< Mui 42 >
1 Ya: igobe da gagoma Idibidi dialebe amo nababeba: le, egefelali ilima amane sia: i, “Dilia da abuli udigili esalabala?
Yakobo atamva kuti ku Igupto kuli tirigu, anati kwa ana ake, “Nʼchifukwa chiyani mukungoyangʼanana wina ndi mnzake?
2 Na da nabi gagoma Idibidi sogega diala. Ninia da ha: iba: le bogosa: besa: le, amoga lala masa.”
Ine ndamva kuti ku Igupto kuli tirigu. Pitani kumeneko mukatigulireko kuti tisafe ndi njala.”
3 Amaiba: le, Yousefe ea yolalali nabuane gala da Idibidi sogega gagoma bidi lamusa: asi dagoi.
Choncho abale ake khumi a Yosefe anapita kukagula tirigu ku Igupto.
4 Be e da se nabasa: besa: le, Ya: igobe da Yousefe eya Bediamini amo hame asunasi.
Koma Yakobo sanamulole Benjamini mngʼono wake wa Yosefe kuti apite nawo chifukwa anaopa kuti choyipa chingamuchitikire.
5 Ga: ina: ne soge da ha: i bagadeba: le, Ya: igobe egefelali da eno dunu gilisili, gagoma ha: i manu bidi lama: ne misi.
Choncho ana a Israeli aja anapita pamodzi ndi gulu la anzawo kukagula tirigu pakuti ku Kanaani kunalinso njala.
6 Yousefe, Idibidi ouligisu hina dunu, da osobo bagade fifi asi gala dunu huluane ilima gagoma bidi lalu. Amaiba: le, Yousefe yolalali da ema misini, ilia odagi osoboa digimusa: begudui.
Pakuti Yosefe anali nduna yayikulu yolamulira dziko la Igupto, ndiye kuti analinso amene ankagulitsa tirigu kwa anthu onse. Choncho abale ake a Yosefe nawonso anabwera, ndipo anamugwadira pansi.
7 Yousefe da ea yolalali ba: beba: le, ili dawa: i galu. Be e da ogogole, e da ili hame dawa: i agoane hamoi. E da gasa fiwane ilima adole ba: i, “Dilia da habidili misibala: ?” Ilia da bu adole i, “Ninia da Ga: ina: ne sogega ha: i manu bidi lamusa: misi.”
Yosefe atangowaona abale ake anawazindikira, koma ananamizira kukhala ngati mlendo nawayankhula mwaukali kuwafunsa kuti, “Mwachokera kuti?” Iwo anayankha, “Ku dziko la Kanaani, tikudzagula chakudya.”
8 Yousefe da ea yolalali dawa: i. Be e da ilia eya amo ilia da hame dawa: i.
Ngakhale Yosefe anawazindikira abale ake, koma iwo sanamuzindikire.
9 E da ilima musa: simasia ba: su amo bu dawa: i. E ilima amane sia: i, “Dilia da desega ahoasu dunu. Dilia da Idibidi soge amo ninia habidili gasa hame gala amo ba: la misi.”
Pamenepo anakumbukira maloto aja amene analota za iwo ndipo anati, “Inu ndinu akazitape! Mwabwera kudzazonda dziko lathu kuti muone pamene palibe chitetezo.”
10 Be ilia bu adole i, “Hame mabu, hina! Ninia da dia udigili hawa: hamosu dunu defele, ha: i manu bidi lamusa: misi.
Iwo anayankha, “Ayi mbuye wathu, antchito anufe tabwera kudzagula chakudya.
11 Ninia huluane da olalali esala. Ninia da desega ahoasu dunu hame. Ninia huluane da moloi dunu.”
Tonse ndife ana a munthu mmodzi. Ndife antchito anu okhulupirika osati akazitape.”
12 Yousefe bu adole i, “Hame mabu! Dilia da ninia soge amo ea gasa hame hou ba: la misi dagoi.”
Iye anawawuza kuti, “Ayi! Inu mwabwera kudzaona pamene palibe chitetezo mʼdziko muno.”
13 Ilia bu amane sia: i, “Ninia da olalali fagoyale galu. Ninia da dunu afae Ga: ina: ne soge ganodini amo ea manolali gala. Be eya afae da bogoi, amola ufi dunu mano da ninia eda amola esala.”
Koma iwo anayankha, “Tinalipo ana aamuna khumi ndi awiri. Abambo athu ndi mmodzi, ndipo kwathu ndi ku Kanaani. Panopo wotsiriza ali ndi abambo athu ndipo wina anamwalira.”
14 Yousefe da bu adole i, “Na sia: i defele dilia da desega ahoasu dunu.
Yosefe anawawuza kuti, “Ndi momwe ndaneneramo: Inu ndinu akazitape.
15 Na dilima adoba: su hou hamomu. Felou ea dioba: le, na da agoane sia: sa. Dilia fa: no lalelegei eya da guiguda: hame manoba, dilia da guiguda: hamedafa yolesimu.
