< 1 Hina 16 >
1 Hina Gode da balofede dunu Yihiu (Hanainai egefe) ema e da Ba: iasiama amane sia: ma: ne sia: si,
Ndipo Yehova anayankhula kudzera mwa Yehu mwana wa Hanani, mawu odzudzula Baasa kuti,
2 “Di da dunu hamedei agoai ba: i. Be Na da di Na fi Isala: ili ouligima: ne ilegei. Be wali di da Yelouboua: me ea hamoi defele, Na fi wadela: le hamoma: ne oule asi dagoi. Ilia da wadela: le hamobeba: le, Na ougi hou da heda: sa.
“Ine ndinakukuza kuchokera pa fumbi ndipo ndinakupanga kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli, koma iwe wakhala ukuyenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchimwitsa anthu anga Aisraeli naputa mkwiyo wanga chifukwa cha machimo awo.
3 Amaiba: le, Na da Yelouboua: me ea sosogo fi amo wadela: lesi dagoi, amo defele Na da dia sosogo fi wadela: lesimu.
Taonani, Ine ndatsala pangʼono kuwononga Baasa pamodzi ndi nyumba yake, ndipo ndidzachitira nyumba yake zimene ndinachita pa nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati.
4 Dia sosogo fi afae da moilai ganodini bogosea da wa: mega mai dagoi ba: mu. Amola sogebi genebogelaga bogosea, buhibaga na dagoi ba: mu.”
Agalu adzadya aliyense wa banja la Baasa amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya iwo amene adzafere kuthengo.”
5 Ba: iasia ea hamonanu huluane, amola ea gesa: i hamosu da “Isala: ili hina bagade ilia Hamonanu Meloa” amo ganodini dedene legei.
Tsono ntchito zina za Baasa ndi zamphamvu zake zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
6 Ba: iasia da bogole, Desa moilai bai bagadega uli dogone sali. Egefe Ila da eda bagia, hina bagade hamoi.
Baasa anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Tiriza. Ndipo Ela mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake.
7 Hina Gode Ea sia: sia: si, amo E da balofede Yihiu ea lafidili Ba: iasia amola ea sosogo fi ilima sia: i, bai Ba: iasia da Hina Godema wadela: le bagade hamobeba: le, agoane sia: i. E da hina bagade Yelouboua: me musa: hamosu defele wadela: le bagade hamobeba: le, Hina Gode da ema ougi galu. Be amo fawane hame. E amolawane Yelouboua: me ea sosogo fi huluane medole legeiba: le, Hina Gode da ougi ba: i.
Komatu Yehova anayankhula kwa Baasa pamodzi ndi banja lake lonse kudzera mwa mneneri Yehu mwana wa Hanani, chifukwa cha zoyipa zonse zimene iye anachita pamaso pa Yehova, kukwiyitsa Yehovayo nakhala ngati nyumba ya Yeroboamu ndiponso chifukwa anawonongeratu banja la Yeroboamu.
8 Yuda hina bagade A: isa da Yuda fi ode 26 agoane ouligilalu, Ila (Ba: iasia egefe) da Isala: ili ilia hina bagade hamoi. E da Desa moilaiga esala, ode aduna Isala: ili fi ouligilalu.
Mʼchaka cha 26 cha ufumu wa Asa mfumu ya Yuda, Ela mwana wa Baasa anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira ku Tiriza zaka ziwiri.
9 Similai da hina bagade Ila ea ‘sa: liode’ wa: i mogili, la: idi ouligisu dunu ba: i. E da Ila medole legema: ne, sadoga sia: dalu ilegei. Eso afaega Desa moilaiga, Ila da dunu ea dio amo Asa (e da hina bagade diasu ouligisu) amo ea diasuga adini maiga feloai.
Zimuri, mmodzi mwa akuluakulu ake, amene ankalamulira theka la magaleta ake, anamuchitira chiwembu. Nthawi imeneyi Ela anali ku Tiriza, akumwa koledzera nako mʼnyumba ya Ariza, munthu amene ankayangʼanira nyumba yaufumu ku Tiriza.
10 Similai da amo diasu golili sa: ili, Ila medole legei. Amalalu, e da Ila bagia Isala: ili hina bagade hamoi. Amo hou da Yuda hina bagade A: isa ea Yuda fi ode 27 ouligilalu, ba: i.
Zimuri anadzalowa, namukantha ndi kumupha mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda. Ndipo Zimuriyo anakhala mfumu mʼmalo mwake.
11 Similai da hina bagade hamonoba, e da Ba: iasia ea sosogo fi amo ganodini dunumusu huluane medole lelegei. Amola Ba: iasia sosogo fi ilia sasamalali huluane medole legei.
Zimuri atangoyamba kulamulira, anapha banja lonse la Baasa. Sanasiyepo munthu wamwamuna ndi mmodzi yemwe, wachibale kapena bwenzi lake.
