< Isigiele 38 >

1 Hina Gode da nama amane sia: i,
Yehova anandiyankhula kuti:
2 “Dunu egefe! Goge da Misiege fi amola Diubale fi (ela da Ma: igoge soge ganodini esala) ilima hina bagade gala. Ema gasa bagade amane mimogoa fofada: ma,
“Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Gogi, wa ku dziko la Magogi, amene ali kalonga wamkulu wa mzinda wa Mesaki ndi Tubala. Umuyimbe mlandu.
3 Na, Ouligisudafa Hina Gode, da dia ha lai.
Umuwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa ku Mesaki ndi Tubala.
4 Na da di delegilisili, dia magado amoga ma: goga badofalesili, di amola dia dadi gagui dunu huluane hiouginana afia: mu. Dia dadi gagui gilisisu da bagadedafa amola hosi amola amoga fila heda: i dunu da afaedidi abula sala. Dadi gagui dunu huluane afae afae da gaga: su liligi gaguli ahoa, amola gegesu gobihei sedade gaguli ahoa.
Ndidzakuzunguza, ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako. Ndidzakutulutsa iweyo pamodzi ndi gulu lako lonse la nkhondo, akavalo ako ndi okwerapo ake. Onse adzakhala atanyamula zida za nkhondo, zishango ndi malihawo ndipo malupanga awo adzakhala osolola.
5 Be Sie dunu amola Sudane dunu amola Libia dunu da gaga: su liligi gaguli amola gegesu habuga figisili, di amola gilisili ahoa.
Pamodzi ndi iwowo, padzakhalanso ankhondo a ku Perisiya, ku Kusi, ndi ku Puti. Onsewa adzakhala atanyamula zishango ndi kuvala zipewa zankhondo.
6 Gegesu dunu huluane amo da Goma amola Bede Dogama amo ga (north) sogega esalu amoga di amola gilisimusa: misi. Amola fifi asi gala bagohame eno da dima gilisili ahoa.
Padzakhalanso Gomeri pamodzi ndi ankhondo ake onse ndiponso banja la Togarima ndi gulu lake lonse lankhondo lochokera kutali kumpoto. Padzakhaladi mitundu yambiri ya anthu pamodzi ndi iwe.
7 Goge! Dia gegesu liligi amola dadi gagui dunu amo momagema.”
“‘Konzekani! Mukhaledi okonzeka, iweyo pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo limene lakusonkhanira. Iweyo udzawatsogolera pokamenya nkhondo.
8 Ode bagohame gidigilalu, Na da e soge afae amo doagala: ma: ne sia: mu. Amo soge fi da musa: fifi asi gala bagohame amoga afagogole, Na da ili amoga fisili masa: ne, ilia sogega bu oule misi. Amola amo ganodini ili gegesu amoga hame beda: iwane, hahawane esalu. E da Isala: ili goumi (amo da ode bagohame wadela: lesili, dunu hamedene dialebe ba: i, be wali dunu da gaga: iwane esala) amo doagala: mu.
Pakapita masiku ambiri ndidzakuyitana. Zaka zikubwerazi ndidzakulowetsa mʼdziko limene lapulumuka ku nkhondo. Anthu ake anasonkhanitsidwa kuchokera ku mitundu ya anthu ambiri nʼkukakhazikika pa mapiri a Israeli amene kwa nthawi yayitali anali ngati chipululu. Anthu onsewa tsopano akukhala mwa mtendere.
9 E amola ea dadi gagui dunu amola fifi asi gala bagohame ema madelale da isu agoane doagala: le, soge huluane mobi agoane dedebomu.”
Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse ndiponso mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe mudzabwera ngati mphepo yamkuntho. Mudzaphimba dziko lonse ngati mitambo.
10 Ouligisudafa Hina Gode da Goge amoma amane sia: sa, “Amo eso doaga: sea, di da wadela: i ilegesu muni dawa: mu.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limenelo mu mtima mwako mudzabwera maganizo ofuna kukonzekera kuchita zoyipa.
11 Di da asaboi soge amoga dunu da olofole, hame gagili sali moilai amo ganodini esala, amoga doagala: musa: , heda: ma: ne dawa: mu.
Iwe udzanena kuti, ‘Ndikukathira nkhondo dziko la midzi yopanda mipanda; ndikathira nkhondo anthu okhala mwamtendere, anthu amene satchinjirizidwa ndi mipanda, zipata kapena mipiringidzo.
12 Di da dunu fi amo da moilai musa: mugululi dialu amo ganodini esala, amoga doagala: le, ilia liligi huluane gegenana lamu. Na da amo fi amo fifi asi gala afagogoi amoga fisili masa: ne, gilisili, ilia sogedafa amoga bu oule misi. Amola wali ilia da ohe amola soge gaguiwane, osobo bagade logo bulufai amoga esalebe.
Ndipita kukalanda chuma chawo ndi kukafunkha zinthu zawo. Ndidzalimbana ndi midzi imene kale inali mabwinja. Ndikathira nkhondo anthu amene anasonkhanitsidwa kuchokera kwa anthu a mitundu ina. Iwowa ali ndi ziweto zambiri, katundu wochuluka ndiponso amakhala pakatikati pa dziko lapansi.’
13 Siba amola Dida: ne soge dunu amola Siba: ini soge bidi lasu dunu da dima adole ba: mu, ‘Dia da gegenana liligi lamusa: , dia dadi gagui gilisibala: ? Di da silifa amola gouli amola liligi amola ohe fofoi amo gegenana laloba, udigili masusa: dawa: bela: ?’”
