< Nihemaia 9 >

1 Amo oubiga eso 24 amo Isala: ili dunu huluane da ilia wadela: i houba: le da: i dioi olelema: ne, ha: i mae nawane gilisi. Ilia da ga fi dunu amoga afafai dagoi. Ilia da wadela: i eboboi abula idiniginisi amola ilia da: i dioi olelema: ne, osobo gulu ilia dialuma da: iya legesu. Amalalu, ilia da wa: legadole, ilia wadela: i hou amola ilia aowalali ilia wadela: i hou hamoi fofada: i.
Pa tsiku la 24 la mwezi womwewo, Aisraeli anasonkhana pamodzi ndi kusala chakudya, kuvala ziguduli ndi kudzithira dothi pa mutu.
2
Aisraeliwa anadzipatula pakati pa anthu a mitundu ina ndipo anayimirira nayamba kuwulula machimo awo ndi zolakwa za makolo awo.
3 Amo eso ilia da biyaduyale momogili, momogi afae amoga ilia da ilia Hina Gode Ea Sema idibi nabalu. Amalalu, momogi afae eno ganodini ilia da ilia wadela: i hou fofada: nanu. Amola ilia da ilia Hina Godema nodone sia: ne gadosu.
Anthuwo anayimirira pomwepo, ndipo anamva mawu a mʼbuku la malamulo a Yehova akuwerengedwa kwa maora enanso atatu ndipo anakhala maora ena atatu akuwulula machimo awo ndi kupembedza Yehova Mulungu wawo.
4 Lifai dunu amoga leloma: ne, fafai gagui dialebe ba: i. Amoga Yesua, Ba: inai, Ga: demiele, Siebanaia, Banai, Sielibaia, Houda: ia, Siebanaia, amola Bedahaia, amoga lelebe ba: i. Ilia dunu huluane nabima: ne, Hina Godema sia: ne gadosu.
Pa makwerero okhalapo alevi anayimirirapo anthu awa: Yesuwa, Bani, Kadimieli, Sebaniya, Buni, Serebiya, Bani ndi Kenani. Iwowa ankapemphera mokweza mawu kwa Yehova Mulungu wawo.
5 Amalalu, Lifai dunu da dunu huluane Godema nodoma: ne sia: i. Amo Lifai dunu ilia dio da Yesua, Ga: demiele, Ba: inai, Hasiabena: ia, Sielibaia, Houda: ia, Siebanaia amola Bedahaia. Ilia da amane sia: i, “Wa: legadole, dilia Hina Godema mae fisili, eso huluane Ema nodonanoma. Dunu huluanedafa da Ea Dio gaguia gadole, nodonanumu da defea. Be E da Hadigidafaba: le, osobo bagade dunu ilia da Ema nodosu hamomu da defele hame ba: sa.”
Ndipo Alevi awa: Yesuwa, Kadimieli, Bani, Hasabaneya, Serebiya, Hodiya, Sebaniya ndi Petahiya anati: “Imirirani ndipo mutamande Yehova Mulungu wanu, amene ndi wamuyaya.” “Litamandike dzina lake laulemerero limene liposa madalitso ndi matamando onse.
6 Amalalu, Isala: ili dunu da Godema amane sia: ne gadoi, “Hina Gode! Di fawane da Godedafa. Di fawane da mu amola gasumuni amo ganodini diala amo hahamoi. Di da osobo bagade amola hano wayabo bagade hahamoi. Di da liligi huluane amoma esalusu i dagoi. Hebene soge ganodini, gasa bagade fi da Dima beguduli, nodone sia: ne gadosa.
Inu nokha ndiye Yehova. Munalenga kumwamba, ngakhale kumwambamwamba, zolengedwa zonse zimene zili mʼmenemo. Munalenga dziko ndi zonse zokhalamo, nyanja ndi zonse zili mʼmenemo. Zonse mumazisunga ndi moyo ndipo zonse za kumwamba zimakupembedzani.
7 Di, Hina Gode, da A: ibala: me ilegei. E da ea moilai Ba: bilone soge amo ganodini esalu. Be Di da e gadili oule asili, ea dio afadenene, A:ibalaha: me dio asuli.
“Inu ndinu Yehova Mulungu amene munasankha Abramu ndi kumutulutsa mʼdziko la Uri wa ku Kaldeya ndi kumutcha dzina lake Abrahamu.
