< 2 Sa:miuele 12 >

1 Hina Gode da balofede dunu Na: ida: ne amo Da: ibidima sia: ma: ne asunasi. Na: ida: ne da Da: ibidima asili, ema amane sia: i, “Dunu aduna da moilai afae amogawi esalu. Dunu afae da bagade gagui. Be dunu eno da hamedafa gaguiwane hahane esalu.
Tsono Yehova anatumiza Natani kwa Davide. Atafika kwa Davide anati, “Panali anthu awiri mʼmizinda ina, wina wolemera ndi wina wosauka.
2 Bagade gagui dunu da bulamagau bagohame amola sibi bagohame gagui galu.
Munthu wolemerayo anali ndi nkhosa ndi ngʼombe zambiri,
3 Be hame gagui dunu da sibi mano afae fawane galu. Amo e da enoma bidiga lai galu. E da amo fofole, sibi da hame gagui dunu ea mano defele hi diasua hina: mano amola sibi mano amo gilisili, e da hina: ha: i manudafa ema iasu. E da hina: faigelei amoga hano nasu. E da amo sibi mano hi fene gagui dialusu. Sibi mano da idiwi agoane esalu.
koma wosaukayo analibe chilichonse kupatula kankhosa kamodzi kakakazi kamene anakagula. Iye anakasunga ndipo kanakula naye pamodzi ndi ana ake. Kamadya chakudya chake, kamamwera chikho chake ndipo kamagona mʼmanja mwake. Kanali ngati mwana wamkazi kwa iyeyo.
4 Eso afaega, sofe misi dunu afae da bagade gagui dunu ea diasuga doaga: i. Bagade gagui dunu da ema aowamusa: dawa: i, be hina: ohe amoga medomu higa: i galu. Amaiba: le, e da hame gagui dunu ea sibi mano samogene, medole legele, gobele, sofemisi dunugili moma: ne i.”
“Ndipo mlendo anafika kwa munthu wolemera uja, koma munthu wolemerayo sanafune kutenga imodzi mwa nkhosa kapena ngʼombe zake kuti akonzere chakudya mlendo amene anafika kwa iye. Mʼmalo mwake anatenga mwana wankhosa wamkazi wa munthu wosauka uja nakonzera chakudya mlendo uja amene anabwera kwa iye.”
5 Bagade gagui dunu ea hou nababeba: le, Da: ibidi da ougi bagade ba: i. E amane sia: , “Na da Fifi Ahoanusu Hina Gode Ea Dioba: le amane ilegesa. Amo hamobe dunu da bogomu da defea.
Davide anapsa mtima kwambiri chifukwa cha munthuyo ndipo anati kwa Natani, “Pali Yehova, munthu amene anachita zimenezi ayenera kufa basi!
6 E da amo hame gagui dunuma hame asigiba: le, e da ea hamoi defele ema biyaduyale agoane dabe ima: mu.”
Iye ayenera kulipira mwana wankhosa wamkaziyo kanayi, chifukwa anachita chinthu chimenechi ndipo analibe chifundo.”
7 Na: ida: ne da Da: ibidima amane sia: i, “Amo dunu da di fawane. Amola Isala: ili fi ilia Hina Gode da amane sia: sa, `Na da di Isala: ili hina bagade hamoi dagoi. Amola Na da di Soloma gaga: i dagoi.
Kenaka Natani anati kwa Davide, “Munthuyo ndinu! Yehova, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakudzoza kukhala mfumu ya Israeli, ndipo ndinakupulumutsa mʼdzanja la Sauli.
8 Na da ea hina bagade hou amola ea idualali amo samogene, dima i. Na da di Isala: ili amola Yuda ouligima: ne ilegei. Be amo iasu da defele hame ba: i ganiaba, Na da dima aduna agoaiwane bu ia: noba.
Ndinakupatsanso banja la mbuye wako ndiponso akazi a mbuye wako mʼmanja mwako. Ine ndinakupatsanso banja la Israeli ndi Yuda. Ndipo ngati zinthu zonse izi zinali zochepa, Ine ndikanakupatsa zambiri.
9 Amaiba: le, di da abuliba: le Na sia: i hame nabasula: ? Di abuliba: le amo wadela: idafa hou hamobela: ? Dia sia: beba: le, Iulaia da gegesu ganodini fane legei dagoi ba: i. Di da A: mone dunu e medole legema: ne, logo doasi dagoi. Amalalu, di da ea uda lai.
Nʼchifukwa chiyani unanyoza mawu a Yehova pochita chimene chili choyipa pamaso pake? Iwe unakantha Uriya Mhiti ndi lupanga ndipo unatenga mkazi wake kukhala wako. Uriyayo unamupha ndi lupanga la Aamoni.
10 Wali, dia fifi masunu amo ganodini, digaga fi mogili da se nabawane fane legei dagoi ba: mu. Bai di da Na sia: i hame nabasu, amola Iulaia ea uda laiba: le.
