< Nnwom 121 >

1 Ɔsoroforo dwom. Mema mʼani so kyerɛ mmepɔw no, ɛhe na me mmoa fi bɛba?
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
2 Me mmoa fi Awurade, ɔsoro ne asase yɛfo no.
Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
3 Ɔremma wo nan nwatiri, nea ɔhwɛ wo no rentɔ nko.
Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
4 Ampa ara, nea ɔhwɛ Israel no rentɔ nko na ɔrenna.
Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
5 Awurade hwɛ wo so; Awurade ne wo nwini wɔ wo nsa nifa so;
Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
6 Owia rensɛe wo wɔ adekyee mu, na ɔsram nso rensɛe wo anadwo.
Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
7 Awurade bɛbɔ wo ho ban afi ɔsɛe nyinaa ho, ɔbɛhwɛ wo nkwa so;
Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
8 Awurade bɛhwɛ wʼadifi ne wo fieba so mprempren ne daa.
Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.

< Nnwom 121 >