8 Dia ba: loba A: ibalaha: me da Dima dafawaneyale dawa: su dunu ba: i. Di da soge ema imunu sia: i. Amo da Ga: ina: ne dunu, Hidaide dunu, A:moulaide dunu, Belesaide dunu, Yebiusaide dunu amola Gegasiaide dunu, amo dunu ilia soge gagui huluane, A:ibalaha: me egaga fi amo ganodini esaloma: ne, ema imunu sia: i. Amola dia imunu sia: i, hamoi dagoi ba: i. Bai Di da mae fisili didili hamosa.
Inu munaona kuti mtima wake unali wokhulupirika kwa inu, ndipo munapangana naye pangano lakuti mudzapereka kwa zidzukulu zake dziko la Akanaani Ahiti, Aamori, Aperezi, Ayebusi ndi Agirigasi. Inu mwasunga lonjezo lanu chifukwa ndinu wolungama.
9 Ninia aowalali ilia se nabasu Idibidi soge ganodini, amo Di da ba: i dagoi. Amola ilia Maga: me Hano degemusa: fidima: ne wele sia: i, amo Di da nabi dagoi.
“Munaona kuzunzika kwa makolo athu ku Igupto. Munamva kufuwula kwawo pa Nyanja Yofiira.
10 Di da Idibidi hina bagade, ea fidisu dunu amola ea fi dunu, ilia Dia Isala: ili fi banenesiba: le, amo hou hedofamusa: , gasa bagade musa: hame ba: su dawa: digima: ne olelesu hou hamoi dagoi. Di da Dia fi dunu ilia dio gaguia gadoi, amola Dia Dio da wali eso, gadodafa ba: sa.
Inu munachita zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa kutsutsana ndi Farao, pamaso pa Farao, nduna zake ndi anthu onse a mʼdziko lake, pakuti Inu munadziwa kuti anazunza makolo athu. Inu munadzipangira nokha dzina, monga zilili mpaka lero lino.
11 Di da Dia fi degemusa: , hano wayabo bagade mogili, Dia dunu da hano hafoga: i logoga hahawane asi. Ili medole legemusa: fa: no bobogei dunu da hanoga na dagoi ba: i. Hano gafului amoga igi gela dasu defele, ilia da hanoga gela sa: i dagoi.
Inu munagawa nyanja anthu anu akupenya, kotero kuti anadutsa powuma, koma munamiza mʼmadzi akuya anthu amene ankawalondola monga mmene uchitira mwala mʼmadzi ozama.
12 Di da mu mobi agoai mogomogoi amoga esoga ili bisili oule asi. Amola gasi ganodini, Di da lalu sawa: amoga ilia logo hadigisu.
Masana munkawunikira ndi chipilala cha mtambo ndipo usiku munkawunikira ndi chipilala cha moto njira yonse imene ankayendamo.
13 Sainai Goumia, Di da Hebene fisili, ilima sia: musa: gudu sa: i. Di da sema noga: iwane amola olelesu noga: i, ilima i.
“Munatsika pa Phiri la Sinai, ndipo munawayankhula kuchokera kumwamba. Munawapatsa malangizo olungama, ziphunzitso zoona ndiponso malamulo abwino.
14 Di da, ilia da Dia Sa: bade eso huluane noga: le ouligima: ne, sia: i. Amola, ilima alofele ima: ne, Dia da Dia hawa: hamosu dunu Mousese ema Dia Sema i.
Inu munawadziwitsa kuti tsiku lanu la Sabata ndi loyera ndipo munawapatsa malamulo ndi ziphunzitso.
15 Ilia ha: iba: le, Dia da Hebene soge amoga ha: i manu i, amola ilia hano hanaiba: le, hano dili moma: ne, igi amoga hano dili i. Di da soge amo ilima imunu sia: i, ilia da amo lale, noga: le ouligima: ne sia: i.
Pamene anali ndi njala munawapatsa buledi wochokera kumwamba. Pamene anali ndi ludzu munawapatsa madzi otuluka mʼthanthwe. Munawawuza kuti apite kukalanda dziko limene munalonjeza kuti mudzawapatsa.”
16 Be ninia aowalali da gasa fiwane heda: le, hame nabasu hou hamosu. Ilia da Dia sia: i nabimu higasu.
“Koma makolo athu anadzikuza ndi kuwumitsa khosi, ndipo iwo sanamvere malamulo anu.
