< 1 Hina 1 >

1 Hina bagade Da: ibidi da da: i hamone fisi. Ea hawa: hamosu dunu da e abulaga sosonesi. Be amomane e da hame dogoloi.
Mfumu Davide atakalamba sankamva kufunda ngakhale akamufunditsa mabulangeti.
2 Amaiba: le, ea hawa: hamosu ouligisu dunu, da ema amane sia: i, “Hina! Ninia uda a: fini afae di ouligisa esaloma: ne hogomu. E da di anegagi gumima: ne, di gadenene golasu hamoma: mu.”
Choncho nduna zake zinamuwuza kuti, “Tiloleni tifune namwali woti azikhala nanu ndi kumakusamalirani. Namwaliyo azigona pafupi nanu kuti mbuye wathu mfumu muzimva kufundira.”
3 Ilia da Isala: ili soge fi huluane amo ganodini uda a: fini afae noga: idafa hohogola lafia: i. Amalalu, ilia da Siuneme soge ganodini, uda a: fini noga: idafa ea dio A: bisia: ge ba: le, amola hina bagadema oule misi.
Kotero anafunafuna mʼdziko lonse la Israeli mtsikana wokongola ndipo anapeza Abisagi wa ku Sunemu, nabwera naye kwa mfumu.
4 E da uda a: fini isisima: goi ba: i. E da hina bagade noga: le ouligi. Be amomane ela da: iga hame gilisi.
Mtsikanayo anali wokongola kwambiri ndipo ankasamalira mfumu ndi kumayitumikira, koma mfumuyo sinakhale naye malo amodzi.
5 A: basalome da bogoloba, A:dounaidia (Da: ibidi amola Ha: gide elea mano) da Da: ibidi ea magobo mano fawane esalu. E da dunu isisima: goidafa esalu. Eso huluane, A:dounaidia da giadofaloba, Da: ibidi da mae hahamone udigili yolesisu. E da hina bagade hou lamusa: hanai galu. E da hisu sa: liode amola hosi amola sigi aligisu dunu 50 agoane, e fidima: ne lai.
Nthawi imeneyi Adoniya, mwana wa Hagiti, anayamba kudzitukumula ndipo anati, “Ndidzakhala mfumu ndine.” Choncho anadzikonzera galeta ndi akavalo, pamodzi ndi anthu 50 woti azithamanga patsogolo pake.
6
(Abambo ake sanalowererepo nʼkamodzi komwe ndipo sanafunsepo kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?” Adoniyayo anali wokongola kwambiri ndipo anali wopondana ndi Abisalomu).
7 E da Youa: be (ea ame da Seluaia) amola gobele salasu dunu Abaia: da, ela e fidima: ne gilisili sia: dasu. Amola ela da e fuligala: musa: sia: i.
Adoniya anagwirizana ndi Yowabu mwana wa Zeruya ndiponso Abiatara wansembe, ndipo iwowa anamuthandiza.
8 Be gobele salasu dunu Sa: idoge, Bina: ia (Yihoiada ea mano), ba: la: lusu dunu Na: ida: ne, Simiai, Liai amola Da: ibidi ea da: i ouligisu dunu, ilia da A: dounaidia emagai hame galu.
Koma Zadoki wansembe, Benaya mwana wa Yehoyada, mneneri Natani, Simei ndi Rei ndiponso asilikali amphamvu a Davide sanamutsate Adoniya uja.
9 Eso afaega, A:dounaidia da sibi, bulamagau amola sefena gala bulamagau mano amo Sania Magufu (Enelougele hano bubuga: su bega: gadenene) Godema gobele sali. E da hina bagade Da: ibidi egefelali oda amola Da: ibidi ea hawa: hamosu dunu Yuda soge amo ganodini esala, amo gobele salasu lolo nabe amoga misa: ne hiougi.
Kenaka Adoniya anapereka nsembe za nkhosa ndi ngʼombe ndiponso ana angʼombe onenepa ku Mwala wa Zohereti kufupi ndi Eni Rogeli. Iye anayitana abale ake onse, ana aamuna a mfumu ndiponso akuluakulu onse a ku Yuda,
10 Be ea hobe Soloumane, ba: la: lusu dunu Na: ida: ne, Bina: ia amola Da: ibidi ea da: i ouligisu dunu, amo e da hame hiougi.
koma sanayitane mneneri Natani kapena Benaya kapenanso asilikali amphamvu a Davide ngakhalenso mʼbale wake Solomoni.
11 Amalalu, Na: ida: ne da Ba: desiba (Soloumane ea ame) ema asili, amane adole ba: i, “Ha: gide ea mano A: dounaidia da higobele hina bagade hamoi, amo di da hame nabibala: ? Amola hina bagade Da: ibidi da amo hamedafa nabi galu.
