< Idisu 10 >

1 Hina Gode da Mousesema amane sia: i,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “Silifa dabagala: le dalabede aduna hahamoma. Amoga, Isala: ili dunu gilisima: ne amola fisisu muguluma: ne eso olelema.
“Sula malipenga awiri a siliva, ndipo uziwagwiritsa ntchito posonkhanitsa anthu pamodzi ndiponso powasamutsa mʼmisasa.
3 Dalabede aduna dusia, ela ga: da badilia lalaba ahoasea, amo da Isala: ili dunu huluanedafa da dima, Na Abula Diasu logo holeiga gilisima: ne, dawa: digima: ne dusa.
Pamene akuliza malipenga onse awiri, anthu onse asonkhane kwa iwe pa khomo la tenti ya msonkhano.
4 Be dalabede afae fawane dusia, fi ouligisu dunu fawane da gilisima: ne galebeya dawa: ma.
Akaliza limodzi lokha, atsogoleri, akulu a mafuko a Aisraeli, asonkhane kwa iwe.
5 Dalabede aduna da dunumugini dusia, fi amo da fisisu eso mabe la: ididili esala da gadili masa: ne sia: ma.
Akaliza lipenga lochenjeza, misasa yomwe ili kummawa iyambe kusamuka.
6 Be dalabede da dunumugini aduna agoane dusia, fi amo da ga (south) la: idili esala da gadili masa: ne sia: ma. Amaiba: le, dilia da dalabede da dunumuni agoane dusu nabasea, fisisu mugulumusa: momagema: ma.
Akaliza lipenga lochenjeza lachiwiri, misasa yakummwera iyambe kusamuka. Kuliza kwa lipenga lochenjeza kudzakhala chizindikiro choyamba ulendo.
7 Be dilia Isala: ili dunu huluane gilisimusa: dawa: sea, sedagiliwane dalabede fulaboma: ma.
Pofuna kusonkhanitsa anthu, muziliza malipenga, koma mosiyana ndi mmene malipenga ochenjeza amalizidwira.
8 Gobele salasu dunu (Elane ea mano) da dalabede fulaboma: ne sia: ma. Eso huluane, mae fisili, amo hamoma: ne sia: i noga: le ouligima.
“Ana a Aaroni, ansembe aja, ndiwo aziliza malipengawo. Zimenezi zikhale zokhazikika kwa inu ndi ku mibado yanu yonse.
9 Dilia soge ganodini, gegesu ba: beba: le, ha lai dunu da dilima doagala: sea, dilia gegemusa: gini, dalabede duma. Na, dilia Hina Gode, da dili fidimu amola dilia ha lai dunu dili mae hasalima: ne gaga: mu.
Pamene mukupita ku nkhondo mʼdziko lanu lomwe, kulimbana ndi mdani amene akukuzunzani, muziliza malipenga ochenjeza ndipo Yehova Mulungu wanu adzakukumbukirani ndi kukulanditsani mʼmanja mwa adani anu.
10 Amola dilia hahawane eso amoga dilia Oubi Gaheabolo Lolo Nasu amola Hina Godema dawa: ma: ne Lolo Nasu eno amoga, dilia Wadela: i Hou Dabe Ima: ne Iasu amola Hahawane Gilisili Olofole Iasu hahamosea, dalabede fulaboma. Amasea, Na da dili fidimu. Bai Na da dilia Hina Gode.”
Komanso pa nthawi yanu ya chisangalalo, pa maphwando anu oyikika ndi maphwando a mwezi watsopano, muziliza malipenga pa nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zanu za chiyanjano, ndipo zidzakhala chikumbutso chanu pamaso pa Mulungu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.”
11 Eso 20 amola oubi ageyadu amola ode ageyadu ganodini, Hina Gode da mumobi ganumu Ea Abula Diasu gadodili dialu amo gaguia gadole asi.
Pa chaka chachiwiri, mwezi wachiwiri, tsiku la 20, mtambo unachoka pamwamba pa chihema cha umboni.