12 Amaiba: le Hina Gode da balofede dunu Yihiu ea lafidili Ba: iasiama sia: i amo defele, Similai da Ba: iasia ea sosogo fi huluane medole legei.
Choncho Zimuri anawononga banja lonse la Baasa, molingana ndi mawu amene Yehova anayankhula motsutsa Baasa kudzera mwa mneneri Yehu,
13 Bai ilia da wadela: i ogogosu ‘gode’ma nodone sia: ne gadobeba: le, amola ilia da Isala: ili fi dunu amo wadela: i hou hamoma: ne oule asi. Ba: iasia amola egefe Ila, elea da Isala: ili ilia Hina Gode Ea ougima: ne, agoane hamoi.
chifukwa cha machimo onse amene Baasa ndi mwana wake Ela anachita nachimwitsa Israeli, anakwiyitsa Yehova, Mulungu wa Israeli ndi mafano awo osapindulitsa.
14 Liligi huluane Ila ea hamoi da “Isala: ili hina bagade ilia Hamonanu Meloa” amo ganodini dedene legei.
Tsono ntchito zina za Ela ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
15 Yuda hina bagade A: isa da ode 27 agoane Yuda fi ouligilalu, Similai da Desa moilaiga esala, Isala: ili fi eso fesuale fawane ouligi. Isala: ili dadi gagui wa: i da Gibidone moilai bai bagade, Filisidini soge ganodini, amo doagala: lebe ba: i.
Mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda, Zimuri analamulira ku Tiriza masiku asanu ndi awiri. Gulu la ankhondo linali litamanga misasa pafupi ndi Gibetoni, mzinda wa Afilisti.
16 Ilia da Similai da Isala: ili hina bagade medoma: ne sadoga sia: sa: ili, e medole legei dagoi, amo nababeba: le, ilia esalusuadafa amoga ilia dadi gagui wa: i ouligisu Omelima Isala: ili hina bagade hamoma: ne ilegei.
Ankhondo amene anali ku misasa atamva kuti Zimuri wachita chiwembu ndi kupha mfumu, tsiku lomwelo ku misasako anasankha Omuri, mkulu wa ankhondo kukhala mfumu ya Israeli.
17 Omeli amola ea dadi gagui wa: i da Gibidone doagala: lalu yolesili, asili, Desa moilai doagala: i.
Tsono Omuri ndi Aisraeli onse amene anali naye anachoka ku Gibetoni ndi kukazinga Mzinda wa Tiriza.
18 Similai da ba: loba, moilai mogi na: iyado hasalabeba: le, e da hina bagade diasu ganodini gagili sali sesei amogano golili sa: ili, hina bagade ea diasu ulagisilalu, amo lalu gona: su da: iya hina: bogola sa: i.
Zimuri ataona kuti mzinda walandidwa, anathawira ku nsanja ya nyumba ya mfumu ndipo anatentha nyumbayo iye ali momwemo. Kotero iyeyo anafa,
19 E da Hina Godema bagadewane wadela: le hamoi. Amaiba: le, e da bogoi dagoi. Ea da Yelouboua: me defele, wadela: le hamoi amola Isala: ili fi wadela: le hamoma: ne, oule asi. Amaiba: le, Hina Gode da ema hahawane hame ba: i.
chifukwa cha machimo amene iye anachita, kuchita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuyenda mʼnjira za Yeroboamu, nachimwitsa nazo Aisraeli.
20 Similai ea hou huluane amola e da Ila medoma: ne sadoga ilegele, Ila medole legei, amo da “Isala: ili hina bagade ilia Hamonanu Meloa” amo ganodini dedene legei.
Tsono ntchito zina za Zimuri ndi chiwembu chake chimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
21 Isala: ili dunu fi da dogoa mogi. Oda ilia da Dibini (Gina: de egefe) amo hina bagade hamoma: ne dawa: i, amola oda ilia da Omeli hanai.
Pambuyo pake Aisraeli anagawikana pakati: theka linatsatira Tibini mwana wa Ginati kuti limulonge ufumu, ndipo theka lina linatsatira Omuri.
22 Amo sia: dalu fa: no, Omelima hanai dunu ilia baligi. Dibini da bogobeba: le, Omeli da hina bagade dunu hamoi.
Koma anthu otsatira Omuri anali amphamvu kupambana amene ankatsatira Tibini mwana wa Ginati. Choncho Tibini anafa ndipo Omuri anakhala mfumu.
23 Amaiba: le, Yuda fi ilia hina bagade A: isa da Yuda fi ode31 ouligilalu, Omeli da Isala: ili hina bagade hamoi. E da ode fagoyale ouligilalu. Bisili ode gafeyale agoanega, e da Desa moilaiga esala, ouligilalu.
