< Hosia 14 >
1 Isala: ili dunu! Dilia Hina Godema bu sinidigima! Dilia da wadela: le hamoiba: le, didigabone dafai dagoi.
Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako. Machimo anu ndi amene akugwetsani!
2 Hina Godema sinidigima! Amola amo sia: ne gadosa gobele iasu defele Ema ima, amane, “Ninia wadela: i hou huluane gogolema: ne olofoma amola ninia sia: ne gadosu nabima! Amalu ninia ilegele sia: i defele, ninia da Dima nodomu.
Bweretsani zopempha zanu ndipo bwererani kwa Yehova. Munene kwa Iye kuti, “Tikhululukireni machimo athu onse ndi kutilandira mokoma mtima, kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.
3 Asilia da nini gaga: mu hame dawa: , amola gegesu hosi da nini gaga: mu gogolesa. Ninia bu ninia loboga hamoi ogogosu ‘gode’ ilima ‘Godedafa’ dio hame asulimu. Hina Gode! Di da dunu amo da fidisu dunu eno hame gala, ilima gogolema: ne olofosu imunusa: dawa:”
Asiriya sangatipulumutse; ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo, sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’ kwa zimene manja athu omwe anazipanga, pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”
4 Hina Gode da amane sia: sa, “Na da Na fi dunu Nama bu hiougia guda: mu. Na da Na dogo huluane amoga ilima asigimu. Na da ilima bu hame ougimu.
Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo ndipo ndidzawakonda mwaufulu pakuti ndaleka kuwakwiyira.
5 Na da gibu amo da hafoga: i soge fidibi defele, Na fi dunu fidimu. Ilia da mosoi agoane sogea falegalesimu. Ilia da Lebanone ifa defele, ifa difi modosa: i agoane ba: mu.
Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo. Adzazika mizu yake pansi ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
6 Ilia da gaheabolo lula heda: su defele, gaheabolo esalusu ba: mu. Amola ilia da olife ifa defele, nina: hamoi dagoi ba: mu. Ilia da Lebanone dolo ifa defele, gabusiga: noga: i nabimu.
mphukira zake zidzakula. Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi, kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
7 Ilia da bu Na Gaga: su hou amoha esalumu. Ilia da ifabi noga: idafa defele, noga: le heda: mu. Ilia da waini sagai defele, fage bagohame legemu. Dunu da Lebanone waini hano amoma nodosa, amo defele fifi asi gala da Na fi dunuma nodomu.
Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake. Iye adzakula bwino ngati tirigu. Adzachita maluwa ngati mphesa ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.
8 Isala: ili dunu da bu loboga hamoi ogogosu ‘gode’ ilima hame dawa: mu. Na da dialui ifa defele, ili ougigala: mu. Na da ilia hahawane dogolegele hou huluane ea bai gala.”
Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano? Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira. Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira; zipatso zako zimachokera kwa Ine.”
9 Bagade dawa: su dunu da amo dedena sa: i sia: noga: le dawa: mu da defea. Amola ilia da amo sia: ilia dogo ganodini ligisimu da defea. Hina Gode Ea hou huluane da moloidafa. Amola moloi dunu da amoga fa: no bobogebeba: le, esalusu ba: lala. Be wadela: i hamosu dunu da Gode Ea hou higabeba: le, didigabone dafasa. Sia: ama dagoi
Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi. Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi. Njira za Yehova ndi zolungama; anthu olungama amayenda mʼmenemo, koma anthu owukira amapunthwamo.