< 1 Hina 2 >

1 Da: ibidi da bogomu galu, e da ea mano Soloumane ema misa: ne sia: i. E da ema dagomusa: fada: i sia: su amane sia: i,
Davide ali pafupi kumwalira, analangiza mwana wake Solomoni kuti:
2 “Na bogomu eso da doaga: i. Di mae beda: ne, gasa fili aligima.
“Ndatsala pangʼono kupita kumene munthu wina aliyense amayenera kupitako. Tsono khala wamphamvu, uvale zilimbe,
3 Amola dia Hina Gode Ea hamoma: ne sia: be amo defele hamoma. Ea sema amola hamoma: ne sia: i Mousese ea Sema Buga ganodini dedei, amo defele hamoma. Di da amane hamosea, di da habodili ahoasea amola di adi hamosea, hahawane ba: mu.
ndipo uzichita zimene Yehova Mulungu wako amafuna, uziyenda mʼnjira zake, uzisunga malangizo ndi malamulo ake monga momwe zinalembedwera mʼMalamulo a Mose, kuti zonse zimene udzachite zidzakuyendere bwino kulikonse kumene udzapite.
4 Hina Gode da nama amane ilegele sia: i, ‘Digaga fi da Na sia: amo mae fisili dafawane noga: le nabawane hamosea, ilia da Isala: ili fi ouligilalumu. Di da Ea sia: nabawane hamosea, Hina Gode da amo ilegele sia: i dafawane dima hamomu.
Ndipo Yehova akwaniritse zimene anandilonjeza kuti, ‘Ngati zidzukulu zako zidzakhala mosamala, niziyenda mokhulupirika pamaso panga ndi mtima wawo wonse ndi moyo wawo wonse, sudzasowa munthu wokhala pa mpando waufumu wa Israeli.’
5 Eno adomu gala. Dia dawa: amo Youa: be da Isala: ili dadi gagui wa: i ouligisu dunu aduna, (Ne ea mano A: bena amola Yidie ea mano Ama: isa) medole legeiba: le, na hou wadela: lesi. Ela da gegesu esoga dunu eno ha lai dunu medole legei. Be Youa: be da olofosu esoga amo dunu elama dabe i. E da wadela: i hame hamosu dunu medole legei. Be waha da amo se nabasu na fawane da naba.
“Tsono iwe ukudziwanso zoyipa zimene Yowabu mwana wa Zeruya anandichitira pakupha atsogoleri awiri a ankhondo a Israeli, Abineri mwana wa Neri ndi Amasa mwana wa Yeteri. Iye anawapha ndi kukhetsa magazi nthawi ya mtendere ngati nthawi ya nkhondo, ndipo anapaka magazi amenewo pa lamba wa mʼchiwuno mwake ndi pa nsapato za ku mapazi ake.
6 Dia hamomu amo di dawa: Amo dunu medole legema: ma. (Sheol h7585)
Iwe uchite kwa iye molingana ndi nzeru zako, koma usalole kuti afe ndi ukalamba ndi kupita ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
7 Be Gilia: de dunu Basila: iai egefelali ilima asigima, amola ili ouligima. Bai na da diaola A: basalomema hobeabeba: le, ilia da nama asigi galu.
“Koma ana a Barizilai wa ku Giliyadi uwakomere mtima ndipo uwalole kuti akhale mʼgulu la anthu amene azidya pamodzi nawe. Pakuti anandisamalira pamene ndinkathawa mʼbale wako Abisalomu.
8 Dunu eno dawa: ma-amo Simiai (Gila ea mano, e da Bahiulimi moilai Bediamini soge ganodini esalu). Na da Ma: ihana: ime sogega ahoanoba, e da nama gasa bagadewane gagabui aligima: ne ilegei. Be na da buhagilaloba, e da Yodane Hano amogai na gousa: i. Amola na da Hina Gode Ea Dioba: le, e hame medole legemu, amane dafawane ilegele sia: i.
“Ndipo kumbukira kuti uli ndi Simei mwana wa Gera, wa fuko la Benjamini wochokera ku Bahurimu, amene ananditemberera koopsa tsiku limene ndimapita ku Mahanaimu. Atabwera kudzakumana nane ku Yorodani, ine ndinalumbira mʼdzina la Yehova kuti, ‘Sindidzakupha iwe ndi lupanga.’