Pamenepo Natani anafunsa Batiseba, amayi ake a Solomoni, kuti, “Kodi simunamve kuti Adoniya, mwana wa Hagiti, walowa ufumu popanda Davide mbuye wathu kudziwa?
12 Di da dia esalusu amola dia mano Soloumane ea esalusu gaga: musa: hanai galea, na da dima sisamu.
Tsopano ine ndikulangizeni inu mmene mungapulumutsire moyo wanu ndi moyo wa mwana wanu Solomoni.
13 Hedolo hina Da: ibidima asili amane adole ba: ma! ‘Hina bagade! Di da nama dafawane ilegele sia: i, amo na mano Soloumane da dia hina bagade sogebi lamusa: sia: i. Amaiba: le, abuliba: le A: dounaidia da hina bagade hamobela: ?’”
Pitani msanga kwa Mfumu Davide ndipo mukanene kuti, ‘Mbuye wanga mfumu, kodi simunalumbire kwa ine mdzakazi wanu kuti, ‘Ndithu mwana wako Solomoni ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwanga, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu?’ Nanga nʼchifukwa chiyani Adoniya walowa ufumu?’
14 Na: ida: ne da eno amane sisia: asi, “Amasea, di da hina Da: ibidi ali gilisili sia: dalea, na da ganodini misini, dia sia: da dafawane sia: mu.”
Pamene inu muzikayankhula ndi mfumu, ine ndidzalowa ndi kuchitira umboni mawu anuwo.”
15 Amaiba: le, Ba: desiba da hina bagade ea golala ahoasu ganodini e ba: la asi. E da da: idafa hamoiba: le, Siuneme a: fini A: bisia: ge e ouligilalebe ba: i.
Choncho Batiseba anapita nakalowa ku chipinda kukaonana ndi mfumu imene inali itakalamba kwambiri, kumene Abisagi wa ku Sunemu uja ankayisamalira.
16 Ba: desiba da hina bagade ea midadi gududafa begudui. Da: ibidi da ema amane adole ba: i, “Di da adi lamusa: misibala: ?”
Batiseba anagwada nalambira mfumu. Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi nʼchiyani chimene ukufuna?”
17 E bu adole i, “Hina bagade! Di da Hina Gode Ea Dioba: le nama amane ilegele sia: i. Na mano Soloumane da di bagia hina bagade hamomu.
Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga, inu mwini munalumbira kwa ine mdzakazi wanu mʼdzina la Yehova Mulungu wanu kuti, ‘Solomoni mwana wako ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwa ine, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.’
18 Be A: dounaidia e da hina bagade hamoi dagoi. Amola di da amo hou hamedafa nabi.
Koma tsopano Adoniya ndiye walowa ufumu, ndipo inu mbuye wanga mfumu, simukuzidziwa zimenezi.
19 E da bulamagau gawali, sibi amola bulamagau mano sefena amo bagohame Godema gobele sali. Amola e da dia mano oda, gobele salasu dunu Abaia: da amola dia dadi gagui wa: i ouligisu dunu Youa: be, ili amo gobele salasu lolo amoga misa: ne hiougi. Be e da dia mano Soloumane misa: ne hame hiougi.
Ndipo wapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndi nkhosa ndi mbuzi ndipo wayitana ana anu onse, wansembe Abiatara ndiponso Yowabu mkulu wa ankhondo, koma sanayitane kapolo wanu Solomoni.
20 Hina bagade! Isala: ili fi dunu huluane ilia hanai da di da dia bagia manebe hina amo di ilima adoma: ne dawa: lala.
Mbuye wanga mfumu, maso a Aisraeli onse ali pa inu, kuti adziwe kuchokera kwa inu amene adzakhala pa mpando waufumu wa mbuye wanga mʼmalo mwanu.
21 Be di da mae adole bogosea, ilia da na mano Soloumane anima wadela: i hamosu dunu ilia se nabasu defele anima se nabasu imunu.”
Mukapanda kutero, mbuye wanga, mukadzangotisiya nʼkulondola kumene kunapita makolo anu, ine pamodzi ndi mwana wangayu Solomoni adzatiyesa owukira.”
22 E da gebe adodalobawane, Na: ida: ne da hina bagade diasuga doaga: i.
Pamene Batiseba amayankhula ndi mfumu, mneneri Natani analowa.
23 Ilia da hina bagadema gobele salasu dunu da amogai esala sia: beba: le, Na: ida: ne da golili sa: ili, hina bagade ea midadi gududafa begudui.
