< 1 Yuhana 4 >

1 Kinnayi, na iwa yinin ni yeme fip ba, bara nanin dumuzunan koyeme nfip inin yene sa min Kutelleri, bara among anan kinu madk gbardan inani malu nuzu udu nanya nye.
Anzanga okondedwa, musakhulupirire mzimu uliwonse, koma yesani mizimu ngati ikuchokera kwa Mulungu, chifukwa aneneri onama ambiri afalikira mʼdziko lapansi.
2 Kikanere ima yinu Nfip Kutelle - nfip mona miyina Yesu Kristi na dak nanya kidawo minare min Kutelle.
Mungathe kuzindikira Mzimu wa Mulungu motere: Mzimu uliwonse umene umavomereza kuti Yesu Khristu anabwera mʼthupi, ndi wochokera kwa Mulungu,
3 Nin vat nfip mona miyinna nin Yesu ba na min Kutelleri ba. Monere infip ni vira Kristi, mona ina malin lanzu adin chinu, amin di nanya inye nene.
koma mzimu uliwonse umene suvomereza Yesu, siwochokera kwa Mulungu. Uwu ndi mzimu wa wokana Khristu umene munawumva kuti ukubwera ndipo ngakhale tsopano wabwera kale mʼdziko lapansi.
4 Anun un Kutelleri, nono ni nibebene, inamalin katu likara mine, bara ame ulena adi nanya bit akatin likara inle na adi nanya inye.
Inu ana okondedwa, ndinu ochokera kwa Mulungu ndipo mwawagonjetsa aneneri onyengawa, chifukwa Iye amene ali mwa inu ndi wamkulu kuposa amene ali mʼdziko lapansi.
5 Inin anan inyeri di, bara nani ilemon na ibele in inyeri di, uye din latiszu nanin.
Aneneri onyengawa ndi ochokera mʼdziko lapansi, nʼchifukwa chake amayankhula za dziko lapansi, ndipo dziko lapansi limawamvera.
6 Arik anan Kutelleri. Ulena yiru Kutelle ama latiszu nari. Bara nanere tima yinu infip min kidegen nin infip min kinu.
Ife ndi ochokera kwa Mulungu, ndipo aliyense amene amadziwa Mulungu amamvera zimene timayankhula. Koma aliyense amene sachokera kwa Mulungu samvera zimene timayankhula. Mmenemu ndiye mmene timasiyanitsira pakati pa mzimu wachoonadi ndi Mzimu wachinyengo.
7 Kinnayi, suu kogha ku ukauna, bara Kutelle ukaunari, vat ulena adini ukauna ina maru ghe kiti Kutelleri ani yiru Kutelle.
Anzanga okondedwa, tiyeni tikondane wina ndi mnzake, pakuti chikondi chimachokera kwa Mulungu. Aliyense amene ali ndi chikondi ndi mwana wa Mulungu ndipo amadziwa Mulungu.
8 Unit ulena adin suu ukauna ba na ayiru Kutelle ba, bara Kutelle ukaunari.
Aliyense amene alibe chikondi sadziwa Mulungu, chifukwa Mulungu ndiye chikondi.
9 Nani ukauna Kutellere ana durso nari, Kutelle na tuu gono me kirum nanya inye ti nan se ulau nuzu me.
Mmene Mulungu anaonetsera chikondi chake pakati pathu ndi umu: Iye anatumiza Mwana wake mmodzi yekha ku dziko lapansi kuti mwa Iyeyo tikhale ndi moyo.
10 Ai ukaunere ule, na arike ti din kauna Kutelle, amere na din suu bit, amini na tuu gono me bara alapi bit.
Chikondi ndi ichi: osati kuti ife ndife amene tinamukonda Mulungu, koma kuti Iyeyo ndiye amene anatikonda ndipo anatumiza Mwana wake kuti akhale nsembe yopepesera machimo athu.
11 Knnayi, andi Kutelle din suu bit kang, ariki wang tisu usuu nwana bit.
Anzanga okondedwa, popeza Mulungu anatikonda chotere, ifenso tiyenera kukondana wina ndi mnzake.
12 Na umomg nayene kutelle ba, andi tidinin suu li nwana bit Kutelle ma soo nanya bite nin usuu me mayitu nanya bit.
Palibe amene anaonapo Mulungu, koma tikakondana wina ndi mnzake, ndiye kuti Mulungu amakhala mwa ife ndipo chikondi chake chafika pachimake penipeni mwa ife.
13 Bara nanere tiyino tidi nanya me ame nanya bit, bara ana ni nari Nfip mi lau.
Ife tikudziwa kuti timakhala mwa Iye ndipo Iyeyo amakhala mwa ife chifukwa anatipatsa Mzimu wake.
14 Tina yene tinani ta suu ushaida ucife na tuu gone ayita unan tucu inye.
Ndipo taona ndipo tikuchitira umboni, kuti Atate anatuma Mwana wake kuti akhale Mpulumutsi wa dziko lapansi.
15 Vat ulena ayina Yesu gono Kutelleri, Kutelle di nanya me ame ma di nanya Kutelle.
Ngati aliyense avomereza kuti Yesu ndi Mwana wa Mulungu, Mulungu amakhala mwa iye ndipo iyeyo amakhala mwa Mulungu.
16 Tiyiru nin yinu sauyenu usuu me na Kutelle dimong nanya bi. Kutelle ukaunari, ulena adini ukauna ama suo nanya me, Kutelle ma suu nanya me.
Tikudziwa ndipo timadalira chikondi chimene Mulungu ali nacho pa ife. Mulungu ndiye chikondi. Aliyense amene amakhala moyo wachikondi, ali mwa Mulungu ndipo Mulungu amakhala mwa iye.
17 Ulel usuware mali tii likara nanya bit, tinan yita nikibinai salin feu mbungme nliri mawucuwuce, bara na adi, nanere tidi nanya nye.
Chikondi chafika pachimake penipeni pakati pathu, kotero kuti pa tsiku lachiweruzo tidzakhala olimba mtima chifukwa mʼdziko lapansi moyo wathu uli ngati wa Khristu.
18 Na ifeu di kiti nsuu ba. Bara usuu likar din kuo infeu piit, bara infeu di kusarin kpizu. Bara ulena adinin infeu na adini likara kitin suu ba.
Mulibe mantha mʼchikondi. Koma chikondi ndi changwiro chimachotsa mantha, chifukwa mantha amabwera chifukwa choopa chilango. Munthu amene ali ndi mantha, chikondi chake sichangwiro.
19 Tidinin suu bara Kutelle na chizu ussu bite.
Ife timakonda Mulungu chifukwa ndiye anayamba kutikonda.
20 Andi umong woro, “Adini suu Kutelle” amine nari gwaname, ame unan kinuwari. Bara ulana adinin suu gwana me ba naadin yejugye, iyizari ama yitu nin suu Kutelle ulena asa tabina uyenugye ba.
Ngati wina anena kuti, “Ine ndimakonda Mulungu,” koma namadana ndi mʼbale wake ndi wabodza ameneyo. Pakuti aliyense amene sakonda mʼbale wake, amene akumuona, sangathenso kukonda Mulungu amene sanamuone.
21 Tone tinare tidokoki tona tina se kitime: Ulena adinin suu Kutelle doleri ayita nin suu gwana me.
Ndipo Iye anatipatsa lamulo lakuti: Aliyense amene amakonda Mulungu ayenera kukondanso mʼbale wake.

< 1 Yuhana 4 >