< Aisaia 22 >

1 Amo sia: da Esala Ba: su Fago sogebi ea hou olelesa. Wali da adi hou hamosala: ? Abuliba: le, dunu huluane da diasu gadodili da: iya heda: le, hahawane gilisisu hamosala: ?
Uthenga wonena za Chigwa cha Masomphenya: Kodi chachitika nʼchiyani, kuti nonsenu mukwere pa madenga?
2 Moilai bai bagade fi huluane da hahawane halasa. Sia: bagade da moilai ganodini nabasa. Be dilia fi dunu amo da gegesu ganodini bogoi da gegebeba: le hame bogoi.
Iwe mzinda wodzaza ndi chisangalalo chodzaza tsaya, iwe mzinda waphokoso ndi wosokonekera? Anthu ako ophedwa aja sanaphedwe ndi lupanga, kapena kufera pa nkhondo.
3 Dilia dadi gagui ouligisu dunu huluane da mae gala: le, hobeale, ilia ha lai amoga suguli lai dagoi ba: i.
Atsogoleri ako onse ngakhale anathawa limodzi; koma anagwidwa osadziteteza nʼkomwe. Inu munapezeka ndipo nonse pamodzi munatengedwa ukapolo, ngakhale munathawa pamene mdani akanali patali.
4 Amaiba: le, dilia na yolesima! Bai na da na fi dunu bagohame bogoiba: le, na da ha: giwane dimusa: dawa: lala. Na dogo denesima: ne mae misa.
Nʼchifukwa chake Ine ndinati, “Chokani pamaso panga; ndilekeni ndilire ndi mtima wowawa. Musayesere kunditonthoza chifukwa cha kuwonongeka kwa anthu anga.”
5 Ninia da Esala Ba: su Fago amo ganodini, ninima hasalasu amola beda: su amola ededenasu hou fawane ba: sa. Amola, Hina Gode Bagadedafa, E da liligi huluanedafa Ouligisu, Hi fawane da amo hou ninima iasi. Ninia moilai gagoi huluane da fabeba: le, mugului dagoi, amola dunu da fidima: ne wele sia: beba: le, ilia sia: da agologa gobagala: lala.
Lero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse walola kuti tione mavuto ndi kugonjetsedwa ndiponso chisokonezo mʼChigwa cha Masomphenya. Malinga agumuka, komanso anthu akanalira mofuwula ku mapiri.
6 Ila: me soge fi dadi gagui dunu da hosi da: iya fila heda: le, oulali amola dadi gaguiwane misi. Eno dadi gagui dunu, ilia da: igene gaga: su liligi gaguiwane, amo Gia sogega misi.
Ankhondo a ku Elamu anadza pa magaleta ndi akavalo ali ndi mivi mʼmanja. Ankhondo a ku Kiri anakonzeka ndi zishango.
7 Nasegagi fago soge Yuda soge amo ganodini diala, da sa: liode amoga nabai dagoi ba: i. Dadi gagui dunu amo hosi da: iya fila heda: i, da Yelusaleme logo ga: su gadenene lelebe ba: i.
Zigwa zanu zachonde ndi zodzaza ndi magaleta, ndipo asilikali okwera pa akavalo ayikidwa pa zipata za mzinda;
8 Yuda soge ea gaga: su liligi huluane wadela: lesi dagoi ba: i. Amalalu, dilia da gegesu liligi huluane, amo gegesu liligi ligisisu diasu amoga lale, gadili gaguli misi.
zonse zoteteza Yuda zachotsedwa. Ndipo tsiku limenelo munayangʼanayangʼana zida zankhondo zomwe zinali mʼnyumba yaufumu ya nkhalango;
9
inu munaona kuti makoma ambiri a mzinda wa Davide anali ndi malo ambiri ogumuka; munasunga madzi mu chidziwe chakumunsi.
10 Dilia da Yelusaleme gagoi ba: lu, amo ganodini sogebi afae afae da wadela: lesi dagoi ba: i. Dilia da Yelusaleme huluane ba: i. Dilia mogili, Yelusaleme gagoi bu hahamoma: ne, igi lamusa: , diasu mogili mugului dagoi.
Munawerenga nyumba zonse za mu Yerusalemu ndipo munagwetsa nyumba zina kuti mulimbitse linga logumuka lija.
11 Dilia da hano amo da hemone wayabo amoga maha, amo hai dialoma: ne dilia da hihiga: le gagui. Be dilia da Gode (amo da hemone waha doaga: be hou ilegele, hamomusa: hamoi) Ema hamedafa dawa: i.
Pakati pa makoma awiri munamanga chitsime chosungiramo madzi ochokera ku dziwe lakale, koma inu simunadalire Mulungu amene anapanga zimenezi, kapena kusamalako za Iye amene anazilenga kale lomwe.
12 Ouligisudafa Hina Gode Bagadedafa da amane wele sia: i, “Dilia da dialuma hinabo waga: ne, gogolole abula eboboi ga: ne, didigia: ma!”
Pa tsiku limenelo, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse anakuyitanani kuti mulire ndi kukhetsa misozi; kumeta mutu wanu mpala ndi kuvala ziguduli.
13 Be amo mae dawa: le, dilia da oufesega: i amola hahawane lolo nasu. Dilia da sibi amola bulamagau moma: ne, medole legei. Amola dilia da waini hano mai. Dilia da amane sia: i, “Ninia da ha: i amola waini hano manu da defea. Bai aya ninia bogomu.”
