< Idisu 3 >
1 Hina Gode da Sainai Goumia Elane amola Mousesema sia: i. Amo esoga, ela sosogo fi da agoane galu.
Iyi ndi mbiri ya banja la Aaroni ndi Mose pa nthawi yomwe Yehova anayankhula ndi Mose pa phiri la Sinai.
2 Elane egefelali da biyaduyale galu. Ilia dio, magobo Na: ida: be. Amo baligia da Abaihiu, Elia: isa amola ufidafa da Idama.
Mayina a ana aamuna a Aaroni anali Nadabu, woyamba kubadwa, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
3 Ilia huluane da gobele salasu dunu hamoma: ne susuligi legele, momogili gagai dagoi ba: i.
Amenewa ndi mayina a ana aamuna a Aaroni, ansembe odzozedwa omwe anapatulidwa kuti azitumikira ngati ansembe.
4 Be Na: ida: be amola Abaihiu da sia: mae nabane, hame hadigi lalu amo Sainai hafoga: i sogega Hina Godema imunusa: dawa: beba: le, Hina Gode da ela medole legei. Ela da mano hame. Amaiba: le, Elane da esalea, Elia: isa amola Idama da eda Elane esalebeba: le, gobele salasu dunu hawa: hamonanu.
Koma Nadabu ndi Abihu, anagwa nafa pamaso pa Yehova pamene ankapereka nsembe ndi moto wachilendo pamaso pa Yehova mʼchipululu cha Sinai. Iwowo analibe ana aamuna. Choncho Eliezara ndi Itamara ndiwo amene ankatumikira ngati ansembe nthawi imene Aaroni abambo awo anali moyo.
5 Hina Gode da Mousesema amane sia: i,
Yehova anati kwa Mose,
6 “Lifai fi dunu oule misini, ilia da gobele salasu dunu Elane amo ea hawa: hamoma: ne, Lifai dunu momogili gagama.
“Bweretsa fuko la Levi ndipo ulipereke kwa Aaroni wansembe kuti lizimutumikira.
7 Ilia da Na Abula Diasu ouligima: ne hawa: hamomu amola gobele salasu dunu amola fi dunu huluane fidima: ne, ilelegema.
Azigwira ntchito yothandiza iyeyo ndi gulu lonse ku tenti ya msonkhano pogwira ntchito ya ku Chihema.
8 Ilia da liligi huluane Na Abula Diasu ganodini sali amo huluane ouligimu. Amola Isala: ili dunu huluane fidima: ne, hawa: hamomu.
Azisamalira zipangizo zonse za mu tenti ya msonkhano, ndipo azigwirira ntchito Aisraeli potumikira mu tenti.
9 Ilia da eno hawa: hamosu hame hamomu. Ilia da Elane amola ea mano fawane fidimu.
Pereka Alevi kwa Aaroni ndi kwa ana ake aamuna. Amenewa ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwa iye kwathunthu.
10 Be dia Elane amola ea mano amo elea gobele salasu hawa: hamosu fawane hamoma: ne ilegema. Be nowa dunu eno da ilia hawa: hamosu amo udigili hamomusa: dawa: sea, amo medole legema!
Usankhe Aaroni ndi ana ake aamuna kuti azitumikira pa ntchito ya unsembe. Koma wina aliyense woyandikira malo opatulika aphedwe.”
11 Hina Gode da Mousesema amane sia: i,
Yehova anawuzanso Mose kuti,
12 “Na da wali Lifai fi amo Na dunu fi ilegei dagoi. Na da Idibidi dunu ilia mano magobo huluane medole legeiba: le, Na da Isala: ili mano magobo huluanedafa amola ohe fi mano magobo huluane, amo Na hawa: hamomusa: gini ilegele momogili gagai dagoi. Be Isala: ili magobo huluane mae lale, Na da wali Lifai fi dunu huluane lalegagumu. Ilia da Na fi dunu esalumu. Bai Na da Hina Gode.
