< 1 Hou Olelesu 19 >

1 Amogalu fa: no, A:mone soge hina bagade amo Na: iha: se da bogoi. Egefe Ha: inane da ea hina bagade sogebi lai.
Patapita nthawi Nahasi mfumu ya Aamoni inamwalira, ndipo mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
2 Hina bagade Da: ibidi da amane sia: i, “Ha: inane ea ada Na: iha: se da nama asigi galu. Amaiba: le, na da ea mano ilima asigimu da defea.” Amaiba: le, Da: ibidi da sia: adole ahoasu dunu, ea asigi sia: sia: ma: ne, Ha: inanema asunasi.
Davide anaganiza kuti, “Ine ndidzachitira chifundo Hanuni mwana wa Nahasi chifukwa abambo ake anandichitira zabwino.” Choncho Davide anatumiza anthu kuti akamupepesere kwa Hanuni chifukwa cha imfa ya abambo ake. Anthu amene Davide anawatuma atafika kwa Hanuni mʼdziko la Aamoni kudzamupepesa,
3 Ilia A: mone sogega doaga: loba, A:mone ouligisu dunu ilia da hina bagadema amane sia: i, “Di adi dawa: bela: ? Da: ibidi da dia adama nodone dawa: beba: le, amo dunu dima asigi sia: sia: mane asunasibala: ? Hame mabu! Amo da desega ahoasu dunu amo Da: ibidi da nini hasalima: ne, ninia soge hou amo abodele ba: musa: asunasi.”
atsogoleri a ankhondo a Aamoni anawuza Hanuni kuti, “Kodi mukuganiza kuti Davide akupereka ulemu kwa abambo anu potumiza anthuwa kwa inu kudzapepesa? Kodi anthuwa sanawatumize kuti adzaone dziko lathu ndi kuchita ukazitape ndi cholinga chofuna kuwulanda?”
4 Amaiba: le, Ha: inane da Da: ibidi ea sia: adola ahoasu dunu amo gagulaligili, ilia mayabo la: idi waga: ne, ilia abula mugagili damunisili, ili buhagima: ne asunasi.
Choncho Hanuni anagwira anthu amene Davide anawatuma aja ndipo anawameta ndi kudula zovala zawo pakati mʼchiwuno mpaka matako kuonekera ndipo anawabweza kwawo.
5 Ilia da buhagimu bagadewane gogosia: i. Da: ibidi da amane hamoi nababeba: le, e da ilima amane sia: si, “Dilia Yeligou moilai bai bagadega ouesalu, dilia mayabo bu sa: i galea, buhagima!”
Munthu wina atafika ndi kufotokozera Davide za anthuwo, iye anatuma amithenga kukakumana nawo, chifukwa anali ndi manyazi kwambiri. Mfumu inati, “Mukhale ku Yeriko mpaka ndevu zanu zitakula, ndipo kenaka mubwere kuno.”
6 Hina bagade Ha: inane amola A: mone dunu ilia da Da: ibidi ilia ha lai hamoi dagoi dawa: i. Amaiba: le, ilia da silifa 40 danese agoane, sa: liode amola amoga fila heda: su dunu bidi lama: ne, Gado Mesoubouda: imia soge amola Silia soge amo Ma: iaga amola Souba, ilima iasili wele guda: i.
Aamoni atazindikira kuti amukwiyitsa kwambiri Davide, Hanuni ndi Aamoni anatumiza siliva wolemera makilogalamu 34,000 kuti akalipirire magaleta ndi okwerapo ake a ku Mesopotamiya; Aramu-Maaka ndi Zoba.
7 Ilia bidiga lai fidisu dunu, amo sa: liode 32,000 agoane amola Ma: iaga hina bagade ea dadi gagui wa: i, ilia da Mediba moilai gadenene misini, wa: i fi esalebe ba: i.
Iwo analipira magaleta okwanira 32,000, pamodzi ndi mfumu ya ku Maaka ndi ankhondo ake. Amenewa anabwera ndi kudzamanga misasa yawo pafupi ndi Medeba. Nawonso Aamoni anabwera kuchokera ku mizinda yawo ndipo anapita kukachita nkhondo.
8 Da: ibidi da amo hou nababeba: le, e da Youa: be amola Isala: ili dadi gagui wa: i huluane ilima gegemusa: asunasi.
Davide atamva zimenezi, anatumiza Yowabu ndi gulu lonse la ankhondo amphamvu.
9 A: mone dadi gagui dunu da gadili mogodigili, ilia da La: ba (ilia moilai bai bagade) amo ea logo holei gadenene dadalei. Amola hina bagade amo da ili fidimusa: misi, ilia dadi gagui dunu da sogebi genebogela asili, amogai dadalei.
Aamoni anatuluka ndi kukhala mʼmizere ya nkhondo pa chipata cha mzinda wawo, pamene mafumu amene anabwera nawo anali kwa wokha, ku malo wopanda mitengo.
