< Mui 17 >

1 A: ibala: me ea lalelegei ode 99 da gidigiloba, Hina Gode da ema misini, amane sia: i, “Na da Gode Bagadedafa. Di da Na hadigi ganodini ahoanoma amola hou moloidafa fawane hamoma.
Pamene Abramu anali ndi zaka 99, Yehova anamuonekera nati, “Ine ndine Mulungu Wamphamvuzonse. Ukhale munthu wochita zolungama nthawi zonse.
2 Na da ania gousa: su hamoi amo dafawane hamomu. Na da digaga dunu bagohame dima imunu.”
Ndipo Ine ndikulonjeza kuti ndidzakupatsa zidzukulu zambiri.”
3 A: ibala: me da beguduli ea odagiga osobo digila sa: i. Amalalu, Gode da ema amane sia: i,
Pomwepo Abramu anadziponya pansi ndipo Mulungu anati kwa iye,
4 “Na gousa: su dima da agoane. Di da dunu fi bagohame ilima eda agoane ba: mu.
“Pangano langa ndi iwe ndi ili: Udzakhala kholo la mitundu yambiri ya anthu.
5 Na da di dunu fi bagohame ilima eda hamoi dagoiba: le, wali dia dio da A: ibala: me hame, be bu afadenene A: ibalaha: me hamoi dagoi.
Sudzatchedwanso Abramu; dzina lako lidzakhala Abrahamu, chifukwa ndakusandutsa kukhala kholo la mitundu yambiri ya anthu.
6 Di da mano bagohame lamu. Di da dunu fi bagohame lamu, amola fi hina bagade dunu bagohame di da lamu.
Ndidzakupatsa zidzukulu zambiri motero kuti mitundu yambiri ya anthu idzatuluka mwa iwe. Mafumunso adzatuluka mwa iwe.
7 Na gousa: su Na da di amola digaga mano dilima Na da hamomu, da mae dagole dialalalumu. Na da dia Gode esalumu amola digaga mano huluane ilia Gode esalumu.
Pangano langa ndi iwe pamodzi ndi zidzukulu za mibado ya mʼtsogolo lidzakhala la muyaya. Ndidzakhala Mulungu wako ndi Mulungu wa zidzukulu zako.
8 Di da wali Ga: ina: ne soge ganodini ga fi dunu agoane ba: sa. Be amo soge huluane, di eso huluane mae yolesili gagulaloma: ne, Na da di amola dia fa: no lalelegemu manolali dilima imunu. Amola Na da ilia Gode esalumu.”
Dziko lonse la Kanaani, limene iwe ukukhala tsopano, ndalipereka kwa iwe ndi kwa zidzukulu zako kuti likhale chuma chanu mpaka muyaya. Ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wa zidzukulu zako.”
9 Amalalu, Gode da A: ibalaha: mema amane sia: i, “Be di da Na gousa: su noga: le ouligima. Di amola digaga fa: no lalelegemu fi.
Kenaka Mulungu anati kwa Abrahamu, “Koma iwe pamodzi ndi zidzukulu zako zobwera pambuyo pako mʼmibado ya mʼtsogolomo, sungani pangano langali.
10 Na gousa: su dima amola dia manolali ilima - amo gousa: su di noga: le agoane ouligima. Dunu huluane dia fi amo ganodini da ilia gadofo damuma: mu.
Iwe pamodzi ndi zidzukulu zako zobwera pambuyo pako muzisunga pangano ili loti mwamuna aliyense pakati panupa azichita mdulidwe.
11 Dilia huluane gadofo damuma: mu. Amo da Na gousa: su dilima amo dawa: digima: ne olelesu gala.
Kuyambira tsopano muzichita mdulidwe ndipo ichi chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi iwe.
12 Dunu huluane dia fi ganodini fa: no lalelegesea, dunu mano huluane da lalelegesea, eso godoane fisili ilia gadofo damuma: mu. Amo da huluanedafa - dia fi amo ganodini lalelegei amola dunu mano ga fi amoga bidilai, amo huluane.
Kuyambira tsopano mpaka mibado ya mʼtsogolomo mwana wamwamuna aliyense pakati panu amene wakwana masiku asanu ndi atatu ayenera kuchita mdulidwe. Awa ndi ana obadwa mʼbanja lako, kapena akapolo ochita kugula ndi ndalama, mlendo osakhala wa mʼmbumba yako.
13 Dia fi amo ganodini lalelegei o ga fi ilima bidi lai - huluane. Na gousa: su defei dilia hu amo ganodini hamoi da eso huluane mae dagole dialalalumu. Amo da Na dilima gousa: su hamoi dagoi olelesa.
Achite mdulidwe ndithu mwana wamwamuna aliyense, mbadwa ngakhale kapolo wochita kugula ndi ndalama, ndipo ichi chidzakhala chizindikiro pa thupi lanu cha pangano langa lamuyaya.
14 Be nowa dunu da dia fi amo ganodini ea hu gadofo hame damui ba: sea, amo dunu da Na gousa: su fi dagoiba: le, fadegale fasima.”
