< Aisaia 35 >

1 Hafoga: i soge da hahawane ba: mu. Ifa lubi da falegale, wadela: i soge ganodini alemu.
Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala; dziko lowuma lidzakondwa ndi kuchita maluwa.
2 Fedege agoane, hafoga: i soge da hahawaneba: le, gesami hea: mu amola wele sia: mu. Hafoga: i soge da ida: iwane Lebanone Goumi defele ba: mu, amola amo soge ea nasegagi da Gamele amola Sia: lane ifabi ela nasegagi defele ba: mu. Dunu huluanedafa da Hina Gode Ea gasa bagade hou amola Ea baligili Hadigi ba: mu.
Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe. Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni, maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni. Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova, ukulu wa Mulungu wathu.
3 Dilia! Nowa ea lobo da helebe, amola nowa da gasa hameba: le ea emo muguni da yagugusa, amoma gasa ima.
Limbitsani manja ofowoka, limbitsani mawondo agwedegwede;
4 Nowa da da: i dioi galea, ilima amane sia: ma, “Gasa lama! Mae beda: ma! Gode da dili gaga: musa: , amola dilia ha lai ilima se imunusa: misunu.”
nenani kwa a mitima yamantha kuti; “Limbani mtima, musachite mantha; Mulungu wanu akubwera, akubwera kudzalipsira; ndi kudzabwezera chilango adani anu; akubwera kudzakupulumutsani.”
5 Si dofoi dunu da bu ba: mu. Ge ga: i dunu da bu nabimu.
Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.
6 Emo gasuga: igi dunu da soagala: le gosa: mu. Amola sia: hamedei dunu da hahawaneba: le, wele sia: mu. Hafoga: i sogega, hano noga: i ahoanebe ba: mu.
Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala, ndipo osayankhula adzayimba mokondwera. Akasupe adzatumphuka mʼchipululu ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,
7 Hafoga: i soge amo ganodini, sa: iboso soge da afadenene, hano wayabo agoane hamomu. Amola hafoga: i sogebi amo ganodini, gu hano bagohame ba: mu. Sogebi amo ganodini sigua wa: me da esalu, amoga fafugisi amola saga: ba: mu.
mchenga wotentha udzasanduka dziwe, nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe. Pamene panali mbuto ya ankhandwe padzamera udzu ndi bango.
8 Amo soge ganodini, logo ea dio amo “Hadigi Logo” dialebe ba: mu. Amoga ahoanebe, dilia da wadela: i hamosu dunu hame ba: mu. Amola gagaoui dunu da amoga ahoabe dunu ilima ogogomu hamedei agoane ba: mu.
Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu; ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika. Anthu odetsedwa sadzayendamo mʼmenemo; zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.
9 Laione wa: me amogai esalebe hame ba: mu, amola nimi bagade ohe fi hame ba: mu. Be nowa dunu amo Hina Gode da gaga: i dagoi, amo dunu da ilia diasudafa amoga doaga: ma: ne, amo logoga ahoanebe ba: mu.
Kumeneko sikudzakhala mkango, ngakhale nyama yolusa sidzafikako; sidzapezeka konse kumeneko. Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.
10 Ilia hahawaneba: le, gesami hea: lala amola wele sia: nana, Yelusalemega doaga: mu. Ilia da da: i dioi amola se nabasu bu hame ba: mu. Be ilia da eso huluane hahawane fifi ahoanumu.
Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera. Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba; kumeneko adzakondwa mpaka muyaya. Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe, ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.

< Aisaia 35 >