9 Be di da ema dawama: ne se dabe ima. Dia hamomu amo di dawa: Amo dunu medole legema: ne sia: ma.” (Sheol h7585)
Koma tsopano usamuyese ngati munthu wosalakwa. Iwe ndiwe munthu wanzeru. Udzadziwa choti uchite naye. Ngakhale ndi wokalamba, aphedwe ndithu.” (Sheol h7585)
10 Da: ibidi da bogole, ilia da ea da: i hodo Da: ibidi Moilai Bai Bagade ganodini uli dogonesi.
Tsono Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Mzinda wa Davide.
11 E da Isala: ili soge ode 40 agoane ouligisu hamoi. Amo ouligisu ganodini, e da ode fesuale agoane Hibalone moilai bai bagadega esala ouligilalu, amola ode 33 agoane Yelusaleme moilai bai bagadega esala ouligisu hamoi.
Iyeyo nʼkuti atalamulira Israeli kwa zaka makumi anayi. Ku Hebroni analamulira zaka zisanu ndi ziwiri ndipo ku Yerusalemu analamulira zaka 33.
12 Soloumane da eda Da: ibidi ea bagia hina bagade hou lai. Ea ouligilalusu da gasa bagade ba: i.
Choncho Solomoni anakhala pa mpando waufumu wa abambo ake Davide, ndipo ufumu wake unakhazikika kwambiri.
13 Amalalu, A:dounaidia (ea ame da Ha: gide) da Ba: desiba (Soloumane eme) ema asi. Ba: desiba da ema amane sia: i, “Di da olofolewane nama misibala: ?” E bu adole i, “Ma! Na da olofoiwane misi.”
Tsono Adoniya, mwana wa Hagiti, anapita kwa Batiseba, amayi ake a Solomoni. Batiseba anamufunsa kuti, “Kodi wabwera mwamtendere?” Iye anayakha kuti, “Eya, ndi zamtendere.”
14 Amalalu, e da amane sisa: asi, “Na da dima adole ba: mu gala.” Ba: desiba da amane adole ba: i, “Di da adi sia: ma: bela: ?”
Ndipo iye anawonjezera kunena kuti, “Ndili ndi mawu oti ndiyankhule nanu.” Batiseba anayankha kuti, “Yankhula.”
15 E bu adole i, “Di dawa: Na da hina bagade hou lamu da defea galu. Amola Isala: ili dunu huluane da na Isala: ili fi ouligima: ne dawa: i galu. Be hou eno da doaga: i. Amola Hina Gode Ea hanaiba: le, naeya da hina bagade hou lai dagoi.
Tsono Adoniya anati, “Monga inu mukudziwa, ufumu unali wanga. Aisraeli onse ankayembekezera kuti ine ndidzakhala mfumu yawo. Koma zinthu zinasintha ndipo ufumu wapita kwa mʼbale wanga; pakuti wapatsa iye ufumuwu ndi Yehova.
16 Amola wali na da adole ba: su afae fawane gala. Na hanai logo mae hedofama.” Ba: desiba da bu adole ba: i, “Dia hanai da adila: ?”
Tsono ndili ndi pempho limodzi kwa inu. Musandikanize ayi.” Batiseba anati, “Nena.”
17 E bu adole i, “Hina bagade Soloumanema amane adole ba: ma (e da dia adole ba: mu hame hedofamu) ‘Siuneme a: fini A: bisia: ge amo A: dounaidia lama: ne ima.’”
Adoniya anapitiriza kunena kuti, “Chonde, inu mupemphe mfumu Solomoni kuti andipatse Abisagi wa ku Sunemu kuti akhale mkazi wanga pakuti mukapempha inu sadzakukanizani.”
18 Ba: desiba da amane sia: i, “Defeawane! Na da hina bagadema dia hanai amo adosimu.”
Batiseba anayankha kuti, “Chabwino. Ndidzakuyankhulira kwa mfumu.”
19 Amaiba: le, Ba: desiba da A: dounaidia ea adole ba: su adosimusa: , hina bagadema asi. Hina bagade da ea ame yosia: musa: , wa: legadole begudui. Amalalu, e da ea fisuga fili, amola e da fisu eno gaguli misa: ne sia: i. Amoga Ba: desiba da ea lobodafa la: ididili fi.
Batiseba atapita kwa Mfumu Solomoni kukayankhula naye mʼmalo mwa Adoniya, mfumu inanyamuka kukumana naye, ndipo inaweramira amayi akewo, kenaka inakhala pa mpando wake waufumu. Iye anayitanitsa mpando wina kuti amayi ake akhalepo ndipo anakhala pansi ku dzanja lake lamanja.
20 E amane sia: i, “Na da dima adole ba: su fonobahadi gala. Na hanai logo mae hedofama.” Soloumane da amane adole ba: i, “Defea, ame! Dia hanai da adila: ? Na da dia hanai hame hihimu.”