12 Isala: ili fi dunu da Sainai hafoga: i soge amo fisili asi. Mumobi ganumu da ahoanu, Ba: ila: ne hafoga: i sogega oulelu.
Ndipo Aisraeli ananyamuka kuchoka mʼchipululu cha Sinai ndipo anayenda malo osiyanasiyana mpaka pamene mtambo unayima mʼchipululu cha Parani.
13 Amaiba: le, ilia da Hina Gode Ea Mousesema hamoma: ne sia: i defele, degabo agoane asi.
Kameneka kanali koyamba kuti Aisraeli anyamuke monga momwe Yehova analamulira Mose.
14 Amola eso huluane ahoabeba: le, ilia da hou ilegei defele ahoasu. Dunu fi amo da Yuda fi ilima gilisi da eso gosagisu fa: no, fi eno fi eno ahoasu. Na: iasione (Aminida: be ea egefe) da amo gilisisu ouligisu.
Magulu a msasa wa Yuda ndiwo anayamba kunyamuka potsata mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu lawo anali Naasoni mwana wa Aminadabu.
15 Nida: niele (Sua ea egefe) da Isaga fi amo ouligisu.
Mtsogoleri wa gulu la fuko la Isakara anali Netanieli mwana wa Zuwara,
16 Ilia: be (Hilone ea mano) da Sebiulane fi amo ouligisu.
Eliabu mwana wa Heloni ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Zebuloni.
17 Amalalu, ilia da Gode Ea Abula Diasu mugululi, Gesione amola Milalai fi dunu da amo gaguli ahoasu.
Kenaka anagwetsa chihema, ndipo Ageresoni ndi Amerari amene ananyamula chihemacho, ananyamuka.
18 Amalalu, fi amo da Liubene fi ilima fa: no bobogesu, ilia da gilisisu eno eno agoane ahoasu. Elaise (Siediua egefe) da ili ouligisu.
Kenaka magulu a msasa wa fuko la Rubeni ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Elizuri mwana wa Sedeuri.
19 Sieliumiele (Siulisia: dai egefe) da Simione fi amo ouligisu.
Mtsogoleri wa fuko la Simeoni anali Selumieli mwana wa Zurisadai,
20 Ilaiasa: fe (Diuele egefe) da Ga: de fi ouligisu.
ndipo Eliyasafu mwana wa Deuweli ndiye ankatsogolera fuko la Gadi.
21 Amalalu, Lifai fi amo Gouha: de da sema liligi gaguli ahoasu. Ilia da asili, fisisu sogebi eno amoga doaga: loba, Gode Ea Abula Diasu bu hiougili dagoi ba: su.
Kenaka Akohati ananyamuka atanyamula zinthu zopatulika. Chihema chinkayenera kuyimikidwa iwo asanafike.
22 Lifai fi da asi dagoi ba: loba, fi gilisisu amo da Ifala: ime fi da ouligisu da logoga ahoanebe ba: su. Ilia ouligisu dunu da Ilisiama (Amihade egefe) ba: i.
Magulu a msasa wa Aefereimu anatsatira potsatira mbendera yawo. Elisama mwana wa Amihudi ndiye anali mtsogoleri wawo.
23 Amo gilisisu ganodini, Gama: iliele (Bedase egefe) da Ma: na: se fi amo ouligisu.
Gamalieli mwana wa Pedazuri ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Manase.
24 Amola Abaida: ne (Gidioni egefe) da Bediamini fi amo ouligisu.
Abidani mwana wa Gideoni ndiye anali mtsogoleri wa mtundu wa Benjamini.
25 Fa: nodafa, fi amo da Da: ne fi gilisili fi da ilia eso gosa: gisu fa: no bobogele ahoasu. Ilia da fi huluane ilia fa: no sosodo ouligisu dunu agoane ba: i. Amo gilisisu ilia ouligisu dunu da Ahaisa (Amisia: dai egefe).
