< Yahuda 1 >

1 Yahuda kucin Yesu Kristi nin gwana Yakubu udu ale na iyicila linwana nanya Kutelle ucif nin ciyu Yesu Kreisti.
Ndine Yuda, mtumiki wa Yesu Khristu, komanso mʼbale wake wa Yakobo. Kwa inu amene Mulungu Atate anakuyitanani, amene amakukondani ndikukusungani mwa Yesu Khristu.
2 Na ayi akunekune udu kitimine nin sheu nibinai nin suu tigbardan
Chifundo, mtendere ndi chikondi zikhale nanu mochuluka.
3 Linwana in wadin shuu liti kang inyerti minu mbelen nlirunse nla, imile na nyertin minu in zazin minu ikpiyin ushu natin nyinu sa uyenu ule na iwa nakpa anit alau.
Okondedwa, ngakhale ndinkafunitsitsa kukulemberani za chipulumutso cha tonsefe, ndakakamizidwa kuti ndikulembereni ndi kukupemphani kolimba kuti mumenye ndithu nkhondo yotchinjiriza chikhulupiriro chimene Mulungu anachipereka kamodzi kokha kwa anthu onse oyera mtima.
4 Bara naamong anit wadak likire ale na uchankuulobmine iyertine uwoeru anan sali fiu Kutelle ale na ina saka alheri Kutelle bit udu nuzu nanm nawani ahhe, nin nale na ita amusu nchikilari nin nan bunbite Yesu Kristi.
Pakuti anthu ena amene za chilango chawo zinalembedwa kale, alowa mobisika pakati panu. Amenewa ndi anthu osapembedza Mulungu, amene amapotoza chisomo cha Mulungu wathu kuchisandutsa ufulu ochitira zonyansa ndiponso amakana Yesu Khristu amene Iye ndiye Mbuye ndi Mfumu yathu.
5 Nene ndin wuru inlizin minu kodashike iyiru vat niming au cikilari wa nutun anit nanya unuzu myin Mmasar bara nani amolu ale na iyina ba.
Ngakhale munazidziwa kale zonsezi, ndafuna kuti ndikukumbutseni kuti Ambuye anapulumutsa anthu ake ndi kuwatulutsa mʼdziko la Igupto, koma pambuyo pake anawononga amene sanakhulupirire.
6 Nin nnono kadura Kutelle ale na iwa cin katwa mine, i suna kiti lisosin mine kicine Kutelle na ce nani nanya nisarka nsirtin sa ligan udu udiya lirulole. (aïdios g126)
Ndipo mukumbukire angelo amene sanakhutire ndi maudindo awo, koma anasiya malo awo. Angelo amenewa Mulungu anawamanga ndi maunyolo osatha, ndipo akuwasunga mʼmalo a mdima mpaka tsiku lalikulu lachiweruzo. (aïdios g126)
7 I masin nafo Usodom nin Gomora nin nigbiri naa na niea di nkiline, ale na iwa libaw lirume na awa ni atimine ni mon inanzang ndurtu kuna nizi kuhem. I wa suu anan gbaduzu na iwa neu un nnla unsa ligang. (aiōnios g166)
Musayiwale mizinda ya Sodomu ndi Gomora ija, ndi mizinda yoyandikana nayo. Anthu mʼmenemo anadziperekanso kuchita zadama ndi kuchita zonyansa zachilendo. Mizinda imeneyi yakhala ngati chitsanzo cha amene adzalangidwa ndi moto wosatha. (aiōnios g166)
8 Nin nani libau lirume alele nanza nidowo mine nanya namoro, inarsi anan natet tigo, nani ibele inun inanzan kusari nanan natt udia.
Nʼchimodzimodzinso zimene akuchita anthu amenewa potsata maloto awo, amadetsa matupi awo, amakana ulamuliro wa Mulungu ndiponso amachitira chipongwe angelo akumwamba.
9 Bara ame Makailu unan kadura Kutelle udiya na awadi ugon nsirti mayardan kitene liben Musa, na awa yinin ada ni mabucubucu sa ti gbulan tizogo ba inworonani aworo, ''Na ucife kpada fi.''
Koma ngakhale mkulu wa angelo Mikayeli, pamene ankalimbana ndi Mdierekezi za mtembo wa Mose, sanamunene kuti wachipongwe, koma anati, “Ambuye akudzudzule iwe!”
10 Bara nani anit alena vat zoguzo imonle na iyino ba vat ni lemong na iyino makeke Kutelle nafo makeke insali nibinai nile imuwne inanza mminu.
Koma anthu awa amachita chipongwe zinthu zimene sakuzidziwa. Ndipo zinthu zimene amazidziwa ndi nzeru zachibadwa, monga za nyama, ndizo zimene zimawawononga.
11 Kash mine! bara na ina cina nanya libau kainu, inanin pira ndina ntanu Balam nsu nikurfun, inani diku zemzamlibau Kora unan mayardan.
Tsoka kwa iwo chifukwa anatsatira njira ya Kaini. Iwo athamangira phindu, nʼchifukwa chake anagwa mʼtchimo la Baalamu. Iwo anawonongedwa chifukwa chowukira monga anachitira Kora.