Amayi akewo anati, “Ndikufuna ndikupempheni kanthu kakangʼono. Chonde musandikanize.” Mfumu inayankha kuti, “Pemphani amayi, ine sindikukanizani.”
21 E bu adole i, “A: fini A: bisia: ge amo dia ola A: dounaidia lama: ne ema ima.”
Ndipo amayiwo anati, “Mulole kuti Abisagi wa ku Sunemu akhale mkazi wa mʼbale wanu Adoniya.”
22 Hina bagade da amane sia: i, “Dia abuliba: le A: bisia: ge amo ema ima: ne sia: sala: ? Di da agoane sia: beba: le, di da defele na hina bagade hou ema ima: ne sia: sa. Bai e da naola. Amola gobele salasu dunu A: baia: da amola Youa: be da e fuligala: sa.”
Koma Mfumu Solomoni inayankha amayi ake aja kuti, “Chifukwa chiyani mukupemphera Adoniya Abisagi wa ku Sunemu? Mungathenso kumupemphera ufumu pakuti iyeyu ndi mkulu wanga ndipo mupemphereninso wansembe Abiatara ndi Yowabu mwana wa Zeruya!”
23 Amalalu, Soloumane da Hina Gode Ea Dioba: le dafawane ilegele sia: i, “A: dounaidia da amo adole ba: beba: le, na da e dabema: ne medole legema: ne sia: sa. Na da amo hame hamosea, Gode da na medole legemu da defea.
Pamenepo Mfumu Solomoni inalumbira mʼdzina la Yehova kuti, “Mulungu andilange ine koopsa ngati Adoniya saphedwa chifukwa cha pempho lakeli!
24 Hina Gode da hamobeba: le, na da gasa fili, na ada Da: ibidi ea hina bagade fisu amoga hahawane ouligilala. Gode da Ea ilegele sia: i hame gogolei. E da Isala: ili ouligisu hou, na amola nagaga fi ninima i dagoi. Na da Hina Gode Esala amo Ea Dioba: le dafawane ilegele sia: sa. Wali esodafa, A:dounaidia da medole legei dagoi ba: mu.”
Tsono pali Yehova wamoyo, amene anandikhazikitsa ine pa mpando waufumu wa abambo anga Davide ndi kundipatsa ufumu monga analonjezera, Adoniya aphedwa lero lomwe lino!”
25 Amaiba: le, hina bagade Soloumane da sia: beba: le, Bina: ia da gadili asili, A:dounaidia medole legei.
Choncho Mfumu Solomoni inalamula Benaya mwana wa Yehoyada ndipo anakantha Adoniyayo, nafa.
26 Amalalu, hina bagade Soloumane da gobele salasu dunu A: baia: dama amane sia: i, “Dia soge gabolo lai A: nadode amoga masa. Na da di medole legemu da defea gala, be na wahadafa di hame medole legemu. Bai di da na ada Da: ibidi musa: se nabaloba, di da e fidilalu amola Hina Gode Ea Gousa: su Sema Gagili amo ouligilalu.”
Ndipo mfumu inati kwa Abiatara wansembe, “Pita ku Anatoti ku minda yako chifukwa ndiwe woyenera kufa, koma sindikupha tsopano, chifukwa unkanyamula Bokosi la Chipangano la Ambuye Yehova pamaso pa abambo anga Davide ndipo unazunzika limodzi ndi abambo angawo.”
27 Amalalu, Soloumane da A: baia: da ea Hina Godema gobele salasu hawa: hamonanu amo fadegai. Amola Hina Gode da musa: Siailou moilaiga sia: i, (1 Sa: miuele 2:27-36 amo gobele salasu dunu Ilai amola ea fi da wadela: lesi dagoi ba: mu), amo sia: da didili hamoi dagoi ba: i.
Kotero Solomoni anachotsa Abiatara pa udindo wokhala wansembe wa Yehova, kukwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula za nyumba ya Eli ku Silo.
28 Youa: be da amo hou nabi dagoi. (E da A: dounaidia fuligala: lalu be A: basalome hame fuligala: i.) Amaiba: le, e da Hina Gode Abula Diasuga hobeale, oloda hegomai da: iya ‘hono’ amo gagui.
Yowabu atamva zimenezi anathawira ku tenti ya Yehova ndipo anakagwira msonga za guwa lansembe, popeza Yowabu ndiye anathandiza Adoniya kuwukira koma sanathandize Abisalomu.