Ndipo anthu anawuza mfumu kuti, “Kwabwera mneneri Natani.” Kotero iye anafika pamaso pa mfumu ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
24 Amalu e da amane sia: i, “Hina bagade! Di da A: dounaidia e dia bagia hina hamoma: ne sisia: i labala?
Natani anafunsa kuti, “Mbuye wanga mfumu, kodi mwalengeza kuti Adoniya adzakhala mfumu mʼmalo mwanu, ndi kuti adzakhala pa mpando wanu waufumu?
25 Wali esoga e da asili, bulamagau gawali, sibi, amola bulamagau mano sefena gala amo bagohame gobele sala asi. E da diagofelali huluane amola dia dadi gagui wa: i ouligisu dunu Youa: be amola gobele salasu dunu Abaia: da amo huluane lolo nabega misa: ne sia: i. Amola wahadafa ilia da lolo naha bagadewane amane welala, ‘Hina bagade A: dounaidia da sedadewane esalumu da defea!’
Lero lomwe lino wakapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndiponso nkhosa ndi mbuzi. Iye wayitana ana anu onse, atsogoleri a nkhondo, ndiponso wansembe Abiatara. Panopa onsewa akudya ndi kumwa naye ndipo akunena kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Adoniya!’
26 Be hina! E da na, gobele salasu Sa: idoge, Bina: ia amola Soloumane, nini hame hiougiya: ba:
Koma ine kapolo wanu, wansembe Zadoki ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndiponso kapolo wanu Solomoni sanatiyitane.
27 Hina bagade! Di da amo dafawane adobela: ? Amola amo hamobeba: le, dia bagia manebe dunu ea dio amo dia eagene ouligisu dunuma hame adobela: ?”
Kodi zimenezi mbuye wanga mfumu mwazichita ndinu, osawawuza atumiki anu kuti adziwe amene adzakhale pa mpando waufumu mʼmalo mwanu?”
28 Hina bagade Da: ibidi da amane sia: i, “Ba: desiba da bu misa: ne sia: ma!” Amalalu, e da misini, ea midadi aligi.
Pamenepo mfumu Davide anati, “Muyitaneni Batiseba.” Kotero Batiseba analowa ndipo anayimirira pamaso pa mfumu.
29 Amalalu, Da: ibidi da ema amane sia: i, “Hina Gode, na bidi hamosu Gaga: su dunu, amo Ea Dioba: le, na da dima dafawane ilegele sia: sa.
Tsono mfumu inalumbira kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene anandipulumutsa ine ku mavuto onse,
30 Wali eso, na musa: Isala: ili fi ilia Hina Gode Ea Dioba: le dima ilegele sia: i, amo na da dafawane hamomu. Diagofe Soloumane da dafawane na bagia hina bagade hamomu.”
ndithu ine lero ndichita zonse zimene ndinalumbira kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, mwana wako Solomoni adzakhala mfumu mʼmalo mwanga ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.”
31 Ba: desiba da gududafa beguduli, amane sia: i, “Na hina bagade! Di da eso huluane esalumu da defea!”
Pamenepo Batiseba anawerama, nagunditsa mutu wake pansi nalambira mfumu, ndipo anati, “Mbuye wanga Mfumu Davide mukhale ndi moyo wautali!”
32 Amalalu, hina Da: ibidi da Sa: idoge, Na: ida: ne amola Bina: ia ili ema misa: ne sia: si. Ilia da ema doaga: le,
Mfumu Davide anati, “Ndiyitanireni wansembe Zadoki, mneneri Natani ndi Benaya mwana wa Yehoyada.” Atafika pamaso pa mfumu,
33 e da ilima amane sia: i, “Dilia asili, na diasu ouligisu dunu ili amola oule masa. Na mano Soloumane da nina: ‘miule’ (dougi agoai) amo da: iya fila heda: le, Gaihone hano bubuga: su amogudu oule masa.
mfumuyo inati kwa iwo, “Tengani atumiki anga ndipo mukweze mwana wanga Solomoni pa bulu wanga ndipo mupite naye ku Gihoni. Mukalize lipenga ndi kufuwula kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Solomoni!’
34 Amogawi, Sa: idoge amola Na: ida: ne alia Soloumane da Isala: ili ilia hina bagade hamoma: ne, susuligi amoga soga: gala: lesima. Amasea, dalabede fulabole, amane wele sia: ma, ‘Hina bagade Soloumane da sedadewane esaloma: ma!’
Kumeneko Zadoki wansembe ndi mneneri Natani akamudzoze kuti akhale mfumu ya Israeli. Kenaka mukalize lipenga ndi kumanena kuti ‘Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni.’