Pambuyo pa magulu onse panali magulu a msasa wa Dani, omwe ankateteza magulu onsewa ndipo ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
26 Ba: idiele (Ogela: ne egefe) da A: sie fi amo ouligisu.
Pagieli mwana wa Okirani ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Aseri,
27 Amola Ahaila (Ina: ne egefe) da Na: fadalai fi amo ouligisu.
ndipo mtsogoleri wa mtundu wa Nafutali anali Ahira mwana wa Enani.
28 Isala: ili dunu da ilia fisisu yolesili, logoga ahoanoba, agoane fi eno fi eno agoane mogodigili ahoasu.
Umenewu ndiwo unali mndandanda wa kayendedwe ka magulu a Aisraeli pamene ankanyamuka ulendo wawo mʼmagulumagulu.
29 Mousese da ea bae amo Houba: be (Midiane dunu Yedelou egefe) ema amane sia: i, “Ninia da soge amo Hina Gode da ninima imunusa: ilegei, amoga doaga: musa: masunu. E da Isala: ili dunu hahawane bagade gaguiwane esalumusa: ilegele sia: i. Amaiba: le, di ani masunu. Ninia da di amola gilisili hahawane bagade gaguiwane hou ba: mu.”
Ndipo Mose anawuza Hobabu mwana wa Reueli Mmidiyani, mpongozi wa Mose kuti, “Tikunyamuka kupita ku malo amene Yehova anati, ‘Ndidzakupatsani.’ Tiye upite nafe ndipo tidzakusamalira bwino, pakuti Yehova analonjeza zinthu zabwino kwa Israeli.”
30 Be Houba: be da bu adole i, “Hame mabu! Na da ni sogega buhagimu.”
Hobabu anayankha kuti, “Ayi, sindipita nanu, ndibwerera ku dziko la kwathu ndi kwa abale anga.”
31 Be Mousese da ema ha: giwane edegei, “Dia nini mae yolesima! Di da hafoga: i soge ganodini nini hahawane fima: ne, sogebi huluane dawa: Dia ninima logo olelema: ne misa. Hina Gode da ninima hahawane bagade imunusa: sia: i.
Ndipo Mose anati, “Pepa usatisiye popeza ukudziwa kumene tingamange misasa mʼchipululu muno ndipo udzakhala maso athu.
32 Di amola ninia gilisili ahoasea, ninia da gilisili Gode Ea hahawane dogolegele iabe hou amo ba: mu.”
Iweyo ukapita nafe, tidzagawana nawe zinthu zabwino zomwe Yehova adzatipatsa.”
33 Isala: ili dunu da hadigi goumi Sainai amo fisili asili, eso udiana agoane logoga asi. Hina Gode Ea Gousa: su Sema Gagili ilima fisisu sogebi hogomusa: , bisili ahoanebe ba: su.
Motero ananyamuka ku Phiri la Yehova nayenda ulendo wa masiku atatu. Bokosi la Chipangano cha Yehova linkayenda patsogolo pawo pa masiku atatuwo kuti apeze malo woti apumulepo.
34 Hou da eso huluane agoane ba: i. Ilia da fisisu fisili ahoabeba: le, Hina Gode Ea mu mobi ganumu da esoga ili gadodili lelebe ba: i.
Mtambo wa Yehova unkawaphimba masana pamene ankasamuka pa misasa yawo.
35 Eso huluane ilia da Sema Gagili amo gaguli ahoabeba: le, Mousese da amane sia: su, ‘Hina Gode! Di wa: legadoma! Dia ha lai dunu amo afagogolisima! Dima higa: i dunu hobeama: ne, sefasima!”
Nthawi iliyonse imene Bokosi la Chipangano likunyamuka, Mose ankanena kuti, “Dzukani, Inu Yehova! Adani anu abalalike; Odana nanu athawe pamaso panu.
36 Amola Sema Gagili da oulelea, e da amane sia: su, “Hina Gode! Dia Isala: ili dunu sosogo fi osea: i, ilima buhagima!”
“Pamene likupumula, ankanena kuti, “Bwererani, Inu Yehova, ku chinamtindi cha Aisraeli.”

< Idisu 10 >