29 Soloumane da Youa: be da Hina Gode Abula Diasuga hobeale, oloda ‘hono’ gagulalebe, amo sia: nababeba: le, e da sia: adole iasu dunu ema asunasi. E da Youa: bema ea hobea: i bai amo adole ba: i. Youa: be da bu adole i, “Na da Hina Gode na gaga: ma: ne hobea: i. Bai na Soloumaneba: le beda: i.” Amaiba: le, Soloumane da Youa: be medole legemusa: , Bina: ia asunasi.
Mfumu Solomoni inawuzidwa kuti Yowabu wathawira ku tenti ya Yehova ndipo ali pambali pa guwa lansembe. Tsono Solomoni analamula Benaya mwana wa Yehoyada kuti, “Pita, kamukanthe!”
30 E da Hina Gode Ea Abula Diasuga asili, Youa: bema amane sia: i, “Hina bagade da dima gadili misa amane sia: sa.” Youa: be da bu adole i, “Hame mabu! Na da guiguda: bogomu.” Bina: ia da hina bagadema buhagili, Youa: be ea sia: i ema olelei.
Choncho Benaya analowa mʼtenti ya Yehova ndipo anati kwa Yowabu, “Mfumu ikuti ‘Tuluka!’” Koma iye anayankha kuti, “Ayi, ine ndifera muno.” Benaya anakafotokozera mfumu kuti, “Umu ndi mmene Yowabu wandiyankhira.”
31 Soloumane da amane sia: i, “Youa: be ea sia: i defele hamoma. Amogawi e medole legema amola ea da: i hodo uli dogoma. Youa: be da wadela: i hame hamosu dunu medole legebeba: le, dunu huluane da Da: ibidi amola ea fi ilima ougili fofogadigi. Be e bogosea, ninia da amo se bu hame nabimu.
Pamenepo mfumu inalamula Benaya kuti, “Kachite monga iye wanenera. Ukamukanthe ndi kumuyika mʼmanda. Ukatero udzandichotsera ine pamodzi ndi nyumba ya abambo anga mlandu wa anthu osalakwa amene Yowabu anawapha.
32 Hina Gode da Youa: bema se iasu imunu. Bai e da na ada Da: ibidima mae adole, wadela: i hame hamosu dunu aduna (ela hou noga: i da Youa: be ea hou baligi) amo medole legei. Amo dunu da A: bena (Isala: ili dadi gagui wa: i ouligisudafa) amola Ama: isa (Yuda dadi gagui wa: i ouligisudafa).
Yehova adzamubwezera zomwe anachita pokhetsa magazi, chifukwa iye anakantha ndi lupanga anthu awiri abwino ndi olungama kuposa iye, nawapha, abambo anga Davide osadziwa. Anthu awiriwo ndi Abineri mwana wa Neri, wolamulira gulu lankhondo la Israeli ndi Amasa mwana wa Yeteri, wolamulira gulu lankhondo la Yuda.
33 Amo medole legesu hou ea se dabe iasu da mae fisili, eso huluane, Youa: be amola ea fi ilima doaga: ga: la: lumu. Be Hina Gode da mae fisili, eso huluane Da: ibidi ea fi amo da ea fisuga fisia, ilima hahawane dogolegesu hou amola hasalasisu hou imunu.”
Magazi amene Yowabu anakhetsa akhale pamutu pake ndi pa zidzukulu zake kwamuyaya. Koma pa Davide ndi zidzukulu zake, nyumba yake ndi mpando wake waufumu pakhale mtendere wochokera kwa Yehova kwamuyaya.”
34 Amaiba: le, Bina: ia da Hina Gode Abula Diasuga asili, Youa: be medole legei. Ilia da ea da: i hodo ea moilai sogega uli dogone sali.
Choncho Benaya mwana wa Yehoyada anapita kukakantha Yowabu nʼkumupha ndipo anayikidwa mʼmanda mʼnyumba yakeyake ya ku chipululu.
35 Soloumane da Bina: iama, Youa: be ea sogebi (dadi gagui wa: i ouligisu) i dagoi. Amola e da gobele salasu sogebi (A: baia: da musa: ouligisu) amo Sa: idogema i dagoi.
Mfumu inayika Benaya mwana wa Yehoyada kuti akhale woyangʼanira gulu lankhondo mʼmalo mwa Yowabu ndipo inayika Zadoki kuti akhale wansembe mʼmalo mwa Abiatara.
36 Amalalu, hina bagade da Simiai ema misa: ne sia: i. E da ema amane sia: i, “Dia diasu amo guiguda: Yelusaleme moilai bai bagade amo ganodini gaguma. Amogawi esaloma amola moilai mae yolesima.