Mʼchaka cha 31 cha Asa mfumu ya Yuda, Omuri anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira zaka 12 ndi miyezi isanu ndi umodzi ku Tiriza.
24 Amalalu, e da Samelia agolo amo silifa fage 6,000 agoane amoga dunu ea dio amo Simia ema bidi lai. Omeli da amo agolo gagili salalu, amogai moilai gaheabolo gagui. E da musa: agolo gagui dunu Simia ea dio dabua, amoma Samelia dio asuli.
Iye anagula phiri la Samariya kwa Semeri pa mtengo wa ndalama 6,000 za siliva ndipo pa phiripo anamangapo mzinda, nawutcha Samariya, potsata dzina la Semeri, dzina la mwini wakale wa phirilo.
25 Omeli da Hina Godema wadela: le hamoi da musa: Isala: ili hina bagade dunu huluane ilia wadela: i hou baligi.
Koma Omuri anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anachimwa kuposa mafumu ena onse amene analipo iye asanakhale mfumu.
26 E da Yelouboua: me ea hou defele, Isala: ili Hina Gode ougima: ne, wadela: le bagade hamoi, amola Isala: ili fi wadela: le hamoma: ne oule asi.
Pakuti iye anayenda mʼnjira zonse za Yeroboamu mwana wa Nebati, ndipo tchimo lake anachimwitsa nalo Aisraeli, nakwiyitsa Yehova Mulungu wa Israeli ndi mafano awo opandapake.
27 Hou huluane Omeli da hamonanusu, amola ea hamoi liligi huluane da “Isala: ili hina bagade ilia Hamonanu Meloa” amo ganodini dedene legei.
Tsono ntchito zina za Omuri ndi zamphamvu zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
28 Omeli da bogole, Samelia soge ganodini uli dogone sali. Amola egefe A: iha: be da eda bagia hina bagade hamoi.
Choncho Omuri anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Samariya. Ndipo Ahabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
29 Yuda hina bagade A: isa da Yuda soge ode 38 agoane ouligilalu, A:iha: be (Omeli egefe) da Isala: ili hina bagade hamoi. E da Samelia soge amo ganodini ode 22 agoane, Isala: ili ouligilalu.
Mʼchaka cha 38 cha ufumu wa Asa, mfumu ya Yuda, Ahabu mwana wa Omuri anakhala mfumu ya Israeli nalamulira Israeli ku Samariya zaka 22.
30 E da Hina Godema wadela: le hamoi, amo da musa: Isala: ili hina bagade ilia wadela: i hou huluane baligi dagoi.
Ahabu mwana wa Omuri anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova kupambana mafumu onse akale.
31 E da Yelouboua: me ea wadela: i hou hamoi defele hamoi, amola amo baligi. E da baligiliwane wadela: i hamonanu asili, Yesebele (Saidone hina bagade Edeba: ile ea idiwi) amo lale, Ba: ile ogogosu ‘gode’ma nodone sia: ne gadosu.
Iye sanachiyese ngati chinthu chochepa chabe kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, koma anakwatiranso Yezebeli, mwana wa Etibaala mfumu ya Asidoni, nayamba kutumikira Baala ndi kumupembedza.
32 E da Samelia soge ganodini, Ba: ilema nodone sia: ne gadoma: ne, debolo diasu gaguli, Ba: ilema oloda hamone, amo debolo diasu ganodini sali.
Iye anapangira Baala guwa lansembe mʼnyumba ya Baala imene anamanga ku Samariya.
33 Amola e da ogogole uda ‘gode’ Asila agoaila hahamone, bugisi. E da Isala: ili Hina Gode Ea ougima: ne wadela: le hamoi, da musa: Isala: ili hina bagade Gode Ea ougima: ne wadela: i hou hamoi amo baligidafa.
Ahabu anapanganso fano la Asera ndi kukwiyitsa kwambiri Yehova Mulungu wa Israeli, kupambana mafumu onse a Israeli amene analipo iye asanakhale mfumu.
34 Ea ouligilaloba, Bedele dunu Haiyele da Yeligou moilai bai bagade bu gagui. Hina Gode da Yosiua (Nane egefe) amo ea lafidili sia: i defele, Haiyele da Yeligou ea bai fa: loba, ea magobo mano Abaila: me fisi. Amola e da moilai gagoi logo ga: su hamonoba, ea ufi mano Sigabe fisi dagoi ba: i.
Pa nthawi ya Ahabu, Hiyeli wa ku Beteli anamanganso mzinda wa Yeriko. Pa nthawi yomanga maziko ake, mwana wake woyamba wa mwamuna, Abiramu anamwalira, ndipo pa nthawi yomanga zipata zake, mwana wa mngʼono wa mwamuna Segubu, anamwaliranso. Izi zinachitika monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa Yoswa mwana wa Nuni.