< Mui 37 >
1 Ya: igobe da soge amo ea eda da musa: amo ganodini esalu (Ga: ina: ne), amogawi esalu.
Yakobo ankakhala mʼdziko la Kanaani kumene abambo ake ankakhala.
2 Ya: igobe ea sosogo fi ilia hou dedei da agoane. Yousefe da lalelegele, ode 17 esalu, ayeligi ba: i. E amola yolalali (ilia da Ya: igobe ea gidisedagi uda Biliha amola Siliba elea mano), amo da gilisili Ya: igobe ea sibi amola goudi ouligisu. E da ea olalali ilia wadela: i hou ba: beba: le, ea edama sia: ne iasu olelei.
Mbiri ya banja la Yakobo ndi iyi: Yosefe, mnyamata wa zaka 17 ankaweta nkhosa ndi abale ake, pamodzi ndi ana a Biliha ndi Zilipa, akazi a abambo ake. Tsono Yosefe ankabwera kudzawuza abambo ake zoyipa za abale ake.
3 Yousefe da Ya: igobe ea da: i hamoi esoga lalelegeiba: le, Ya: igobe ea asigi hou ema da ea asigi hou amo Yousefe yolalali ilima baligisu. E abula ida: iwane hamone, Yousefema i.
Tsono Israeli ankakonda Yosefe koposa ana ake ena onse, chifukwa anali mwana wobadwa muukalamba wake. Ndipo anamusokera mkanjo wa manja aatali.
4 Yousefe ea yolalali da Ya: igobe ea asigi hou Yousefema da ea asigi ilima baligi amo ba: beba: le, mudasu hamoi. Ilia da Yousefema bagade higasu. Ilia da ema asigiwane sia: mu hamedeiwane ba: i.
Pamene abale ake anaona kuti abambo awo ankakonda Yosefe kuposa aliyense wa iwo, anayamba kumuda Yosefe ndipo sankayankhula naye zamtendere.
5 Eso afaega, Yousefe da simasia ba: i. Amo e da ea yolalalima olelebeba: le, ilia da bu baligili ema mi hanai galu.
Tsiku lina Yosefe analota maloto ndipo pamene anawuza abale ake za malotowo, iwo anawonjeza kumuda.
6 E da ilima amane sia: i, “Nabima! Na da agoane simasia ba: i.
Iye anawawuza kuti, “Tamvani maloto amene ndinalota:
7 Ninia huluane da widi sagai amo ganodini widi la: gi dudalebe ba: i. Amalalu, na widi la: gi da wa: legadole moloiwane lelu. Amalalu, dilia widi la: gi da na widi la: gi amoga sisiga: le, begudui.”
Ife timamanga mitolo ya tirigu ku munda ndipo mwadzidzidzi mtolo wanga unayimirira chilili, pamene mitolo yanu inazungulira mtolo wangawo nʼkumawugwadira.”
8 Ea yolalali da ema amane adole ba: i, “Di da ninima hina bagade esalumu dawa: bela: ?” Amaiba: le, e da simasia ba: beba: le amola amoga sia: beba: le, ilia da ema baligili mi hanai galu.
Abale ake aja anamufunsa nati, “Kodi ukuyesa kuti ungakhale mfumu yathu? Ungadzatilamuliredi iweyo?” Ndipo anamuda kuposa kale chifukwa cha maloto ake ndi zimene ankakonda kunena kwa abambo awo.
9 Amalalu, Yousefe da eno simasia ba: i. E da ea yolalali ilima amane sia: i, “Na da eno simasia ba: i. Amo ganodini, na da eso, oubi amola gasumuni gidayale gala, huluane nama begudulalebe ba: i.”
Tsiku lina analotanso maloto ena, ndipo anafotokozera abale ake za malotowo. Iye anati, “Tamverani, ndinalotanso maloto ena. Ulendo uno dzuwa ndi mwezi pamodzi ndi nyenyezi khumi ndi imodzi zimandigwadira.”
10 Amo simasia ba: i e da ea adama olelei. Ea eda da ema gagabole sia: i, “Amo da adi simasia ba: sula: ? Dia ame, dia yolalali amola na da dima misini, beguduma: bela: ?”
Atawuza abambo ake ndi abale ake malotowa, abambo ake anamukalipira nati, “Ndi maloto anji umalotawa? Kodi uganiza kuti ine, amayi ako pamodzi ndi abale ako onsewa tingadzabwere kudzakugwandira iwe?”
11 Yousefe ea yolalali da ema mudale dawa: i, be ea ada da amo liligi huluane ea asigi dawa: su ganodini dawa: lalu.
Abale ake anamuchitira nsanje, koma abambo ake anasunga nkhaniyi mu mtima.
