरेरी बत तियार केरेलो, तैस अग्री-अग्री च़लेलो ताके हाज बव्वां केरो दिल औलादरे पासे ते परमेशर न मन्नेबाले लोकन धेर्मी लोकां केरे बत्तां केरे पासे बदलेलो, ताके ज़ैखन प्रभु एज्जे त लोक तियार भोन।”
Ndipo iye adzabwera Ambuye asanabwere mu mzimu ndi mphamvu ya Eliya. Adzatembenuzira mitima ya abambo kwa ana awo ndi osamvera ku nzeru ya olungama, kuthandiza anthu kuti akonzekere kubwera kwa Ambuye.”
18 जकर्याहे स्वर्गदूते पुच़्छ़ू, “अवं केन्च़रे मेन्नी एन असन सेइं भोनूए, अवं त बुढोइं ते मेरी कुआन्श भी बुढी भोरीए।”
Zakariya anamufunsa mngeloyo kuti, “Kodi ndingatsimikize bwanji zimenezi? Ine ndine wokalamba ndipo mkazi wanga ali ndi zaka zambiri.”
19 स्वर्गदूते जुवाब दित्तो, “अवं जिब्राईल आईं अवं परमेशरे कां खड़ो भोताईं, अवं एल्हेरेलेइ भेज़ोरोईं, कि अवं तीं सेइं गल केरि ते तीं ए खुशखबरी शुनेई।
Mngeloyo anayankha kuti, “Ine ndine Gabrieli. Ndimayima pamaso pa Mulungu, ndipo ndatumidwa kwa iwe kudzakuwuza uthenga wabwinowu.
20 ते हेर ज़ां तगर एना गल्लां पूरी न भोन तेरी ज़बान बंद भोली, ते तू गल न केरि सकेलो किजोकि तीं मेरी गल्लां केरू याकीन नईं कियेरू ज़ैना अपने वक्ते पुड़ पूरी भोनिन।”
Ndipo kuyambira tsopano sudzatha kuyankhula kufikira izi zitachitika chifukwa sunakhulupirire mawu awa, amene adzakwaniritsidwe pa nthawi yake yoyenera.”
21 ते ज़ैखन जकर्याह ते स्वर्गदूत मन्दरे मां गल्लां लोरे थिये केरने त लोक मन्दरेरे बेइर अंगने मां जकर्याहे बलगने लोरे थिये, तैना बड़े हैरान भोइजेइ कि जकर्याहे मन्दरे मां एत्रू च़िर किजो लाव।
Pa nthawiyi, anthu ankadikira Zakariya ndipo anadabwa chifukwa anatenga nthawi yayitali ali mʼNyumba ya Mulungu.
22 ज़ैखन तै बेइर निस्सो, त तै कुजी न बटो ते तैन लोकेईं बुझ़ी छ़डू, कि एनी मन्दरे मां किछ दर्शन लाहेरूए किजोकि तै इशारो केरतो थियो, पन कुजी न थियो बटतो।
Atatuluka sanathe kuyankhulana nawo. Anazindikira kuti anaona masomphenya mʼNyumbamo, chifukwa ankasonyeza zizindikiro kwa iwo koma sankatha kuyankhula.
23 ज़ेइस यरूशलेम नगरेरे मन्दरे मां जकर्याहरू एक्की हफतेरे याजकेरी सेवारू कम पूरू भोवं, त तै अपने घरे जो च़लो जेव।
Nthawi yake yotumikira itatha, anabwerera kwawo.
24 किछ वक्तेरां बाद तैसेरी कुआन्श एलीशिबा दोज़ींतीए भोइ, ते तै पंच़ महीन्न तगर बेइर लोकन मां न जेई। तैसां ज़ोवं,
Zitatha izi, mkazi wake Elizabeti anakhala ndi pakati ndipo anadzibisa kwa miyezi isanu.
