< Isigiele 17 >

1 Hina Gode da nama amane sia: i,
Yehova anayankhula nane kuti,
2 “Dunu egefe! Isala: ili dunuma fedege sia: olelema.
“Iwe mwana wa munthu, aphere mwambi anthu a Israeli ndi kuwawuza fanizo.
3 Amo fedege sia: da Na, Ouligisudafa Hina Gode, Na sia: ilima olelesa. ‘Buhiba bagade ea hinabo nina: hamoi amola ea ougia dalegagili gale, esalebe ba: i. E da hagili asili, Lebanone Goumi da: iya, dolo ifa balu fi.
Uwawuze kuti Ambuye Yehova akuti, chiwombankhanga chachikulu, cha mapiko amphamvu, nthenga zitalizitali zamathothomathotho chinabwera ku Lebanoni. Chinagwira nthambi ya pamwamba pa mtengo wa mkungudza.
4 E da amo gaguli asili, bidi lasu soge amoga asili, bidi lasu dunu ilia moilai bai bagade ganodini ligisi.
Chinabudula msonga yeniyeni ya nthambiyo nʼkupita nayo ku dziko lamalonda ndipo anakayika mu mzinda wa anthu amalonda.
5 Amalalu, e da hawa: a:le gaguli, asili, Isala: ili nasegagi soge, hano dialoba, amo heda: ma: ne bugi.
“‘Kenaka chinatenga mbewu ina ya mʼdziko ndi kukayidzala ku malo a chonde kumene kunali madzi ambiri. Anayidzala ngati mmene amadzalira mtengo wa msondozi.
6 Amo hawa: bugi da heda: le, waini efe gudu magufalesi. Ea amoda da heda: le, buhiba esalebe amoga doaga: musa: heda: i. Amola ea difi da gududafa sa: i. Waini efe da amoda amola lubi, amoga dedeboi dagoi ba: i.
Ndipo inaphuka nisanduka mtengo wa mpesa wotambalala chamʼmunsi. Nthambi zake zinaloza mmwamba kumene kunali chiwombankhangacho, koma mizu yake inalowa pansi. Kotero unakhala mtengo wamphesa ndipo unasanduka wa nthambi ndiponso wa masamba ambiri.
7 Buhiba bagade eno, ea ougia da bagade amola ea hinabo da dialui ba: i. Amalalu waini efe ea difi da ema soyasi, amola ea lubi da ema da: lasi. Waini efe da ea bugi soge da hano fonobahadi fawane gala dawa: i. Amaiba: le, waini efe da buhiba ema hano eno ima: ne dawa: i galu.
“‘Koma panali chiwombankhanga chinanso chachikulu, cha mapiko amphamvu ndi cha nthenga zambiri. Tsopano mtengo wamphesa uja unakhotetsera mizu yake kwa chiwombankhangacho kuchokera pa malo amene unadzalidwa ndipo unatambalitsa nthambi zake kwa chiwombankhangacho kufuna kuthiridwa madzi.
8 Be waini efe ea bugi soge da nasegagi, amola hano galebe soge, amo bugi noga: le heda: le, fage bagohame legema: ne defele galu.
Koma mtengowo unadzalidwa kale pa nthaka yabwino mʼmbali mwa madzi kuti ukhale ndi nthambi zambiri, ubereke zipatso ndi kukhala wokongola.’
9 Amaiba: le, Na, Ouligisudafa Hina Gode da amane adole ba: sa, ‘Amo waini efe da noga: le heda: ma: bela: ? Musa: buhiba ba: i da amo a: le fasili, fage faili fasili, amola amoda bioma: ne damuni fasima: bela: ? Gasa hamedei dunu o gasa hame fifi asi gala da amo a: le fasimu, defele ba: mu.
“Ukawawuze Aisraeli kuti, ‘Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Kodi udzakula bwino? Kodi chiwombankhanga chija sichidzawuzula mizu ndi kubudula nthambi zake kuti ufote? Masamba ake onse anthete adzafota. Sipadzafunika dzanja lamphamvu kapena anthu ambiri kuti awuzule.
10 Dafawane! Amo waini efe da bugi dagoi. Be fo gusudili mabe da e fusia, e da bioma: bela: ? E da ea bugi sogebi amogawi bioma: bela: ?
Ngakhale utawokedwa pena, kodi udzaphuka? Kodi sudzafoteratu mphepo ya kummawa ikadzawomba, kufotera pa malo pamene anawuwokerapo?’”
11 Hina Gode da nama amane sia: i,
Kenaka Yehova anandiyankhula nati:
12 “Amo odoga: su dunu ilia amo fedege sia: ea ba: i dawa: bela: le, ilima adole ba: ma. Ilima amane adoma, Ba: bilone hina bagade da Yelusalemega misini, Yuda hina bagade amola ea eagene ouligisu dunu bu Ba: bilone sogega afugili oule asi.
“Tawafunsa anthu owukirawa kuti, ‘kodi mukudziwa tanthauzo la zinthu zimenezi?’ Uwafotokozere kuti, ‘Mfumu ya Babuloni inapita ku Yerusalemu ndikukatengako mfumu ndi anthu ake otchuka ndi kubwera nawo ku Babuloni.
13 E da hina bagade ea sosogo fi dunu afae lale, ema gousa: su hamoi. E da gasa bagade sia: beba: le, amo dunu da ema mae fisili, fa: no bobogemu sia: i. Ba: bilone hina bagade da Yuda mimogo dunu gagulaligi.