12 Eso afaega, Yousefe yolalali da Siegeme sogega ilia eda ea lai gebo fi amo ouligimusa: asi dagoi ba: i.
Tsono abale ake anapita kukadyetsa ziweto za abambo awo ku Sekemu,
13 Ya: igobe da Yousefema amane sia: i, “Dia yolalali ilia da Siegeme sogega lai gebo gilisisu ouligilala. Di amoga masa!” Yousefe da amane bu adole i, “Na masunu!”
ndipo Israeli anati kwa Yosefe, “Tsono, ndikufuna kukutuma kwa abale ako.” Iye anayankha nati, “Chabwino.”
14 Ea ada da ema amane sia: i, “Defea! Masa! Dia yolalali da hahawane esalabala? Sibi gilisisu da hahawanela: ? Amo huluane abodemusa: masa. Amasea, amo sia: ne iasu bu nama iamisa.” Ea eda da Hibalone Fago esalu. E da Yousefe asunasiba: le, Yousefe da asili, Siegeme sogega doaga: i.
Choncho anati kwa iye, “Pita ukaone ngati abale ako ali bwino. Ukaonenso nkhosa ngati zili bwino. Kenaka ubwere udzandiwuze.” Choncho Israeli anatuma Yosefe kuchokera ku chigwa cha Hebroni. Yosefe atafika ku Sekemu,
15 E da amo sogega udigili laloba, dunu afae da e ba: loba amane sia: i, “Di da adi hogosala: ?”
munthu wina anamupeza akungozungulirazungulira mʼmunda ndipo anamufunsa, “Ukufunafuna chiyani?”
16 Yousefe da bu adole i, “Na da nolalali amo ilia lai gebo gilisisu ouligilala, amo hogosa. Di da ili ba: bela: ?
Iye anayankha, “Ndikufuna abale anga. Mungandiwuze kumene akudyetsa ziweto zawo?”
17 Amo dunu bu adole i, “Ilia da fisili asi dagoi. Ilia sia: na da nabi, amo ilia da Douda: ne sogega masusa: dawa: i galu.” Amaiba: le, Yousefe da ea yolalali ilima fa: no bobogele, Douda: ne sogega ilima doaga: i.
Munthuyo anayankha nati, “Anasamukako kuno. Ndinawamva akuti, ‘Tiyeni tipite ku Dotani.’” Choncho Yosefe analondola abale ake ndipo anakawapeza ku Dotani.
18 Ilia da Yousefe sedagaga manebe ba: beba: le, e fane legemusa: gilisili sia: dasu.
Abale ake aja anamuonera patali. Ndipo asanafike nʼkomwe kumene kunali iwo kuja, anayamba kale kumupangira chiwembu choti amuphe.
19 Ilia gilisili sia: dasu, amane, “Amo simasia ba: su dunu da manebe goea!
Iwo anawuzana nati, “Uyo akubwera apo wamaloto uja.
20 Defea! Ninia da medole legele amola ea da: i hodo amo hafoga: i hano uli dogoi amo ganodini ha: digimu. Ninia da gasonasu ohe fi da e medole legei sia: mu. Amasea, ea simasia ba: i liligi da hamedei liligi ba: mu.”
Tsono tiyeni timuphe ndi kuponya thupi lake mu chimodzi mwa zitsime izi ndipo tidzati anadyedwa ndi nyama zakuthengo zolusa. Tsono timuonera zomwe ziti zichitike ndi maloto ake aja.”
21 Liubene da amo sia: nababeba: le, Yousefe gaga: musa: dawa: i galu. E amane sia: i, “Ninia da e hame fane legemu.
Koma Rubeni atamva izi, anapulumutsa Yosefe. Iye anati kwa abale ake, “Ayi, tisamuphe,
22 Be udigili amo hafoga: i uli dogoi amo ganodini sanasimu. Be ema se mae ima.” E da Yousefe gaga: le, ea edama bu oule masusa: ilegei galu.
tisakhetse magazi. Tiyeni timuponye mʼchitsime ku chipululu konkuno. Koma tisamuvulaze nʼkomwe. Rubeni ananena zonsezi kuti apulumutse Yosefe ndi kuti pambuyo pake akamupereke kwa abambo awo.”
23 Yousefe da ea yolalali ilima doaga: loba, ilia da ea nina: hamoi abula sedade amo fadegai.
Choncho Yosefe atafika kwa abale ake, iwo anamuvula mkanjo wake wamanja aatali uja umene anavala
24 Amalalu, ilia da Yousefe amo hafoga: i uli dogoi amo ganodini sanasi.
ndipo anamutenga namuponya mʼchitsime chopanda madzi komanso mopanda chilichonse.
25 Ilia da ha: i nanoba, Isiama: ile (Midia: ne) fi dunu amo Gilia: de soge fisili Idibidi amoga doaga: musa: logoga ahoanebe ba: i. Ilia ga: mele da hedama: ne fodole nasu amola gamali agui ahoanebe ba: i.