17 Ilia da hame nabasu. Ilia da Dia gasa bagade fidisu hou gogolei dagoi. Ilia gasa fi hamobeba: le, ilisu da hina dunu amo Idibidi sogega se dabe hawa: hamomusa: gini, ili bisili oule masa: ne ilegei dagoi. Be Di da gogolema: ne olofosu bagade dawa: Di da haha bagade, asigidafa amola hedolo hame ougisa. Amaiba: le, Di da ninia aowalali hame yolesi.
Anakana kumvera ndipo sanakumbukire zodabwitsa zimene munachita pakati pawo. Koma iwo anawumitsa khosi, nakuwukirani podzisankhira okha mtsogoleri kuti awatsogolere kubwerera ku ukapolo ku dziko la Igupto. Koma ndinu Mulungu wokhululukira, wokoma mtima ndi wachifundo wosapsa mtima msanga ndi wachikondi chachikulu chosasinthika. Choncho Inu simunawasiye.
18 Ilia da ogogosu ‘gode’ agoaila liligi gouliga hamoi. Ilia giadofale amo ogogosu ‘gode’ da ili bisili, Idibidi sogega fisili gadili oule asi dagoi, sia: i. Hina Gode! Ilia da Dia dio wadela: lesi dagoi.
Ngakhale pamene iwo anadziwumbira fano la mwana wangʼombe ndi kuti, ‘Uyu ndi mulungu wanu amene anakutulutsani mʼdziko la Igupto,’ kapena pamene anachita chipongwe choopsa.
19 Be Di da amo dunu wadela: i hafoga: i soge ganodini hame yolesi. Bai Dia hou da asigidafa. Di da mu mobi agoai mogomogoi amola lalu sawa: amola amo liligi hame samogei. Eso amola gasi ganodini, Di da logo ilima noga: le olelesu.
“Koma Inu ndi chifundo chanu chachikulu, simunawasiye mʼchipululu. Chipilala cha mtambo sichinasiye kuwatsogolera pa njira yawo masana ndipo chipilala cha moto sichinasiye kuwatsogolera pa njira yawo usiku.
20 Dia hahawane hou amoga, di da ilima agoane hamoma: ne adoi. Di da ilima “ma: na” ha: i manu amola hano moma: ne iasu.
Inu munawapatsa mzimu wanu wabwino kuti uwalangize. Inu simunawamane chakudya cha mana chija, ndipo munawapatsa madzi akumwa.
21 Ode 40 amoga ilia da wadela: i hafoga: i soge amo ganodini esaloba, Di da ilia hanai liligi defele fidi. Ilia abula da hamedafa abubula ahoasu, amola ilia emo da hame se nabasu amola hame fofasu.
Munawasunga zaka makumi anayi mʼchipululu ndipo sanasowe kanthu kalikonse. Zovala zawo sizinathe kapena mapazi awo kutupa.”
22 Dia da logo doasiba: le, ilia da dunu fi bagade amo hasalasi. Ilia Hesiabone soge fi (ilia hina bagade da Saihone galu) amola Ba: isia: ne soge fi (ilia hina bagade da Oge galu) amo hasasali.
“Inu munawapatsa mafumu ndi mayiko mʼmanja mwawo. Munawagawiranso mayiko achilendo akutali kwambiri. Munabwera nawo mʼdziko la Sihoni mfumu ya Hesiboni ndi dziko la Ogi mfumu ya Basani kuti alowemo nʼkulitenga kukhala lawo.
23 Di da ilima mano amo ilia idi da gasumuni mu amo ganodini aligi ilia idi defele ba: i, amo ilima i. Dia fidibiba: le, ilia da soge amo Di da ilia aowalali ilima imunu ilegele sia: i, amo ilia da hasalali, ganodini gesowale fi.
Munachulukitsa ana awo aamuna ngati nyenyezi za mlengalenga. Ndipo munawabweretsa mʼdziko limene munawuza makolo awo kuti alilowe ndi kulitenga.
24 Ilia da Ga: ina: ne soge fi ili amo hasasali. Di da ilima gasa iabeba: le, ilia da ilia hanaiga, Ga: ina: ne dunu amola ilia hina bagade amoga hamosu.
