< Nihemaia 2 >

1 Oubi biyadu uduli, eso afaega hina bagade Adasegesisi da ea diasuga ha: i naha esaloba, na da waini ema gaguli misini iasu. Na da da: i dioiwane esalebe ba: i. Be e da musa: na hou amo ganodini fofagi hame ba: i.
Pa mwezi wa Nisani, mʼchaka cha makumi awiri cha ufumu wa Aritasasita, atabwera ndi vinyo pamaso pa mfumu ine ndinatenga vinyoyo ndi kupereka kwa mfumu. Koma ndinali ndisanakhalepo ndi nkhope yachisoni pamaso pake.
2 Amaiba: le, e da nama amane adole ba: i, “Di da abuliba: le da: i dioiwane ba: sala: ? Di da oloi hame. Amaiba: le di da hahawane hame ganabela: ?” Na da ea sia: nababeba: le, fofogadigi.
Tsono mfumu inandifunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani nkhope yako ikuoneka yachisoni pamene iwe sukudwala? Ichi si chinthu china koma chisoni cha mu mtima.” Ine ndinachita mantha kwambiri.
3 Na da ema bu adole i, “Hina bagade! Di eso huluane esalalalumu da defea. Moilai bai bagade amo ganodini na aowalali da bogole uli dogoi, amo da mugululi, wadela: lesi dagoi diala amola ea logo ga: su da laluga nei dagoi. Amaiba: le, na da da: i dioi.”
Ndinawuza mfumu kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wamuyaya! Kodi nkhope yanga ilekerenji kuoneka yachisoni pamene mzinda umene kuli manda a makolo anga, wasanduka bwinja ndipo zipata zake zinawonongedwa ndi moto?”
4 Hina bagade da bu adole ba: i, “Di da adi hanai ganabela: ?” Na da Gode Hebene ganodini esala Ema sia: ne gadole,
Apo mfumu inandifunsa kuti, “Tsono ukufuna kundipempha chiyani?” Ndipo ine ndinapemphera kwa Mulungu Wakumwamba.
5 ema amane sia: i, “Di da na hahawane ba: sea amola na edegesu amo nama imunusa: dawa: sea, defea, na da Yuda soge ganodini moilaiga na aowalali da uli dogoi, amoga amo moilai mugului bu gagumusa: masa: ne, na logo doasima.”
Ndipo ndinayankha kuti, “Ngati amfumu chingakukondweretseni, ngati mungakomere mtima mtumiki wanune, mundilole kuti ndipite ku Yuda, ku mzinda kumene kuli manda a makolo anga kuti ndikawumangenso.”
6 Hina bagade ea uda da e dafulili esalebe ba: i. Adasegesisi da na edegei amo hahawane nabi. E da nama amane adole ba: i, “Di da habowali asili esaloma: bela: ? Amola habogala buhagima: bela: ?” Na da na hou hamomu ema adole i.
Tsono mfumu, mfumukazi itakhala pambali pake, anandifunsa kuti, “Kodi kumeneko ukakhalako masiku angati ndipo udzabwera liti?” Ndinayiwuza mfumu nthawi yake ndipo inandilola kuti ndipite.
7 Amalalu, na da ema eno adole ba: i amo, e da Iufala: idisi Guma: dini Soge eagene ouligisu dunu ilima meloa dedene nama imunusa: edegei. Amo meloa ganodini, e da amo dunuma, na da Yuda sogega masa: ne logo doasima: ne e da sia: mu, na edegei.
Ndipo ndinatinso kwa mfumu, “Ngati zikondweretse mfumu, mundipatse makalata oti ndikapereke kwa abwanamkubwa a ku chigawo cha Patsidya pa Yufurate, kuti akandilole kudutsa mwamtendere mpaka nditakafika ku Yuda.