Ndiye ndikuyesani motere: Ine ndikulumbira pali Farao ndithu, inuyo simudzachoka malo ano mpaka wotsirizayo atabwera kuno.
16 Dilia fi dunu afae e lala masa: ma! Dilia eno huluane da guiguda: se iasu diasu ganodini esalumu. Dilia sia: da dafawane o dafawane hame, amo ninia ba: mu.”
Tumizani mmodzi wa inu akamutenge mʼbale wanuyo ndipo ena nonsenu musungidwa mʼndende, kuti titsimikize ngati zimene mukunenazi ndi zoona. Apo ayi, pali Farao ndithu, inu ndinu akazitape!”
17 Amalalu, e da ili se iasu diasu ganodini sali. Amoga ilia eso udiana esalu.
Ndipo onse anawayika mʼndende kwa masiku atatu.
18 Eso udiana amoga Yousefe da ilima amane sia: i, “Na da Godema beda: i dunu. Dilia liligi afadafa hamosea fawane, na da dili hame fane legemu.
Pa tsiku lachitatu Yosefe anawawuza kuti, “Popeza ine ndimaopa Mulungu, ndipo inuyo ngati mukufuna kukhala ndi moyo muchite izi:
19 Dilia sia: da dafawane olelema: ne, dunu afae fawane da se iasu diasu ganodini esalumu. Dilia eno da dilia ha: i bagade fi ilima ha: i manu dilia lai gaguli masa.
Ngati muli anthu achilungamo, mmodzi wa inu atsale mʼndende, pamene ena nonse mupite kwanu kuti muwatengere chakudya anthu akwanu kuli njalako.
20 Amasea, dilia fa: no lalelegei eya amo guiguda: oule misa. Amasea, dilia da hame ogogoi, na da dawa: mu amola na da dili hame fane legemu.” Amo da defea ilia sia: i dagoi.
Mukabwere naye kuno mngʼono wanu wotsirizayo kuti titsimikizire zimene munanena kuti musafe.” Ndipo anachita zomwezo.
21 Ilia gilisili sia: dasu, “Dafawane! Wali ninia se nabasu da dabe agoane ninia eya ema wadela: le hamoiba: le lasa. E da ninima e fidima: ne se nabawane edegei, be ninia da hame nabi. Amaiba: le, ninia wali dabe agoane se naba.”
Iwo anati kwa wina ndi mnzake, “Ndithu ife tinalakwira mʼbale wathu uja popeza kuti ngakhale tinaona kuvutika kwake ndi kumva kulira kwake pamene ankatidandaulira kuti timuchitire chifundo, koma ife sitinamvere. Nʼchifukwa chake masautso awa atigwera.”
22 Liubene da amane sia: i, “Na da goi maedafa wadela: ma: ne sia: i; be dilia da hame nabi. Wali ea bogoi amoga ninia da dabe laha.”
Rubeni anayankha, “Kodi sindinakuwuzeni kuti musamuchite kanthu mnyamata uja? Koma inu simunamvere! Tsopano tikulandira malipiro a magazi ake.”
23 Yousefe da ilia sia: huluane dawa: i. Be amo hou ilia da hame dawa: i. Ilia da ema sia: noba, sia: adole iasu dunu, amoga fawane sia: su.
Koma sanadziwe kuti Yosefe ankawamva popeza kuti ankagwiritsa ntchito wotanthauzira poyankhula naye.
24 Yousefe da ili yolesili, disu. Amalalu, e da ilima bu misini, ilima sia: dasu. Ea sia: beba: le, ea dadi gagui da Simiane lale, ilia huluane ba: ma: ne lala: gi dagoi.
Yosefe anapita pambali payekha kukalira. Kenaka anabweranso nadzayankhula nawo. Iye anatenga Simeoni namumanga iwo akuona.
25 Yousefe da sia: beba: le, ea hawa: hamosu dunu da ilia esa amo gagoma amoga nabalesi. Ilia da Yousefe yolalali ilia esa afae afae amo ganodini, silifa muni ilia musa: i, amo sali. Amola ilia da ha: i manu ilia logoga ahoasea moma: ne, ilima i.
Yosefe analamula kuti awadzazire matumba awo ndi tirigu, awayikiremo ndalama zawo momwemo ndiponso awapatse chakudya cha panjira. Izi anawachitiradi.
26 Amalalu, Yousefe yolalali da ilia gagoma lai, amo ilia dougi baligiga ligisili, yolesili asi.
Abale a Yosefe aja anasenzetsa abulu awo tirigu amene anagula uja ndipo ananyamuka ulendo wawo.
27 Asili, ilia da sogebi amo golamusa: ouesalu, dunu afae da ea dougi amo ha: i manu imunusa: ea esa doasilaloba, ea muni amo gagoma gadodili ligisi dialebe ba: i.
Atafika pamalo pena poti agone, mmodzi mwa iwo anatsekula thumba lake kuti atapemo chakudya cha bulu wake. Atangomasula anaona kuti ndalama zake zili pakamwa pa thumba.
