< Hosia 1 >

1 Hina Gode da Hosia (Bialai egefe) ema sia: adole i. Amo esoha galu, Asaia, Youdame, A:ihase amola Hesigaia da Yuda dunu fi ilima hina bagade galu. Amola Yelouboua: me (Yihoua: se egefe) da Isala: ili fi amo ilia hina bagade esalu.
Awa ndi mawu amene Yehova anayankhula kwa Hoseya mwana wa Beeri pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda ndiponso pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Yowasi mfumu ya ku Israeli.
2 Hina Gode da bisili Hosia ea lafidili Isala: ili fi ilima adomusa: galea, E da Hosiama amane sia: i, “Di da asili uda lama. Be dia uda da di baligi fa: mu, amola dia mano da dia uda ea hou defele, hame nabasu mano ba: mu. Amo defele, Na fi dunu ilia da Na yolesili, baligi fa: i dagoi.
Yehova atayamba kuyankhula kudzera mwa Hoseya, Yehova anati kwa Hoseyayo, “Pita kakwatire mkazi wachiwerewere ndipo ubereke naye ana mʼchiwerewere chake pakuti anthu a mʼdziko muno achimwa pochita chigololo choyipitsitsa, posiya Yehova.”
3 Amaiba: le, Hosia da Dibala: ime ea uda mano Gouma amo lai dagoi. Amalalu ela da dunu mano lalelegei.
Motero Hoseya anakwatira Gomeri mwana wamkazi wa Dibulaimu, ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna.
4 Amalalu, Hina Gode da Hosiama amane sia: i, “Dia mano ea dio Yeseliele asulima. Bai Na da gadenenewane Isala: ili hina bagade ema se nabasu bagade imunu. Amo se imunu ea bai da ea aowa Yihiu da musa: Yeseliele moilai bai bagadega dunu bagohame medole lelegei. Na da Yihiu ea fi ouligisu hou dagolesimu.
Tsono Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti Yezireeli, pakuti ndili pafupi kulanga banja la Yehu chifukwa cha anthu amene anawapha ku Yezireeli ndipo ndidzathetsa ufumu wa Israeli.
5 Amola amo esoha, Na da Yeseliele Fago ganodini, Isala: ili fi ilia gegemusa: sasanega: nanusu wadela: lesimu.
Tsiku limenelo ndidzathyola uta wa Israeli mʼchigwa cha Yezireeli.”
6 Gouma da mano eno lalelegei. Waha lalelegei amo da uda mano. Hina Gode da Hosiama amane sia: i, “Ea dio ‘Ema hame asigisa’ asulima. Bai Na da Isala: ili dunu huluanema bu hame asigimu, amola ilia wadela: i hou bu hame gogolema: ne olofomu.
Gomeri anakhala woyembekezeranso ndipo anabereka mwana wamkazi. Ndipo Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti ‘Sakondedwa’ pakuti sindidzaonetsanso chikondi changa pa nyumba ya Israeli, kuti ndingawakhululukire konse.
7 Be Na da Yuda dunuma asigimu. Na, ilia Hina Gode, da ili gaga: mu. Be amo gaga: su hou Na da gegesu amoga amola gegesu dadi amola gegesu gobihei sedade amola hosiga fila heda: le gegesu dunu, amoga hame hamomu.
Komatu ndidzaonetsa chikondi pa nyumba ya Yuda; ndipo ndidzawapulumutsa, osati ndi uta, lupanga kapena nkhondo, kapena akavalo ndi okwerapo ake, koma ine Yehova Mulungu wawo ndidzawapulumutsa.”
8 Gouma da ea uda mano dodo fisilalu, abula eno agui ba: i. Amalu dunu mano eno lalelegei.
Sakondedwa ataleka kuyamwa, Gomeri anabereka mwana wina wamwamuna.
9 Hina Gode da Hosiama amane sia: i, “Mano ea dio ‘Na fi dunu hame’ amo asulima. Bai wali Isala: ili dunu da Na fi dunu hame. Amola Na da ilia Gode hame.”
Pamenepo Yehova anati, “Umutche dzina loti Sianthuanga,” pakuti inu si ndinu anthu anga ndipo Ine si ndine Mulungu wanu.
10 Isala: ili dunu fi da afadenene hano bega: bosoda: i dialebe agoai ba: mu. Bagadeba: le, idimu da hamedei ba: mu. Wali, Gode da ilima amane sia: sa, “Dili da Na dunu hame,” be eso da misunu amoga E da ilima amane sia: mu, “Dilia da Esalalalusu Gode Ea mano esala.”
“Komabe Aisraeli adzachuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja umene sangathe kuwuyeza kapena kuwuwerenga. Pamalo omwe ananena kuti, ‘Sindinu anthu anga,’ pomweponso adzawatchula kuti ‘Ana a Mulungu wamoyo.’
11 Yuda fi dunu amola Isala: ili fi dunu ilia da bu gilisili fi afae hamoi ba: mu. Amola ilia da dunu afae amo ili ouligima: ne ilegemu. Amola ilia fi da bu heda: mu amola ilia soge ganodini hahawane esalumu. Dafawane! Yeseliele ea eso misunu hou da hou bagadedafa ba: mu.”
Anthu a ku Yuda ndi anthu a ku Israeli adzasonkhananso pamodzi ndipo adzasankha mtsogoleri mmodzi ndi kutuluka mʼdzikomo, pakuti tsiku la Yezireeli lidzakhala lalikulu kwambiri.”

< Hosia 1 >