< Eseda 5 >

1 Eseda da ha: i mae nawane esaloba, eso osodaga, e da ea hina bagade uda abula sanawane, hina bagade ea diasu gagoi ganodini sa: ili, hina bagade ea fisu sesei amo midadi lelu. Hina bagade da amo sesei ganodini, ea fisu da: iya fila heda: le, hagomodini ba: le gale esalebe ba: i.
Tsiku lachitatu Estere anavala zovala zake zaufumu ndipo anayima mʼbwalo la mʼkati la nyumba yaufumu choyangʼana ku chipinda chachikulu cha mfumu. Mfumu inakhala pa mpando waufumu mʼchipinda chachikulu moyangʼana ku chipata cholowera mʼnyumba yaufumu.
2 Hina bagade da hina bagade idua Eseda gadili lelebe ba: beba: le, e da ema asigiba: le, ea gouli hamoi galiamo Eseda ema disiagai. Amalalu, Eseda da misini, galiamo bidiga digili ba: i.
Mfumu itaona Estere atayima mʼbwalomo inakondwera naye ndipo anamuloza ndi ndodo yagolide imene inali mʼdzanja lake. Choncho Estere anayandikira ndi kukhudza msonga ya ndodoyo.
3 Hina bagade Segesisi da amane adole ba: i, “Hina bagade uda Eseda! Di adi lamu? Dia hanai nama adosea, na da amo defele dima imunu. Di da na fifi asi gala dogoa fili la: idi afae lamusa: dawa: sea, na da amo dima imunu.”
Kenaka mfumu inati kwa iye, “Kodi mukufuna chiyani, inu mfumukazi Estere? Nanga pempho lanu ndi chiyani? Ngakhale mutapempha theka la ufumu, ndidzakupatsani.”
4 Eseda da bu adole i, “Hina bagade! Di da hanai galea, na da di amola Ha: ima: ne da lolo nabe na da aligili hamonana, amoga ali hiougimusa: dawa: lala.”
Ndipo Estere anayankha kuti, “Ngati chingakukomereni, mfumu, mubwere lero pamodzi ndi Hamani kuphwando limene ndakonzera inu mfumu.”
5 Hina bagade da amo sia: hahawane nababeba: le, e da Ha: ima: nema e da hedolo Eseda ea lolo nabe amoga misa: ne sia: i. Ela da lolo manusa: asi.
Mfumu inati, “Muwuzeni abwere Hamani msanga, kotero kuti tichite monga Estere wapempha.” Choncho mfumu ndi Hamani anafika kuphwando limene Estere anakonza.
6 Ilia da waini hano nanoba, hina bagade da Esedama amane adole ba: i, “Di da dia hanai nama adole ba: sea, na da dia hanai dima imunu. Di da na fifi asi gala huluane dogoa fili la: idi afae lamusa: adole ba: sea, na da amo defele dima imunu.”
Akumwa vinyo, mfumu inamufunsano Estere kuti, “Kodi ukupempha chiyani tsopano? Chimene uti upemphe ndikupatsa. Chopempha chako ndi chiti? Ngakhale utafuna mpaka theka la ufumu, ndidzakupatsa.”
7
Estere anayankha kuti, “Pempho langa ndi chofuna changa ndi ichi:
8 Eseda da bu adole i, “Di da na adole ba: su amoma asigi galea, na da di amola Ha: ima: ne aligili aya ha: i manu aowamu. Amogala, na dawa: i liligi dima adole imunu.”
Ngati mwandikomera mtima mfumu ndiponso ngati chingakukondweretseni mfumu kundipatsa chimene ndapempha ndi kuchita zimene ndifuna, mubwere mawa inu mfumu ndi Hamani ku phwando limene ndidzakukonzerani. Ndipo ndidzakuyankhani mfumu funso lanu.”
9 Ha: ima: ne da lolo nabe yolesili, hahawane asi. Be e da Modigai da hina bagade ea diasu logo holei gadenene esalebe ba: i. Amola Modigai da hame wa: legadobeba: le, amola ema hame nodobeba: le, Ha: ima: ne da ougi bagade ba: i.
Tsiku limenelo Hamani anatuluka wokondwa ndi wosangalala kwambiri. Koma ataona Mordekai pa chipata cha mfumu ndi kuti sanayimirire kapena kumupatsa ulemu pamene iye amadutsa, Hamani anamukwiyira kwambiri,
10 Be e da hi ougi amowane denesini, hi diasuga asi. Amalalu, ea dogolegei dunu ea diasua misa: ne sia: si. Amola e da idua Silese, amo ili gilisili sia: sa: imusa: wei.
komabe Hamani anadziletsa ndipo anapita ku nyumba kwake. Anayitana abwenzi ake pamodzi ndi mkazi wake Zeresi.
11 E da idua amola ea dogolegei, ilia ba: ma: ne hidai. E da muni bagade gagui, amola dunu mano bagohame galu, amola hina bagade da ea hawa: hamosu gaguia gadoi, amola ea hou da eagene ouligisu dunu eno huluane ilia hou baligi dagoi, e agoane hidai.
Hamani anawawuza za kuchuluka kwa chuma chake ndi kuti anali ndi ana aamuna ambiri. Anawawuzanso za mmene mfumu inamukwezera ndi kumuyika kukhala woposa nduna ndi olemekezeka onse.
12 Amola e da eno amane hidale sia: i, “Hina bagade idua Eseda da aya lolo manu, amo da enogili hame, be hina bagade ani fawane hiougi.
Hamani anawonjeza kuti, “Ndipotu si zokhazi. Ndine ndekha amene ndayitanidwa pamodzi ndi mfumu kuphwando limene mfumukazi Estere anatikonzera. Ndipo mawa wandiyitananso pamodzi ndi mfumu.
13 Be na da Yu dunu Modigai amo hina bagade ea diasu logo holei gadenene esalebe ba: lalebeba: le, na da eno liligi noga: i mae dawa: le, hahawane hame ba: sa.”
Koma zonsezi sindikhutira nazo ndikamaona nthawi zonse Myuda uja Mordekai atakhala pa chipata cha mfumu.”
14 Amaiba: le, ea uda amola ea dogolegei da ema amane sia: i, “Di da dia hawa: hamosu dunu ilima, ilia da ifa duni bugi sedade gadole defei 22 mida amoga, dunu hegoa: nesima: ne fugalesu, amo ilia da gaguma: ne sia: ma. Aya hahabe, di da hina bagadema amane adole ba: ma, ‘Dia hawa: hamosu dunu da Modigai bogoma: ne, ifa duni bugi amoga hegoa: nesimu da defeala: ?’ amane dia adole ba: ma.” Ha: ima: ne da amo sia: noga: iale dawa: i. Amaiba: le, e da sia: beba: le, ea hawa: hamosu dunu da amo ifa hegoa: nesisu gagui dagoi.
Mkazi wake Zeresi ndi abwenzi ake onse aja anamuwuza kuti, “Anthu apange mtanda wotalika mamita 23 ndipo mmawa upemphe mfumu kuti anthu akhomerepo Mordekai. Kenaka upite ndi mfumu kuphwando mokondwa.” Hamani anakondwera ndi uphungu umenewu ndipo mtanda unapangidwa.

< Eseda 5 >