Ndipo tsopano lupanga silidzachoka pa nyumba yako, chifukwa unandinyoza ine ndi kutenga mkazi wa Uriya Mhiti kukhala wako.’
11 Na dafawane ilegesa! Dia sosogo fi dunu da dima bidi hamosu bagade ima: ne, Na da hamomu. Na dia udalali amo dima samogene, eno dunuma imunu. E da eso hayoga, dunu huluane ba: lea, ili adole lamu. Amola di da amo hou ba: mu.
“Yehova akuti, ‘Ine ndidzabweretsa tsoka pa iwe lochokera mʼbanja lako. Ndidzatenga akazi ako iwe ukuona ndi kuwapereka kwa wina amene ali pafupi nawe, ndipo iye adzagona ndi akazi ako masanasana Aisraeli onse akuona.
12 Di da wamowane wadela: le hamoi. Be Na da dima se iasu hou amo eso hadigia, Isala: ili dunu huluane ba: ma: ne, hamomu.’”
Iwe unachita zimenezi mwamseri koma Ine ndidzachita izi masanasana Aisraeli onse akuona.’”
13 Da: ibidi da amane sia: i, “Dafawane! Na da Hina Godema wadela: le hamoi dagoi.” Na: ida: ne da bu adole i, “Hina Gode da dima gogolema: ne olofoi. Di da hame bogomu.
Kenaka Davide anati kwa Natani, “Ine ndachimwira Yehova.” Natani anayankha kuti, “Yehova wachotsa tchimo lanu. Simufa ayi.
14 Be dia mano da bogomu. Bai di da amane hamobeba: le, di da Hina Godema mae nodone, higasu.”
Komabe, popeza pochita zimenezi mwachititsa kuti adani a Yehova amunyoze, mwana amene akubalireniyo adzafa.”
15 Amanoba, Na: ida: ne da hi diasuga asi. Hina Gode da hamobeba: le, Iulaia idua amoma Da: ibidima ea mano lalesi, mano da oloi bagade ba: i.
Natani atapita kwawo, Yehova anakantha mwana amene mkazi wa Uriya anabereka ndipo anayamba kudwala.
16 Da: ibidi da mano uhima: ne, Godema sia: ne gadoi. E da ha: i manu bagade higasu amola gasi huluane, hi sesei amo ganodini, hada: i da: iya dialusu.
Davide anapempherera mwanayo kwa Mulungu. Iye anasala chakudya ndipo analowa mʼnyumba mwake nagona pansi usiku wonse.
17 Ea eagene ouligisu dunu da ema asili, e wa: legadoma: ne sia: i. Be e da hame wa: legadoi, amola ili gilisili ha: i manu hamedafa mai.
Akuluakulu a banja lake anayima pambali pake kuti amudzutse, koma iye anakana, ndipo sanadye chakudya chilichonse pamodzi ndi iwo.
18 Hi afae aligili, mano da bogoi. Da: ibidi ea eagene ouligisu dunu da ema adomu beda: i galu. Ilia da amane sia: i, “Mano da esaloba, ninia da Da: ibidima sia: noba, e da ninima bu hame adole iasu. Amaiba: le, ninia da habodane mano da bogoi, ema adoma: bela: ? E da hi gobele hima se iasa: besa: le, ninia da hedolo hame adomu.”
Mwana anamwalira pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Antchito a Davide anaopa kumuwuza kuti mwanayo wamwalira, popeza ankaganiza kuti, “Pamene mwanayu anali ndi moyo, ife tinayankhula Davide koma sanatimvere. Nanga tingamuwuze bwanji kuti mwana wamwalira? Mwina atha kudzipweteka.”
19 Be Da: ibidi da ili gilisili sadoga sia: dabe ba: beba: le, e da mano da bogoi dawa: i galu. Amaiba: le, e da ilima amane adole ba: i, “Mano da bogobela: ?” Ilia bu adole i, “Ma! E da bogoi dagoi.”
Davide anaona kuti antchito ake amanongʼonezana pakati pawo ndipo anazindikira kuti mwanayo wamwalira. Iye anafunsa kuti, “Kodi mwanayo wamwalira?” Iwo anayankha kuti, “Inde wamwalira.”
20 Da: ibidi da hada: i da: iya dialu wa: legadole, hano ulalu, ea dialuma hinabo fesega: nu, abula afadenei. Amalalu, e da asili, Hina Gode Ea diasu ganodini Ema nodone sia: ne gadoi. E da hina bagade diasuga buhagili, ha: i manusa: adole ba: i. Ilia da ha: i manu ema gaguli misini, e da amogaluwane hedolo mai.
Ndipo Davide anayimirira. Anakasamba nadzola mafuta ndi kusintha zovala zake. Pambuyo pake anapita ku nyumba ya Yehova kukapembedza. Kenaka anapita ku nyumba kwake ndipo atapempha chakudya anamupatsa nadya.