25 “प्रभुए मीं पुड़ दया केरतां केत्रू महान कम कियूं, ते अवं दोज़ींती भोइ, ते ज़ैस गल्लरे वाजाई सेइं लोक मीं घटिया समझ़ते थिये, तै गल दूर की।”
Iye anati, “Ambuye wandichitira izi, kuti mʼmasiku ano wandionetsera kukoma mtima kwake ndi kuchotsa manyazi anga pakati pa anthu.”
26 एलीशिबारे दोज़ींती भोनेरे शेइयोवं महीने जिब्राईल स्वर्गदूत परमेशरेरी तरफां गलील इलाकेरे नासरत नगरे मां,
Mwezi wachisanu ndi chimodzi, Mulungu anatuma mngelo Gabrieli ku Nazareti, mudzi wa ku Galileya,
27 एक्की अड्लैई कुइये कां भेज़ो। तैसारी कुड़माइ दाऊदेरे खानदाने मरां एक्की मड़दे सेइं भोरी थी ज़ेसेरू नवं यूसुफ थियूं, ते तैस कुइयरू नवं मरियम थियूं।
kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi Yosefe, wa fuko la Davide. Dzina la namwaliyo linali Mariya.
28 स्वर्गदूते तैस कां एइतां ज़ोवं, “आनन्द ते ज़ींत तेरी भोए, तीं पुड़ परमेशरेरी बड़ी दया भोरीए, प्रभु तीं सेइं साथिये!”
Mngeloyo anafika kwa iye nati, “Moni, inu amene Ambuye wakukomerani mtima kwambiri! Ambuye ali ndi inu.”
29 मरियम स्वर्गदूतेरी गल शुन्तां परेशान भोइतां सोचने लगी एन केरहु नमस्कारे?
Mariya anavutika kwambiri ndi mawu awa ndipo anadabwa ndi kulonjera kotere.
30 स्वर्गदूते तैस सेइं ज़ोवं “हे मरियम, डर न, किजोकि परमेशरेरो तीं पुड़ बड़ो अनुग्रह भोरोए।
Koma mngeloyo anati kwa iye, “Usachite mantha Mariya, pakuti wapeza chisomo pamaso Mulungu.
31 तू दोज़ींती भोली तीं अक मट्ठू भोलू, ते तू तैसेरू नवं यीशु रेखां।
Udzakhala woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna ndipo udzamupatse dzina loti Yesu.
32 तैन महान भोलू ते तैस जो परमप्रधान परमेशरेरू मट्ठू ज़ोले, ते परमेशर तैस तैसेरे पूर्वज दाऊद राज़ेरू ज़ेरो राज़ो बनालो।
Iye adzakhala wamkulu ndipo adzatchedwa Mwana wa Wammwambamwamba. Ambuye Mulungu adzamupatsa Iye mpando waufumu wa abambo ake Davide,
33 ते तै याकूबेरे खानदाने पुड़ हमेशा राज़ केरेलो, ते तैसेरू राज़ कधे खतम न भोलू।” (aiōn )
ndipo adzalamulira pa nyumba ya Yakobo ku nthawi zonse; ufumu wake sudzatha.” (aiōn )
34 मरियमा स्वर्गदूते पुच़्छ़ू, “एन केन्च़रे भोइ सकते? अवं त अड्लाई आईं।”
Mariya anafunsa mngeloyo kuti, “Izi zingatheke bwanji popeza ine sindidziwa mwamuna?”
35 स्वर्गदूते जुवाब दित्तो, “पवित्र आत्मा तीं पुड़ उतरेलो, ते परमप्रधान परमेशरेरी शक्ति तीं पुड़ सैयो केरेली एल्हेरेलेइ तै बच्चो ज़ै ज़र्मएलो तै पवित्र भोलो तैस जो परमेशरेरू मट्ठू ज़ोले।
Mngelo anayankha kuti, “Mzimu Woyera adzabwera pa iwe ndipo mphamvu ya Wammwambamwamba idzakuphimba, ndipo Woyerayo amene adzabadwe adzatchedwa Mwana wa Mulungu.