8 Na meloa dedei eno edegei. Amo da hina bagade ea ifa iwila ouligisu dunu A: isa: fema dedene ima: ne, na edegei. Amo meloa ganodini, e da A: isa: fe amoma e da ifa amo da logo ga: su gagoi dobea amo da Debolo diasu sisiga: sa, moilai bai bagade gagoi dobea amola diasu amo ganodini na da esalumu amo huluane gaguma: ne, e da amo nama ima: ne A: isa: fema adoma: ne, na da edegei. Gode da na noga: le fidibiba: le, na edegei huluane, hina bagade da nama i dagoi.
Mundipatsenso kalata yokapereka kwa Asafu woyangʼanira nkhalango ya mfumu, kuti akandipatse mitengo yokapangira mitanda ya zipata za nsanja yoteteza Nyumba ya Mulungu, mitanda ya khoma la mzinda ndi ya nyumba yokhalamo ine.” Mfumu indipatse zomwe ndinapempha popeza Yehova wokoma mtima anali nane.
9 Adasegesisi da dadi gagui ouligisu dunu amola dadi gagui dunu gilisisu hosi amoga fila heda: i dunu, amo na fidila asunasi. Na da asili, Iufala: idisi Guma: dini Sogega doaga: i. Amalalu, na da hina bagade ea meloa dedei amo eagene ouligisu dunuma i.
Choncho ndinanyamuka ulendo wanga ndipo ndinafika kwa abwanamkubwa a chigawo cha Patsidya pa Yufurate ndipo ndinawapatsa makalata a mfumu. Mfumu nʼkuti itatumiza akulu ankhondo ndi okwera pa akavalo kuti atsagane nane.
10 Be eagene dunu ea dio amo Sa: naba: la: de (e da moilai Bede Houlone amoga esalu) amola Doubaia (A: mone soge eagene ouligisu dunu) ela da dunu da Isala: ili dunu fidimusa: misi, amo sia: nababeba: le, mi hanai galu.
Sanibalati wa ku Horoni ndi Tobiya wa ku Amoni atamva zimenezi, iwo anayipidwa kwambiri kuti wina wabwera kudzachitira zabwino Aisraeli.
11 Na da baligili asili, Yelusalemega doaga: i. Eso udiana ouesalu,
Ndinafika ku Yerusalemu, ndipo ndinakhala kumeneko masiku atatu.
12 Gode da nama Yelusaleme moilai amo fidima: ne sia: i, amo na dunu enoma hame adoi. Be gasimogoa, na da wa: legadole amola na fidisu dunu mogili oule asili, soge abodemusa: asi. Ohe afae amo dougi amoga na fila heda: i, ninia da amo fawane oule asi.
Sindinawuze munthu aliyense za zimene Yehova anayika mu mtima mwanga kuti ndichitire mzinda wa Yerusalemu. Choncho ndinanyamuka usiku pamodzi ndi anthu ena owerengeka. Ndinalibe bulu wina aliyense kupatula amene ndinakwerapo.
13 Be amo gasi da mae hagili dialobawane, na da moilai fisili, gagoi dobea logo ga: su amo ea dio da Fago Ga: su amoga guma: dini golili, gadili asili, Da: la: gone Hano bubuga: su amo baligili, Isu Salasu Logo Ga: su amoga doaga: i. Na da ahoana ba: loba, moilai gagoi dobea amo mugului amola logo ga: su laluga nei dagoi ba: i.
Ndinatuluka usiku podzera ku Chipata cha ku Chigwa ndi kuyenda kupita ku Chitsime cha Chirombo Chamʼmadzi mpaka ku Chipata cha Zinyalala. Ndinayangʼana makoma a Yerusalemu, amene anagwetsedwa, ndi zipata zake, zimene zinawonongedwa ndi moto.
14 Amalalu, moilai ea eso mabe la: ididili, na da ganogoe (north) asili, Hano Bubuga: su Logo Ga: su amoga asili, hina bagade Wayabo amoga doaga: i. Be isu bagade dialebeba: le, dougi amoga na fila heda: i, da logo hame ba: beba: le, masunu gogolei.