“Pakati pa Aisraeli onse ndatenga Alevi kulowa mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa kwa amayi a Chiisraeli. Alevi ndi anga,
pakuti ana onse oyamba kubadwa ndi anga. Nditakantha ana onse oyamba kubadwa mu Igupto, ndinadzipatulira ndekha mwana aliyense woyamba kubadwa mu Israeli, wa munthu ndi nyama. Azikhala anga. Ine ndine Yehova.”
14 Sainai hafoga: i soge ganodini, Hina Gode da Mousese amola Lifai dunu huluane, dunu mano amo da oubi afae lalelegele esala, amola dunu eno huluane, ilia fi amola sosogo fi defele, idili, dedema: ne sia: i.
Yehova anawuza Mose mʼchipululu cha Sinai kuti,
“Werenga Alevi monga mwa mabanja awo ndi mafuko awo. Werenga mwamuna aliyense kuyambira wa mwezi umodzi kapena kupitirirapo.”
16 Mousese da Hina Gode Ea hamoma: ne sia: i defele hamoi.
Choncho Mose anawawerenga potsatira zomwe Yehova anamulamulira.
17 Lifai da dunu mano udiana galu. Ilia dio da Gesione, Gouha: de amola Milalai. Ilia da amo dio udiana ilia fi udiana ilima asuli. Gesione da dunu mano aduna galu. Elea dio da Libini amola Simiai. Gouha: de da dunu mano biyaduyale galu. Ilia dio da A: mala: me, Isiha, Hibalone amola Asaiele. Milalai da dunu mano aduna galu. Elea dio da Malai amola Musiai. Iligaga fi da amo dunu ilia dio lai dagoi.
Mayina a ana aamuna a Levi ndi awa: Geresoni, Kohati ndi Merari.
Mayina a ana a Geresoni potsata mabanja awo ndi awa: Libini ndi Simei.
Ana a Kohati potsata mabanja awo ndi awa: Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli.
Ana a Merari potsata mabanja awo ndi awa: Mali ndi Musi. Amenewa ndiwo anali mabanja a Alevi monga mwa makolo awo.
21 Libini amola Simiai elea sosogo fi da Gesione fi hamoi galu.
Kwa Geresoni kunali banja la Alibini, banja la Asimei. Amenewa ndiwo anali mabanja a Ageresoni.
22 Amo fi dunu huluane amo da lalelegele, oubi afae baligi, ilia idi da 7,500!
Chiwerengero cha amuna onse amene anawawerenga a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 7,500.
23 Amo fi ilia fisisu sogebi da Hina Gode Ea Abula Diasu amoga guma: dini ilegei galu.
Mabanja a Ageresoni azimanga misasa yawo kumadzulo, kumbuyo kwa Chihema.
24 Ilia ouligisudafa da Ilaiasa: fe (La: iele egefe) galu.
Mtsogoleri wa mabanja a Ageresoni anali Eliyasafu mwana wa Laeli.
25 Ilia da Hina Gode Ea Abula Diasu liligi huluane ouligima: ne ilegei. Amo da ea ganodini dedebosu, ea gadili dedebosu abula amo ea logo holei dedebosu, gagoi amo Abula Diasu amola oloda sisiga: su amo ea abula liligi, amola gagoi logo holei amo ea abula dedebosu. Ilia da amo liligi hahamoma: ne, ouligisu.
Ntchito imene Ageresoni anapatsidwa ku tenti ya msonkhano inali yosamalira Chihema ndi tenti, pamodzi ndi zophimbira zake, katani ya pa khomo la ku tenti ya msonkhano,
ndi makatani wotchinga bwalo, katani ya pa chipata cholowera ku bwalo lozungulira Chihema ndi guwa lansembe, zingwe ndi zonse zokhudzana ndi ntchito yawo.
27 A: mala: me, Isiha, Hibalone amola Asaiele, amo ilia sosogo fi da Gouha: de fi hamoi.
Kwa Kohati kunali mabanja a Amramu, Aizihara, Ahebroni ndi Auzieli. Awa ndiye anali mabanja a Akohati.