36 ते हेर तेरी रिशतेदार एलीशिबाई भी बुढ़े बारे मट्ठू भोने बालूए तैस जो लोक बाँझ ज़ोते थिये, तैस दोज़ींती शा महीने भोरेन।
Ngakhale Elizabeti mʼbale wako adzakhala ndi mwana mu ukalamba wake ndipo iye amene amati ndi wosabereka, uno mwezi wake wachisanu ndi chimodzi.
37 किजोकि परमेशरेरे लेइ किछ भी नमुमकिन नईं।”
Pakuti palibe chinthu chosatheka ndi Mulungu.”
38 मरियमा स्वर्गदूते जुवाब दित्तो, “अवं परमेशरेरी सेवा केरती ज़ैन तीं ज़ोरूए तैन भोए।” तैखन स्वर्गदूत तैस करां च़लो जेव।
Mariya anayankha kuti, “Ine ndine mtumiki wa Ambuye. Zikhale kwa ine monga mwanenera.”
39 किछ दिहाड़न पत्ती मरियम तियार भोइतां यहूदियारे इलाकेरे एक्की पहाड़ी नगरे मां जेई।
Nthawi imeneyo anakonzeka ndipo anapita mofulumira ku mudzi wa ku mapiri a dziko la Yudeya,
40 ते जकर्याहरे घरे मां गेइतां एलीशिबा जो नमस्कार कियूं।
kumene anakalowa mʼnyumba ya Zakariya nalonjera Elizabeti.
41 ज़ैखन एलीशिबा मरियमारू नमस्कार शुनू त बच्चो तैसारे पेटे मां उछ़ड़ने लगो ते एलीशिबा पवित्र आत्माई सेइं भेरोई जेई।
Elizabeti atamva moni wa Mariya, mwana anatakataka mʼmimba mwake, ndipo Elizabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera.
42 ते बड़े ज़ोरे सेइं ज़ोने लगी, “तू कुआन्शन मां धन आस ते ज़ै बच्चो तीं ज़ांनोए तै भी धने!
Anafuwula ndi mawu akulu kuti, “Ndiwe wodala pakati pa akazi, ndipo ndi wodala mwana amene udzabereke!
43 ते मेरे लेइ बड़ी इज़्ज़तरी गल आए कि, मेरे प्रभुएरी अम्मा मीं कां आई!
Koma nʼchifukwa chiyani andikomera mtima kuti amayi a Ambuye anga abwere kwa ine?
44 किजोकि हेर ज़ेरि तेरे नमस्कारेरी आवाज़ मीं शुनी त बच्चे खुशी सेइं मेरे पेटे मां छालां लगो मारने।
Nthawi yomwe ndinamva mawu akulonjera kwanu, mwana anatakataka mʼmimba mwanga chifukwa cha chimwemwe.
45 तू धन आस तीं तैन गल्लन पुड़ विश्वास कियो ज़ैना प्रभुए तीं सेइं ज़ोई कि, तैना पूरी भोली।”
Wodala iye amene wakhulupirira kuti chimene Ambuye wanena kwa iye chidzakwaniritsidwa!”
46 ते मरियमा ज़ोवं, “अवं प्रभुएरी तारीफ़ केरती।
Ndipo Mariya anati: “Moyo wanga ulemekeza Ambuye.
47 ते मेरी आत्मा मेरे मुक्ति देनेबाले परमेशरे सेइं खुशी भोइ।
Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,
48 किजोकि तैनी अपनि सेवा केरने बैलरी गिरोरी हालती पुड़ नज़र की, अज़ेरां देइतां हर ज़मानेरे लोक मींजो धन ज़ोले।
pakuti wakumbukira kudzichepetsa kwa mtumiki wake. Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,
49 किजोकि परमेशरे मेरे लेइ बड़ां-बड़ां कम्मां कियोरन ते तैसेरू नवं पवित्र भोए।
pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu, dzina lake ndi loyera.
50 तैसेरी दया तैस करां डरने बालन पुड़ पीड़ी-पीड़ी तगर राचे।
Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye kufikira mibadomibado.
51 तैनी अपने शेक्ति सेइं बड्डां-बड्डां कम्मां कियोरन तैनी घमण्डी तितर-बितर किये।
Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake; Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.