Atakhala pansi kuti adye chakudya, anatukula maso naona gulu la Aismaeli akubwera kuchokera ku Giliyadi. Ngamira zawo zinanyamula zonunkhiritsa bwino zakudya zamitundumitundu, ndipo zimenezi ankapita nazo ku Igupto.
26 Yuda da ea eya ilima amane sia: i, “Ninia eya amo medole legele amola amo hou dedebomu da ninima fidisu liligi hame.
Yuda anafunsa abale ake nati, “Kodi tidzapindula chiyani tikapha mʼbale wathuyu ndi kuphimbitsa magazi ake?
27 Ninia da Yousefe amo Isiama: ile dunu ilima bidi lamu da defea. Amane hamosea, ninia da ema se hame imunu. E da ninia eya ninia hu amola maga: me afae hamoi.” Amane dawa: lalu, ea eya ilia da gilisili defea dawa: i.
Bwanji timugulitse kwa Aismaeliwa, koma ife tisamuchite kanthu kalikonse. Ameneyu ndi mʼbale wathu thupi limodzi ndi ife.” Abale ake anavomereza zimenezi.
28 Amalalu, Midia: ne bidi lasu dunu da doaga: loba, Yousefe yolalali da Yousefe amo uli dogoiga fadegale, silifa 20 amoga Yousefe Isiama: ile dunu ilima bidi lai. Amalalu, Isiama: ile dunu da Yousefe Idibidi sogega afugili asi.
Amalonda ena a ku Midiyani ankadutsa pomwepo. Tsono abale ake a Yosefe anamutulutsa Yosefe uja mu chitsime chija ndipo anamugulitsa kwa Aismaeli aja pamtengo wa masekeli makumi awiri. Choncho anapita naye Yosefe ku Igupto.
29 Liubene da uli dogoiga bu misini, Yousefe da amo ganodini hame esalu ba: beba: le, bagadewane da: i dione, ea abula gadelai.
Rubeni atabwerera ku chitsime kuja anapeza kuti Yosefe mulibe mʼchitsimemo. Pamenepo iye anangʼamba zovala zake
30 E da yolalali ilima bu misini amane sia: i, “Goi da uli dogoiga hame. Na da adi hamoma: bela: ?”
nabwerera kwa abale ake nati, “Mnyamata uja mulibemo! Nanga ndilowere kuti ine tsopano?”
31 Amalalu, ilia da goudi medole legele, Yousefe ea abula goudi ea maga: me amo ganodini gela sa: i.
Tsono anapha kamwana ka mbuzi, natenga mkanjo wa Yosefe ndi kuwunyika mʼmagazi ake.
32 Ilia da amo abula ilia adama gaguli asili, amane sia: i, “Ninia da amo ba: i dagoi. Amo da dia gofe ea abulala: ?”
Iwo anatenga mkanjo uja nabwerera nawo kwa abambo awo nati, “Ife tapeza mkanjowu. Tawuyangʼanitsitsani muone ngati uli wa mwana wanu.”
33 Ya: igobe da amo abula dawa: i galu. E amane sia: i, “Amo da Yousefe ea: Gasonasu ohe fi da nagofe Yousefe medole legele ea da: i dadegale fasi dagoi.”
Iye anawuzindikira ndipo anati, “Ndi mkanjo wa mwana wanga umenewu! Nyama yakuthengo yolusa yamudya. Mosakayika, mwana wanga Yosefe wakhadzulidwa.”
34 Ya: igobe da se bagade nababeba: le, ea abula gadelale, eboboi abula ea da: i amoga sali. E da ea manoma asigiba: le, eso bagohame digini lalalusu.
Pamenepo Yakobo anangʼamba zovala zake, navala chisaka mʼchiwuno mwake. Iye analira maliro a mwana wake masiku ambiri.
35 Egefelali amola idiwi huluane da ema ea dogo denesima: ne doaga: i, be e da dogo denesimu amola olofomu hamedei ba: i. E amane sia: i, “Na da mae yolesili, da: i dione amola dinana bogomu.” Amaiba: le, ea da: i dioi e da mae yolesili da: i diolalu. (Sheol )
Ngakhale kuti ana ake onse aamuna ndi aakazi anasonkhana kudzamutonthoza, iye anakana kutonthozedwa. Iye anati, “Ayi. Ndidzalira mpaka ndidzapite kwa mwana wanga ku manda.” Choncho Israeli anapitirirabe kulira mwana wake. (Sheol )
36 Be Idibidi sogega, Midia: ne dunu da Yousefe amo Bodifa (hina bagade dunu ea sosodo aligisu dunu ilima hina dunu) ema bidi lai dagoi.
Amidiyani aja anagulitsa Yosefe kwa Potifara, mmodzi mwa nduna za Farao ku Igupto. Potifarayu anali mkulu wa asilikali olonda nyumba ya Farao.