Anthu a ku Seba, a ku Dedani ndiponso amalonda a ku Tarisisi pamodzi ndi midzi yake yonse adzakufunsa kuti, ‘Kodi wabwera kudzafunkha? Kodi wasonkhanitsa gulu lako la nkhondo kudzalanda chuma, kudzatenga siliva ndi golide, ziweto ndi katundu kuti zikhale zofunkha zochuluka?’”
14 Amaiba: le, Ouligisudafa Hina Gode da na Gogema Ea sia: adola masa: ne asunasi. Na da ema, Gode Ea sia: amane olelei, “Wali, Na Isala: ili fi dunu da olofole gaga: iwane esaloba,
“Nʼchifukwa chake, iwe mwana wa munthu, nenera ndipo uwuze Gogi kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene anthu anga adzakhala pa mtendere, iwe udzanyamuka.
15 dia sogebi gadafa (north) amoga di dadi gagui wa: i bagade (ilia da fifi asi gala bagohame amoga misi amola huluane da hosi da: iya fila heda: i) amo oule masa.
Udzabwera kuchokera ku dziko lako kutali kumpoto, iwe pamodzi ndi mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe, onse okwera akavalo, gulu lankhondo lalikulu ndi lamphamvu.
16 Di da Na dunu fi Isala: ili ilima, isu ifalabo ladili mabe defele doagala: ma. Amo eso da doaga: sea, Na da di fifi asi gala ilima Na da Hina Gode, amola Na da dia loboga Na Hadigi olelesa amo ilia dawa: ma: ne, Na da di Isala: ili sogega doagala: musa: asunasimu.
Udzabwera kudzalimbana ndi anthu anga Aisraeli ngati mtambo wophimba dziko. Masiku amenewo, iwe Gogi, ndidzabwera nawe kuti ulimbane ndi dziko langa, kuti anthu a mitundu ina andidziwe Ine, pamene ndidzaonetsa kuyera kwanga pa zimene ndidzakuchite iweyo.
17 Na da musa: hemonega, Na hawa: hamosu dunu amo Isala: ili balofede dunu, ilia lafidili, Na da dunu Isala: ili sogega doagala: ma: ne asunasimu sia: i. Amo dunu da di fawane.” Ouligisudafa Hina Gode da sia: i dagoi.
“‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi iwe si amene ndinayankhula za iwe masiku amakedzana kudzera mwa atumiki anga aneneri a Israeli? Pa zaka zambiri iwo ankalengeza kuti ndidzawutsa iwe kuti udzalimbane ndi Israeli.
18 Ouligisu Hina Gode da amane sia: sa, “Eso amoga Goge da Isala: ili soge amoma doagala: le, golili ahoasea, Na da ougi bagade ba: mu.
Zimene chidzachitika pa tsiku limenelo ndi izi: Gogi akadzathira nkhondo dziko la Israeli, mkwiyo wanga woopsa udzayaka. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.
19 Na da ougi bagadeba: le, bebeda: nima bagadedafa Isala: ili sogega iasimu.
Chifukwa cha mkwiyo ndi ukali wanga woyakawo Ine ndikunenetsa kuti pa nthawi imeneyo padzakhala chivomerezi chachikulu mʼdziko la Israeli.
20 Menabo huluane amola sio huluane, amola ohe bagade amola fonobahadi, amola dunu huluane osobo bagadega esalebe, ilia da Naba: le beda: gia: mu. Goumi da agele sa: imu, agolo damui da agele sa: imu amola dobea huluane da mugululi sa: imu.
Nsomba za mʼnyanja, mbalame zamumlengalenga, zirombo zakuthengo, cholengedwa chilichonse chimene chimakwawa pansi, ndiponso anthu onse okhala pa dziko lapansi, adzanjenjemera pamaso panga. Mapiri adzangʼambika, malo okwera kwambiri adzagumuka ndipo khoma lililonse lidzagwa pansi.
21 Na da bidi hamosu bagohame iasibiba: le, Goge da bagade beda: mu. Na, Ouligisudafa Hina Gode da sia: i dagoi. Dia dadi gagui dunu da sinidigili ilia gegesu gobiheiga iligobele gegemu.
Ndidzawutsira Gogi nkhondo kuchokera ku mapiri anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. Anthu a Gogiyo adzaphana okhaokha ndi malupanga.
22 Ilima se ima: ne, Na da olo amola gegene bogogia: su ilima iasimu. Gibu bagade amola mugene amola lalu amola salafa gilisi da dia dadi gagui dunu amola fifi asi gala dunu da dimagale misi ilima gugudili sa: imu.
Ine ndidzamulanga ndi mliri ndi imfa. Ndidzagwetsa mvula yoopsa ya matalala, ndiponso sulufule ndi miyala ya moto pa iye ndi pa asilikali ake ndiponso pa mitundu yambiri ya anthu imene ili naye.
23 Na da amane hamosea, Na da fifi asi gala huluane Na da gasa bagade amola hadigidafa, amo ilima olelema. Amasea, ilia da Na da Hina Gode dawa: mu.”
Motero ndidzadzionetsa kuti ndine wamphamvu ndi woyera. Ndiponso ndidzadziwika pamaso pa anthu a mitundu ina yambiri. Momwemo adzadziwadi kuti Ine ndine Yehova.’”

< Isigiele 38 >