< Aisaia 31 >

1 Dunu da Idibidi sogega fidisu lama: ne ahoana, da wadela: lesi dagoi ba: mu. Ilia da Idibidi dadi gagui gilisisu bagade, hosi, sa: liode amola dadi gagui dunu, amo ili gaga: musa: dawa: lala. Be Hina Gode, Isala: ili ilia hadigi Gode, amo E da ili gaga: musa: ilia hame dawa: , amola E da ili fidima: ne Ema hame adole ba: sa.
Tsoka kwa amene amapita ku Igupto kukapempha chithandizo, amene amadalira akavalo, nakhulupirira kuchuluka kwa magaleta awo ankhondo ndiponso mphamvu za asilikali awo okwera pa akavalo, koma sakhulupirira Woyerayo wa Israeli, kapena kupempha chithandizo kwa Yehova.
2 Hina Gode E da Hi hou dawa: E da wadela: lesisu iaha. E da wadela: i hamosu dunu amola ilia gaga: su dunu ilima se imunusa: sia: beba: le, E da se imunu.
Komatu Yehovayo ndi wanzeru ndipo angathe kuwononga, ndipo sasintha chimene wanena. Adzalimbana ndi anthu ochita zoyipa, komanso ndi amene amathandiza anthu ochita zoyipa.
3 Idibidi dunu da Gode hame. Ilia da osobo bagade dunu fawane. Ilia hosi da hu liligi fawane, a:silibu hame. Hina Gode da hawa: hamosea, gasa bagade fi amola gasa hame fi amo ilia fidilala, amo da gilisili dafane, wadela: lesi dagoi ba: mu.
Aigupto ndi anthu chabe osati Mulungu; akavalo awo ndi nyama chabe osati mizimu. Yehova akangotambasula dzanja lake, amene amapereka chithandizo adzapunthwa, amene amalandira chithandizocho adzagwa; onsewo adzathera limodzi.
4 Hina Gode da nama amane sia: i, “Sibi ouligisu dunu da bagadewane wele sia: sa, be ilia da laione wa: me amo da ohe fi fane legele naha, amoga sefasimu da hamedei. Amo defele, Na, Hina Gode Bagadedafa da Saione Goumi gaga: sea, enoga Na logo hedofamu da hamedei.
Zimene Yehova akunena kwa ine ndi izi: “Monga mkango kapena msona wamkango umabangula ukagwira nyama yake, ndipo suopsedwa kapena kusokonezeka ndi kufuwula kwa abusa amene akulimbana nayo, momwemonso palibe chingaletse Yehova Wamphamvuzonse kubwera kudzatchinjiriza phiri la Ziyoni ndi zitunda zake.
5 Sio da ea mano gaga: ma: ne, ea bibi amo da: iya ougiaga hahadomabe, amo defele Na da Yelusaleme gaga: mu.”
Monga mbalame zowuluka pamwamba pa zisa zake, Yehova Wamphamvuzonse adzatchinjiriza Yerusalemu; ndi kumupulumutsa, iye adzawupitirira ndi kuwulanditsa.”
6 Hina Gode da amane sia: i, “Isala: ili dunu! Dilia da Nama wadela: le hamoi amola Nama gegei. Be wali, Nama sinidigima!”
Inu Aisraeli, bwererani kwa Iye amene munamuwukira kwakukulu.
7 Eso da misunu amoga dilia da wadela: i gouli amola silifa loboga hamoi ‘gode’ liligi amo huluane galadigimu.
Pakuti tsiku limenelo nonsenu mudzataya mafano anu a siliva ndi golide amene mumapanga ndi manja anu auchimo.
8 Asilia da gegesu ganodini wadela: lesi dagoi ba: mu. Be osobo bagade dunu ilia gasaga hame. Na fawane da ili gugunufinisimu. Ilia da amo gegesuga hobeamu, amola ilia ayeligi dunu da udigili se dabe iasu hawa: hamosu dunu ba: mu.
“Aasiriya adzaphedwa ku nkhondo ndi mphamvu osati za munthu. Lupanga, osati la munthu, lidzawawononga. Adzathawa ku nkhondo ndipo anyamata awo adzagwira ntchito yathangata.
9 Ilia hina bagade da bagadewane beda: iba: le hobeamu, amola ilia dadi gagui ouligisu dunu da beda: iba: le, ilia gegesu eso gosa: gisu huluane fisili, hobeamu.” Hina Gode (amoma dunu da Yelusaleme amo ganodini nodone sia: ne gadosa, amola Ea lalu da gobele salimusa: , nesa) E da sia: i dagoi.
Mfumu yawo idzamwalira ndi mantha, ndipo atsogoleri awo ankhondo adzathawa ndi mantha kusiya pambuyo mbendera yawo ya nkhondo.” Akutero Yehova, amene moto wake uli mu Ziyoni, ndipo ngʼanjo yake ili mu Yerusalemu.

< Aisaia 31 >