Mwamuna aliyense amene adzakhala wosachita mdulidwe adzachotsedwa pakati pa anthu ake chifukwa sanasunge pangano langa.”
15 Gode da A: ibalaha: mema eno amane sia: i, “Dia uda Selai ema Selai dio bu mae sia: ma. Ea dio da wali Sela.
Mulungu anatinso kwa Abrahamu, “Sarai mkazi wako, sudzamutchanso Sarai; dzina lake lidzakhala Sara.
16 Na da ema hahawane dogolegele ilegemu. Amola e da diagofe lalelegemu. E da dunu fi bagohame ilima eme esalumu. Dunu fi hina dunu bagohame da ema lalelegemu.”
Ndidzamudalitsa ndipo adzakubalira mwana wamwamuna. Ndidzamudalitsa kuti akhale mayi wa mitundu ya anthu; mafumu a anthuwo adzachokera mwa iye.”
17 A: ibalaha: me da beguduli ea odagiga osobo digila sa: ili, hahawane bagade ousu. E da ea dogo ganodini amane sia: i, “Dunu da 100 ode lai, amo mano lamu da defelela: ? Sela amola da ode 90 lai dagoiba: le, mano lama: bela: ?”
Abrahamu anadzigwetsa pansi pamaso pa Yehova, Iye anaseka nati, “Kodi munthu wa zaka 100 nʼkubala mwana? Kodi Sara adzabereka mwana pa msinkhu wa zaka makumi asanu ndi anayi?”
18 E da Godema amane adole ba: i, “Isiama: ile da na fi ganodini na sogebi lamu da defeala: ?”
Ndipo Abrahamu anati kwa Mulungu, “Bwanji mumudalitse Ismaeli.”
19 Be Gode bu adole i, “Hame mabu! Dia uda Sela da dia manodafa dia da: i amoga hamoi, amo lalelegemu. Di da ema Aisage dio asulima. Na da Na gousa: su ema amola egaga mano ilima hamoi, amo hamedafa yolesimu. Amo gousa: su da mae dagole eso huluane dialalalusu liligi.
Koma Mulungu anati, “Ayi, koma mkazi wako Sara adzakubalira mwana wamwamuna, ndipo udzamutcha Isake. Ndidzasunga pangano langa losatha ndi iyeyu komanso ndi zidzukulu zobwera pambuyo pake.
20 Dia adole ba: su amo Isiama: ile fidima: ne Na da nabi dagoi. Amaiba: le, Na da ema amola hahawane dogolegele ilegemu. Na da ema mano bagohame imunu. Ema da fi hina bagade dunu fagoyale amo lalelegemu, amola ea mano da dunu fi bagadedafa hamomu.
Koma za Ismaeli, ndamva. Ndidzamudalitsadi, ndipo adzakhala ndi zidzukulu zambiri. Iye adzakhala kholo la mafumu khumi ndi awiri ndipo mwa iye mudzatuluka mtundu waukulu wa anthu.
21 Be Na gousa: sudafa da dia mano Aisage ema dialumu. Waha oubi wewaba amo ode enoga e da Selama lalelegemu.”
Koma ndidzasunga pangano langali ndi Isake amene Sara adzakubalira pofika nthawi ngati ino chaka chamawa.”
22 Gode da A: ibalaha: mema sia: i dagoiba: le, yolesili asi.
Atatha kuyankhula, Mulungu anamuchokera Abrahamu.
23 Amo esoga A: ibalaha: me da hedolo nabasu hou hamoi. E da Isiama: ile amola ea fi dunu huluane amola dunu da ea fi amo ganodini lalelegei amola udigili hawa: hamosu dunu e bidi lai, amo huluane ilia gadofo damui.
Tsono Abrahamu anachita mdulidwe mwana wake Ismaeli ndi onse amene anali mʼbanja lake, mbadwa ngakhale kapolo ochita kugula ndi ndalama, monga mmene Mulungu analamulira.
24 A: ibalaha: me da lalelegele, ode 99 doaga: le, gadofo damui.
Abrahamu anali ndi zaka 99 pamene anachita mdulidwe,
25 Amola Isiama: ile da ea ode 13 amoga gadofo damui ba: i.
ndipo mwana wake Ismaeli anali ndi zaka khumi ndi zitatu;
26 A: ibalaha: me amola egefe Isiama: ile ela da eso afae ganodini gadofo damui.
Onse, Abrahamu ndi mwana wake Ismaeli, anachita mdulidwe tsiku limodzi.
27 Amola dunu huluane A: ibalaha: me ea sosogo fi ganodini-amo da ea fi ganodini lalelegei, amola ga fi dunu e da bidilai dagoi-huluane da e amola gilisili gadofo damui ba: i.
Aliyense wamwamuna wa pa banja pa Abrahamu, kuphatikizapo iwo amene anabadwira pa banja pomwepo kapena akapolo ogula ndi ndalama kwa alendo, anachita mdulidwe.

< Mui 17 >