35 E da na fisuga fimusa: buhagili goeguda: masea, dilia e bobogema. E da na bagia hina bagade hamomu. Bai na da e fawane, Isala: ili fi amola Yuda fi ouligima: ne ilegei dagoi.”
Ndipo pobwera muzikamutsata pambuyo. Iyeyo akabwere kuno ndi kudzakhala pa mpando wanga waufumu ndi kudzalamulira mʼmalo mwanga. Ndamusankha kukhala wolamulira Israeli ndi Yuda.”
36 Bina: ia da bu adole i, “Amanewane hamomu! Amola dia Hina Gode da amo dafawane hamoma: mu.
Benaya mwana wa Yehoyada anayankha mfumu kuti, “Ameni! Yehova Mulungu wa mbuye wanga mfumu akhazikitse kuti zichitike motero.
37 Hina Gode da di, hina bagade, amo noga: le fidisu. E da amo defele, Soloumane noga: le fidimu da defea. Amola E fidibiba: le, Soloumane ea ouligisu da bagadewane gaguiba: le, dia ouligisu hou baligimu da defea.”
Monga momwe Yehova wakhalira ndi inu mbuye wanga mfumu, momwemonso akhale ndi Solomoni ndi kukhazikitsa ufumu wake kuti ukhale waukulu kuposa ufumu wa mbuye wanga Mfumu Davide!”
38 Amaiba: le, Sa: idoge, Na: ida: ne, Bina: ia amola hina bagade ea da: i ouligisu dunu da Soloumane amo hina bagade Da: ibidi ea miule da: iya fisili, oule, Gaihone hano bubuga: su amoga oule asi.
Kotero Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndiponso Apeleti, anthu oteteza mfumu, anapita kukamukweza Solomoni pa bulu wa Mfumu Davide ndi kupita naye ku Gihoni.
39 Sa: idoge da olife susuligi buniga di (amo e da musa: Hina Gode Ea abula diasuga lai) amo lale, Soloumane amoga soga: gala: le, e mogili gagale ilegei. Ilia da dalabede fulabole amola dunu huluane da amane wele sia: i, “Hina bagade Soloumane da sedadewane esaloma: mu.”
Wansembe Zadoki anatenga nyanga ya mafuta yochokera ku malo opatulika ndi kumudzoza Solomoni. Kenaka analiza lipenga ndipo anthu onse anafuwula kuti, “Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni!”
40 Amalalu, ilia huluane da e bobogele, hahawane wele sia: i, amola fulabosu baidama fulaboi. Ilia bagadewane gugulubiba: le, osobo da fofogoi.
Ndipo anthu onsewo anapita namutsatira pambuyo akuyimba zitoliro ndi kukondwerera kwambiri, kotero nthaka inagwedezeka chifukwa cha phokoso lawo.
41 A: dounaidia amola ea hiougi dunu da lolo mai gilalaloba, ilia da gugulubi amo nabi. Amola Youa: be da dalabede fulabobe nababeba: le, e da amane adole ba: i, “Amo moilai ganodini gugulubi ea bai da adila: ?”
Adoniya pamodzi ndi anthu onse oyitanidwa amene anali naye anamva zimenezi pamene ankamaliza madyerero awo. Atamva kulira kwa malipenga, Yowabu anafunsa kuti, “Kodi phokoso lonselo mu mzindamo likutanthauza chiyani?”
42 E da sia: dagomusa: gala, Yonada: ne (gobele salasu A: baia: da ea mano) da doaga: i. A: dounaidia da ema amane sia: i, “Misa! Di da dunu noga: idafa. Di da sia: noga: idafa gaguli maha ganumu.”
Iye akuyankhula, Yonatani mwana wa wansembe Abiatara anafika. Adoniya anati, “Lowa. Munthu wabwino ngati iwe ayenera kubweretsa nkhani yabwino.”
43 Yonada: ne da amane sia: i, “Sia: noga: idafa hame. Hina bagade Da: ibidi da Soloumane hina bagade hamonesi dagoi.
Yonatani anayankha Adoniya kuti, “Ayi ndithu, zinthu sizili bwino! Mbuye wathu Mfumu Davide walonga Solomoni ufumu.
44 E da Sa: idoge, Na: ida: ne, Bina: ia amola ea da: i ouligisu dunu amo Soloumane oule masa: ne asunasi. Ilia da Soloumane hina bagade ea miule fila heda: ma: ne fisi.