21 Ea eagene ouligisu dunu da ema amane sia: , “Ninia amo hou gogolesa. Mano esalea, di da ema asigiba: le, dinanu amola ha: i mae nawane esalu. Be e da bogobeba: le, di hedolowane wa: legadole, ha: i mai!”
Antchito ake anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuchita zinthu motere? Pamene mwana anali ndi moyo, munkasala chakudya ndi kulira, koma tsopano pamene mwana wamwalira inu mukudzuka ndi kudya!”
22 Da: ibidi da bu adole i, “Ma! E da esaloba na da dinanu amola ha: i mae nawane esalu. Na da Hina Gode Ea nama asigima: bela: le amola mano ea bogomu logo hedofama: bela: le amane hamoi.
Iye anayankha kuti, “Pamene mwana anali ndi moyo ine ndinkasala zakudya ndi kulira. Ine ndinkaganiza kuti, ‘Akudziwa ndani? Yehova atha kundikomera mtima kuti mwanayo akhale ndi moyo.’
23 Be e bogoi dagoiba: le, na da bu ha: i mae nawane esalumu da bai hame gala. Na da amo mano bu esaloma: ne hamomu da hamedei. Na da fa: no ema masunu, be e nama buhagimu da hamedei.”
Koma tsopano wamwalira ndisaliranji chakudya? Kodi ndingathe kumubwezanso? Ine ndidzapita kumene kuli iyeko, koma iye sadzabwerera kwa ine.”
24 Amalalu, Da: ibidi da idua Ba: desiba ea dogo denesi. E da ela gilisili golale, amalu dunu mano eno lalelegei. Da: ibidi da amo mano ea dio Soloumane asuli. Hina Gode da amo manoma asigi galu.
Ndipo Davide anatonthoza mkazi wake Batiseba, napita kwa iye ndi kugona naye. Iye anabereka mwana wamwamuna, ndipo anamutcha dzina lake Solomoni. Yehova ankamukonda iye.
25 E da balofede dunu Na: ida: nema, e da amo mano ea dio Yedidaia (dawa: loma: ne da `Hina Gode da ema asigisa’) amo asulima: ne sia: i. Bai Hina Gode da ema asigi galu.
Ndipo chifukwa chakuti Yehova ankamukonda iyeyo, Yehovayo anatumiza mawu kwa mneneri Natani kuti akamutchule Yedidiya.
26 Be Youa: be da La: ba (A: mone sogega moilai bai bagade) amo doagala: lalu. Amo fedele lamu da gadenei ba: i.
Pa nthawi imeneyi Yowabu anamenyana ndi Raba ku Amoni ndipo analanda nsanja yaufumu.
27 E da Da: ibidima sia: adola ahoasu dunu ilia ema amane sia: na masa: ne asunasi, “Na da La: ba doagala: lalu, amo ea hano sagai huluane sasamogene lai dagoi.
Ndipo Yowabu anatumiza amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Ine ndamenyana ndi Raba ndipo ndatenga zitsime zake za madzi.
28 Amaiba: le, dia dadi gagui dunu gagadole, disu amo moilai doagala: le fefedele lama. Bai dunu da na hame be difa fefedele lai dagoi, amo sia: mu da defea.”
Ndipo tsopano sonkhanitsani asilikali onse ndipo muzungulire mzindawo ndi kuwulanda.”
29 Amaiba: le, Da: ibidi da ea dadi gagui dunu gagadole, La: ba moilai bai bagade amo doagala: lalu fefedele lai.
Kotero Davide anasonkhanitsa ankhondo onse ndipo anapita ku Raba kukawuthira nkhondo ndi kuwulanda.
30 E da A: mone loboga hamoi ogogosu ‘gode’ Miligome, amo ea dialumaga gouli habuga lai. Amo habuga ea dioi defei da 35 gilougala: me agoane amola amoga gele noga: idafa legei ba: i. Da: ibidi da amo gele noga: i habuga lale, ea habuga da: iya legei. Amola amo moilaiga e da liligi bagohame odagiaba lasu.
Davide anachotsa chipewa chaufumu pamutu pa mfumu yawo ndipo Davide anavala chipewacho. Chipewacho chinkalemera makilogalamu asanu agolide, ndiponso chinali ndi miyala yokongola. Iye anatenga katundu wambiri kuchokera mu mzindawo,
31 Amalalu, e da La: ba dunu huluane udigili hawa: hamoma: ne logei. E logebeba: le, ilia da sasahei, gula uwasu amola goahei amoga hamosu amola diasu gagumusa: osoboga `baligi’ hamosu. E da A: mone soge moilale gagaiga esalebe dunu amo huluane hawa: hamoma: ne logei. Amalalu, e amola ea dunu da Yelusaleme moilaiga buhagi.
ndipo anatulutsa anthu amene anali mʼmenemo, nawayika kuti azigwira ntchito ya macheka, yosula makasu ndi nkhwangwa, ndiponso yowomba njerwa. Davide anachita izi ndi mizinda yonse ya Aamoni. Kenaka iye pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo anabwerera ku Yerusalemu.

< 2 Sa:miuele 12 >