< Mousese Ea Malasu 30 >

1 Na da wali logo aduna dilima olelei. Afae da Hahawane dogolegele aligima: ne logo, eno da gagabusu aligima: ne logo. Na sia: i liligi da dilima doaga: sea, amola dilia da ga fi (amoga Hina Gode da dili afagogomu) amo ganodini esalea, dilia da logo aduna na da dilima olelei amo bu dawa: mu.
Madalitso ndi matemberero awa onse amene ndawayika pamaso panu akadzafika pa inu, inu nʼkukumbukira kulikonse kumene Yehova Mulungu wanu wakubalalitsirani pakati pa mitundu ya anthu,
2 Dilia amola diligaga fi da Hina Godema bu sinidigisia amola Ea hamoma: ne sia: i na da wali eso dilima olelesa amo noga: le nabawane hamosea,
ndipo inu pamodzi ndi ana anu nʼkudzatembenukira kwa Yehova Mulungu wanu ndi kumumvera ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse molingana ndi chilichonse chimene ndakulamulani lero lino,
3 amasea dilia Hina Gode da dili gogolema: ne olofomu. E da fifi asi gala amoga E da dili afagogomu, amoga E da bu fadegale, dilia sogega bu oule misini, dili bu hahawane bagade gaguiwane esaloma: ne fidimu.
pamenepo Yehova Mulungu wanu adzakukhalitsani monga kale ndi kukuchitirani chifundo, ndipo adzakusonkhanitsani kukuchotsani ku mitundu ina ya anthu kumene anakubalalitsirani.
4 Dilia da osobo bagade bega: bega: afagogoi ba: sea, dilia Hina Gode da dili bu gilisili, buhagima: ne oule misunu.
Ngakhale atakupirikitsirani ku malekezero a dziko lapansi, adzakusonkhanitsani kuchokera kumeneko ndi kukubweretsaninso.
5 Amasea, dilia da soge amo ganodini dilia aowalali da musa: esalu, amo ganodini dilia da bu fimu. Amola dilia hou huluane amola dilia idi da dilia aowalali ilia musa: hou amola idi bagadewane baligimu.
Adzakubweretsani ku dziko limene linali la makolo anu, ndipo lidzakhala lanu. Iye adzakulemeretsani ndi kukuchulukitsani kupambana makolo anu.
6 Dilia Hina Gode da nabasu dogo amo dilima amola diligaga fi ilima imunu. Amaiba: le, dilia da dilia dogo huluane amoga Godema asigimu amola dilia da amo soge ganodini esalalalumu.
Yehova Mulungu wanu adzasintha mitima yanu pamodzi ndi mitima ya zidzukulu zanu, kotero kuti mudzamukonda ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse, ndipo mudzakhala ndi moyo.
7 Amola E da gagabusu huluane sinidigili, dilima ha lai ilia dili bagadewane higasu amola se iasu, E da amo gagabusu aligima: ne ilima imunu.
Yehova Mulungu wanu adzayika matemberero awa onse pa adani anu amene amadana nanu ndi kukuzunzani.
8 Amola dilia da bu Ema nabasu hou hamomu amola Ea hamoma: ne sia: i huluane na da wali eso dilima olelesa, amo huluane nabawane hamomu.
Inu mudzamveranso Yehova ndi kutsatira malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino.
9 Hina Gode da dilia labe hou huluane hahawane fidimu. Dilia da mano bagohame, ohe fi bagohame amola ha: i manu bagade ba: mu. E da hahawane dilia aowalali fidisu amo defele dili fidimuba: le, hahawane ba: mu.
Pamenepo Yehova Mulungu wanu adzakulemeretsani pa zochita zanu zonse ndipo adzakupatsani ana ambiri, zoweta zambiri, ndiponso mudzakhala ndi zokolola zambiri za mʼdziko lanu. Yehova adzakondwera nanunso ndi kukulemeretsani monga momwe anakondwera ndi makolo anu,
10 Be dilia da Ea sia: noga: le nabasea amola Ea sema huluane Ea olelesu buga ganodini dedei amoga noga: le fa: no bobogesea fawane, amo hahawane hou ba: mu. Dilia da dilia dogo huluane amoga Ema sinidigisia, amo hou ba: mu.
ngati mudzamvera Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ake ndi mawu ake amene alembedwa Mʼbuku ili la Malamulo ndi kutembenukira kwa Yehova Mulungu wanu ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.
11 Hamoma: ne sia: i na da wali eso dilima olelelala da gasa bagade hame amola dilima hamedei liligi hame.
Tsopano zimene ndikukulamulirani leroli sizovuta kapena zapatali.