Mfumu yatuma Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndi Apeleti ku Gihoni ndipo iwo amukweza pa bulu wa mfumu,
45 Amola Sa: idoge amola Na: ida: ne da Gaihone hano bubuga: su amoga Soloumanema susuligi soga: gala: le ilegei. Amalalu ilia da moilai ganodini golili sa: ili, hahawaneba: le bagade wele sia: i. Dunu huluane da wali bagadewane hahawane dogolegesa. Waha gugulubi dia nabi amo da goa.
ndipo Zadoki wansembe ndi mneneri Natani adzoza Solomoni ku Gihoni kuti akhale mfumu. Ndipo kuchokera kumeneko akhala akululutira, kotero kuti mu mzinda monse muli phokoso lokhalokha. Ndiyetu phokoso limene mukulimvalo.
46 Soloumane da wali hina bagade esala.
Ndipo Solomoni wakhala kale pa mpando wake waufumu.
47 Sia: eno da hina bagade hawa: hamosu dunu da hina bagade Da: ibidima asigi sia: sia: musa: asili, ilia amane sia: i, ‘Dia Gode da dunu ilia dima nodone dawa: digi hou amo baligili Soloumanema imunu da defea. Amola dia ouligisu da bagade gaguiwane ba: i. Be Soloumane ea ouligisu da amo baligimu da defea.’ Amalalu, hina bagade Da: ibidi da ea dia heda: su da: iya Godema nodone sia: ne gadomusa: beguduli,
Kuwonjezera pamenepo, nduna za mfumu zabwera kale kudzayamika mbuye wathu Mfumu Davide, pomanena kuti, ‘Mulungu wanu atchukitse dzina la Solomoni kuposa dzina lanu ndipo ufumu wake ukule kupambana ufumu wanu!’ Ndipo mfumu inawerama niyamba kupembedza pa bedi lake,
48 amane sia: ne gadoi, ‘Ninia Isala: ili Hina Godema nodone sia: na: di! Bai E da wali nagaga fifi misi afae amo na bagia hina bagade hamoma: ne hamoi. Amola na da mae bogole, amo hou ba: musa: , E da logo doasi dagoi.’”
inati, ‘Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wasankha wolowa mʼmalo mwanga ine ndikanali ndi moyo lero lino.’”
49 Amalalu, A:dounaidia ea hiougi dunu da beda: igia: le, amola ilia huluane wa: legadole, afagogole, afia: i.
Anthu onse amene Adoniya anawayitana ananjenjemera ndi mantha, ndipo anayimirira, kenaka anamwazikana.
50 A: dounaidia da Soloumaneba: le bagade beda: ne, Hina Gode Ea Abula Diasuga asili, oloda hegomai da: iya ‘hono’ biyaduyale, e da amo gaguli lelebe ba: i.
Koma Adoniya, poopa Solomoni, anapita ku Nyumba ya Mulungu nakagwira msonga za guwa lansembe.
51 Ilia da hina bagade Soloumanema amane sia: i, “A: dounaidia da diba: le beda: ga oloda ea ‘hono’ gaguiwane esala,’ amane ema sia: i. Amola A: dounaidia ea sia: amo da agoane sia: i, “Na da amo gagui mae fisili, hina bagade Soloumane da na hame medole legema: ne ilegele sia: beba: le fawane fisimu,” amane ilia da Soloumanema sia: i.
Tsono Solomoni anawuzidwa kuti, “Adoniya akukuopani inu Mfumu Solomoni ndipo wagwira msonga za guwa lansembe. Iye akuti, ‘Mfumu Solomoni alumbire kuti sadzapha kapolo wake ndi lupanga.’”
52 Soloumane da bu adole i, “E da nama noga: le fa: no bobogesea, na da ea dialuma hinabo afaewane hame wadela: lesimu. Be e da noga: le hame bobogesea, e da bogosu ba: mu.”
Solomoni anayankha kuti, “Ngati iyeyo aonetse kuti ndi munthu wakhalidwe labwino, ngakhale tsitsi la mʼmutu mwake silidzathothoka ndi kugwera pansi, koma akapezeka kuti ali ndi khalidwe loyipa, adzafa ndithu.”
53 Amalalu, hina bagade Soloumane da A: dounaidia ema misa: ne sia: si. Ea hawa: hamosu dunu da A: dounaidia oloda amoga lale, hina bagadema oule asi. A: dounaidia da hina bagadema asili, ema gududafa begudui. Hina bagade da ema amane sia: i, “Di diasua ahoabada!”
Pamenepo Mfumu Solomoni inatuma anthu ndipo anakamutenga paguwa paja. Adoniya anabwera ndi kudzalambira Mfumu Solomoni, ndipo Solomoni anati, “Pita ku nyumba yako.”

< 1 Hina 1 >