28 Amo fi ilia dunu mano huluane lalelegele, oubi afae baligi, ilia idi da 8,600.
Chiwerengero cha amuna onse a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 8,600. Akohati ankagwira ntchito yosamalira malo wopatulika.
29 Amo fi ilia fisisu sogebi da Hina Gode Ea Abula Diasu gadili (south) ilegei dagoi ba: i.
Mabanja a ana a Kohati ankamanga misasa yawo kummwera kwa Chihema.
30 Ilia ouligisudafa da Elisa: ifa: ne (Asaiele egefe) galu.
Mtsogoleri wa magulu a mabanja a Kohati anali Elizafani mwana wa Uzieli.
31 Ilia da Gode Ea Gousa: su Sema Gagili, fafai, gamali bai, oloda huluane, hawa: hamosu liligi amo gobele salasu dunu da Hadigi Malei Sesei amoga hamosu amola Hadigidafa Momei Sesei logo holei ea abula, amo huluane noga: le ouligima: ne ilegei.
Iwo ankagwira ntchito yosamalira Bokosi la Chipangano, tebulo, choyikapo nyale, maguwa, zipangizo za kumalo wopatulika zimene ansembe ankagwiritsa ntchito, katani, ndi zonse zomwe ankagwiritsa ntchito.
32 Lifai fi dunu ilia bisilua da Elia: isa (Gobele salasu dunu Elane ea mano). E da dunu huluane amo da Hadigi Malei Sesei hawa: hamosu hamoma: ne ouligisu.
Mtsogoleri wamkulu wa Alevi anali Eliezara mwana wa Aaroni wansembe. Iye anasankhidwa kukhala woyangʼanira omwe ankasamalira malo wopatulika.
33 Malai amola Musiai ela sosogo fi da Milalai fi hamoi galu.
Kwa Merari kunali banja la Mali ndi banja la Musi. Amenewa ndiye anali mabanja a Amerari.
34 Amo fi dunu huluane lalelegele, oubi afae baligili, ilia idi da 6,200.
Chiwerengero cha amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 6,200.
35 Amo fi ilia fisisu sogebi da Hina Gode Ea Abula diasuga ga (north) agoane, ilegei dagoi ba: i. Ilia ouligisudafa da Siuliele (A: biha: ile egefe) galu.
Mtsogoleri wa magulu a mabanja a Amerari anali Zuriyeli mwana wa Abihaili. Iwo ankamanga misasa yawo kumpoto kwa Chihema.
36 Mousese da amo fi dunu ilia Abula Diasu amo gagui liligi, golasu ifa, fa: i liligi amola disisili hahamomusa: liligi huluane amo ouligima: ne ilegei.
Amerari anapatsidwa ntchito yosamalira mitengo ya chihema, nsichi zake, mizati yake, matsinde ake, ndi zida zake zonse, ndi zonse zomwe ankagwiritsa ntchito,
37 Amola ilia hawa: hamosu da gadili gagoi ea golasu ifa, amo ea bai, duni bugisu amola efe huluane ouligima: ne sia: i.
pamodzi ndi mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema ndi zingwe zake.
38 Mousese, Elane amola egefelali ilia fisisu da Hina Gode Ea Abula Diasu midadi, eso mabe gusudili ilegei. Ilisu da Isala: ili dunu fidima: ne, Hadigi Malei Sesei amo ganodini hawa: hamonanu. Be dunu eno da amo hawa: hamomusa: dawa: i ganiaba, ilia amo dunu medole legemusa: ilegei.
Mose ndi Aaroni ndi ana ake aamuna ankamanga misasa yawo kummawa kwa chihema, kuyangʼana kotulukira dzuwa, kutsogolo kwa tenti ya msonkhano. Anali ndi ntchito yosamalira malo wopatulika mʼmalo mwa Aisraeli. Aliyense woyandikira malo wopatulika ankayenera kuphedwa.
39 Hina Gode da ema sia: beba: le, Mousese da dunu huluane amo da lalelegele, oubi afae baligiba: le, ilia dunu momogi defele idili gagale dedei. Ilia idi huluane da 22,000.