28 E da yolalalima amane sia: i, “Na muni ilia da nama bu i. Amo da na esa ganodini dialebe ba: sa.” Ilia bagade beda: i galu. Ilia da gilisili amane sia: dasu, “Gode da anima adi hamobela: ?”
Iye anati kwa abale akewo, “Ndalama zanga andibwezera, izi zili mʼthumba mwangamu.” Mitima yawo inachita ngati yachokamo ndipo anali ndi mantha ambiri, nati, “Ndi chiyani chimene Mulungu watichitira?”
29 Ilia da eda Ya: igobema doaga: loba, ilia da hou huluane ilima misi amo huluane ema amane adoi,
Atafika kwa abambo awo Yakobo mʼdziko la Kanaani anafotokoza zonse zimene zinawachitikira nati,
30 “Idibidi ouligisu hina dunu da ninima gasa bagade ougiwane sia: i. E da nini ea soge wadela: musa: , desega ahoanebe sia: i.
“Nduna yayikulu ya mʼdzikomo inatiyankhula mwa ukali kwambiri ndipo inkatiyesa kuti ndife akazitape.
31 Be ninia ema bu adole i, ‘Ninia da desega ahoasu dunu hame. Ninia moloidafa dunu.
Koma tinamuwuza kuti, ‘Ndife anthu woona mtima osati akazitape.
32 Ninia da olalali fagoyale galu. Ninia dunu afae amo egefelali gala. Ninia eya da bogoi amola fa: no lalelegei eya da ninia eda amola Ga: ina: ne soge ganodini esala.’
Ife tonse tinalipo ana aamuna khumi ndi awiri, abambo mmodzi. Mmodzi anamwalira, ndipo wamngʼono ali ndi abambo athu ku Kanaani.’”
33 Amalalu, Idibidi hina da amane sia: i, ‘Dilia da moloidafa dunu o hame, amo ninia da amoga ba: mu. Dunu afadafa da nama ouesalumu. Eno da dilia ha: i bagade fi ilima ha: i manu gaguli masa.
Ndipo nduna ija inati kwa ife, “Kuti ndidziwedi kuti ndinu anthu owona mtima muchite izi: Mmodzi mwa inu atsale ndi ine kuno, ndipo enanu mutenge chakudya ndi kubwerera kwanu kumene kuli njalako.
34 Dia eya fa: no lalelegei, amo nama oule misa. Amasea, dilia da desega ahoasu dunu hame be moloidafa amo na da dawa: mu. Na da dilia ola dilima bu imunu. Amola dilia da guiguda: bidi lasu hamomusa: ouesalumu da defea.”
Koma mundibweretsere wotsirizayo kuti ndidziwedi kuti sindinu akazitape koma anthu achilungamo. Kenaka ndidzakubwezerani mʼbale wanuyu ndipo mukhoza kuchita malonda mʼdzikoli.”
35 Amalalu, ilia da gagoma esa ganodini sali amo huluane gugudili legeiya, ilia huluane muni ganodini sali dialebe ba: i. Amo ba: beba: le, ilia, amola ilia eda Ya: igobe, da bagade beda: i galu.
Pamene amakhuthula matumba awo a tirigu aliyense anapeza kuti kathumba kake ka ndalama kali momwemo. Ataona zimenezi, iwo pamodzi ndi abambo awo anachita mantha kwambiri.
36 Ilia eda da ilima amane sia: i, “Dilia da na mano huluane fisimu, amo dilia da hanabala: ? Yousefe da fisi dagoi. Simiane da fisi dagoi. Wali dilia da Bediamini fadegamusa: dawa: lala. Ni fawane da se naba.”
Abambo awo Yakobo anawawuza kuti, “Mwandilanda ana anga ine. Yosefe anamwalira ndipo Simeoni palibenso, ndiye tsopano mukufuna mutengenso Benjamini. Zonsezi zandigwera ine!”
37 Liubene da ea edama amane sia: i, “Na da Bediamini dima bu hame oule masea, di da na dunu mano aduna fane legemu da defea. Na ouligima: ne, Bediamini nama ima. Na da e bu oule misunu.”
Koma Rubeni anati kwa abambo ake, “Ngati sindidzabwera naye kwa inu, mudzaphe ana anga aamuna awiri. Muperekeni mʼmanja mwangamu ndipo ndidzamusamala ndi kubwera naye kwa inu.”
38 Be Ya: igobe da amane sia: i, “Na gofe da dili sigi masunu hamedei. Ea ola da bogoi amola hisu da esala. E da logoga se nabasa: besa: le, hamedafa masunu. Na da dunu da: i hamoi dagoi. Di da amo se nabasu nama iasea, na bogomu.” (Sheol )
Koma Yakobo anati, “Mwana wanga sapita nanu kumeneko; mkulu wake anamwalira ndipo watsala yekha. Ngati choyipa chitamuchitikira pa ulendo mukupitawu, ndiye kuti ndi mmene ndakalambiramu inu mudzandipha ndi chisoni chotere.” (Sheol )