< Mmɛbusɛm 3 >

1 Me ba, mma wo werɛ mfiri me nkyerɛkyerɛ, kora me mmara yi wɔ wʼakoma mu,
Mwana wanga, usayiwale malangizo anga, mtima wako usunge malamulo anga.
2 na ɛbɛma wo nkwa aware, mfeɛ bebree na ɛde yiedie abrɛ wo.
Ukatero zaka za moyo wako zidzachuluka ndipo udzakhala pa mtendere.
3 Mma adɔeɛ ne nokorɛ mfiri wo nkyɛn fa yane wo kɔn mu twerɛ gu wʼakoma ɛpono so.
Makhalidwe ochitira ena chifundo ndi owonetsa kukhulupirika asakuchokere. Uwamangirire mʼkhosi mwako ngati mkanda ndi kuwalemba pa mtima pako.
4 Na wobɛnya adom ne din pa wɔ Onyankopɔn ne nnipa anim.
Ukatero udzapeza kuyanja ndi mbiri yabwino pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Fa wʼakoma nyinaa to Awurade so na mmfa wo ho nto wʼankasa nteaseɛ so;
Uzikhulupirira Yehova ndi mtima wako wonse ndipo usadalire nzeru zako za kumvetsa zinthu.
6 hunu no wʼakwan nyinaa mu, na ɔbɛtene wʼakwan.
Pa zochita zako zonse uvomereze kuti Mulungu alipo, ndipo Iye adzawongola njira zako.
7 Nnye wo ho nni sɛ woyɛ onyansafoɔ suro Awurade na kyiri bɔne.
Usamadzione ngati wa nzeru. Uziopa Yehova ndi kupewa zoyipa.
8 Ɛde ahoɔden bɛbrɛ wo onipadua na ayɛ aduane ama wo nnompe.
Ukatero thupi lako lidzakhala la moyo wabwino ndi mafupa ako adzakhala olimba.
9 Fa wʼahonya hyɛ Awurade animuonyam, ne wo nnɔbaeɛ a ɛdi ɛkan nyinaa;
Uzilemekeza Yehova ndi chuma chako chonse; zokolola zonse zoyamba kucha uzilemekeza nazonso Yehova.
10 na ɛno na ɛbɛma wo pata ayɛ ma abu so, na nsã foforɔ abu afa wʼankorɛ so
Ukatero nkhokwe zako zidzadzaza ndi zinthu zambiri, ndiponso mitsuko yako idzadzaza ndi vinyo.
11 Me ba, sɛ Awurade tene wo so a, tie no yie, na sɛ ɔka wʼanim a, mpa aba,
Mwana wanga usanyoze malangizo a Yehova, ndipo usayipidwe ndi chidzudzulo chake.
12 Ɛfiri sɛ, obiara a Awurade pɛ nʼasɛm no, ɔtwe nʼaso, sɛdeɛ agya tene ɔba a ɔdɔ no so no.
Paja Yehova amadzudzula amene amamukonda, monga abambo achitira mwana amene amakondwera naye.
13 Nhyira nka onipa a ɔhunu nyansa, onipa a ɔnya nteaseɛ,
Wodala munthu amene wapeza nzeru, munthu amene walandira nzeru zomvetsa zinthu,
14 ɛfiri sɛ, nimdeɛ ho mfasoɔ sene dwetɛ, na deɛ ɛfiri mu ba sene sikakɔkɔɔ.
pakuti phindu la nzeru ndi labwino kuposa la siliva, phindu lakelo ndi labwino kuposanso golide.
15 Ne boɔ yɛ dene sene bota; na worentumi mfa wʼapɛdeɛ biara ntoto ho.
Nzeru ndi yoposa miyala yamtengowapatali; ndipo zonse zimene umazikhumba sizingafanane ndi nzeru.
16 Nkwa tenten wɔ ne nsa nifa mu; ahonyadeɛ ne animuonyam wɔ ne nsa benkum mu.
Mʼdzanja lake lamanja muli moyo wautali; mʼdzanja lake lamanzere muli chuma ndi ulemu.
17 Nʼakwan yɛ ahomeka, na nʼasa nyinaa yɛ asomdwoeɛ.
Njira zake ndi njira zosangalatsa, ndipo mu njira zake zonse muli mtendere.
18 Ɔyɛ nkwa dua ma wɔn a wɔsɔ ne mu; wɔn a wɔkura ne mu no bɛnya nhyira.