Ndipo anatenga mmodzi wa banja laufumu ndi kuchita naye mgwirizano, ndipo anamulumbiritsa kuti akhale womvera. Inatenganso akulu onse a mʼdzikomo
14 Yuda dunu da bu wa: legadole, ema gegesea o gousa: su hamoi amo fisia, e da amo gagulaligi dunu medole legemusa: sia: i.
kuti ufumu wa dzikolo utsitsidwe, usadzaphukenso, koma kuti ukhalepobe posunga pangano limene unachita.
15 Be Yuda hina bagade da odoga: le, sia: alofele iasu dunu amo Idibidi sogega, hosi amola gegesu dunu lama: ne, asunasi. E da agoane hamomu da defeala: ? E da gousa: su fi dagoiba: le, se bidi iasu ba: mu.
Koma mfumu inawukira mfumu ya ku Babuloni potumiza nthumwi ku dziko la Igupto kukatenga akavalo ndi gulu lalikulu la nkhondo. Kodi mfumu yotereyi ingapambane? Kodi wochita zinthu zoterezi angapulumuke? Kodi angaphwanye mgwirizano ndi kupulumuka?
16 Na, Ouligisudafa Fifi Ahoanusu Hina Gode, Na da dafawane sia: sa! Amo Yuda hina bagade da Ba: bilone soge ganodini bogomu. Bai e da ea dafawane sia: i gua: su, amola gousa: su e da Ba: bilone hina bagade (amo da e Yuda soge ouligima: ne hina bagade ilegei) amoma hamoi bu fi dagoi.
“‘Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, mfumuyo idzafera ku Babuloni, mʼdziko la mfumu imene inayika pa mpando waufumu. Inapeputsa lumbiro lake nʼkuphwanya pangano limene inachita ndi mfumu inayo.
17 Idibidi hina bagade ea gegesu dunu gilisisu da gasa bagade. Be Ba: bilone gegesu dunu da Yelusaleme fi dunu medole legema: ne, gegesu hagali dogosea, amola moi mogosa heda: su hamosea, Idibidi hina bagade da ili gaga: mu hamedei ba: mu.
Farao ndi gulu lake lankhondo lamphamvu sadzatha kumuthandiza pa nkhondo, pamene mfumu ya Babuloni idzapanga mitumbira ya nkhondo ndi nsanja za nkhondo kuti iwononge miyoyo yambiri.
18 E da ea dafawane ilegele sia: i, amola gousa: su hamoi amo fi dagoi. Amo huluane hamobeba: le, e da hobeale masunu hamedei ba: mu.”
Mfumu ya ku Yuda inanyoza lumbiro lake pophwanya pangano. Inalonjeza komabe sinatsatire malonjezo ake. Choncho sidzapulumuka.
19 Ouligisudafa Hina Gode da amane sia: sa, “Na da Fifi Ahoanusu Hina Gode amola Na da dafawane sia: sa, e da gousa: su Na Dioba: le dafawane dialoma: ne sia: i, amo fiba: le, Na da ema se bidi imunu.
“‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndithu pali Ine wamoyo, Ine ndidzalanga mfumu imeneyi chifukwa inanyoza lumbiro langa, ndi kuphwanya pangano langa.
20 Na da fedege agoane, e sa: ima: ne, efe gelesimu. Na da e Ba: bilone sogega oule asili, amogai ema se bidi imunu. Bai e da Na sia: defele hame hamosa.
Ndidzayitchera ukonde ndipo idzakodwa mu msampha wanga. Ndidzapita nayo ku Babuloni ndi kuyilanga kumeneko chifukwa inali yosakhulupirika kwa Ine.
21 Ea baligili noga: i dadi gagui dunu da gegenana bogomu, amola hame bogoi esalebe da afagogole fasi dagoi ba: mu. Amasea, dilia da, Na, Hina Gode da sia: i dagoi, amo dawa: mu.”
Asilikali ake onse amene akuthawa adzaphedwa ndi lupanga, ndipo opulumuka adzabalalitsidwa ku mbali zonse. Ndipo iwo adzadziwa kuti Ine Yehova ndayankhula.
22 Ouligisu Hina Gode da amane sia: sa, “Na da dolo ifa sedade amo ea balu asaboi hedofale, goumi sedade amo da: iya sagamu.
“‘Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndidzatenga nthambi pamwamba penipeni pa mkungudza ndi kuyidzala; ndidzathyola nthambi yanthete kuchokera pa nthambi zapamwamba penipeni ndi kuyidzala pamwamba pa phiri lalitali.
23 Na da Isala: ili ea sedadedafa goumi da: iya sagamu. Ifa da heda: le, amoda afufuli, dulu legele, ifi ida: iwane ba: mu. Sio fi huluane da amo ea ougiha esalumu.
Ndidzayidzaladi pa phiri lalitali la Israeli. Idzaphuka nthambi ndi kubereka zipatso. Choncho idzasanduka mkungudza wamphamvu. Mbalame za mtundu uliwonse zidzamanga zisa zawo mʼmenemo; zidzapeza malo okhala mu mthunzi wa nthambi zake.
24 Ifa huluane soge ganodini lefulubi, da Na da Hina Gode dawa: mu. Na da ifa sedade aba sala. Amola Na da ifa nono bu heda: le alema: ne hamosa. Na da ifa gahe bioma: ne hamosa amola bioi ifa bu gahegima: ne hamosa. Na, Hina Gode, da sia: i dagoi. Na da Na hamoma: ne sia: i defele dafawane hamomu.”
Mitengo yonse yakuthengo idzadziwa kuti Ine ndine Yehova amene ndimafupikitsa mitengo yayitali ndi kutalikitsa mitengo yayifupi. Ndimawumitsa mitengo yabiriwiri ndi kubiriwitsa mitengo yowuma. “‘Ine Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichita.’”

< Isigiele 17 >