Koma mʼmalo mwake inu munakondwa ndi kusangalala; munapha ngʼombe ndi nkhosa; munadya nyama ndi kumwa vinyo. Inu mumati, “Tiyeni tidye ndi kumwa pakuti mawa tifa!”
14 Hina Gode Ouligisu Bagadedafa Hisu da nama amane sia: i, “Ilia da baligili wadela: idafa hamobeba: le, ilia da osobo bagadega esalea, Na da ilia hou hamedafa gogolema: ne olofomu. Na, Hina Gode Ouligisu Bagadedafa da sia: i dagoi.”
Yehova Wamphamvuzonse wandiwululira mondinongʼoneza kuti, “Tchimo limeneli sindidzakhululuka mpaka tsiku la kufa kwanu,” akutero Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse.
15 Ouligisudafa Hina Gode Bagadedafa da na da Siebena (hina bagade diasu ouligisu dunu) amoma asili, ema sisasu amane iasima: ne sia: i,
Chimene Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pita, ukanene kwa Sabina kapitawo, amene amayangʼanira nyumba yaufumu:
16 “Di dawa: loba, di da nowayale dawa: bela: ? Disu da dia bogoi uli dogoi igi agolo la: ididili dogomu, amo di hamoma: ne da hame ilegei.
Kodi ukuchita chiyani kuno, nanga ndani anakupatsa chilolezo kuti udzikumbire manda kuno, kudzikumbira manda pa phiri ndi kudzisemera malo opumulira mʼthanthwe?
17 Disu da dia hou da bagadedafa dawa: Be Hina Gode da di gaguia gadole galagamu.
“Samalira, Yehova watsala pangʼono kukugwira zolimba ndi kukuponya mwamphamvu, iwe munthu wamphamvu.
18 E da di bolo agoane gaguia gadole, soge eno amo dia soge bagade baligisa, amoga di galadigimu. Amo ganodini, di da sa: liode amo di da hahawane ba: sa, amoga dafulili di da bogomu. Dia hou hamobeba: le, dia hina bagade ea fi da gogosiamu.
Iye adzakukulunga kwambiri ngati mpira ndipo adzakuponyera mʼdziko lalikulu. Kumeneko ndiko ukafere ndipo kumeneko ndiko kudzatsalire magaleta ako. Ndipo udzasanduka wochititsa manyazi nyumba ya mbuye wako.
19 Hina Gode da dia ouligisu sogebi amoga di fadegamu. Dia da gaguia gadoi, be Hina Gode da di hedofale gisalugala: mu.”
Ine ndidzakuchotsa pa ukapitawo wako ndipo ndidzakutsitsa pa udindo wako.
20 Hina Gode da Siebenama amane sia: i, “Na da amo hou hamosea, Na da Na hawa: hamosu dunu amo Ilaiagime (Hiligaia egefe) amo misa: ne sia: mu.
“Tsiku limenelo ndidzayitanitsa mtumiki wanga, Eliyakimu mwana wa Hilikiya.
21 Na da dia hawa: hamomusa: ilegei abula amola dia bulu ema idiniginisimu, amola dia ouligisu hou huluane ema imunu. E da Yelusaleme fi dunu amola Yuda soge fi dunu ilima ada agoane esalumu.
Ndidzamuveka mkanjo wako ndi kumangira lamba wako mʼchiwuno mwake ndi kumupatsa ulamuliro wako. Iye adzakhala kholo la amene amakhala mu Yerusalemu ndiponso a fuko la Yuda.
22 Na da e Da: ibidi egaga fi hina bagade amo fawane hagudu ouligisudafa agoane hamomu. E da fedege agoane, ouligisu doasisu “gi” gagulaligi agoane ba: mu. Ea doasi liligi enoga ga: mu da hamedei ba: mu, amola ea ga: si liligi, enoga doasimu da hamedei ba: mu.
Ndidzamupatsa ulamuliro wa banja la Davide. Adzatsekula ndipo palibe adzatseke, adzatseka popanda wina kutsekula.
23 Na da fedege agoane Ilaiagime gosagisisu liligi agoane, ea sogebi amoga mae muguluma: ne, gasawane lala: gimu. Amola ea sosogo fi dunu huluane da ea houba: le nodomu.
Ufumu wake udzakhala wokhazikika ngati chikhomo chokhomedwa pa malo olimba. Anthu adzalemekeza nyumba ya abale ake chifukwa cha iye.
24 Be fa: no, ea sosogo fi amola ea ouligi dunu huluane da ema dioi liligi bagadewane ba: mu. Ilia da fedege agoane, ofodo amola gaga amola gosagisisu liligi amo defele ema gosagisi dialebe ba: mu.
Ana ndi abale a nyumba ya abambo ake adzakhala ngati katundu pa iye ngati ziwiya zopanda ntchito zimene zapachikidwa pa chikhomo.
25 Amo hou doaga: sea, agenesi gosagisisu musa: gasawane lala: gi dialu da hoholigili fadegale, sa: imu. Amasea, liligi amoga gosagisi dialu da wadela: lesi dagoi ba: mu,” Hina Gode da sia: i dagoi.
“Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Tsiku limeneli chikhomo chokhomedwa kwambiri chija sichidzalimbanso; chidzazuka ndipo chidzagwa ndipo zonse zopachikidwa zidzawonongedwa.’” Yehova wayankhula chomwechi.

< Aisaia 22 >