Kenaka mfumu inatuma anthu kukayitana Simei ndipo inamuwuza kuti, “Udzimangire nyumba mu Yerusalemu ndipo uzikhala kumeneko, koma usatuluke mu mzinda kupita kwina kulikonse.
37 Be di da moilaiga ga asili, Gidalone Hano amo baligisia, di da bogosu ba: mu. Amola di da dia hamobeba: le fawane amo se dabe iasu ba: mu.”
Tsiku lomwe udzatulukemo ndi kuwoloka Chigwa cha Kidroni, udziwiretu kuti udzafa ndipo magazi ako adzakhala pamutu pako.”
38 Simiai da amane sia: i, “Defea hina bagade! Na da dia sia: i defele hamomu.” Amaiba: le, e da eso bagohame Yelusaleme amo ganodini esalu.
Simei anayankha mfumu kuti, “Zimene mwanenazi nʼzabwino. Kapolo wanu adzachita monga mbuye wanga mfumu mwanenera.” Choncho Simei anakhala mu Yerusalemu nthawi yayitali.
39 Be ode udiana gidigili, ea udigili hawa: hamosu dunu aduna da hobeale, Ga: de soge hina bagade A: igisi (Ma: iaga ea mano) ema asi. Simiai da ela da Ga: de sogega doaga: i nababeba: le,
Koma patatha zaka zitatu, akapolo awiri a Simei anathawira kwa Akisi mwana wa Maaka, mfumu ya ku Gati, ndipo Simei anawuzidwa kuti, “Akapolo anu ali ku Gati.”
40 e da ea dougi da: iya fisu ligisili, fila heda: le, ea udigili hawa: hamosu dunu hogomusa: , Ga: de soge hina bagade A: igisima asi. E da ea udigili hawa: hamosu dunu ba: beba: le, ela ea diasuga bu oule misi.
Atamva zimenezi, anakwera bulu wake ndipo anapita kwa Akisi ku Gati kukafunafuna akapolo ake. Choncho Simei anapita ndi kukatenga akapolo ake ku Gati ndipo anabwera nawo.
41 Soloumane da ea hamoi nababeba: le,
Solomoni atawuzidwa kuti Simei anatuluka mu Yerusalemu ndi kupita ku Gati ndipo kuti wabwerako,
42 e da ema misa: ne sia: sili, ema amane sia: i, “Na sia: beba: le, di da Hina Gode Ea Dioba: le amo Yelusaleme hamedafa yolesima: ne ilegele sia: i. Amola na da dima sisane sia: i, di da Yelusaleme yolesea, dafawane bogomu. Di da amo sia: dafawaneyale ilegei amola na sia: nabawane hamoma: ne sia: i.
mfumu inamuyitanitsa Simei ndipo inamufunsa kuti, “Kodi sindinakulumbiritse mʼdzina la Yehova ndi kukuchenjeza kuti, ‘Tsiku limene udzatuluka kupita kwina kulikonse, udziwe kuti udzafa’? Nthawi imeneyo iwe unandiwuza kuti, ‘Zimene mwanena nʼzabwino. Ine ndidzamvera.’
43 Amaiba: le, di da abuliba: le dia ilegele sia: i wadela: lesibala: ? Amola na hamoma: ne sia: i hame nabibala: ?
Chifukwa chiyani tsono sunasunge lumbiro lako kwa Yehova? Bwanji nanga sunamvere lamulo limene ndinakuwuza?”
44 Di da na ada Da: ibidima wadela: le bagade hamoi. Amo di dawa: Amaiba: le, Hina Gode da dima dawa: ma: ne se dabe imunu.
Mfumuyo inawuzanso Simei kuti, “Ukudziwa mu mtima mwakomo zoyipa zonse zimene unachitira abambo anga Davide. Tsopano Yehova akubwezera zoyipa zakozo.
45 Be E da nama hahawane dogolegele imunu amola Da: ibidi ea hina bagade ouligisu hou da gasa fili, eso huluane dialumu.”
Koma Mfumu Solomoni idzadalitsidwa ndipo mpando waufumu wa Davide udzakhazikika pamaso pa Yehova kwamuyaya.”
46 Amalalu, hina bagade da Bina: iama hamoma: ne sia: beba: le, e da ga asili, Simiai medole legei. Amalalu, Soloumane da gasa fili, Isala: ili ouligisu hou gaguiwane ba: i.
Pamenepo mfumu inalamula Benaya mwana wa Yehoyada ndipo iye anapita kukakantha Simei ndi kumupha. Tsono ufumu unakhazikika mʼdzanja la Solomoni.

< 1 Hina 2 >