12 Alelere ale na i yeshin nagilitin nsufe na ina lii ninfi, sancin idin pillu ma atiminere mung iso a wut sa wuru ale na ufunu asu uyira aca akune sa kumat, ukul tiba, tijiye martiza.
Anthu amenewa ndiwo amayipitsa maphwando anu achikondi. Amadya nanu mopanda manyazi ndipo ali ngati abusa amene amangodzidyetsa okha. Anthuwa ali ngati mitambo yowuluzika ndi mphepo, yopanda mvula. Ali ngati mitengo ya nthawi ya masika, yopanda zipatso, yozuka mizu, mitengo yoferatu.
13 Ufunu nanya kurawa, anutuzuno kupunjetnceen mine, iyinin galu bara inunye usiriu nanya insirti na na yashe nani se saligan. (aiōn g165)
Iwowa ali ngati mafunde awukali apanyanja, amene amatulutsa thovu la zonyansa zawo. Amenewa ali ngati nyenyezi zosochera, ndipo Mulungu akuwasungira mdima wandiweyani mpaka muyaya. (aiōn g165)
14 Nin bara anit alele nan Enok unan zur unuzu Adamu iwa beling aworo, ' Yene! Ucif bit nda nin namiu m likure nanit alau,
Enoki, wachisanu ndi chiwiri kuyambira pa Adamu, ananeneratu za anthu amenewa kuti, “Onani, Ambuye akubwera ndi oyera ake osawerengeka
15 inin suu ma wucuwucu udu kin kogha, anin tecu anan sali ncin dert nin nitwa ninanzan mine nanya na isu nanya nibinai ni nanzan nin nimun ididya ile na ann kulapi na malu belinghe.
kuti adzaweruze aliyense, ndi kudzagamula kuti onse osapembedza ndi olakwa, chifukwa cha ntchito zawo zosalungama zimene anachita mʼmoyo wawo osaopa Mulungu. Adzawatsutsa chifukwa cha mawu onse achipongwe amene osapembedzawa ananyoza nawo Ambuye.”
16 Alelere anan tibula na idin su mun ile na nibinai mere taa usuwe, anan foo figiri ruu namong inan se ulin bun.
Anthu amenewa amangʼungʼudza ndi kudandaula. Amatsatira zilakolako zawo zoyipa. Amayankhula zodzitamandira ndipo amanamiza ena pofuna kupeza phindu.
17 Bara nani anum linwa na lizinong tigbulan too na iwa belu nin burne na nann lirinu ncif bite Yesu Kristi.
Koma okondedwa, kumbukirani zimene atumwi a Ambuye athu Yesu Khristu ananeneratu.
18 Iwa woro minu nayiri nimalinghe anan sissuu ma dak, ima dofunu kata kanazan ka nibinai mine.
Iwo anakuwuzani kuti, “Mʼmasiku otsiriza kudzafika anthu onyoza, otsatira zofuna zawo zoyipa.”
19 Ale anite di nin suu nanti, na idinin nfip milauwa ba.
Anthu amenewa ndi amene akubweretsa mipatuko pakati panu, amatsatira nzeru zachibadwa ndipo alibe Mzimu Woyera.
20 Bara nani anu n linwana, bara na ina kee atimine ketene u yinu sa u yenu udya nin nlira muu na idin tizu nanya infep milau.
Koma inu okondedwa, muthandizane kuti mukule pa chikhulupiriro chanu choyera, ndipo muzipemphera ndi mphamvu ya Mzimu Woyera.
21 Ceu atimine nanya nsu Kutelle, Iyerje ikunekunwe ncef bite Yesu Kristi unan lai sa ligang. (aiōnios g166)
Khalani mʼchikondi cha Mulungu pamene mukudikira chifundo cha Ambuye athu Yesu Khristu kuti akubweretsereni moyo wosatha. (aiōnios g166)
22 Nin yerju nkunekune nati na mong anit ale na idi nin nibinai nibaba
Muwachitire chifundo amene akukayika.
23 Nin tucu na mo, ikpalizin nani nanya nla nin namong lanzan nkunekune nin fiu nafo na inari kultuk koo na indinong kidowo nnanza.
Ena muwapulumutse powalanditsa ku moto. Enanso muwachitire chifundo, koma mwa mantha, ndipo muzidana ngakhale ndi mwinjiro yomwe yayipitsidwa ndi machimo.
24 Nene udu ule na ama kesu fi utirzu a ceu fi nbun nle na ama yantifi sa kulapi nanya mmang sa ligan,
Kwa Iye amene angathe kukusungani kuti mungagwe mʼmachimo, ndiponso amene angathenso kukufikitsani pamaso pake pa ulemerero wopanda cholakwa muli okondwa,
25 udu iti Kutelle cas unan tucubite nanya Yesu Kristi Ucif bite, liru, tigo nin likara uburnu nin nene, nin salingang. Usonani. (aiōn g165)
kwa Mulungu yekhayo, Mpulumutsi wathu, kwa Iye kukhale ulemerero, ukulu, mphamvu ndi ulamuliro, mwa Yesu Khristu Ambuye athu, kuyambira isanayambe nthawi, tsopano mpaka muyaya. Ameni. (aiōn g165)

< Yahuda 1 >