< 2 Yuhana 1 >

1 Uune kurti kulau na ina tarda nghe acara udu kitin ngantiwani ning nono me ule na ayi niyinghe duku ning kidegene na myeng cas ba, ning vat nale na idining kidegene.
Ndine mkulu wampingo, kulembera: Mayi wosankhidwa ndi Mulungu ndi kwa ana ake amene ndimawakonda mʼchoonadi. Ndipo sindine ndekha amene ndimawakonda, komanso onse odziwa choonadi.
2 Bara kidegeng ka na kidi nanya bite na kiba yitu nanya bite saligang. (aiōn g165)
Timakukondani chifukwa cha choonadi chimene chimakhala mwa ife ndipo chidzakhala mwa ife mpaka muyaya. (aiōn g165)
3 Ubolu Kutelle, nkunekune, ununku kibinai mayifu nang narik, unuzu Kutelle nin Yesu Kristi Gonon Cif nanya kidegen ning nan soning.
Chisomo, chifundo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi kwa Yesu Khristu, Mwana wa Atate, zikhale ndi ife mʼchoonadi ndi mʼchikondi.
4 Nlanzanmang midiya bara nang nsennang nono fe din cinu nanya kideene na tina seru adualele kitin ncif.
Ndinakondwera kwambiri nditapeza ana anu ena akuyenda mʼchoonadi, monga Atate anatilamulira.
5 Tutung indi likerafe nene, gantiwani na nafo nang na yertin lidu lipese kitife ba ana too na tina lanza mburne. Au wu titii usuu linwana.
Ndipo tsopano, amayi wokondedwa, sindikukulemberani lamulo latsopano koma lomwe lija takhala nalo kuyambira pachiyambi. Ine ndikukupemphani kuti tidzikondana wina ndi mnzake.
6 Usuuwere une auwu ti cinu dert ning nadume. Adumere alele, nafo na una lanza mburne auwu ucinu nanya ni.
Ndipo chikondi ndiye kuyenda momvera malamulo ake. Lamulo lake ndi lakuti mukhale moyo wachikondi monga munamva kuyambira pachiyambi.
7 Bara na anang rusuzu kiti gbardan nuzu nanya inye ale na inari yinu nin Yesu Kristi ku na adak nanya kidawo. Alelere among rusuzu kiti ning namong nari Kristi.
Ndikunena zimenezi chifukwa anthu ambiri onyenga, amene savomereza kuti Yesu Khristu anabwera monga munthu, akuyenda mʼdziko lapansi. Munthu aliyense otere ndi wonyenga ndiponso wokana Khristu.
8 Yejen atimine, auwu iwa dira imon ine vat na tina suu katwa we mang.
Chenjerani kuti mungataye chimene mwagwirira ntchito, koma chitani khama kuti mukalandire mphotho yanu yonse.
9 Ule na ame nya ubun na ayisina nanya ma dursuzu Kristi ba, na adining Kutelle ba. Ulena na yisna nanya madursuzuz adi nin cife nin Gonome.
Aliyense amene sasunga chiphunzitso cha Khristu, alibe Mulungu. Koma amene amasunga chiphunzitsochi, ameneyo alinso ndi Atate ndi Mwana.
10 Wase umong daa minu na daa nin dursuzu ulele ba na iwa serughe ba nanya ngamine ba, na i wa liseghe tutun ba.
Ngati wina aliyense abwera kwa inu osaphunzitsa zimenezi, musamulandire mʼnyumba mwanu kapena kumupatsa moni.
11 Ulena alisoghe amunu litme nin katwa ka nanzan.
Aliyense wolandira munthu wotere ndiye kuti akuvomerezana nazo ntchito zake zoyipa.
12 Indinin nimong gbardan na ima nyertinu minu nang dinin suu in nyertin ba nanya kubaga nin mmen ni nyert ba. Bara nani men din cisu kibinai ima dak tida suu uliru ti yerte ateumuro nin muro bara mmamng bite minan kulo kang.
Ndili nazo zambiri zoti ndikulembereni, koma sindikufuna kuzilemba mʼkalata. Mʼmalo mwake, ndikuyembekeza kufika kwanuko kuti tidzakambirane nanu pamaso ndi pamaso, potero chimwemwe chathu chidzakhala chathunthu.
13 Nonon ngwanafe unan feruwe din lisuu fi.
Ana a mlongo wanu wosankhidwa ndi Mulungu akupereka moni.

< 2 Yuhana 1 >