12 Amo sia: da muagado hame gala. Dilia amo dawa: ma: ne, ‘Nowa da muagado heda: le amo sia: ninia nabima: ne gaguli misa: bela: ?’ amane sia: mu da hamedei.
Sizili kumwamba, kuti muzichita kufunsa kuti, “Kodi ndani amene akwere kumwamba kuti akazitenge ndi kudzatilalikira kuti timvere?”
13 Amola amo sia: da hano wayabo bagade na: iyado bega: hame gala. Dilia da amo dawa: ma: ne, ‘Nowa da hano wayabo bagade degele, amo sia: ninia nabalu fa: no bobogemusa: gaguli misa: bela: ?’ amo sia: mu da hamedei.
Komanso sizili pa tsidya la nyanja, kuti muzichita kufunsa kuti, “Kodi ndani amene adzawoloke nyanja kuti akatenge ndi kudzatilalikira kuti timvere?”
14 Hame mabu! Amo sia: da dilima gadenene diala. Dilia noga: le nabima: ne, amo sia: da dilia lafi ganodini amola dilia dogo ganodini diala.
Ayi, mawu ali pafupi ndi inu; ali mʼkamwa mwanu ndi mu mtima mwanu kuti muwamvere.
15 Na da wali logo aduna dilia afae lalegaguma: ne, dilima olelesa. Logo afae da noga: i, eno da wadela: i. Afae da Esalusu, eno da Bogosu.
Taonani, lero ine ndayika pamaso panu moyo ndi zokoma, imfa ndi chiwonongeko.
16 Dilia da dilia Hina Gode amo Ea hamoma: ne sia: i na da wali eso dilima olelesa amo nabasea, dilia da Ema asigisia, Ema nabasu hou hamosea amola Ea sema amola hamoma: ne sia: i huluane amoma fa: no bobogesea, amasea dilia labe hou huluane da hahawane heda: mu amola dilia idi da bagade heda: mu. Dilia Hina Gode da soge amoga dilia da gesowale fimu amo ganodini dili hahawane dogolegelewane fidimu.
Pakuti lero ndikukulamulani kuti mukonde Yehova Mulungu wanu, kuti muyende mʼnjira zake, ndi kusunga malamulo ake, malangizo ake. Mukatero mudzakhala ndi moyo ndi kuchulukana, ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene mukulowa kukakhalamo.
17 Be dilia da hame nabasea, amola nabasu hou higasea amola eno dunu fa: no bobogebeba: le, eno ogogosu ‘gode’ liligi ilima nodone sia: ne gadosea,
Koma ngati mtima wanu udzatembenuka, inu nʼkukhala osandimvera, ndipo ngati mudzatengeka ndi kupita kukagwadira milungu ina ndi kuyipembedza,
18 na da wali guiguda: sisasu dilima olelesa. Dilia da gugunufinisi dagoi ba: mu. Amo soge Yodane Hano bega: dilia da gesowale fimu, amo ganodini dilia ode bagahame fawane esalumu.
lero ndikulengeza kwa inu kuti mudzawonongeka ndithu. Simudzakhala nthawi yayitali mʼdziko limene mukulowamo pamene mukuwoloka Yorodani kuti mulitenge.
19 Amaiba: le, na da wali dili afae lalegaguma: ne logo aduna olelesa. Afae da Esalusu, eno da Bogosu. Afae da Gode Ea hahawane dogolegelewane fidisu, eno da Gode Ea gagabusu aligima: ne ilegesu. Wali, na da Hebene amola osobo bagade amoma ilia fedege sia: agoane amo dilima hou ba: su dunu elama wele sia: sa. Amaiba: le, dilia Esalusu lalegaguma.
Lero kumwamba ndi dziko lapansi zikhale mboni zodzakutsutsani pakuti ndayika pamaso panu moyo ndi imfa, madalitso ndi matemberero. Tsopano sankhani moyo kuti inu ndi ana anu mukhale ndi moyo.
20 Dilia Hina Godema asigima! Ema nabasu hou hamoma amola mae yolesima! Amasea, dilia amola diligaga fi da ode bagohame, soge amo Hina Gode da dilia aowalali eda A: ibalaha: me, Aisage amola Ya: igobe ilima imunu ilegele sia: i, amo ganodini esalumu.
Ndi kuti mukonde Yehova Mulungu wanu, kumvera mawu ake, ndi kukhulupirika kwa Iye. Pakuti Yehova ndiye moyo wanu, ndipo mudzakhala zaka zambiri mʼdziko limene analumbira kulipereka kwa makolo anu, Abrahamu, Isake ndi Yakobo.

< Mousese Ea Malasu 30 >