Choncho zidzukulu zawo zinapita ndi kukalandira dzikolo. Inu munagonjetsa pamaso pawo, Akanaani amene amakhala mʼdzikolo. Inde munapereka mʼmanja mwawo mafumu awo pamodzi ndi anthu a mʼdzikomo kuti achite nawo monga angafunire.
25 Hina Gode! Dia fi dunu da gasa bagade gagili sali moilai amo lai dagoi. Ilia da osobo noga: idafa, diasu amo ganodini liligi noga: idafa ba: i, hano uli dogoi, olife ifa, ha: i manu ifa amola waini sagai amo bagohame lai. Ilia da ilia hanaiga ha: i nanu, ilia da: i da bagade alele, Dia iasu liligi noga: idafa ilia da hahawane lai.
Iwo analanda mizinda yotetezedwa ndi dziko lachonde. Anatenganso nyumba zodzaza ndi zinthu zonse zabwino, zitsime zokumbidwa kale, mitengo ya mphesa, mitengo ya olivi ndi mitengo yambiri ya zipatso. Ndipo anadya nakhuta ndipo anali athanzi. Choncho ankakondwa chifukwa cha ubwino wanu wopambana.
26 Be Dia fi da sinidigili, Dia sia: hame nabasu. Ilia da Dia sema amo baligifa: su. Ilia da ilima sisasu olelesu dunu (balofede dunu) amo da ilia Dima sinidigili bu fa: no bobogema: ne sia: i, amo ilia da medole legesu. Eso bagohame amoga ilia da Dia Dio wadela: lesi.
“Komabe iwo anakhala osamvera ndipo anakuwukirani nafulatira malamulo anu. Anapha aneneri anu, amene anakawadandaulira kuti abwerere kwa Inu. Anachita chipongwe choopsa.
27 Amaiba: le, ilima ha lai da ilima hasalasima: ne, Di da logo doasi dagoi. Amogawi, ilia da se bagade nababeba: le, Dima fidima: ne wele sia: su. Dia da asigiba: le, ouligisu dunu ilima asunasi. Amo ouligisu dunu ilia da Dia fi ilima ha lai dunu ilima gaga: i dagoi.
Pamene anazunzidwa anafuwulira kwa Inu, ndipo Inu munawamvera muli kumwambako. Ndipo mwa chifundo chanu chachikulu munkawapatsa atsogoleri amene ankawapulumutsa mʼmanja mwa adani awo.”
28 Be olofosu da bu doaga: loba, ilia da bu eno wadela: le hamoi. Amalalu, Di da ilima ha lai dunu amo ilima hasalasima: ne, Di da logo bu doasi. Be ilia da bu Gode Dima sinidigiloba, Di da Hebene ganodini ilia wele sia: su nabalu, Di da bagadewane asigiba: le, eso bagohame amoga Dia fi dunu bu gaga: i.
“Koma akangokhala pa mtendere ankayambanso kuchita zoyipa pamaso panu. Choncho munkawapereka mʼmanja mwa adani awo amene ankawalamulira. Komabe pamene ankabwerera ndi kumalira kwa Inu, Inu munkawamva muli kumwambako. Chifukwa cha chifundo chanu chochuluka, nthawi zonse munkawapulumutsa.
29 Ilia da Dia olelesu amoma noga: le fa: no bobogema: ne, Di da ilima sisasu olelei. Dia sema amo da esalusu logo olelesa. Be ilia da gasa fili, Dia Sema hamedafa nabasu.
“Inu munkawachenjeza kuti abwerere ndi kuyamba kutsata malamulo anu. Koma iwo ankadzitukumula ndipo sankamvera malamulo anu. Iwo anachimwira malangizo anu amene munati ‘Amapatsa moyo kwa munthu wowamvera.’ Iwo ankakufulatirani, nawumitsa makosi awo osafuna kukumverani.
30 Ode bagohame, Di da ili sinidigima: ne gebewane sia: su, amola Dia balofede dunu ilima sia: ma: ne asunasisu. Be ilia da ge ga: i agoai galusu. Amaiba: le, Di da eno fi ilima hasalimusa: yolesi.
Munapirira nawo kwa zaka zambiri. Munkawachenjeza ndi Mzimu wanu kudzera mwa aneneri anu, koma iwo sankakumverani. Choncho munawapereka mʼmanja mwa anthu a mayiko ena.
