< Isigiele 39 >

1 Ouligisudafa Hina Gode da amane sia: i, “Dunu egefe! Misiege fi amola Diubale fi ela ouligisu bagade dunu Goge amoma fofada: nanu, Na da ea ha lai amo ema sia: ma.
“Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala.
2 Na da e delegilisili, ga (north) soge amoga oule asili, Isala: ili goumi doaga: musa: logo gaheabolo ema olelemu.
Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli.
3 Amasea, Na oulali ea fofadi gagui amola dadi ea lobodafa gagui, amo huluane fisima: ne daba fasimu.
Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja.
4 Goge amola ea dadi gagui dunu amola ea fidisu fifi asi gala dunu, ilia da goumi da: iya dafane bogogia: mu. Amola Na da ilia da: i hodo huluane sio amola ohe moma: ne, iligili imunu.
Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo.
5 Ilia da soge hame fufua amoga dafane bogogia: mu. Na, Ouligisudafa Hina Gode da sia: i dagoi.
Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
6 Na da Ma: igoge sogega amola soge hano wayabo bagade bega: amo ganodini dunu da olofole esalebe, amo sogega lalu bagade didimu. Amasea, dunu huluane da Na da Hina Gode dawa: mu.
Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
7 Na da Na fi Isala: ili ilia da Na hadigi Dio dawa: ma: mu, amola ilia da Na Dio bu mae wadela: ma: mu. Amasea, fifi asi gala da Na da Hina Gode, Isala: ili fi ilia Hadigi Gode, amo dawa: mu.”
“Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli.
8 Ouligisudafa Hina Gode da amane sia: i, “Amo eso Na sia: i da dafawanedafa misunu.
Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.
9 Isala: ili fi dunu moilai ganodini esalebe da gadili asili, gegesu liligi fisi amo laluyale, lidili didimu. Ilia da gegesea gaga: su amola oulali amola sou amola dadi amola gigi amoga lalu didisa heda: le, dialeawane, ode fesu lalu didima: ne defele dialebe ba: mu.
“Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
10 Ilia da gegesu liligi fisi amoga lalu didibiba: le, ifabia o iwilaga lalu hame habela masunu. Ilia da dunu amo da ilima doagala: le ilia liligi lai, amo ilima doagala: le, ilia liligi gegenana lamu.” Ouligisudafa Hina Gode da sia: i dagoi.
Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
11 Hina Gode, da amane sia: i, “Amo hou hamoi dagoi ba: sea, Na da Goge ema bogoi uli dogosu Isala: ili soge ganodini imunu. Amo da Logoga Ahoasu Dunu Fago, Bogoi Hano Wayabo gusudili dialebe ba: mu. Isala: ili dunu da Goge amola ea dadi gagui dunu huluane amogawi uli dogolesimu amola amo fago ilia da ‘Goge ea Dadi Gagui Wa: i Fago’ dio asulimu.
“Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
12 Ilia da amo bogogia: i uli dogolaleawane amola osobo foloma: ne hamonaneawane, oubi fesu da udumu.
“Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko.
13 Dunu huluane Isala: ili soge ganodini da amo uli dogosu hou fidimu. Amola ilia da amo hamobeba: le, Na da Na hasalasisu eso amoga ilima nodomu. Na, Ouligisudafa Hina Gode, da sia: i dagoi.
Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
14 Amo oubi fesu baligili, fa: no ilia da dunu amo soge huluane amodili bogoi da: i hodo dialebe amo hogole, osobo foloma: ne uli dogoma: ne, ilegemu.
“Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo.
15 Ilia da sogega amodili ahoasea, bogoi gasa ba: sea, amo uli dogosu dunu ilia da amo gasa lale, Goge ea Dadi Gagui Wa: i Fago amo ganodini uli dogoma: ne, ifa ado bugisimu.
Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
16 (Ilia da moilai amo soge gadenene dialebe, amoga Goge Dadi Gagui Wa: i dawaloma: ne dio asulimu). Amasea, soge da fofoloi ba: mu.”
(Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.
17 Ouligisudafa Hina Gode da nama amane sia: i, “Dunu egefe! Ohe fi amola sio fi huluane, ilia da gobele salasu ha: i nabe Na da iligili ima: ne momagesa, amo manusa: misa: ne wele sia: ma. Amo da lolo nasu bagadedafa Isala: ili goumia hahamoi ba: mu. Ilia da hu amola maga: me manu.
“Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi.
18 Dadi gagui dunu amola osobo bagade ouligisu dunu, da sibi gawali amola sibi mano amola goudi amola gawali sefena bulamagau defele fane legei dagoi ba: mu. Sio amola ohe da ilia maga: me amola hu manu.
Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani.
19 Na da amo dunu gobele salasu agoane medole legesea, ohe fi amola sio fi da sadima: ne, ilia sefe manu amola feloama: ne, ilia maga: me manu.
Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera.
20 Na lolo nasu amoga ilia da sadima: ne, hosi amola amoga fila heda: i dunu amola dadi gagui gegesu dunu, bagohame manu. Na, Ouligisudafa Hina Gode da sia: i dagoi.”
Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.
21 Hina Gode da amane sia: i, “Na da fifi asi gala huluane ba: ma: ne, Na Hadigi hou amola Na ilegesu hamoma: ne gasa bagade hou ilima olelemu.
“Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo.
22 Amasea, amoganini, Isala: ili dunu da Na da ilia Hina Gode dawa: mu.
Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
23 Amola fifi asi gala da Isala: ili dunu da Nama wadela: le hamoiba: le, mugululi asi dagoi, amo dawa: mu. Na da ilima baligi fa: le, ilia ha lai ilima hasalasima: ne amola gegesu ganodini medole legema: ne, logo doasi dagoi.
Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo.
24 Ilia da wadela: i amola gugunufi hou bagade hamobeba: le, ilia hamobe defele se iasu. Na da ilima baligifa: i dagoi.”
Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.
25 Ouligisu Hina Gode da amane sia: i, “Be wali, Na da Ya: igobe egaga fi (Isala: ili dunu) ilima bu asigili, ilia bu bagade gaguiwane esaloma: ne fidimu. Na da Na hadigi Dio gaga: mu.
“Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera.
26 Ilia da bu ilia sogedafa amo ganodini hahawane gaga: iwane esalebe ba: sea, ilia da musa: Nama hohonoiba: le gogosia: i, amo gogolemusa: dawa: mu.
Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine.
27 Na da fifi asi gala bagohame ilima Na da Hadigi olelemusa: , Na da Na fi dunu wali ilia ha lai ilia sogega esala, amo fisili masa: ne, bu oule misunu.
Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera.
28 Amasea, Na fi dunu ilia da Na da ilia Hina Gode dawa: mu. Bai Na da ili mugululi masa: ne asunasi, amola wali Na da ili gagadole, ilia sogedafa bu oule ahoa. Afae da hame yolesimu.
Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo.
29 Na da Na A: silibu ilima imunu amola bu eno ilima hamedafa baligi fa: mu. Na, Ouligisudafa Hina Gode da amane sia: i dagoi.”
Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

< Isigiele 39 >