52 तैनी राज़े राज़ केरने करां रोके, ते तैनी नम्र लोकन आदर दित्ती।
Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu, koma wakweza odzichepetsa.
53 तैनी नियन्ने रोड़ी-रोड़ी चीज़ेइं सेइं रज़ांने ते धन दौलती बाले खाली हथेइं भेज़े।
Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino koma anachotsa olemera wopanda kanthu.
54 तैनी अपने वादे ज़ैना तैनी इश्शे दादन-पड़दादन सेइं कियोरे थिये याद किये, तैनी अपनि सेवा केरनेबाले इस्राएली लोकां केरि मद्दत की,
Iye anathandiza mtumiki wake Israeli, pokumbukira chifundo chake.
55 तैनी हमेशारे लेइ अब्राहमे पुड़ ते तैसेरी औलादी पुड़ दया केरनि याद रख्खी।” (aiōn )
Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse monga ananena kwa makolo athu.” (aiōn )
56 मरियम कोई ट्लाई महीन्न तगर एलीशिबा सेइं साथी राई ते फिरी अपने घरजो आई।
Mariya anakhala ndi Elizabeti pafupifupi miyezi itatu ndipo kenaka anabwerera kwawo.
57 एलीशिबारो गल्हे बिशनेरो वक्त एज्जी अव ते तैस मट्ठू भोवं।
Itakwana nthawi yoti Elizabeti abereke, anabereka mwana wamwamuna.
58 तैसारे आसेपासेरे रिशतेदारेइं एन शुनू कि परमेशरे तैस पुड़ बड़ी दया कियोरिये ते तैस सेइं साथी खुशी मनाई।
Anansi ndi abale ake anamva kuti Ambuye anamuchitira chifundo chachikulu ndipo anakondwera naye pamodzi.
59 अठोवं दिहाड़े तैना मट्ठेरो खतनो केरने आए, ते तैना तैसेरू नवं तैसेरे बाजी केरे नव्वें पुड़ जकर्याह रखनू चाते थिये।
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu anabwera ndi mwana kuti adzachitidwe mdulidwe, ndipo anafuna kumupatsa dzina la abambo ake Zakariya,
60 पन तैसेरी अम्मा ज़ोने लगी, “नईं एसेरू नवं यूहन्ना भोलू।”
koma amayi ake anayankhula nati, “Ayi, atchulidwe kuti Yohane.”
61 किछ तैस जो ज़ोने लगे, “तुश्शी खानदेंनी मां कोई भी एस नव्वेंरो नईं।”
Iwo anati kwa iye, “Palibe mmodzi mwa abale ake amene ali ndi dzina limeneli.”
62 तैखन तैन लोकेईं जकर्याहरे पासे इशारे सेइं पुच़्छ़ू कि तू मट्ठेरू नवं कुन रखनू चातस?
Pamenepo anapanga zizindikiro kwa abambo ake kuti adziwe dzina limene akanakonda kumutcha mwanayo.
63 ते तैनी पटारी मगी ते तैस पुड़ लिखू, “एसेरू नवं यूहन्ना आए,” ते सब लोक हैरान रेइजे।
Iye anapempha poti alembepo, ndipo chodabwitsa kwa aliyense analemba kuti, “Dzina lake ndi Yohane.”
64 तैखने तैसेरी ज़िभ खुल्ली ते जकर्याह गल्लां लगो केरने ते परमेशरेरी तारीफ़ केरने लगो।
Nthawi yomweyo pakamwa pake panatsekuka ndi lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula, nayamika Mulungu.
65 ते आसे-पासेरे लोक एस तमाशे हेरतां हैरान रेइजे, ते यहूदियारे इलाकेरे एक्की पहाड़ी नगर मां एस गल्लरी चरचा भोने लगी।
Anansi onse anachita mantha kwambiri, ndipo ku madera onse a kumapiri a Yudeya, anthu anayankhula zinthu zonsezi.