31 Be Dia asigidafa hou da bagadedafa. Amaiba: le, Di da amo dunu hame yolesi, amola hame wadela: lesi. Di da hahawane amola Asigidafa hou ea bai esala.
Komabe mwachifundo chanu chachikulu simuwatheretu kapena kuwataya pakuti ndinu Mulungu wokoma mtima ndi wachifundo.
32 “Gode! Ninia Gode! Di da gasa bagadedafa! Dia gasa bagade hou ba: beba: le, dunu huluane da Diba: le beda: be. Di da mae fisili, Dia Gousa: su hou defele hamonana. Asilia hina bagade da ninima hasalasili, amo ganini waha, amo eso huluane amoga ninia da se bagade nabasu. Ninia ouligisu hina dunu, ouligisu dunu, gobele salasu dunu, balofede dunu amola dunu huluane da se nabawane hahanisu. Amo Di mae gogolema.
“Nʼchifukwa chake, tsono, Inu Mulungu wathu, Mulungu wamkulu, wamphamvu ndi woopsa kwambiri mumasunga pangano ndi chikondi chosasinthika. Musalole kuti mavuto onse amene atigwera ife, mafumu athu, atsogoleri athu, ansembe athu, aneneri athu, makolo athu ndi anthu ena onse kuyambira nthawi ya mafumu a ku Asiriya mpaka lero aoneke ochepa pamaso panu.
33 Di da ninima se dabe iasu da moloidafa. Ninia da wadela: i hou bagade hamosu. Be Dia moloidafa hou, Di da hame yolesi.
Koma Inu mwakhala wolungama pa zonse zimene zakhala zikutichitikira. Mwachita zokhulupirika, koma ife tachita zolakwa.
34 Ninia aowalali, hina bagade, fi ouligisu dunu amola gobele salasu dunu, amo da Dia sema amoma hame fa: no bobogesu. Ilia da Dia hamoma: ne sia: i amola Dia sisasu hamedafa nabasu.
Ndipotu mafumu athu, atsogoleri athu, ansembe athu ndi makolo athu sanatsatire mawu anu. Iwo sanalabadire za malamulo anu ngakhale mawu anu owachenjeza amene munawapatsa.
35 Dia da hahawane fidibiba: le, Di da Dia fi dunuma soge bagade noga: idafa ilima i. Amola ilia da amo ganodini hahawane esalu. Amola, hina bagade da ili ouligisu. Be ilia da wadela: i hou fisili, Dima hawa: hamomu, amo hame hamosu.
Ngakhale ankadzilamulira okha, nʼkumalandira zabwino zochuluka mʼdziko lalikulu ndi lachonde limene munawapatsa, koma iwo sanakutumikireni kapena kusiya ntchito zawo zoyipa.
36 Amaiba: le, ninia da wali udigili se dabe hawa: hamosu dunu agoai, soge Di da musa: ninima i, amola amoga ninia ha: i manu faisa, amo soge ganodini esala.
“Tsono, taonani! Ife lero ndife akapolo, ndife akapolo mʼdziko limene munapereka kwa makolo athu kuti azidya zipatso zake ndi zabwino zake zonse.
37 Ninia da wadela: le hamoiba: le, eno fi hina bagade da nini ouligima: ne, Di da logo doasi. Wali ninia soge ganodini ha: i manu heda: le legeiya, huluane da ilima fawane iaha. Amola amo hina bagade da ilia hanaiga ninima amola ninia ohe ilima hamosa. Ninia da se bagade naba.”
Tsono chifukwa cha machimo athu, mafumu amene munawayika kuti azitilamulira angodzilemeretsa ndi chuma chambiri cha dzikoli. Iwo ali ndi mphamvu zolamulira matupi athu ndi ngʼombe zathu momwe afunira. Zedi, ife tili mʼmavuto aakulu.”
38 “Amo hou huluane da doaga: beba: le, ninia, Isala: ili dunu huluane, da amo sia: dedei hahamosa. Ninia ouligisu dunu, Lifai dunu amola gobele salasu dunu, amo da ilia dio dedene, amo sia: gobele salasu legei amoga ilegesa.”
“Chifukwa cha zonsezi, ife tikuchita mgwirizano wokhazikika, pochita kulemba, ndipo atsogoleri athu, Alevi athu ndi ansembe athu asindikiza chidindo chawo pa mgwirizanowo.”

< Nihemaia 9 >