Alevi onse amene Mose ndi Aaroni anawawerenga potsatira lamulo la Yehova monga mwa magulu a mabanja awo, amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo anali 22,000.
40 Hina Gode da Mousesema amane sia: i, “Isala: ili dunu ilia mano magobo huluanedafa da Na: Amaiba: le, Isala: ili magobo dunu mano amo da oubi afae baligi, amo dedema. Be amo mae lale, Na da Lifai fi huluane amo lamu. Na da Hina Gode! Amola Isala: ili ohe fi mano magobo huluane mae lale, Na da Lifai fi dunu ilia ohe huluanedafa lamu.”
Yehova anawuza Mose kuti, “Werenga ana onse aamuna oyamba kubadwa mu Israeli, omwe ali ndi mwezi umodzi kapena kupitirirapo ndipo ulembe mndandanda wa mayina awo.
Unditengere Alevi onse mʼmalo mwa ana oyamba kubadwa onse a Aisraeli, ndiponso ziweto zazimuna za Alevi mʼmalo mwa ziweto zonse zazimuna zoyamba kubadwa za Aisraeli. Ine ndine Yehova.”
42 Mousese da Hina Gode Ea sia: nababeba: le, Isala: ili dunu ilia mano magobo huluane amo da lalelegele, oubi afae baligi galea, ilia dio huluane dedei. Ilia idi huluane da 22,273 agoane ba: i.
Choncho Mose anawerenga ana aamuna onse oyamba kubadwa a Aisraeli monga momwe Yehova anamulamulira.
Chiwerengero chonse cha ana aamuna oyamba kubadwa kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 22, 273.
44 Hina Gode da Mousesema amane sia: i,
Ndipo Yehova anawuzanso Mose kuti,
45 “Wali, Isala: ili magobo dunu mano huluane ilia sogebi lama: ne, Lifai fi dunu huluane ilegele, Nama ima. Amola Isala: ili dunu ilia ohe fofoi mano magobo ilia sogebi lama: ne, Lifai fi dunu ilia ohe fofoi mano magobo huluanedafa ilegele, Nama ima.
“Tenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna oyamba kubadwa onse a Aisraeli, ndiponso zoweta zonse za Alevi mʼmalo mwa zoweta za Aisraeli. Alevi ndi anga. Ine ndine Yehova.
46 Be Isala: ili dunu ilia dunu mano magobo ilia idi da Lifai fi dunu huluane ilia idi273agoane baligisa. Amaiba: le, di amo 273 dunu bu bidi lama.
Pofuna kuwombola ana aamuna 273 oyamba kubadwa a Aisraeli amene anaposa chiwerengero cha aamuna a fuko la Levi,
47 Bidi lasu ilegesu amo defele Isala: ili ilia dunu mano magobo amo silifa biyale gala amoga bu bidi lama.
utenge masekeli asanu pa munthu aliyense. Masekeliwo akhale ofanana ndi masekeli a ku malo wopatulika, kumene sekeli imodzi imakwanira magera makumi awiri.
48 Amo muni lale amo Elane amola egefelali ilima ima: mu.”
Ndalama zimenezi uzipereke kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kuti ukhale mtengo woombolera Aisraeli woonjezerawo.”
49 Mousese da Hina Gode Ea hamoma: ne sia: i defele hamoi dagoi.
Choncho Mose anatenga ndalama zowombolera zija kuchokera kwa Aisraeli amene chiwerengero chawo chinaposa chiwerengero cha omwe anawomboledwa ndi Alevi.
50 E da silifa fage 1,365 amo lale, Elane amola egefelali ilima i.
Anatenga masekeli a siliva okwana 1,365 molingana ndi masekeli a ku malo opatulika, kuchokera kwa ana aamuna oyamba kubadwa a Aisraeli.
Mose anapereka ndalama zowombolera zija kwa Aaroni ndi ana ake aamuna monga mwa mawu amene Yehova analamulira.