Nzeru ili ngati mtengo wopatsa moyo kwa oyigwiritsitsa; wodala munthu amene amayigwiritsa kwambiri.
19 Nyansa mu na Awurade yɛɛ asase fapem, na nteaseɛ mu na ɔde ɔsoro timii hɔ.
Yehova anakhazikitsa dziko lapansi pogwiritsa ntchito nzeru. Anagwiritsanso ntchito nzeru zakudziwa bwino zinthu pamene ankakhazikitsa zakumwamba.
20 Ɛfiri ne nimdeɛ mu na ɔkyekyɛɛ ebunu mu, na omununkum nso tɔɔ bosuo.
Mwa nzeru zake Yehova anatumphutsa madzi kuchokera mʼnthaka ndiponso mitambo inagwetsa mvula.
21 Me ba, fa atemmuo pa ne nhunumu sie, na mma ɛmfiri wʼani so;
Mwana wanga usunge nzeru yeniyeni ndi khalidwe lomalingarira zinthu bwino. Zimenezi zisakuchokere.
22 ɛbɛyɛ nkwa ama wo, ahyehyɛdeɛ a ɛma wɔ kɔn nya animuonyam.
Zimenezi zidzakupatsa moyo, moyo wake wosangalatsa ndi wabwino ngati mkanda wa mʼkhosi.
23 Afei wo kwan so bɛyɛ wo dwoodwoo, na wo nan rensunti;
Choncho udzayenda pa njira yako mosaopa kanthu, ndipo phazi lako silidzapunthwa;
24 sɛ woda a worensuro; sɛ woda a wʼani bɛkum.
pamene ugona pansi, sudzachita mantha; ukadzagona pansi tulo tako tidzakhala tokoma.
25 Nsuro mpofirim amanehunu anaa ɔsɛeɛ a ɛba amumuyɛfoɔ so,
Usaope tsoka lobwera mwadzidzidzi kapena chiwonongeko chimene chidzagwera anthu oyipa,
26 Ɛfiri sɛ, Awurade bɛyɛ wʼawerɛhyɛm na ɔbɛkora wo nan afiri afidie mu.
pakuti Yehova adzakulimbitsa mtima ndipo adzasunga phazi lako kuti lisakodwe mu msampha.
27 Mfa ade pa nkame wɔn a wɔfata, ɛberɛ a tumi wɔ wo nsam.
Usaleke kuchitira zabwino amene ayenera kulandira zabwino, pamene uli nazo mphamvu zochitira zimenezi.
28 Nka nkyerɛ wo yɔnko sɛ: “Kɔ na bra; mede bɛma wo ɔkyena” wɔ ɛberɛ a wowɔ no saa ɛberɛ no.
Usanene kwa mnansi wako kuti, “Pita, uchite kubweranso. Ndidzakupatsa mawa” pamene uli nazo tsopano.
29 Mpam ɔhaw mma wo yɔnko ɛberɛ a ɔne wo te yie.
Usamukonzere chiwembu mnansi wako, amene anakhala nawe pafupi mokudalira.
30 Mfa ɛso nto obi so kwa ɛberɛ a ɔnyɛɛ wo bɔne biara.
Usakangane ndi munthu wopanda chifukwa pamene iye sanakuchitire zoyipa.
31 Mma wʼani mmere basabasayɛfoɔ, na mfa nʼakwan no mu biara,
Usachite naye nsanje munthu wachiwawa kapena kutsanzira khalidwe lake lililonse.
32 ɛfiri sɛ Awurade kyiri basabasayɛfoɔ na ɔde ne werɛ hyɛ ɔteneneeni mu.
Pakuti Yehova amanyansidwa ndi munthu woyipa koma amayanjana nawo anthu olungama.
33 Awurade nnome wɔ omumuyɛfoɔ efie so, na ɔhyira ɔteneneeni fie.
Yehova amatemberera nyumba ya munthu woyipa, koma amadalitsa nyumba ya anthu olungama.
34 Ɔdi fɛdifoɔ a wɔyɛ ahantan ho fɛ na ɔdom ahobrɛasefoɔ.
Anthu onyoza, Iye amawanyoza, koma amakomera mtima anthu odzichepetsa.
35 Anyansafoɔ bɛnya animuonyam adi, nanso nkwaseafoɔ deɛ, ɔma wɔn anim gu ase.
Anthu anzeru adzalandira ulemu, koma zitsiru adzazichititsa manyazi.

< Mmɛbusɛm 3 >