66 ते शुन्ने बाले अपने-अपने मन्न मां सोचते थिये, “एन मट्ठू बड्डू भोइतां केरहु भोनूए?” किजोकि परमेशरेरी शक्ति अज़्ज़ेरी देंतीं एस सेइं साथीए?
Aliyense amene anamva izi anadabwa nazo nafunsa kuti, “Kodi mwana uyu adzakhala wotani?” Pakuti dzanja la Ambuye lili pa iye.
67 तैखन तैसेरो बाजी जकर्याह पवित्र आत्माई सेइं भेरोवं ते भविष्यिवाणी केरने लगो।
Abambo ake, Zakariya, anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo ananenera kuti,
68 “प्रभु इस्राएलेरो परमेशर धन भोए, किजोकि तैनी एइतां अपने लोकन मुक्ति दित्तोरिये।
“Alemekezeke Ambuye, Mulungu wa Israeli chifukwa wabwera ndi kuwombola anthu ake.
69 ते तैसेरे दास दाऊदेरे घराने मरां इश्शे लेइ अक मुक्ति देनेबालो भेज़ोरोए।
Iye wakweza nyanga yachipulumutso kwa ife mu nyumba ya mtumiki wake Davide.
70 (बड़े पेइले ज़ेन्च़रे पवित्र नेबी केरे ज़िरिये ज़ोरू थियूं, ज़ैन शुरू करां देंते ओरूए।) (aiōn )
(Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera), (aiōn )
71 असां अपने दुश्मन करां ते बैर रखने बालन करां मुक्ति हासिल केरम।
chipulumutso kuchoka kwa adani athu ndi kuchoka mʼdzanja la onse otida,
72 ते तै इश्शे दादे पड़दादन पुड़ दया केरे ते अपनो पवित्र करार याद केर।
kuonetsa chifundo kwa makolo athu ndi kukumbukira pangano lake loyera,
73 तै करार ज़ै तीं इश्शे पूर्वज अब्राहमे सेइं कियोरो थियो।
lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:
74 कि तै असन हिम्मत देलो, कि असां अपने दुश्मन करां बगैर केन्ची भी डरे सेइं बेंच़ी सखम।
kutilanditsa ife mʼdzanja la adani athu, ndi kutipanga ife timutumikire Iye mopanda mantha,
75 ते अपनि ज़िन्दगी तैस सोंफम ते सारी ज़िन्दगी पवित्रेइ ते धार्मिकता ज़ींम।
mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.
76 ते हे बच्चां तू नबी भोलो किजोकि तू परमेशरेरे अग्री-अग्री च़ेलतां लोकन तियार केरेलो कि परमेशर एजनोए।
“Ndipo iwe mwana wanga udzatchedwa mneneri wa Wammwambamwamba; pakuti udzapita patsogolo pa Ambuye kukonza njira yake,
77 तै अपने लोकन तैन केरे पाप माफ़ केरनेरे ज़िरिये मुक्तरे बारे मां ज्ञान देलो।
kupatsa anthu ake chidziwitso cha chipulumutso kudzera mwa chikhululukiro cha machimo awo,
78 ते इश्शे परमेशरेरी दया एरी भोली ज़ेन्च़रे दिहाड़ो लौ देते तेन्च़रे मसीह स्वर्गेरां एज्जेलो।
chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzafikira ife kuchokera kumwamba,
79 ताके तैन केरे लेइ ज़ैना पापे मां ज़ीतन ते हमेशारे मौतरे खतरे मां रातन लौ दे, ते तै असन बत हिराए ताके अस सुखे सेइं ज़िन्दगी ज़ींम।”
kuwalira iwo okhala mu mdima ndi mu mthunzi wa imfa, kutsogolera mapazi athu mu njira yamtendere.”
80 तैन मट्ठू यानी यूहन्ना बेडोतो जेव ते आत्माई मां बद्धतो जेव ते इस्राएलेरे लोकन प्रचार केरने तगर सुनसान ठैरन मां राव।
Ndipo mwanayo anakula nakhala wamphamvu mu mzimu; ndipo anakhala ku chipululu mpaka pamene anaonekera poyera mu Israeli.