< Mui 39 >
1 Isiama: ile fi dunu da Yousefe amo Idibidi sogega oule asili, Bodifa (Idibidi hina bagade dunu ea sosodo aligisu dunu ilima hina dunu) ema bidi lai dagoi.
Tsopano Yosefe anatengedwa kupita ku Igupto. Potifara Mwigupto amene anali mmodzi wa akuluakulu a Farao ndiponso mkulu wa asilikali olonda ku nyumba kwa Farao, anagula Yosefe kwa Aismaeli amene anapita naye kumeneko.
2 Hina Gode da Yousefe noga: le fidilalu. Ea hawa: hamosu da noga: idafa ba: i. E da ea Idibidi hina ea diasu ganodini esalu.
Koma Yehova anali ndi Yosefe ndipo zake zonse zimayenda bwino. Iye ankakhala mʼnyumba ya mbuye wake wa ku Igupto.
3 Bodifa da Hina Gode da Yousefe noga: le fidi amola ea hawa: hamosu da noga: idafa, amo ba: i dagoi.
Mbuye wake anaona kuti Yehova anali naye Yosefe ndi kuti pa chilichonse chimene anachita Yehova ankaonetsetsa kuti achite bwino.
4 Bodifa da ema hahawane bagade. E da Yousefe amo ea fidisu dunu ea diasu amola liligi huluane, amo ouligima: ne hamoi dagoi.
Potifara anakondwera ndi Yosefe chifukwa cha matumikiridwe ake. Choncho anamusandutsa woyangʼanira nyumba yake ndi zonse za mʼnyumba yake.
5 Amalalu, Yousefe dawa: beba: le, Hina Gode da amo Idibidi dunuma hahawane dogolegele hamoi. Liligi huluane ea diasu ganodini amola ea soge ganodini, Gode da noga: le fidi.
Kuchokera pa nthawi imene anamuyika kukhala woyangʼanira wa nyumbayo ndi zonse za mʼnyumbamo, Yehova anadalitsa nyumba ya Mwiguptoyo chifukwa cha Yosefe. Madalitso a Yehova anali pa chilichonse chimene Potifara anali nacho, za mʼnyumba komanso za ku munda.
6 Bodifa da ea hou huluane ouligima: ne, Yousefema sia: i. Bodifa da liligi huluane mae dawa: le, ea ha: i manu fawane dawa: i galu. Yousefe ea da: i amola ea odagi, da ida: iwane ba: su.
Choncho anasiyira mʼmanja mwa Yosefe chilichonse chomwe anali nacho, kotero kuti samadandaula ndi chilichonse kupatula chakudya chimene ankadya. Tsopano Yosefe anali wa thupi labwino ndi wokongola.
7 Asili, Bodifa idua da Yousefe amo hanaiwane ba: lalu. E da ema gilisili golama: ne adole ba: lalu.
Patapita kanthawi, mkazi wa mbuye wake anayamba kusirira Yosefe nati, “Bwanji ugone nane!”
8 Yousefe da, “Hame mabu!” sia: i. Yousefe da ema amane sia: i, “Na da ouligibiba: le, na hina da ea diasu amola liligi amo hame dawa: lala. E da na ea liligi huluane ouligima: ne ilegei dagoi.
Koma iye anakana namuwuza kuti, “Inu mukuona kuti mbuye wanga sadandaula ndi kena kalikonse mʼnyumba muno, ndipo chawo chilichonse anachiyika mʼmanja mwanga.
9 Na da amo diasu ganodini, e defele hina hou hamosa. Liligi huluane e da nama i, be di fawane nama hame i. Na da habodane amo wadela: i hou hamoma: bela: ? Na da habodane Godema wadela: le hamoma: bela: ?”
Motero kuti palibe wina wamkulu kuposa ine mʼnyumba muno. Ndipo palibe chilichonse chimene mbuye wanga sanachipereke kwa ine kupatula inuyo, chifukwa ndinu mkazi wake. Tsono ndingachite bwanji choyipa choterechi ndi kuchimwira Mulungu?”
10 Bodifa idua da eso huluane mae fisili Yousefe da ema gilisili golamusa: sia: su, be Yousefe da ea sia: hame nabi.
Ndipo ngakhale kuti iye anayankhula mawu omwewa ndi Yosefe tsiku ndi tsiku, Yosefe sanalole kugona naye ngakhale kukhala naye pafupi.
11 Be eso afaega, Yousefe da ea diasu ganodini ea hawa: hamosu hamoma: ne golili sa: ili, hawa: hamosu dunu eno hamedafa ba: i.