10 Youa: be da ba: loba, ea ha lai da midadi amola bagia ema doagala: mu ba: i. Amaiba: le, e da Isala: ili dadi gagui dunu baligili noga: idafa amo ilegele, ilia da Silia dadi gagui dunu ilima ba: le gusuli aligima: ne asunasi.
Yowabu ataona kuti kunali mizere ya ankhondo kutsogolo kwake ndi kumbuyo kwake; iye anasankha ena mwa ankhondo a Israeli odziwa kuchita bwino nkhondo ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aaramu.
11 E da ea eya Abisia: i amo Isala: ili dadi gagui dunu eno ouligima: ne sia: i. Abisia: i da sia: beba: le, amo Isala: ili dadi gagui da A: mone dunu ilima ba: le gusuli dadalei.
Iye anayika ankhondo ena otsalawo mʼmanja mwa Abisai mʼbale wake ndipo anawayika kuti amenyane ndi Aamoni.
12 Youa: be da Abisia: ima amane sia: i, “Di da Silia dunu na hasalimusa: heda: be ba: sea, na fidila misa. Amola na da A: mone dunu di hasalimusa: heda: be ba: sea, na da di fidila masunu.
Yowabu anati, “Ngati Aaramu andipose mphamvu, iwe ubwere udzandipulumutse; koma ngati Aamoni akupose mphamvu, ine ndidzabwera kudzakupulumutsa.
13 Di mae beda: ne gasa fima! Ninia fi dunu amola Gode Ea moilai huluane gaga: musa: , gasa fili hamoma. Amola Hina Gode Ea hamomusa: ilegei, amo ba: mu da defea!”
Limba mtima ndipo timenyane nawo mopanda mantha chifukwa cha anthu athu ndi mizinda ya Mulungu wathu. Yehova achite chomukomera pamaso pake.”
14 Youa: be amola ea dunu da doagala: musa: midadi manebeba: le, Silia dunu ilia da hobea: i.
Choncho Yowabu ndi ankhondo amene anali naye anapita kukamenyana ndi Aaramu, ndipo iwo anathawa pamaso pake.
15 A: mone dunu da Silia dunu hobealebe ba: lu, ilia da Abisia: i amoma hobeale, moilai amo ganodini hehenane golili sa: i. Amalalu, Youa: be da A: mone dunuma gegenanu yolesili, Yelusaleme moilai bai bagadega buhagi.
Aamoni atazindikira kuti Aaramu akuthawa, iwo anathawanso pamaso pa Abisai mʼbale wake ndi kulowa mu mzinda. Motero Yowabu anabwerera ku Yerusalemu.
16 Silia dunu da Isala: ili dunu ili hasali dagoi amo dawa: loba, ilia da ilia dadi gagui dunu huluanedafa gilisima: ne wele sia: i. Hina bagade Ha: da: disa da Silia dunu huluane amo Iufala: idisi Hano gusudili esalu, amo ema misa: ne sia: si. Ilia da Hila: me moilaiga misi. Sioubage (Souba hina bagade Ha: da: disa, amo ea dadi gagui wa: i ouligisudafa dunu galu) da ili ouligisu.
Aaramu ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anatumiza amithenga kukayitana Aaramu amene anali ku tsidya la Mtsinje, pamodzi ndi mtsogoleri wa ankhondo wa Hadadezeri, Sofaki akuwatsogolera.
17 Da: ibidi da amo sia: nababeba: le, e da Isala: ili dadi gagui dunu gilisili, Yodane Hano degei. Amogawi, ea sia: beba: le, ilia da Silia dunu ilima ba: le gusuli dadalele, gegesu da mui.
Davide atawuzidwa zimenezi, iye anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kuwoloka Yorodani. Iyeyo anapita kukakumana nawo ndipo anakhala mʼmizere yankhondo moyangʼanana ndipo iwo anamenyana naye.
18 Isala: ili dunu da Silia dunuma gegesa fula se bobogei. Da: ibidi amola ea dunu da Silia sa: liode amoga fila heda: i dunu 700 agoane amola emoga ahoasu dadi gagui dunu 40,000 agoane fane lelegei. Ilia da Sioubage (ilia ha lai ouligisudafa) amo fa: ginisili, e da gegesu sogebi amogawi bogoi.
Koma iwo anathawa pamaso pa Aisraeli, ndipo Davide anapha anthu okwera pa magaleta 7,000 ndi ankhondo oyenda pansi 40,000. Iye anaphanso Sofaki, mtsogoleri wawo wankhondo.
19 Hina bagade Ha: da: disa da eno hina bagade fonobahadi ouligisu. Ilia da Isala: ili dunu da ilima hasali dagoi ba: i. Amaiba: le, ilia da Isala: ili dunuma olofomusa: gousa: i. Amalalu, Isala: ili dunu da ili ouligilalu. Amola Silia dunu da beda: iba: le, bu A: mone dunu fidimu higa: i galu.
Mafumu amene ali pansi pa Hadadezeri ataona kuti agonjetsedwa ndi Aisraeli, anachita mtendere ndi Davide ndipo anakhala pansi pa ulamuliro wake. Motero Aaramu anaopa kuthandizanso Aamoni.

< 1 Hou Olelesu 19 >