Kenaka ndinapita ku Chipata cha Kasupe ndi ku Dziwe la Mfumu. Koma panalibe malo okwanira akuti bulu wanga adutse.
15 Amaiba: le, na da Gidalone Fago amoga asili, gagoi dobea amo boba: la asi. Amalalu, na da buhagili, na musa: asi logoga amodili asili, Fago Logo Ga: su amoga moilaiga golili sa: i.
Kotero usikuwo ndinapita ku chigwa, ndikuyangʼana khomalo. Pomaliza ndinabwerera ndi kukalowanso mu mzinda kudzera ku Chipata cha ku Chigwa.
16 Yelusaleme eagene dunu amo ilia da na da habi asi, amola adi hamonana, ilia hame dawa: i. Amola na da na na: iyado Yu dunu, gobele salasu dunu amola hina dunu eno dunu ilia fa: no hawa: hamoma: ne amoma hame adosu.
Akuluakulu sanadziwe kumene ndinapita kapena zimene ndimachita, chifukwa pa nthawiyi nʼkuti ndisananene kalikonse kwa Ayuda kapena ansembe, anthu olemekezeka kapena akuluakulu, kapena wina aliyense amene anali woyenera kugwira ntchitoyi.
17 Be wali na da ilima amane sia: i, “Yelusaleme moilai da mugului dagoiba: le, amola ea logo ga: su da wadela: lesi dagoiba: le, ninia se bagade naba. Ninia da amo gogosiasu fisili, gagoi dobea mugului bu gagomu da defea.”
Ndinawawuza kuti, “Inu mukuona mavuto amene tili nawo. Mukuona kuti mzinda wa Yerusalemu wasanduka bwinja ndipo zipata zake zatenthedwa ndi moto. Tsono tiyeni timangenso makoma a Yerusalemu ndipo sitidzachitanso manyazi.”
18 Amola Gode da na noga: le fidi amola hina bagade da nama asigiba: le fidi, nama na hanaiga hamoma: ne sia: i, amo amola na da ilima olelei. Amo sia: nababeba: le, ilia da amane nodone sia: i, “Ninia da bu buga: le muni hawa: hamola: di!” Amola ilia amo hawa: hamomusa: , liligi momagele ouesalu.
Ndinawawuza za mmene Yehova Mulungu wanga anandichitira zabwino ndiponso mawu amene mfumu inandiwuza. Tsono anati, “Tiyeni tiyambenso kumanga.” Kotero analimbitsana mtima kuti ayambenso ntchito yabwinoyi.
19 Be Sa: naba: la: de, Doubaia amola A: la: be dunu ea dio amo Giseme ilia da ninia hawa: hamomusa: sia: sa: i nabaloba, ilia da niniba: le oufesega: lu, amane sia: i, “Dia hamobe go da adi dawa: bela: ? Di da eagene hina bagade ea sia: mae nabawane, ema odoga: sala: ?”
Koma Sanibalati wa ku Horoni, Tobiya wa ku Amoni ndi Gesemu Mwarabu atamva zimenezi, anatiseka ndi kutinyoza. Iwo anafunsa kuti, “Kodi muti ndi chiyani chimene mukuchitachi? Kodi mufuna kuwukira mfumu?”
20 Be na da bu adole i, “Hebene Gode da ninima gasa defele imunu. Ninia da Ea hawa: hamosu dunu. Amaiba: le, ninia da amo hawa: hamosu muni hamomu. Be Yelusaleme moilai amo ganodini, soge da dilima hame ilegei. Amola Isala: ili dunu ilia hou dilia hame dawa:”
Koma ndinawayankha kuti, “Mulungu Wakumwamba atithandiza kuti zinthu zitiyendere bwino. Ife antchito ake tiyambapo kumanga. Koma inu mulibe gawo lanu muno mu Yerusalemu. Mulibe chokuyenerezani kulandira malo ano. Mulibenso chilichonse muno chokumbutsa za inu.”

< Nihemaia 2 >