Tsiku lina Yosefe analowa mʼnyumbamo kukagwira ntchito zake, ndipo munalibe wina aliyense wantchito mʼnyumbamo.
12 Bodifa idua da Yousefe ea abula gaguli, amane sia: i, “Nama gilisili golama!” Be e da ea abula fadegale, gadili hobea: i dagoi. Ea abula da Bodifa idua ea lobo ganodini gagui dialebe ba: i.
Mkazi uja anamugwira mkanjo Yosefe nati, “Tiye ugone nane!” Koma Yosefe anasiya mkanjo wake mʼmanja mwa mkaziyo nathawira kunja kwa nyumba.
13 E da Yousefe ea abula fisili gadili hobea: i dagoi amo ba: loba,
Pamene mkazi uja anaona kuti Yosefe wamusiyira mkanjo wake mʼmanja mwake nathawira kunja kwa nyumba,
14 e da ea hawa: hamosu dunu ilima welalu, amane sia: i, “Ba: ma! Amo Hibulu dunu nagoa da diasuga oule misi, amo da ninima gadele hamosa. E da na seseiga golili misini, na gasawane hi aie heda: le na wadela: lesimusa: dawa: i galu. Be na da bagade a: i gusa: i.
iye anayitana antchito ake a mʼnyumba nati, “Taonani mwamuna wanga anabwera ndi Mhebri uyu mʼnyumba muno kuti adzagone nane. Iyeyu analowa ku chipinda kwanga kuti adzagone nane ndipo ine ndinakuwa kwambiri.
15 E da na a: i gusa: i nababeba: le, ea abula fisili gadili hobea: i dagoi.”
Atandimva ndikukuwa, anandisiyira mkanjo wakewu nʼkuthawira kunja.”
16 Amo abula gaguli, e da Yousefe ea hina amo bu misa: ne ouesalu.
Tsono mkazi wa Potifara uja anasunga mkanjowo mpaka mbuye wake wa Yosefe atabwera ku nyumba.
17 Amalalu, e da Bodifama ea musa: sia: i defele olelei, amane, “Amo Hibulu udigili hawa: hamosu dunu di guiguda: oule misi da na sesei golili misini, nama hi aie heda: le wadela: le hamomusa: dawa: i galu.
Tsono anamuwuza nkhaniyi nati: “Wantchito Wachihebri amene munatibweretsera uja anabwera kuti adzagone nane.
18 Be na da bagade a: i gusa: ne, e da ea abula fisili, gadili hobea: i dagoi.”
Koma pamene ndinakuwa, iye anandisiyira mkanjo wake nathawira kunja.”
19 Yousefe ea hina (Bodifa) da bagadewane mi hanai galu.
Mbuye wake wa Yosefe atamva nkhani imene mkazi wake anamuwuza kuti, “Ndi zimene anandichitira wantchito wanu,” anapsa mtima kwambiri.
20 Ea sia: beba: le, ilia Yousefe afugili, se iasu diasu (amo ganodini Idibidi hina bagade dunu da wadela: i hamosu dunu sanasu) amo ganodini ha: digili, Yousefe da amo ganodini esalu.
Tsono iye anatenga Yosefe namuyika mʼndende mmene ankasungiramo amʼndende a mfumu. Ndipo Yosefe anakhala mʼndendemo
21 Be Hina Gode da Yousefe hahawane dogolegele fidisu. Amola se iasu diasu ouligisu dunu da Yousefe ea hou hahawane ba: i.
koma Yehova anali naye, ndipo anamuonetsa kukoma mtima kwake, kotero kuti woyangʼanira ndende anakondwera ndi Yosefe.
22 E da Yousefe amo se iasu diasu hamosu dunu huluanema, ouligisu hamoi dagoi. Hou huluane amo se iasu diasu ganodini hamosu, amo huluane Yousefe hi da ouligilalu.
Choncho woyangʼanira ndende uja anamuyika Yosefe kukhala woyangʼanira onse amene anayikidwa mʼndende. Ndiponso anamupatsa udindo woyangʼanira zonse zochitika mʼndendemo.
23 Se iasu diasu ouligisu hina da liligi huluane hame dawa: lalu. Bai Hina Gode da Yousefe noga: le fidisu. Ea hou huluane e da noga: le hamoi amola hahawane ba: i.
Woyangʼanira ndende uja sankayangʼaniranso china chilichonse chimene chinali mu ulamuliro wa Yosefe, chifukwa Yehova anali ndi Yosefe. Ndipo Yehova anaonetsetsa kuti chilichonse chimene Yosefe ankachita chimuyendere bwino.